< 1 Samueli 17 >

1 Afilisti anasonkhanitsa ankhondo awo ku Soko mʼdziko la Yuda. Iwo anamanga misasa yawo ku Efesi-Damimu, pakati pa Soko ndi Azeka.
培肋舍特人調集了軍隊,準備作戰,集合在猶大,在索苛與阿則卡之間的厄斐斯達明紮了營。
2 Sauli ndi Aisraeli anasonkhana namanga misasa mʼchigwa cha Ela ndipo anandandalitsa ankhondo kuti amenyane ndi Afilisti.
撒烏耳和以色列人齊集起來,在厄拉谷紮了營,擺陣準備迎擊培肋舍特人。
3 Afilisti anali phiri lina ndipo Aisraeli analinso phiri lina, ndipo pakati pawo panali chigwa.
培肋舍特人站在這邊一座山上,以色列人站在那邊一座山上,中間隔著山谷。
4 Tsono munthu wina wamphamvu, dzina lake Goliati wochokera ku Gati anatuluka ku misasa ya Afilisti. Msinkhu wake unali pafupipafupi mamita atatu.
從培肋舍特人陣地中走出一個挑戰的人,名叫哥肋雅,是加特人,身高六肘又一柞,
5 Iye ankavala chipewa chamkuwa ndi malaya achitsulo olemera makilogalamu 57.
頭帶銅盔,身穿鎧衣,鎧衣的重銅重五千「協刻爾」,
6 Ankavalanso zokuta miyendo yake zamkuwa, ndipo ankanyamula nthungo ya mkuwa pa phewa pake.
腿裹銅葉,肩插銅槍。
7 Thunthu la mkondo wake linali ngati mkombero wowombera nsalu, ndipo mutu wa mkondowo unkalemera makilogalamu asanu ndi awiri. Patsogolo pake pamakhala munthu wonyamula zida zake za nkhondo.
矛桿像織布機的大軸,矛頭重六百「協刻爾」;有個持盾的人給他開道。
8 Goliatiyo anayimirira ndi kufuwula kwa ankhondo a Israeli, nati, “Nʼchifukwa chiyani mwakonzekera nkhondo chotere? Kodi sindine Mfilisiti ndipo inu sindinu akapolo a Sauli? Sankhani munthu kuti abwere kwa ine.
他站在以色列人的陣地前,喊說:「你們為什麼出來擺陣作戰﹖我不是培肋舍特人嗎﹖你們不是撒烏耳的奴才嗎﹖你們挑選一人,下來同我對敵!
9 Ngati angathe kumenyana nane ndi kundipha, ife tidzakhala akapolo anu, koma ngati ine ndimugonjetsa ndi kumupha, inu mudzakhala akapolo athu ndi kumatitumikira.”
假使他能同我決鬥,殺了我,我們就作你們的奴隸;但是,如果我得勝,殺了他,你們就應服事我們,作我們的奴隸」。
10 Ndipo Mfilisitiyo anati, “Bwerani lero timenyane basi! Patseni munthu kuti ndimenyane naye.”
那培肋舍特人還說:「今天我向以色列罵陣,你們給我個人來,讓我們彼此決鬥」。
11 Atamva mawu a Mfilisitiyo, Sauli ndi Aisraeli onse anataya mtima nachita mantha kwambiri.
撒烏耳和全以色列聽見那培肋舍特說的這些話,都非常驚慌害怕。
12 Davide anali mwana wa munthu wa fuko la Efurati dzina lake Yese amene amachokera ku Betelehemu mʼdziko la Yuda. Yese anali ndi ana aamuna asanu ndi awiri. Pa nthawi ya Sauli nʼkuti ali wokalamba.
達味是猶大白冷的一個厄弗辣大人的兒子,那人名叫葉瑟,他有八個兒子。此人在撒烏耳時,已經老了。
13 Ana atatu oyamba kubadwa a Yese nʼkuti atapita nawo ku nkhondo pamodzi ndi Sauli. Woyamba dzina lake anali Eliabu, wachiwiri anali Abinadabu, ndipo wachitatu anali Sama.
葉瑟的三個大兒已跟撒烏耳出征作戰;從軍的三個兒子:長子叫厄里雅布,次子名叫阿彼納達布,三子名叫沙瑪。
14 Davide ndiye anali mzime. Ana aakulu atatuwo ndiwo anapita ku nkhondo ndi Sauli.
達味最小,三個年長的已跟撒烏耳出征。
15 Koma Davide ankapita ku misasa ya Sauli ndi kubwerako kuti azikaweta nkhosa za abambo ake ku Betelehemu.
達味有時服侍撒烏耳,有時離開,回白冷放父親的羊。
16 Kwa masiku makumi anayi, Mfilisiti uja ankabwera mmawa ndi madzulo kumadzionetsera.
那培肋舍特人早晨晚上常出來挑戰,一連四十天之久。
17 Tsiku lina Yese anawuza mwana wake Davide kuti, “Atengere abale ako makilogalamu khumi a tirigu wokazinga ndi malofu a buledi khumi ndipo upite nazo mofulumira ku misasa yawo.
葉瑟對他的兒子達味說:「你給你哥哥們帶去這一「厄法」炒麥和十個餅,快往營裏給你哥哥們送去。
18 Utengerenso wolamulira wa gulu lawo tchizi khumi uyu. Ukaone mmene abale ako akukhalira ndipo ubwere ndi kanthu kosonyeza kuti ali bwino.
將這十塊奶餅送給千夫長.然後看望你的哥哥們是否平安,並把他們的薪俸帶回來。
19 Sauli, abale akowo ndi asilikali onse a Israeli ali ku chigwa cha Ela, akumenyana ndi Afilisti.”
他們與撒烏耳和全以色列人都在厄拉谷,同培肋舍特人作戰」。
20 Mʼmamawa mwake Davide anasiya nkhosa mʼmanja mwa munthu wina ndipo anatenga zakudyazo nanyamuka monga momwe Yese abambo ake anamulamulira. Anakafika ku misasa pamene asilikali ankapita kukandanda pa mzere ku nkhondo, nʼkufuwula mfuwu wankhondo.
達味清早起來,把羊群托給一個看羊的人,就照他父親葉瑟吩咐的起身去了。他來到營中時,軍隊正出來擺陣,喊著衝鋒的口號。
21 Aisraeli ndi Afilisti anandanda pa mzere wankhondo moyangʼanana.
以色列人和培肋舍特人列陣相對。
22 Tsono Davide anasiyira zakudya zija munthu wosunga katundu nathamangira kumene kunali ankhondo kuja ndi kukalonjera abale ake.
達味把自己的行囊交給一個看守輜重兵的1 內,跑入陣內,向他的哥哥們問安。
23 Pamene iye ankayankhula nawo anangoona Goliati wa ku Gati uja akuchoka pa mzere wa Afilisti akufuwula mawu onyoza monga mwa masiku onse, ndipo Davide ankawamva.
當他和他們談話時,名叫哥肋雅的挑戰者,──加特的培肋舍特人──從培肋舍特人的陣裏上來,說了以所述的話,達味聽見了。
24 Aisraeli ataona munthuyo, anamuthawa ndi mantha aakulu.
所有的以色列人一看見那人,都非常害怕,便由他面前逃避了。
25 Ndipo Aisraeli ankanena kuti, “Kodi mwamuona munthu akubwerayo? Iye amangobwera kudzanyoza Israeli. Tsono mfumu inati kuti idzapereka chuma chambiri kwa munthu amene adzamuphe. Idzaperekanso mwana wake wamkazi kuti amukwatire ndiponso banja la abambo ake silidzaperekanso msonkho mu Israeli.”
那時有個以色列人宣佈說:「你們看見了上來的這人嗎﹖這人上來是辱罵以色列。若有人把他殺死,君王要賜給他許多財富,將自己是女兒嫁給他為妻,並使他的父家在以色列內豁免繳稅」。
26 Davide anafunsa anthu amene anayima pafupi naye kuti, “Kodi adzamuchita chiyani munthu amene adzapha Mfilisiti uyu ndi kuchotsa chitonzo pakati pa Israeli? Mfilisiti wosachita mdulidweyu ndi ndani kuti azinyoza gulu lankhondo la Mulungu wamoyo?”
達味問站在他旁邊的人說:「殺死這培肋舍特人,給以色列雪恥的人得什麼賞﹖這未受割損培肋舍特人是誰﹖他竟敢辱罵永生天主的軍旅! 」
27 Anthu anamuwuzanso zonse zimene mfumu inanena kuti idzachitira munthu amene adzapha Mfilisitiyo.
人就把上邊那些話告訴他說:「殺死這人的,要得這樣這樣的報酬」。
28 Eliabu, mkulu wake wa Davide, atamumva akuyankhula ndi anthuwo, anamukwiyira ndipo anamufunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani wabwera kuno? Ndipo wasiyira yani nkhosa zochepazo mʼchipululu? Ndikudziwa kuti ndiwe wodzikuza ndiponso woyipa mtima. Unabwera kuno kuti udzaonere nkhondo.”
他的大哥厄里雅布一聽見達味對那些人所說的話,便對達味大發憤怒說:「你為什麼下來﹖你在曠野中放的那幾隻羊,託給了誰﹖我知道你驕傲,心中不懷好意;你下來只是要看作戰」。
29 Davide anati, “Kodi ndachita chiyani ine? Kodi ndisamayankhule?”
達味回答說:「我究竟作的什麼不對﹖連句話也不能說嗎﹖」
30 Ndipo anamuchokera napita kwa munthu wina ndipo anamufunsa nkhani yomweyo, ndipo anthu anamuyankha iye monga poyamba paja.
達味就離開那裏,到了另一處,又問了同樣的事,人回答的話也和先前一樣。
31 Mawu amene Davide anayankhula atamveka, anthu anakafotokozera Sauli ndipo Sauli anamuyitanitsa.
有人聽見了達味說的話,就去報告給撒烏耳;撒烏耳就命他前來。
32 Davide anati kwa Sauli, “Munthu aliyense asataye mtima chifukwa cha Mfilisitiyu. Ine kapolo wanu ndipita kukamenyana naye.”
達味對撒烏耳說:「請我主不必為那人而沮喪,你僕人要去同這培肋舍特人決鬥」。
33 Sauli anayankha Davide kuti, “Iwe sungathe kupita kukamenyana ndi Mfilisitiyu. Iwe ukanali mnyamata, koma iyeyu ndi amene wakhala akumenya nkhondo kuyambira unyamata wake.”
撒烏耳對達味說:「你不能去對抗這培肋舍特人,同他決鬥,因為你還年輕,而他自幼便是習於戰鬥的人」。
34 Koma Davide anati kwa Sauli, “Kapolo wanune ndinkaweta nkhosa za abambo anga. Ndipo mkango kapena chimbalangondo chikamabwera ndi kugwira mwana wankhosa pakati pa nkhosazo,
達味回答撒烏耳說:「你的僕人是為他父親牧羊的人,幾時有獅子或狗熊闖來,由羊群中奪去一隻羊,
35 ine ndinkatsatira ndi kupha chirombocho. Choncho ndinkapulumutsa mwana wankhosa uja mʼkamwa mwake. Ndipo chinkati chikandiwukira, ine ndinkagwira tchowa lake, nʼkuchikantha mpaka kuchipha.
我就追上去,打死牠,從牠口中救出那隻來;假使獅子起來撲我,我就抓住牠的鬚,將牠打死。
36 Ine kapolo wanu ndinapha mkango ngakhalenso chimbalangondo. Tsono Mfilisiti wosachita mdulidweyu adzaphedwa monga zinazo chifukwa wanyoza ankhondo a Mulungu wamoyo.
你的你的僕人連獅子帶狗熊都打死了,這未受割損的培肋舍特人也不過像其中的一個,因為他竟敢辱罵永生天主的軍旅」。
37 Yehova amene anandilanditsa mʼkamwa mwa mkango ndi chimbalangondo adzandilanditsa mʼmanja mwa Mfilisiti uyu.” Sauli anati kwa Davide, “Pita, ndipo Yehova akhale nawe.”
達味又接著說:「由獅子和狗熊中拯救我的上主,也必從這培肋舍特人手中拯救我」。撒烏耳對達味說:「去吧! 望上主與你同在! 」
38 Ndipo Sauli anamveka Davide mwinjiro wake. Anamuveka zovala zankhondo ndi chipewa cha mkuwa.
撒烏耳給達味穿上自己的武裝,給他頭上帶上銅盔,身上穿上鎧甲,
39 Davide anamangirira lupanga pa mwinjirowo. Atayesa kuyenda nazo, analephera chifukwa anali asanazizolowere. Iye anati kwa Sauli, “Sindingathe kuyenda nazo chifukwa sindinazizolowere.” Ndipo anazivula.
又在鎧甲上偑上自己的刀。達味試走了兩步,因他沒有穿慣,遂對撒烏耳說:「穿戴這些東西,不能行動,因為先前總沒有穿過」。所以他又將盔甲從身上脫下。
40 Pambuyo pake anatenga ndodo yake mʼmanja. Kenaka anasankha miyala yosalala bwino mu mtsinje ndi kuyiika mʼthumba lake la ku ubusa. Legeni ili mʼmanja mwake, Davide ananyamuka kukakumana ndi Mfilisiti uja.
達味手裏拿著自己的棍子,在河裏揀了五塊很光滑的石頭,放在牧童隨身所帶的袋子內,即裝石囊內,手內拿著投石器,向那培肋舍特人走去。
41 Tsono Mfilisiti uja anayambapo kupita kumene kunali Davide, mnyamata wonyamula zida zake za nkhondo ali patsogolo pake.
那培肋舍特人也大搖大擺走近了達味,給他持盾的走在他開路。
42 Mfilisitiyo atangomuona Davide, anamunyoza popeza kuti Davide anali mnyamata chabe wofiirira ndi wa maonekedwe abwino.
那培肋舍特人瞪眼一看,見了達味,遂看不起他,因達味還很年輕,面色紅潤,眉清目秀。
43 Iye anati kwa Davide, “Kodi ndine galu, kuti ubwere kwa ine ndi ndodo?” Ndipo Mfilisitiyo anamutemberera Davide potchula mayina a milungu yake.
那培肋舍特人對達味說:「莫非我是隻狗,你竟拿棍子來對付我﹖」達味回答說:「你比一隻狗還不如! 」那培肋舍特人就指著自己的神詛咒達味,
44 Iye anatinso, “Bwera kuno ndipo ndidzapereka mnofu wako kwa mbalame zamlengalenga ndi kwa zirombo zakuthengo!”
且對達味說:「你到我這裏來,我要把你的肉,給空中的飛鳥和田野的走獸吃」。
45 Koma Davide anati kwa Mfilisitiyo, “Iwe wabwera kwa ine ndi lupanga, mkondo ndi nthungo, koma ine ndikubwera kwa iwe mʼdzina la Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa ankhondo Aisraeli amene iwe ukuwanyoza.
達味回答那培肋舍特說:「你仗著刀槍箭戟來對付我,但我是仗著你所淩辱的萬軍的上主,以色列的天主的聖名來對付你。
46 Anatinso lero lino Yehova adzakupereka mʼmanja mwanga. Ndidzakukantha ndi kudula mutu wako. Ndidzapereka mitembo ya asilikali a Afilisti kwa mbalame za mlengalenga, ndi kwa zirombo zakuthengo ndipo dziko lonse lapansi lidzadziwa kuti mu Israeli muli Mulungu.
今天上主定把你交在我手中,我必打死你割下你的頭來;今天我要把你的屍體和培肋舍特軍人的屍體,給空中的飛鳥和田野的走獸吃:這樣:全地都要知道在以色列有天主。
47 Onse amene asonkhana pano adzadziwa kuti Mulungu sapulumutsa anthu ndi lupanga kapena mkondo, pakuti nkhondo ndi ya Yehova. Iye adzakuperekani mʼmanja mwathu.”
在埸的眾人也要知道,上主不賴刀槍賜人勝利,戰爭勝負只屬於上主,衪已把你們交我們手中了」。
48 Mfilisitiyo akusendera pafupi kuti akumane naye, Davideyo anathamangira mofulumira ku mzere wa nkhondo kukakumana naye.
正當那培肋舍特人起身,大搖大擺向達味走來時,達味趕快由陣中跑出來,迎那培肋舍特人;
49 Davideyo anapisa dzanja lake mʼthumba lake natengamo mwala ndipo anawuponya, nalasa pa mphumi pa Mfilisitiyo. Mwalawo unalowa pa chipumi chake, ndipo anagwa chafufumimba.
同時伸手,由囊中取出一塊石頭,套在投石器上打過去,正打在那培肋舍特人的額上,石頭穿入額內,那人就跌倒在地上。
50 Kotero Davide anamupambana Mfilisitiyo pomugenda ndi mwala wa legeni ndi kumupha. Mʼmanja mwa Davide munalibe lupanga.
如此,達味用投石器和石頭,得勝了那培肋舍特人,打中了他,將他殺死,雖然手無寸鐵。
51 Davide anathamanga nakayimirira pamwamba pa Mfilisiti uja. Anasolola lupanga lake lomwe moyikamo mwake, namupha pomudula mutu wake. Afilisti ataona kuti ngwazi yawo yafa, anathawa.
達味遂跑過去,站在培肋舍特人身上,拿起他的刀,從鞘內拔出,殺了他,砍下他的頭。所有培肋舍特人看見他們的英雄死了,就囡散奔逃。
52 Ndipo Aisraeli ndi anthu a ku Yuda ananyamuka, ndipo akufuwula anathamangitsa Afilisti aja mpaka ku Gati ndi ku zipata za Ekroni. Anthu akufa awo amagwa njira yonse ya ku Saaraimu mpaka ku Gati ndi ku Ekroni.
以色列人和猶大人就起來吶喊,追擊培肋舍特人直到加特關,直到厄刻龍城門。沿沙阿辣因的路上,直到加特和厄刻龍,遍地是培肋舍特人的屍首。
53 Aisraeli anabwerako kothamangitsa Afilisti kuja ndipo anadzatenga zonse zimene zinali mʼmisasa ya Afilistiwo.
以色列人追殺培肋舍特人回來,又搶劫了他們的幕。
54 Pambuyo pake Davide anatenga mutu wa Mfilisitiyo napita nawo ku Yerusalemu, koma anayika zida za Mfilisitiyo mu tenti yake.
以後,達味取了那培肋舍特人的頭,送到耶路撒冷;至於那人的武器,卻放在會幕內。
55 Sauli ataona Davide akupita kukakumana ndi Mfilisitiyo anafunsa Abineri, mkulu wa ankhondo kuti, “Abineri, kodi mnyamatayu ndi mwana wa yani?” Abineri anayankha kuti, “Ndithu mfumu muli apa ine sindikumudziwa.”
當撒烏耳看見達味去和那培肋舍特人迎戰時,就問統帥阿貝乃爾說:「阿貝乃爾,這少年人是誰的兒子﹖」阿貝乃爾回答說:「大王萬歲,我不知道」。
56 Mfumu inati, “Pita kafufuze kuti mnyamata ameneyu ndi mwana wa yani.”
君王說:「你查一下,這少年人是誰的兒子﹖」
57 Davide atangobwerako kokapha Mfilisiti kuja, Abineri anamutenga nabwera naye kwa Sauli, mutu wa Mfilisiti uja uli mʼmanja mwake.
達味殺死那培肋舍特人回來時,阿貝乃爾帶他去見撒烏耳,他手中還拿著那培肋舍特人的頭。
58 Sauli anamufunsa, “Mnyamata iwe, kodi paja ndiwe mwana wayani?” Davide anati, “Ndine mwana wa mtumiki wanu Yese wa ku Betelehemu.”
撒烏耳問他說:「少年人你是誰的兒子﹖」達味答說:「我是你僕白冷人葉瑟的兒子」。

< 1 Samueli 17 >