< 1 Samueli 15 >

1 Samueli anawuza Sauli kuti, “Yehova anandituma ine kuti ndikudzozeni kukhala mfumu ya anthu ake, Aisraeli. Tsopano imvani zimene Yehova akunena.
Şamuelee Şauluk'le eyhen: – Rəbbee zı g'axuvuna, q'ış qadğu vake Cune milletıs İzrailis paççah ha'as. Həşde ğu Rəbbee eyhençıl k'ırı alixhxhe.
2 Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndidzalanga Aamaleki chifukwa cha zimene anawachita Aisraeli. Paja iwo analimbana ndi Aisraeli pa njira pamene Aisraeliwo ankachoka ku Igupto.
Xəəne G'oşunbışde Rəbbee, inıd eyhe: «İzrailybı Misireençe əlyhəəmee, Amalekaaşe manbışda yəq avqu. Zı mançil-alla manbışilqa yiğbı allya'as.
3 Tsopano pita kathire nkhondo Aamaleki ndi kuwononga kwathunthu zinthu zonse zimene ali nazo. Musakasiyeko munthu ndi mmodzi yemwe. Mukaphe amuna ndi akazi, ana ndi makanda, ngʼombe ndi nkhosa, ngamira ndi abulu.’”
Hoora, hark'ın Amalekaar gyapxe. Manbışiqa vodunmeen gırgın kar giyxvər he'e, coyub oot'al-ooxal he'e. Manbı qivmiykkan, manbışin adamerıb, yedarıb, uşaxarıb, gyooqanbıb gyapt'e. Manbışin yatsbıd, vəq'əbıd, devabıd, əməlerıd gyat'e».
4 Kotero Sauli anayitana ankhondo ake nawawerenga ku Telaimu. Ankhondo oyenda pansi analipo 200,000 ndipo mwa iwowa 10,000 anali a fuko la Yuda.
Şaulee millet qot'ul, manbı Telaim eyhene şaharee qəbəqqənbı: maa'ar q'öd vəş aazır İzrailyne eskerıle hexxana, Yahudeeşina yits'ıd aazır eskerır eyxhena.
5 Sauli anapita ku mzinda wa Aamaleki nawubisalira mʼkhwawa.
Şaul Amalekaaşine şaharısqana qarı, maane q'adaalil manbı gyapt'asva dyugul eyxhe.
6 Tsono Sauli anawuza Akeni kuti, “Samukani, muchoke pakati pa Aamaleki kuti ine ndisakuwonongeni pamodzi ndi iwo pakuti inu munaonetsa kukoma mtima kwa Aisraeli onse pamene ankatuluka mʼdziko la Igupto,” Choncho Akeni anachoka pakati pa Aamaleki.
Mang'vee Genbışik'le eyhen: – Amalekaaşisse hudoora, manbışike cureepxhe. Şunab manbışika sacigee gidyapt'as. Şu, İzrailybı Misirğançe qığəəmee, manbışis yugvallaniy hav'u. Genbı Amalekaaşike cureepxha avayk'ananbı.
7 Tsono Sauli anakantha Aamaleki kuchokera ku Havila mpaka ku Suri, kummawa kwa Igupto.
Şaul Xavila eyhene şahareençe girğıl, Misirne şargılyne Şur eyhene şaharılqamee Amalekbı gyabat'a ıxha.
8 Sauli anatenga Agagi mfumu ya Aamaleki, koma anthu ake onse anawapha ndi lupanga.
Mang'vee Amalekaaşina paççah Agag üç'ürra aqqaqqa, mang'un milletmee, gırgıda g'ılıncıke alğayhe.
9 Koma Sauli ndi ankhondo ake sanaphe Agagi, sanaphenso nkhosa ndi ngʼombe zabwino ngakhalenso ana angʼombe ndi ana ankhosa onenepa. Chilichonse chimene chinali chabwino sanachiphe. Koma zonse zimene zinali zoyipa ndi zachabechabe anaziwononga.
Amalekaaşina paççah Agagiy manbışin nekke yugun vəq'əbı, yatsbı, kokuiyn q'ıkariy urgbı Şaulusiy cune milletıs qiykkın, gyat'u ak'an ha'a deş. Amalekaaşin gıranın, yugun karbıd manbışis qiykkın, haq'var-hiyxvər ha'as ıkkiykan deş. Nimeeniy Amalekaaşiqa karaı'dəən, pisın kar vod İzrailybışe giyxvər hı'ı ak'an ha'an.
10 Kenaka Yehova anawuza Samueli kuti,
Mane gahıl Rəbbee Şamuelik'le inəxüd eyhe:
11 “Ine ndikumva chisoni chifukwa ndinayika Sauli kukhala mfumu. Wabwerera mʼmbuyo, waleka kunditsata ndipo sanamvere malangizo anga.” Samueli anapsa mtima, ndipo analira kwa Yehova usiku wonse.
– Zı Şauluke paççah hı'ı paşmanxhana. Mang'vee Zalqa yı'q' sak'al hı'ı, Yizın cuvab ç'iyelqa g'a'aççu. Mançike Şamuelis qəl vuxha, xəmvolle Rəbbilqa düə haa'a.
12 Samueli anadzuka mmamawa ndipo anapita kukakumana ndi Sauli. Koma anthu anamuwuza kuti, “Sauli anabwera ku Karimeli, ndipo kumeneko wadziyimikira mwala wachikumbutso cha iye mwini. Tsopano wachokako ndipo wapita ku Giligala.”
Şamuel miç'eeqana Şaul g'acesva suğotsumee, mang'uk'le şavame eyhen: – Şaul Karmel eyhene şahareeqa ark'ın. Maa'ab mang'vee, cus haykal gyuvxhu, mançer Gilgalqa ayk'an.
13 Samueli atamupeza Sauli, Sauliyo anati kwa Samueli, “Yehova akudalitseni! Ndachita zonse zimene Yehova analamula.”
Şamuel Şauluqa avarq'ılymee, Şaulee eyhen: – Hasre Rəbbee vas xayir-düə hevlecen! Zı Rəbbee eyhen hı'iyn.
14 Koma Samueli anati, “Nanga bwanji ndikumva kulira kwa nkhosa ndi ngʼombe?”
Şamueleeme mang'uk'le eyhen: – Nya'a manke yizde k'ıriysqa vəq'əbışiniy yatsbışin heghan sesbı qöö?
15 Sauli anayankha, “Zimenezi Asilikali azitenga kuchokera kwa Aamaleki. Iwo anasungako nkhosa ndi ngʼombe zabwino kuti akapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu, koma zina zonse anaziwononga.”
Şaulee eyhen: – Manbı Amalekaaşike adı. Milletıs vəq'əbıyiy yatsbı qiykkıniynbı, manbışe inekke yugunbı Rəbbis, yiğne Allahıs, q'urbanna allya'as havacı. İnsanar gyapt'ıynbı, mansa axuyn karbımee giyxvər hı'ı.
16 Koma Samueli anati kwa Sauli, “Khala chete! Ima ndikuwuze zimene Yehova wandiwuza usiku wathawu.” Sauli anayankha kuti, “Ndiwuzeni.”
Şamuelee Şaulık'le eyhen: – Ç'əv, g'iyna xəmde Rəbbee zak'le uvhuyn, zı vak'le eyhes. Şaulee, «Eyheva» cuvab qele.
17 Apo Samueli anati, “Munali wamngʼono pa maso pa anthu, koma tsopano mwasanduka mtsogoleri wa mafuko a Israeli. Yehova anakudzozani kuti mukhale mfumu yolamulira Aisraeli.
Şamuelee eyhen: – Ğucar vasqa k'ırra qööng'ə, nya'a vake İzrailyne nasılbışda xərna ıxha dişde? Rəbbee, q'ış qadğu, vake İzrailyna paççah hı'ı dişde?
18 Ndipo Yehova anakutumani kuti, ‘Pitani mukawononge kwathunthu Aamaleki, anthu oyipa aja. Mukachite nawo nkhondo mpaka kuwatheratu.’
Rəbbee ğu g'ıxelemee, inva dişde uvhu: «Hark'ın bınahıka gyavts'uyne milletıkın Amalekaaşikın he'e, manbı gırgıba gyapt'e. Manbışde gırgınbışikın ha'asdesmee, dəv'ə hee'e».
19 Chifukwa chiyani simunamvere mawu a Yehova? Chifukwa chiyani munathamangira zofunkha ndi kuchita choyipira Yehova?”
Nya'a ğu Rəbbil k'ırı ilydiyxhı? Manbışike g'ayşuyne karal qıxha, Rəbbee ilydyaat'asın kar hı'ı?
20 Koma Saulo anawuza Samueli kuti, “Ine ndinamveradi mawu a Yehova. Ndinapita kukachita zimene Yehova anandituma. Ndinabwera naye Agagi, mfumu ya Amaleki, koma Aamaleki ena onse anaphedwa.
Şaulee Şamuelik'le eyhen: – Zı Rəbbee eyhençil k'ırı gyaqqıyn. Mang'vee eyhene cigeeqa hark'ınna. Manbışda paççah Agag aqqı inyaqa qarı, gırgın Amalekbı gyapt'ıynbı.
21 Koma pa zofunkhazo anthu anatengapo nkhosa, ngʼombe ndi zabwino zina zoyenera kuwonongedwa kuti akapereke ngati nsembe kwa Yehova Mulungu wanu ku Giligala.”
Saccu eskeraaşe şenbışike g'ayşuyne çavra-vəq'əyke, gyat'u ak'an ha'asınçike, nekke yugun yatsbıyiy vəq'əbı g'əyxı' Rəbbis, yiğne Allahıs, Gilgalee q'urbanbı allya'asva havacı.
22 Koma Samueli anayankha kuti, “Kodi Yehova amakondwera ndi nsembe zopsereza ndi nsembe zina kapena kumvera mawu a ake? Taona, kumvera ndi kwabwino kuposa nsembe, ndipo kutchera khutu ndi kwabwino kuposa kupereka mafuta a nkhosa.
Şamueleeme mang'uk'le eyhen: – Gyoxhxhan ha'aneyiy menne q'urbanbışile geed, Rəbbis Cune cuvabıl k'ırı alixhxhıniy ıkkan. Rəbbine cuvabıl k'ırı alixhxhiy, q'urbanbışileeyiy nekke kokun g'argbışile nimeexheyid yugdaniy vod.
23 Pakuti kuwukira kuli ngati tchimo lowombeza, ndipo kukhala nkhutukumve kuli ngati tchimo lopembedza mafano. Chifukwa mwakana mawu a Yehova. Iyenso wakukana kuti iweyo ukhale mfumu.”
Rəbbee eyhen hidi'iyna bınah, cadubı hı'iyna xhineecab vob. Culed-alqan karbı hı'iyid, byuttyaaşis ı'bəədat ha'an xhineecad vod. Ğu Rəbbin cuvab əq'əna qı'ı, Mang'veeyir ğu paççahiyvalike hı'ı.
24 Tsono Sauli anati kwa Samueli, “Ine ndachimwa. Ndaphwanya malamulo a Yehova ndiponso malangizo anu. Ndinkaopa anthu ndipo ndinawamvera.
Şaulee Şamuelik'le eyhen: – Zı bınah hav'u, Rəbbine əmrıliy, yiğne cuvabıl k'ırı ilydiyxhı. Zı yizde g'oşunule qərq'ı'nna, dişe manbışil k'ırı alixhxhı.
25 Tsopano ndikukupemphani, khululukireni tchimo langa ndipo mubwerere nane kuti ndikapembedze Yehova.”
Hucoona ixhes, həşde ğu yizde bınahıle ilyheç'e, qora zaka yıq'əlqa sak'le, zı Rəbbis ı'bəədat ha'as.
26 Koma Samueli anawuza Sauli kuti, “Ine sindibwerera nawe. Inu mwakana mawu a Yehova. Choncho Iyenso wakukanani kuti musakhale mfumu yolamulira Aisraeli.”
Şamuelee Şauluk'le eyhen: – Zı vaka sak'alas deş. Ğu Rəbbee uvhuyn hı'ı deş, Mang'veeyib vasse İzrailyna paççahiyvalla g'avşuna.
27 Samueli akutembenuka kuti azipita, Sauli anagwira mpendero wa mkanjo wake, ndipo unangʼambika.
Şamuel mançe əlyhəəsva sak'ımee, Şaulee mana plaşike aqqaqqa, manıd qoxan.
28 Samueli anati kwa iye, “Yehova wangʼamba ufumu wanu kuchoka kwa inu, ndipo waupereka kwa mnzanu woposa inu.
Şamuelee mang'uk'le eyhen: – Nəxdiy ğu yizın plaş qotxu məxbı'b g'iyna Rəbbee yiğne xılençe İzrailyna paççahiyvalla qooxas. Mang'vee vas k'anerıng'une, vale yugung'une xılyaqa qevles.
29 Mulungu wa ulemerero wa Israeli sanama kapena kusintha maganizo ake; pakuti iye si munthu, kuti asinthe maganizo ake.”
İzrail Ğamaa'ane Allahee, horbıd ha'a deş, fıkırıb badal haa'a deş, Mana insan deş vor fıkır badal haa'as.
30 Sauli anati, “Ine ndachimwa. Komabe, chonde mundilemekeze pamaso pa akuluakulu, anthu anga, ndiponso pamaso pa Israeli. Mubwerere nane kuti ndikapembedze Yehova Mulungu wanu.”
Şaulee eyhen: – Zı bınah hav'u. Hucoona ixhes, həşde xalq'ıne ağsaqqalaaşineyiy İzrailyne ögil zas hı'rmat givxhe. Zakasana sak'le, yiğne Allahıs, Rəbbis, ı'bəədat ha'as.
31 Pamenepo Samueli anabwerera ndi Sauli, ndipo Sauli anapembedza Yehova.
Şamuel Şauluqar qihna qaraylena, Şauleeyid Rəbbis ı'bəədat ha'a.
32 Kenaka Samueli anati, “Bwera nayeni kuno Agagi, mfumu ya Amaleki ija.” Choncho Agagi anapita kwa Samueli mokondwa chifukwa ankaganiza kuti, “Ndithu zowawa za imfa zapita.”
Şamuelee eyhen: – Amalekaaşina paççah Agag inyaqa yizde k'anyaqa qale. Agagır vuççud dexhesda xhinne qaraylena. Agagee culed-alqa eyhe ıxha: – Mıts'an, zı qik'uyke g'attirxhınna.
33 Koma Samueli anati, “Monga momwe lupanga lako linasandutsira amayi kukhala wopanda ana, momwemonso amayi ako adzakhala opanda mwana pakati pa amayi.” Ndipo Samueli anapha Agagi pamaso pa Yehova ku Giligala.
Şamuelee eyhen: – Yiğne g'ılıncın nəxübiy yedar kulyfatbı dena g'alyav'u, yiğna yedir həməxür kulyfat dena eexvas. Şamuelee Gilgalee, Rəbbine ögil Agag gyaraxana.
34 Ndipo Samueli anapita ku Rama, koma Sauli anapita ku mudzi kwawo ku Gibeya wa Sauli.
Mançile qiyğa Şamuel ayk'anna Ramayeeqa, Şaulur Giveayeene, cune xaaqa siyk'al.
35 Samueli sanamuonenso Sauli mpaka imfa yake ngakhale kuti ankamulira Sauliyo. Yehova anamva chisoni kuti anasankha Sauli kuti akhale mfumu ya Israeli.
Şamuelee, Şaulna geeb haa'a, geed uts'ur ts'ıts'a'a. Mang'uk'le mana qik'asmee, g'ece deş. Rəbbir Şauluke İzrailyna paççah hı'ıva paşman eyxhena.

< 1 Samueli 15 >