< 1 Samueli 15 >

1 Samueli anawuza Sauli kuti, “Yehova anandituma ine kuti ndikudzozeni kukhala mfumu ya anthu ake, Aisraeli. Tsopano imvani zimene Yehova akunena.
and to say Samuel to(wards) Saul [obj] me to send: depart LORD to/for to anoint you to/for king upon people his upon Israel and now to hear: hear to/for voice: message word LORD
2 Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndidzalanga Aamaleki chifukwa cha zimene anawachita Aisraeli. Paja iwo analimbana ndi Aisraeli pa njira pamene Aisraeliwo ankachoka ku Igupto.
thus to say LORD Hosts to reckon: list [obj] which to make: do Amalek to/for Israel which to set: put to/for him in/on/with way: journey in/on/with to ascend: rise he from Egypt
3 Tsopano pita kathire nkhondo Aamaleki ndi kuwononga kwathunthu zinthu zonse zimene ali nazo. Musakasiyeko munthu ndi mmodzi yemwe. Mukaphe amuna ndi akazi, ana ndi makanda, ngʼombe ndi nkhosa, ngamira ndi abulu.’”
now to go: went and to smite [obj] Amalek and to devote/destroy [obj] all which to/for him and not to spare upon him and to die from man till woman from infant and till to suckle from cattle and till sheep from camel and till donkey
4 Kotero Sauli anayitana ankhondo ake nawawerenga ku Telaimu. Ankhondo oyenda pansi analipo 200,000 ndipo mwa iwowa 10,000 anali a fuko la Yuda.
and to hear: proclaim Saul [obj] [the] people and to reckon: list them in/on/with Telaim hundred thousand on foot and ten thousand with man Judah
5 Sauli anapita ku mzinda wa Aamaleki nawubisalira mʼkhwawa.
and to come (in): come Saul till city Amalek and to ambush in/on/with torrent: valley
6 Tsono Sauli anawuza Akeni kuti, “Samukani, muchoke pakati pa Aamaleki kuti ine ndisakuwonongeni pamodzi ndi iwo pakuti inu munaonetsa kukoma mtima kwa Aisraeli onse pamene ankatuluka mʼdziko la Igupto,” Choncho Akeni anachoka pakati pa Aamaleki.
and to say Saul to(wards) [the] Kenite to go: went to turn aside: depart to go down from midst Amalekite lest to gather you with him and you(m. s.) to make: do kindness with all son: descendant/people Israel in/on/with to ascend: rise they from Egypt and to turn aside: depart Kenite from midst Amalek
7 Tsono Sauli anakantha Aamaleki kuchokera ku Havila mpaka ku Suri, kummawa kwa Igupto.
and to smite Saul [obj] Amalek from Havilah to come (in): towards you Shur which upon face: surface Egypt
8 Sauli anatenga Agagi mfumu ya Aamaleki, koma anthu ake onse anawapha ndi lupanga.
and to capture [obj] Agag king Amalek alive and [obj] all [the] people to devote/destroy to/for lip: edge sword
9 Koma Sauli ndi ankhondo ake sanaphe Agagi, sanaphenso nkhosa ndi ngʼombe zabwino ngakhalenso ana angʼombe ndi ana ankhosa onenepa. Chilichonse chimene chinali chabwino sanachiphe. Koma zonse zimene zinali zoyipa ndi zachabechabe anaziwononga.
and to spare Saul and [the] people upon Agag and upon best [the] flock and [the] cattle and [the] second and upon [the] ram and upon all [the] good and not be willing to devote/destroy them and all [the] work vile and to melt [obj] her to devote/destroy
10 Kenaka Yehova anawuza Samueli kuti,
and to be word LORD to(wards) Samuel to/for to say
11 “Ine ndikumva chisoni chifukwa ndinayika Sauli kukhala mfumu. Wabwerera mʼmbuyo, waleka kunditsata ndipo sanamvere malangizo anga.” Samueli anapsa mtima, ndipo analira kwa Yehova usiku wonse.
to be sorry: relent for to reign [obj] Saul to/for king for to return: turn back from after me and [obj] word my not to arise: establish and to be incensed to/for Samuel and to cry out to(wards) LORD all [the] night
12 Samueli anadzuka mmamawa ndipo anapita kukakumana ndi Sauli. Koma anthu anamuwuza kuti, “Sauli anabwera ku Karimeli, ndipo kumeneko wadziyimikira mwala wachikumbutso cha iye mwini. Tsopano wachokako ndipo wapita ku Giligala.”
and to rise Samuel to/for to encounter: meet Saul in/on/with morning and to tell to/for Samuel to/for to say to come (in): come Saul [the] Carmel [to] and behold to stand to/for him hand: themselves and to turn: turn and to pass and to go down [the] Gilgal
13 Samueli atamupeza Sauli, Sauliyo anati kwa Samueli, “Yehova akudalitseni! Ndachita zonse zimene Yehova analamula.”
and to come (in): come Samuel to(wards) Saul and to say to/for him Saul to bless you(m. s.) to/for LORD to arise: establish [obj] word LORD
14 Koma Samueli anati, “Nanga bwanji ndikumva kulira kwa nkhosa ndi ngʼombe?”
and to say Samuel and what? voice: sound [the] flock [the] this in/on/with ear my and voice: sound [the] cattle which I to hear: hear
15 Sauli anayankha, “Zimenezi Asilikali azitenga kuchokera kwa Aamaleki. Iwo anasungako nkhosa ndi ngʼombe zabwino kuti akapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu, koma zina zonse anaziwononga.”
and to say Saul from Amalekite to come (in): bring them which to spare [the] people upon best [the] flock and [the] cattle because to sacrifice to/for LORD God your and [obj] [the] advantage to devote/destroy
16 Koma Samueli anati kwa Sauli, “Khala chete! Ima ndikuwuze zimene Yehova wandiwuza usiku wathawu.” Sauli anayankha kuti, “Ndiwuzeni.”
and to say Samuel to(wards) Saul to slacken and to tell to/for you [obj] which to speak: speak LORD to(wards) me [the] night (and to say *Q(K)*) to/for him to speak: speak
17 Apo Samueli anati, “Munali wamngʼono pa maso pa anthu, koma tsopano mwasanduka mtsogoleri wa mafuko a Israeli. Yehova anakudzozani kuti mukhale mfumu yolamulira Aisraeli.
and to say Samuel not if small you(m. s.) in/on/with eye: appearance your head: leader tribe Israel you(m. s.) and to anoint you LORD to/for king upon Israel
18 Ndipo Yehova anakutumani kuti, ‘Pitani mukawononge kwathunthu Aamaleki, anthu oyipa aja. Mukachite nawo nkhondo mpaka kuwatheratu.’
and to send: depart you LORD in/on/with way: journey and to say to go: went and to devote/destroy [obj] [the] sinner [obj] Amalek and to fight in/on/with him till to end: destroy they [obj] them
19 Chifukwa chiyani simunamvere mawu a Yehova? Chifukwa chiyani munathamangira zofunkha ndi kuchita choyipira Yehova?”
and to/for what? not to hear: obey in/on/with voice LORD and to pounce to(wards) [the] spoil and to make: do [the] bad: evil in/on/with eye: seeing LORD
20 Koma Saulo anawuza Samueli kuti, “Ine ndinamveradi mawu a Yehova. Ndinapita kukachita zimene Yehova anandituma. Ndinabwera naye Agagi, mfumu ya Amaleki, koma Aamaleki ena onse anaphedwa.
and to say Saul to(wards) Samuel which to hear: obey in/on/with voice LORD and to go: went in/on/with way: journey which to send: depart me LORD and to come (in): bring [obj] Agag king Amalek and [obj] Amalek to devote/destroy
21 Koma pa zofunkhazo anthu anatengapo nkhosa, ngʼombe ndi zabwino zina zoyenera kuwonongedwa kuti akapereke ngati nsembe kwa Yehova Mulungu wanu ku Giligala.”
and to take: take [the] people from [the] spoil flock and cattle first: best [the] devoted thing to/for to sacrifice to/for LORD God your in/on/with Gilgal
22 Koma Samueli anayankha kuti, “Kodi Yehova amakondwera ndi nsembe zopsereza ndi nsembe zina kapena kumvera mawu a ake? Taona, kumvera ndi kwabwino kuposa nsembe, ndipo kutchera khutu ndi kwabwino kuposa kupereka mafuta a nkhosa.
and to say Samuel pleasure to/for LORD in/on/with burnt offering and sacrifice like/as to hear: obey in/on/with voice LORD behold to hear: obey from sacrifice pleasant to/for to listen from fat ram
23 Pakuti kuwukira kuli ngati tchimo lowombeza, ndipo kukhala nkhutukumve kuli ngati tchimo lopembedza mafano. Chifukwa mwakana mawu a Yehova. Iyenso wakukana kuti iweyo ukhale mfumu.”
for sin divination rebellion and evil: wickedness and teraphim to press because to reject [obj] word LORD and to reject you from king
24 Tsono Sauli anati kwa Samueli, “Ine ndachimwa. Ndaphwanya malamulo a Yehova ndiponso malangizo anu. Ndinkaopa anthu ndipo ndinawamvera.
and to say Saul to(wards) Samuel to sin for to pass: trespass [obj] lip: word LORD and [obj] word your for to fear [obj] [the] people and to hear: obey in/on/with voice their
25 Tsopano ndikukupemphani, khululukireni tchimo langa ndipo mubwerere nane kuti ndikapembedze Yehova.”
and now to lift: forgive please [obj] sin my and to return: return with me and to bow to/for LORD
26 Koma Samueli anawuza Sauli kuti, “Ine sindibwerera nawe. Inu mwakana mawu a Yehova. Choncho Iyenso wakukanani kuti musakhale mfumu yolamulira Aisraeli.”
and to say Samuel to(wards) Saul not to return: return with you for to reject [obj] word LORD and to reject you LORD from to be king upon Israel
27 Samueli akutembenuka kuti azipita, Sauli anagwira mpendero wa mkanjo wake, ndipo unangʼambika.
and to turn: turn Samuel to/for to go: went and to strengthen: hold in/on/with wing robe his and to tear
28 Samueli anati kwa iye, “Yehova wangʼamba ufumu wanu kuchoka kwa inu, ndipo waupereka kwa mnzanu woposa inu.
and to say to(wards) him Samuel to tear LORD [obj] kingdom Israel from upon you [the] day: today and to give: give her to/for neighbor your [the] pleasant from you
29 Mulungu wa ulemerero wa Israeli sanama kapena kusintha maganizo ake; pakuti iye si munthu, kuti asinthe maganizo ake.”
and also perpetuity Israel not to deal and not to be sorry: relent for not man he/she/it to/for to be sorry: relent
30 Sauli anati, “Ine ndachimwa. Komabe, chonde mundilemekeze pamaso pa akuluakulu, anthu anga, ndiponso pamaso pa Israeli. Mubwerere nane kuti ndikapembedze Yehova Mulungu wanu.”
and to say to sin now to honor: honour me please before old: elder people my and before Israel and to return: return with me and to bow to/for LORD God your
31 Pamenepo Samueli anabwerera ndi Sauli, ndipo Sauli anapembedza Yehova.
and to return: turn back Samuel after Saul and to bow Saul to/for LORD
32 Kenaka Samueli anati, “Bwera nayeni kuno Agagi, mfumu ya Amaleki ija.” Choncho Agagi anapita kwa Samueli mokondwa chifukwa ankaganiza kuti, “Ndithu zowawa za imfa zapita.”
and to say Samuel to approach: bring to(wards) me [obj] Agag king Amalek and to go: come to(wards) him Agag bond and to say Agag surely to turn aside: depart bitter [the] death
33 Koma Samueli anati, “Monga momwe lupanga lako linasandutsira amayi kukhala wopanda ana, momwemonso amayi ako adzakhala opanda mwana pakati pa amayi.” Ndipo Samueli anapha Agagi pamaso pa Yehova ku Giligala.
and to say Samuel like/as as which be bereaved woman sword your so be bereaved from woman mother your and to hew Samuel [obj] Agag to/for face: before LORD in/on/with Gilgal
34 Ndipo Samueli anapita ku Rama, koma Sauli anapita ku mudzi kwawo ku Gibeya wa Sauli.
and to go: went Samuel [the] Ramah [to] and Saul to ascend: rise to(wards) house: home his Gibeah Saul
35 Samueli sanamuonenso Sauli mpaka imfa yake ngakhale kuti ankamulira Sauliyo. Yehova anamva chisoni kuti anasankha Sauli kuti akhale mfumu ya Israeli.
and not to add: again Samuel to/for to see: see [obj] Saul till day death his for to mourn Samuel to(wards) Saul and LORD to be sorry: relent for to reign [obj] Saul upon Israel

< 1 Samueli 15 >