< 1 Samueli 14 >

1 Tsiku lina Yonatani mwana wa Sauli anawuza mnyamata wake womunyamulira zida zake za nkhondo kuti, “Tiye tiwoloke tipite ku kaboma ka Afilisti tsidya ilo.” Koma iye sanawuze abambo ake.
Ngelinye ilanga uJonathani indodana kaSawuli wathi ejaheni elalithwala izikhali zakhe, “Woza, kasiye enkambeni yebutho lamaFilistiya ngakwelinye icele.” Kodwa kamtshelanga uyise.
2 Sauli ankakhala mʼmalire a Gibeya pa tsinde pa mtengo wamakangadza ku Migironi. Anthu amene anali naye analipo 600.
USawuli wayehlala emaphethelweni eGibhiya ngaphansi kwesihlahla sephomegranathi eMigironi. Amadoda ayelaye ayengaba ngamakhulu ayisithupha,
3 Pakati pawo panalinso Ahiya amene ankavala efodi. Iye anali mwana wa Ahitubi, mʼbale wake wa Ikabodi mwana wa Finehasi, mwana wa Eli, wansembe wa Yehova wa ku Silo. Koma palibe amene anadziwa kuti Yonatani wachoka.
phakathi kwawo kulo-Ahija, owayegqoke isigqoko samahlombe. Wayeyindodana yomfowabo ka-Ikhabhodi u-Ahithubi indodana kaFinehasi, indodana ka-Eli umphristi kaThixo eShilo. Kakho owayesazi ukuthi uJonathani wayehambile.
4 Pa mpata pamene Yonatani ankafuna kudutsa kukafika ku kaboma ka nkhondo ka Afilisti kunali thanthwe lotsetsereka mbali ina ndi lina lotsetsereka mbali inayo. Thanthwe limodzi linkatchedwa Bozezi ndipo linalo linkatchedwa Seni.
Eceleni ngalinye lomkhandlu ayehlose ukuwuchapha ukuze ayefika enkambeni yebutho lamaFilistiya kwakuleliwa; elinye lalithiwa yiBhozezi elinye liyiSene.
5 Thanthwe limodzi linali chakumpoto kuyangʼanana ndi Mikimasi, ndipo thanthwe linalo linali chakummwera kuyangʼanana ndi Geba.
Elinye iliwa lalingasenyakatho ngokuya eMikhimashi, elinye lingasezansi ngokuya eGebha.
6 Yonatani anawuza mnyamata wake womunyamulira zida uja kuti, “Tiye tiwoloke tipite ku kaboma ka anthu osachita mdulidwewo. Mwina Yehova adzatigwirira ntchito. Palibe chomuletsa Yehova kutipulumutsa, ngakhale tikhale ambiri kapena ochepa.”
UJonathani wathi ejaheni elalithwala izikhali zakhe, “Woza, siwelele enkambeni yalabayana abantu abangasokanga. Engxenye uThixo uzasimela, ngoba akulalutho olungavimbela uThixo ekukhululeni, loba kungabanengi kumbe abalutshwana.”
7 Mnyamata uja anati, “Chitani chilichonse chimene mtima wanu ukhumba. Ine ndili nanu pamodzi. Chimene mtima wanu ukhumba ndi chomwenso ine ndikhumba.”
Umthwali wezikhali zakhe wathi, “Yenza konke olakho engqondweni yakho. Qhubeka, mina ngilawe ngenhliziyo langomphefumulo.”
8 Yonatani anati, “Tiye tsono tiwoloke kupita kumene kuli anthuwo ndi kukadzionetsa kwa iwo.
UJonathani wasesithi, “Ngakho-ke, woza sikhuphuke siqonde kulabaya abantu senze ukuba basibone.
9 Akatiwuza kuti, ‘Imani pomwepo mpaka tikupezeni,’ ife tikangoyima pomwepo osapita kumene kuli iwoko.
Bangathi kithi, ‘Manini khonapho size sifike kini,’ sizahlala lapho esikhona singayi kubo.
10 Koma akadzati, ‘Bwerani kuno,’ ndiye ife tikapitedi, chifukwa ichi chidzakhala chizindikiro chakuti Yehova wapereka mʼmanja mwathu.”
Kodwa bangathi, ‘Wozani kithi,’ sizakhwela siye phezulu ngoba lokho kuzakuba yisibonakaliso sethu sokuthi uThixo usebanikele ezandleni zethu.”
11 Choncho awiriwa anadzionetsa ku kaboma ka nkhondo ka Afilisti. Tsono Afilistiwo anati, “Taonani! Aheberi akutuluka mʼmaenje mʼmene anabisala.”
Ngakho bobabili bazibonakalisa enkambeni yamabutho amaFilistiya. AmaFilistiya athi, “Khangelani, amaHebheru asehohoba ephuma emilindini abecatshe kuyo.”
12 Anthu a ku kaboma kaja anafuwula kwa Yonatani ndi mnyamata wake uja kuti, “Bwerani kuno ndipo tikuphunzitsani phunziro.” Ndipo Yonatani anati kwa mnyamata wake. “Nditsate pakuti Yehova wapereka Afilistiwa mʼmanja mwa Aisraeli.”
Amadoda ayesenkambeni yamabutho amemeza uJonathani lomthwali wezikhali zakhe athi, “Wozani kithi sizalifundisa isifundo.” Ngakho uJonathani wathi kumthwali wezikhali zakhe, “Khwela ungilandele; uThixo usebanikele esandleni sika-Israyeli.”
13 Choncho Yonatani anakwera mokwawa, ndipo mnyamata wake uja ankamutsata. Tsono Yonatani anathira nkhondo Afilisti aja namawagwetsa, ndipo mnyamata wake uja ankawapha pambuyo pa iyeyo.
UJonathani wakhwela, esebenzisa izandla lezinyawo zakhe, lomthwali wezikhali zakhe ekhonapho ngemva kwakhe. AmaFilistiya awa phambi kukaJonathani, njalo umthwali wezikhali zakhe walandela ebulala abantu ngemva kwakhe.
14 Nthawi yoyambayo Yonatani ndi mnyamata wake uja anapha anthu makumi awiri ndipo anawaphera pa malo ochepa okwanira ngati theka la ekala.
Ngalokho kuhlasela kokuqala uJonathani lomthwali wezikhali zakhe babulala abantu abangamatshumi amabili endaweni eyayingaba yingxenye yendima.
15 Tsono gulu lonse la ankhondo, ndiye kuti iwo amene anali mʼmisasa ndi mʼminda ndiponso iwo amene anali ku kaboma ka ankhondo kaja, onse anagwidwa ndi mantha aakulu. Dzikonso linagwedezeka, choncho anthu anachita mantha koopsa.
Emva kwalokho ibutho lonke lathuthumela, ababesezihonqweni lababesegangeni, lalabo ababesezinkambeni zamabutho lamaqembu abahlaseli, iphansi lanyikinyeka. Kwakuyikuthuthumela okwakulethwe nguNkulunkulu.
16 Alonda a Sauli a ku Gibeya dziko la Benjamini atangomwaza maso anangoona chigulu cha asilikali chikumwazikana uku ndi uku.
Abalindi bakaSawuli eGibhiya koBhenjamini babona ibutho lisabalele ezinhlangothini zonke.
17 Kenaka Sauli anawawuza anthu amene anali naye kuti, “Awerengeni asilikali kuti muona amene wachoka.” Atawawerenga anapeza kuti Yonatani ndi mnyamata wake womunyamulira zida zake za nkhondo palibe.
USawuli wasesithi ebantwini ababelaye, “Qoqani amabutho libone ukuthi ngubani ongekho.” Sebekwenzile, ababengekho kwakunguJonathani lomthwali wezikhali zakhe.
18 Tsono Sauli anawuza Ahiya kuti, “Bwera nalo Bokosi la Mulungulo.” (Nthawi imeneyo nʼkuti efodiyo ili ndi Ahiya pamaso pa Aisraeli).
USawuli wasesithi ku-Ahija, “Letha ibhokisi lesivumelwano sikaNkulunkulu.” (Ngalesisikhathi lalikwabako-Israyeli.)
19 Pamene Sauli amayankhula ndi wansembe, phokoso limanka likulirakulira mu msasa wa Afilisti, Kotero Sauli anati kwa wansembe, “Leka kuwombeza.”
Kwathi uSawuli esakhuluma lomphristi, ukuxokozela ezihonqweni zamaFilistiya kwakhula kakhulu kakhulukazi. Ngakho uSawuli wathi kumphristi, “Susa isandla sakho.”
20 Ndipo Sauli ndi asilikali onse amene anali naye anasonkhana kupita kukamenya nkhondo, ndipo anangoona chisokonezo chachikulu kwambiri. Afilisti akuphana okhaokha.
Emva kwalokho uSawuli labantu bakhe bonke babuthana basebesiya empini. Bafica amaFilistiya ephakathi kwesiyaluyalu esipheleleyo, egalelana ngezinkemba zawo.
21 Aheberi ena amene kale anali ndi Afilisti mpaka kukakhala ku misasa yawo, iwonso anatembenuka nakhala pamodzi ndi Aisraeli amene ankatsata Sauli ndi Yonatani.
AmaHebheru ayelamaFilistiya kuqala ehambe lawo ezihonqweni zawo abuyela kwabako-Israyeli ababeloSawuli loJonathani.
22 Ngakhale Aisraeli amene ankabisala ku dziko lamapiri la Efereimu atamva kuti Afilisti akuthawa, nawonso anawathamangitsa Afilistiwo nawathira nkhondo.
Kwathi lapho bonke abako-Israyeli ababecatshe elizweni lezintaba elako-Efrayimi sebezwile ukuthi amaFilistiya ayesebaleka empini bangena, baxotshana lawo.
23 Nkhondo inapitirira mpaka kufika ku Beti-Aveni. Choncho Yehova anapulumutsa Aisraeli tsiku limenelo.
Uthixo wamhlenga kanjalo u-Israyeli ngalolosuku, njalo ukulwa kwaya ngale kweBhethi-Aveni.
24 Koma asilikali a Israeli anavutika tsiku limenelo, chifukwa Sauli anawalumbirira Aisraeli kuti, “Wotembereredwa munthu aliyense amene adzadya kusanade, ine ndisanalipsire adani anga!” Kotero palibe wankhondo aliyense amene analawa chakudya.
Ngalolosuku abantu bako-Israyeli babedanile ngoba uSawuli wayebophe abantu ngesifungo esithi, “Uqalekisiwe lowomuntu odla ukudla kungakahlwi, ngingakaphindiseli ezitheni zami!” Ngakho akukho butho elanambitha ukudla.
25 Gulu lonse la ankhondo linalowa mʼnkhalango mmene munali uchi.
Ibutho lonke langena ehlathini, lapho okwakuloluju phansi khona.
26 Atalowa mʼnkhalango, anaona uchi ukukha, koma palibe amene anadya, pakuti ankaopa lumbiro lija.
Ekungeneni kwabo ehlathini, babona uluju lujuluka, kodwa kakho owaludlayo, ngoba babesesaba isifungo.
27 Koma Yonatani sanamve kuti abambo ake anawalumbirira anthu aja choncho anatenga ndodo yake imene inali mʼdzanja lake ndipo anayipisa mu chisa cha njuchi. Choncho iye anadya uchiwo ndipo mʼmaso mwake munayera.
Kodwa uJonathani wayengezwanga ukuthi uyise wayebophe abantu ngesifungo, welula isiduku somqwayi ayewuphethe wawuhloma ohlangeni loluju. Waphakamisela isandla sakhe emlonyeni wakhe, amehlo akhazimula.
28 Kenaka mmodzi mwa Asilikali anamuwuza kuti, “Abambo ako alumbirira anthu nati, ‘Wotembereredwa munthu aliyense amene adye chakudya lero.’ Nʼchifukwa chake anthu alefuka.”
Lapho-ke omunye wamabutho wamtshela wathi, “Uyihlo ubophe ibutho ngesifungo esinzima, esithi, ‘Uqalekisiwe lowomuntu odla ukudla lamhla!’ Yikho-nje abantu bemdambiyana.”
29 Yonatani anati, “Abambo anga achita chinthu choyipira dziko. Taonani mʼmaso mwanga mwayera chifukwa ndalawa uchiwu pangʼono.
UJonathani wathi, “Ubaba usedalele ilizwe uhlupho. Khangela ukuthi amehlo ami athe dlwe ekunambitheni kwami okuncane koluju lolu.
30 Zikanakhala zabwino kwambiri anthuwa akanadya lero zofunkha za adani awo. Zikanatero tikanapha Afilisti ochuluka.”
Kade kuzakuba ngcono kakhulu aluba lamhla abantu bebedlile enye yempango abayithethe ezitheni zabo. Ukubulawa kwamaFilistiya kade kungayikuba kukhulu kulalokhu na?”
31 Tsiku limenelo Aisraeli anapha Afilisti kuchokera ku Mikimasi mpaka ku Ayaloni. Koma Aisraeliwo analefuka kwambiri ndi njala.
Ngalolosuku, emva kokuba ama-Israyeli esebulele amaFilistiya kusukela eMikhimashi kusiyafika e-Ayijaloni, ayesediniwe.
32 Choncho iwo anathamangira pa zofunkha ndipo anatenga nkhosa, ngʼombe ndi ana angʼombe. Iwo anazipha zonsezi nazidya pamodzi ndi magazi omwe.
Baphuthuma impango, kwathi sebethethe izimvu lenkomo kanye lamathole, bazibulala khonapho bazidla kanye legazi.
33 Koma anthu ena anawuza Sauli kuti, “Taona anthu akuchimwira Yehova pakudya nyama yomwe ili ndi magazi.” Ndipo Sauli anati, “Mwaonetsa kusakhulupirika. Tsopano gubuduzirani mwala waukulu pano.”
Omunye wasesithi kuSawuli, “Khangela abantu benza isono kuThixo ngokudla inyama elegazi.” Yena wathi, “Selephule ukuthenjwa. Giqelani ilitshe elikhulu ngapha khathesi nje.”
34 Kenaka Sauli anati, “Mwazikanani pakati pa anthu ndi kukawawuza kuti aliyense abwere ndi ngʼombe yake kapena nkhosa yake, ndipo adzayiphe pomwe pano ndi kuyidya. Musachimwire Yehova pakudya nyama imene ili ndi magazi.” Kotero aliyense anabwera ndi ngʼombe yake usiku womwewo ndi kuyipha pomwepo.
Wasesithi, “Yanini phakathi kwabantu libatshele lithi, ‘Lowo lalowo wenu kangilethele inkomo lezimvu zakhe azibulalele lapha azidle. Lingenzi isono kuThixo ngokudla inyama eseselegazi.’” Ngakho ngalobobusuku umuntu wonke waletha inkabi yakhe wayihlabela khonapho.
35 Ndipo Sauli anamangira Yehova guwa. Ili linali guwa loyamba limene Sauli anamangira Yehova.
USawuli wasesakhela uThixo i-alithari; wayeqala ukwenza lokhu.
36 Sauli anati, “Tiyeni titsatire Afilisti usikuwu ndi kulanda zinthu zawo mpaka mmawa. Tisasiyepo wamoyo ndi mmodzi yemwe.” Ankhondowo anayankha kuti, “Chitani chilichonse chimene chikukomerani.” Koma wansembe anati, “Tipemphe uphungu kwa Mulungu poyamba.”
USawuli wathi, “Kasehleni silandele amaFilistiya ebusuku siwahlasele kuze kuse, singatshiyi lalinye lawo liphila.” Bathi, “Yenza lokho okubona kulungile kuwe.” Kodwa umphristi wathi, “Kasibuzeni uNkulunkulu lapha.”
37 Choncho Sauli anafunsa Mulungu kuti, “Kodi ndiwatsatire Afilisti? Kodi mukawapereka mʼmanja mwathu?” Koma Mulungu sanamuyankhe tsiku limenelo.
USawuli wabuza uNkulunkulu wathi, “Ngehle ngilandele amaFilistiya na? Uzawanikela esandleni sika-Israyeli na?” Kodwa uNkulunkulu kamphendulanga ngalolosuku.
38 Choncho Sauli anati, “Bwerani kuno nonse atsogoleri a anthu, ndipo tiyeni tione kuti kodi tchimo limeneli lachitika bwanji lero?
Ngakho uSawuli wathi, “Wozani lapha, lonke lina bakhokheli bebutho, sidinge ukuthi yisono bani esenziwe lamhla.
39 Pali Yehova amene amapulumutsa Israeli, ngakhale tchimolo litapezeka ndi mwana wanga Yonatani, iye afe ndithu.” Koma palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthuwo amene anamuyankha.
Ngeqiniso elinjengoba uThixo ohlenga u-Israyeli ephila, lanxa sisendodaneni yami uJonathani, kumele ife.” Kodwa akukho lamunye wabantu owatsho ilizwi.
40 Tsono Sauli anawuza Aisraeli onse kuti, “Inu mukhale mbali imodzi. Ine ndi mwana wanga Yonatani tikhala mbali inayo.” “Chitani chilichonse chimene chikukomerani.”
USawuli wasesithi kubo bonke abako-Israyeli, “Manini laphayana; mina lendodana yami uJonathani sizakuma ngapha.” Abantu baphendula bathi, “Yenza lokho okukhanya kulungile kuwe.”
41 Ndipo Sauli anapemphera kwa Yehova Mulungu wa Israeli kuti, “Chifukwa chiyani simunandiyankhe ine mtumiki wanu lero lino? Ngati tchimoli lipezeka ndi ine kapena ndi Yonatani mwana wanga, Inu Mulungu wa Israeli, aoneke ndi Urimu. Koma ngati wochimwa ndi anthu anu, Aisraeli aoneke Tamimu.” Maere anagwera Sauli ndi Yonatani ndipo anthu anapezeka osalakwa.
Emva kwalokho uSawuli wakhuleka kuThixo, uNkulunkulu ka-Israyeli wathi, “Kungani ungayiphendulanga inceku lamuhla? Nxa isono sikimi kumbe kuJonathani indodana yami, inkatho kayibe yi-Urimi; kodwa nxa isono sisebantwini bako-Israyeli, inkatho kayibe yiThumimi.” UJonathani loSawuli badliwa yinkatho, abantu bagezeka.
42 Sauli anati, “Chitani maere pakati pa ine ndi Yonatani mwana wanga.” Ndipo maere anagwera Yonatani.
USawuli wasesithi, “Phosani inkatho phakathi kwami loJonathani indodana yami.” UJonathani wabanjwa.
43 Kenaka Sauli anati kwa Yonatani, “Ndiwuze chimene wachita.” Ndipo Yonatani anamuwuza kuti, “Ine ndinangolawa uchi pangʼono ndi ndodo yangayi. Ndiye ine ndili wokonzeka kufa.”
USawuli wasesithi kuJonathani, “Ngitshela lokho okwenzileyo.” Ngakho uJonathani wamtshela wathi, “Nginambithe uluju nje kuphela ngesihloko somqwayi wami. Khathesi-ke sokumele ngife!”
44 Sauli anati, “Mulungu andilange ngakhale kufa kumene, ngati sufa iwe Yonatani.”
USawuli wathi, “UNkulunkulu kangijezise, kube nzima kakhulu, nxa ungafi, Jonathani.”
45 Koma anthuwo anafunsa Saulo kuti, “Kodi Yonatani afe, iye amene wagwira ntchito iyi yayikulu yopulumutsa Aisraeli? Osatheka! Pali Yehova ngakhale tsitsi ndi limodzi lomwe lapamutu pake silidzathothoka, pakuti wachita zimenezi lero ndi thandizo la Mulungu.” Choncho anthuwo anamupulumutsa Yonatani, ndipo sanaphedwe.
Kodwa abantu bathi kuSawuli, “UJonathani kumele afe yini, yena olethe lokhukuhlengwa okukhulu ko-Israyeli na? Hatshi bo! Ngeqiniso elinjengoba uThixo ekhona, akulanwele lwekhanda lakhe oluzawela phansi, ngoba lokhu ukwenze lamhla ngosizo lukaNkulunkulu.” Ngakho abantu bamhlenga uJonathani, kasabulawanga.
46 Pambuyo pake Sauli analeka kulondola Afilisti, kenaka anabwerera ku dziko lawo.
USawuli wayekela ukuxotshana lamaFilistiya, njalo amaFilistiya abuyela elizweni lakibo.
47 Sauli ali mtsogoleri wa Israeli, anachita nkhondo ndi adani awa omuzungulira: Mowabu, Amoni, Edomu mafumu a ku Zoba ndi Afilisti. Kulikonse kumene ankapita ankawagonjetsa.
Kwathi uSawuli esebusa ko-Israyeli, walwa lezitha zabo inxa zonke: iMowabi, ama-Amoni, i-Edomi, amakhosi aseZobha kanye lamaFilistiya. Loba kungaphi lapho aya khona, wababhuqa.
48 Anachita nkhondo mwamphamvu ndi kugonjetsa Aamaleki. Choncho anapulumutsa Aisraeli mʼmanja mwa anthu amene ankawalanda zinthu zawo.
Walwa ngesibindi wehlula ama-Amaleki, wakhulula u-Israyeli ezandleni zalabo ababebaphangile.
49 Ana aamuna a Sauli anali Yonatani, Isivi ndi Maliki-Suwa. Analinso ndi ana aakazi awiri, dzina la mwana wake wamkulu wamkazi linali Merabi ndipo la mwana wake wamngʼono wamkazi linali Mikala.
Amadodana kaSawuli ayenguJonathani, lo-Ishivi kanye loMalikhi-Shuwa. Ibizo lendodakazi yakhe endala lalinguMerabi, elomcinyane linguMikhali.
50 Dzina la mkazi wake linali Ahinoamu. Iyeyu anali mwana wa Ahimaazi. Dzina la mkulu wa ankhondo a Sauli linali Abineri mwana wa Neri, mʼbale wa abambo a Sauli.
Ibizo lomkakhe lalingu-Ahinowama indodakazi ka-Ahimazi. Umlawuli webutho likaSawuli wayengu-Abhineri indodana kaNeri, uNeri wayengumfowabo kayise kaSawuli.
51 Kisi abambo a Sauli ndi Neri abambo a Abineri anali ana a Abieli.
UKhishi uyise kaSawuli, loNeri uyise ka-Abhineri babengamadodana ka-Abhiyeli.
52 Pa moyo wake wonse, Sauli ankakhalira kuchita nkhondo pakati pa Israeli ndi Afilisti. Ndipo Sauli ankati akaona munthu aliyense wamphamvu kapena wolimba mtima ankamulemba ntchito mu gulu lake lankhondo.
Kuzozonke insuku zikaSawuli kwakulempi enzima lamaFilistiya, njalo loba kungaphi uSawuli abona khona indoda elamandla kumbe elesibindi, wayingenisa ebuthweni lakhe.

< 1 Samueli 14 >