< 1 Samueli 14 >

1 Tsiku lina Yonatani mwana wa Sauli anawuza mnyamata wake womunyamulira zida zake za nkhondo kuti, “Tiye tiwoloke tipite ku kaboma ka Afilisti tsidya ilo.” Koma iye sanawuze abambo ake.
Or, il arriva un jour que Jonathan, fils de Saül, dit au jeune homme qui portait ses armes: Viens, et passons vers le poste des Philistins qui est de l'autre côté. Mais il ne le dit point à son père.
2 Sauli ankakhala mʼmalire a Gibeya pa tsinde pa mtengo wamakangadza ku Migironi. Anthu amene anali naye analipo 600.
Et Saül se tenait à l'extrémité de Guibea, sous un grenadier qui était à Migron; et le peuple qui était avec lui, formait environ six cents hommes;
3 Pakati pawo panalinso Ahiya amene ankavala efodi. Iye anali mwana wa Ahitubi, mʼbale wake wa Ikabodi mwana wa Finehasi, mwana wa Eli, wansembe wa Yehova wa ku Silo. Koma palibe amene anadziwa kuti Yonatani wachoka.
Et Achija, fils d'Achitub, frère d'Icabod, fils de Phinées, fils d'Héli, sacrificateur de l'Éternel à Silo, portait l'éphod. Le peuple ne savait point que Jonathan s'en fût allé.
4 Pa mpata pamene Yonatani ankafuna kudutsa kukafika ku kaboma ka nkhondo ka Afilisti kunali thanthwe lotsetsereka mbali ina ndi lina lotsetsereka mbali inayo. Thanthwe limodzi linkatchedwa Bozezi ndipo linalo linkatchedwa Seni.
Or, entre les passages par lesquels Jonathan cherchait à passer jusqu'au poste des Philistins, il y avait une dent de rocher d'un côté, et une dent de rocher, de l'autre; l'une s'appelait Botsets et l'autre Séné.
5 Thanthwe limodzi linali chakumpoto kuyangʼanana ndi Mikimasi, ndipo thanthwe linalo linali chakummwera kuyangʼanana ndi Geba.
L'une de ces dents est au nord, vis-à-vis de Micmash, et l'autre au midi, vis-à-vis de Guéba.
6 Yonatani anawuza mnyamata wake womunyamulira zida uja kuti, “Tiye tiwoloke tipite ku kaboma ka anthu osachita mdulidwewo. Mwina Yehova adzatigwirira ntchito. Palibe chomuletsa Yehova kutipulumutsa, ngakhale tikhale ambiri kapena ochepa.”
Et Jonathan dit au jeune homme qui portait ses armes: Viens, passons vers le poste de ces incirconcis; peut-être que l'Éternel agira pour nous; car rien n'empêche l'Éternel de délivrer, avec beaucoup de gens ou avec peu.
7 Mnyamata uja anati, “Chitani chilichonse chimene mtima wanu ukhumba. Ine ndili nanu pamodzi. Chimene mtima wanu ukhumba ndi chomwenso ine ndikhumba.”
Et celui qui portait ses armes lui dit: Fais tout ce que tu as au cœur, vas-y; j'irai avec toi où tu voudras.
8 Yonatani anati, “Tiye tsono tiwoloke kupita kumene kuli anthuwo ndi kukadzionetsa kwa iwo.
Et Jonathan lui dit: Voici, nous allons passer vers ces hommes, et nous nous montrerons à eux;
9 Akatiwuza kuti, ‘Imani pomwepo mpaka tikupezeni,’ ife tikangoyima pomwepo osapita kumene kuli iwoko.
S'ils nous disent: Attendez jusqu'à ce que nous soyons venus à vous! alors nous demeurerons à notre place, et nous ne monterons point vers eux.
10 Koma akadzati, ‘Bwerani kuno,’ ndiye ife tikapitedi, chifukwa ichi chidzakhala chizindikiro chakuti Yehova wapereka mʼmanja mwathu.”
Mais s'ils disent: Montez vers nous! alors nous monterons; car l'Éternel les aura livrés entre nos mains. Que cela nous serve de signe.
11 Choncho awiriwa anadzionetsa ku kaboma ka nkhondo ka Afilisti. Tsono Afilistiwo anati, “Taonani! Aheberi akutuluka mʼmaenje mʼmene anabisala.”
Ils se montrèrent donc tous deux au poste des Philistins; et les Philistins dirent: Voilà les Hébreux qui sortent des antres où ils s'étaient cachés.
12 Anthu a ku kaboma kaja anafuwula kwa Yonatani ndi mnyamata wake uja kuti, “Bwerani kuno ndipo tikuphunzitsani phunziro.” Ndipo Yonatani anati kwa mnyamata wake. “Nditsate pakuti Yehova wapereka Afilistiwa mʼmanja mwa Aisraeli.”
Et les hommes du poste crièrent à Jonathan et à celui qui portait ses armes, et dirent: Montez vers nous, et nous vous montrerons quelque chose. Alors Jonathan dit à celui qui portait ses armes: Monte après moi; car l'Éternel les a livrés entre les mains d'Israël.
13 Choncho Yonatani anakwera mokwawa, ndipo mnyamata wake uja ankamutsata. Tsono Yonatani anathira nkhondo Afilisti aja namawagwetsa, ndipo mnyamata wake uja ankawapha pambuyo pa iyeyo.
Et Jonathan monta en s'aidant des mains et des pieds, suivi de celui qui portait ses armes; et les Philistins tombèrent devant Jonathan, et celui qui portait ses armes les tuait derrière lui.
14 Nthawi yoyambayo Yonatani ndi mnyamata wake uja anapha anthu makumi awiri ndipo anawaphera pa malo ochepa okwanira ngati theka la ekala.
Et cette première défaite, que fit Jonathan et celui qui portait ses armes, fut d'environ vingt hommes, tués sur un espace d'environ la moitié d'un arpent de terre.
15 Tsono gulu lonse la ankhondo, ndiye kuti iwo amene anali mʼmisasa ndi mʼminda ndiponso iwo amene anali ku kaboma ka ankhondo kaja, onse anagwidwa ndi mantha aakulu. Dzikonso linagwedezeka, choncho anthu anachita mantha koopsa.
Et il y eut grand effroi au camp, dans la campagne, et parmi tout le peuple; le poste et ceux qui étaient allés faire du dégât, furent effrayés eux aussi, et le pays trembla; ce fut comme une frayeur envoyée de Dieu.
16 Alonda a Sauli a ku Gibeya dziko la Benjamini atangomwaza maso anangoona chigulu cha asilikali chikumwazikana uku ndi uku.
Et les sentinelles de Saül, qui étaient à Guibea de Benjamin, regardèrent, et voici, la multitude s'écoulait et s'en allait en déroute.
17 Kenaka Sauli anawawuza anthu amene anali naye kuti, “Awerengeni asilikali kuti muona amene wachoka.” Atawawerenga anapeza kuti Yonatani ndi mnyamata wake womunyamulira zida zake za nkhondo palibe.
Alors Saül dit au peuple qui était avec lui: Faites donc la revue, et voyez qui s'en est allé d'avec nous. Ils firent donc la revue, et voici, Jonathan n'y était point, ni celui qui portait ses armes.
18 Tsono Sauli anawuza Ahiya kuti, “Bwera nalo Bokosi la Mulungulo.” (Nthawi imeneyo nʼkuti efodiyo ili ndi Ahiya pamaso pa Aisraeli).
Et Saül dit à Achija: Fais approcher l'arche de Dieu (car l'arche de Dieu était ce jour-là avec les enfants d'Israël).
19 Pamene Sauli amayankhula ndi wansembe, phokoso limanka likulirakulira mu msasa wa Afilisti, Kotero Sauli anati kwa wansembe, “Leka kuwombeza.”
Mais il arriva, pendant que Saül parlait au sacrificateur, que le tumulte, qui était au camp des Philistins, allait croissant de plus en plus, et Saül dit au sacrificateur: Retire ta main!
20 Ndipo Sauli ndi asilikali onse amene anali naye anasonkhana kupita kukamenya nkhondo, ndipo anangoona chisokonezo chachikulu kwambiri. Afilisti akuphana okhaokha.
Et Saül et tout le peuple qui était avec lui, fut assemblé à grand cri, et ils vinrent jusqu'au lieu du combat; et voici, les Philistins avaient l'épée tirée les uns contre les autres; c'était un désordre extrême.
21 Aheberi ena amene kale anali ndi Afilisti mpaka kukakhala ku misasa yawo, iwonso anatembenuka nakhala pamodzi ndi Aisraeli amene ankatsata Sauli ndi Yonatani.
Or, les Philistins avaient, comme auparavant, des Hébreux qui étaient montés des environs avec eux dans le camp; mais eux aussi se joignirent aux Israélites qui étaient avec Saül et Jonathan.
22 Ngakhale Aisraeli amene ankabisala ku dziko lamapiri la Efereimu atamva kuti Afilisti akuthawa, nawonso anawathamangitsa Afilistiwo nawathira nkhondo.
Et tous les Israélites qui étaient cachés dans la montagne d'Éphraim, ayant appris que les Philistins fuyaient, s'attachèrent eux aussi à leur poursuite dans la bataille.
23 Nkhondo inapitirira mpaka kufika ku Beti-Aveni. Choncho Yehova anapulumutsa Aisraeli tsiku limenelo.
En ce jour-là l'Éternel délivra Israël, et la bataille s'étendit jusqu'au delà de Beth-Aven.
24 Koma asilikali a Israeli anavutika tsiku limenelo, chifukwa Sauli anawalumbirira Aisraeli kuti, “Wotembereredwa munthu aliyense amene adzadya kusanade, ine ndisanalipsire adani anga!” Kotero palibe wankhondo aliyense amene analawa chakudya.
En ce jour-là les Israélites furent harassés. Or Saül avait fait faire au peuple ce serment, disant: Maudit soit l'homme qui prendra de la nourriture jusqu'au soir, jusqu'à ce que je me sois vengé de mes ennemis! Et tout le peuple ne goûta d'aucune nourriture.
25 Gulu lonse la ankhondo linalowa mʼnkhalango mmene munali uchi.
Cependant tout le peuple du pays vint dans une forêt, où il y avait du miel à la surface du sol.
26 Atalowa mʼnkhalango, anaona uchi ukukha, koma palibe amene anadya, pakuti ankaopa lumbiro lija.
Le peuple entra donc dans la forêt, et vit le miel qui coulait, mais nul ne porta la main à sa bouche; car le peuple respectait le serment.
27 Koma Yonatani sanamve kuti abambo ake anawalumbirira anthu aja choncho anatenga ndodo yake imene inali mʼdzanja lake ndipo anayipisa mu chisa cha njuchi. Choncho iye anadya uchiwo ndipo mʼmaso mwake munayera.
Or, Jonathan n'avait point entendu lorsque son père avait fait jurer le peuple; et il étendit le bout du bâton qu'il avait à la main, le trempa dans un rayon de miel, et ramena sa main à sa bouche, et ses yeux furent éclaircis.
28 Kenaka mmodzi mwa Asilikali anamuwuza kuti, “Abambo ako alumbirira anthu nati, ‘Wotembereredwa munthu aliyense amene adye chakudya lero.’ Nʼchifukwa chake anthu alefuka.”
Alors quelqu'un du peuple prit la parole, et dit: Ton père a fait expressément jurer le peuple, en disant: Maudit soit l'homme qui prendra aujourd'hui de la nourriture! et le peuple est fatigué.
29 Yonatani anati, “Abambo anga achita chinthu choyipira dziko. Taonani mʼmaso mwanga mwayera chifukwa ndalawa uchiwu pangʼono.
Et Jonathan dit: Mon père a troublé le pays; voyez donc comme mes yeux se sont éclaircis, pour avoir goûté un peu de ce miel;
30 Zikanakhala zabwino kwambiri anthuwa akanadya lero zofunkha za adani awo. Zikanatero tikanapha Afilisti ochuluka.”
Certes, si le peuple avait aujourd'hui mangé de la dépouille de ses ennemis, qu'il a trouvée, combien la défaite des Philistins n'aurait-elle pas été plus grande?
31 Tsiku limenelo Aisraeli anapha Afilisti kuchokera ku Mikimasi mpaka ku Ayaloni. Koma Aisraeliwo analefuka kwambiri ndi njala.
Ils battirent donc, en ce jour-là, les Philistins depuis Micmash jusqu'à Ajalon, et le peuple fut extrêmement fatigué.
32 Choncho iwo anathamangira pa zofunkha ndipo anatenga nkhosa, ngʼombe ndi ana angʼombe. Iwo anazipha zonsezi nazidya pamodzi ndi magazi omwe.
Et le peuple se jeta sur le butin, et ils prirent des brebis, et des bœufs et des veaux, et ils les égorgèrent sur la terre; et le peuple les mangeait avec le sang.
33 Koma anthu ena anawuza Sauli kuti, “Taona anthu akuchimwira Yehova pakudya nyama yomwe ili ndi magazi.” Ndipo Sauli anati, “Mwaonetsa kusakhulupirika. Tsopano gubuduzirani mwala waukulu pano.”
Et on le rapporta à Saül, en disant: Voici, le peuple pèche contre l'Éternel, en mangeant la chair avec le sang. Et il dit: Vous avez péché; roulez à l'instant vers moi une grande pierre.
34 Kenaka Sauli anati, “Mwazikanani pakati pa anthu ndi kukawawuza kuti aliyense abwere ndi ngʼombe yake kapena nkhosa yake, ndipo adzayiphe pomwe pano ndi kuyidya. Musachimwire Yehova pakudya nyama imene ili ndi magazi.” Kotero aliyense anabwera ndi ngʼombe yake usiku womwewo ndi kuyipha pomwepo.
Et Saül dit: Allez partout parmi le peuple, et dites-leur que chacun amène vers moi son bœuf, et chacun sa brebis; et vous les égorgerez ici, et vous les mangerez, et vous ne pécherez point contre l'Éternel, en mangeant la chair avec le sang. Et le peuple amena chacun son bœuf, à la main, pendant la nuit, et ils les égorgèrent là.
35 Ndipo Sauli anamangira Yehova guwa. Ili linali guwa loyamba limene Sauli anamangira Yehova.
Et Saül bâtit un autel à l'Éternel; ce fut le premier autel qu'il bâtit à l'Éternel.
36 Sauli anati, “Tiyeni titsatire Afilisti usikuwu ndi kulanda zinthu zawo mpaka mmawa. Tisasiyepo wamoyo ndi mmodzi yemwe.” Ankhondowo anayankha kuti, “Chitani chilichonse chimene chikukomerani.” Koma wansembe anati, “Tipemphe uphungu kwa Mulungu poyamba.”
Puis Saül dit: Descendons à la poursuite des Philistins, pendant la nuit, et pillons-les jusqu'à la clarté du matin, et n'en laissons pas un de reste. Et ils dirent: Fais tout ce qui te semble bon. Mais le sacrificateur dit: Approchons-nous ici de Dieu.
37 Choncho Sauli anafunsa Mulungu kuti, “Kodi ndiwatsatire Afilisti? Kodi mukawapereka mʼmanja mwathu?” Koma Mulungu sanamuyankhe tsiku limenelo.
Alors Saül consulta Dieu: Descendrai-je à la poursuite des Philistins? Les livreras-tu entre les mains d'Israël? Mais il ne lui donna point de réponse ce jour-là.
38 Choncho Sauli anati, “Bwerani kuno nonse atsogoleri a anthu, ndipo tiyeni tione kuti kodi tchimo limeneli lachitika bwanji lero?
Et Saül dit: Approchez ici, vous tous les chefs du peuple; et sachez et voyez comment ce péché a été commis aujourd'hui;
39 Pali Yehova amene amapulumutsa Israeli, ngakhale tchimolo litapezeka ndi mwana wanga Yonatani, iye afe ndithu.” Koma palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthuwo amene anamuyankha.
Car l'Éternel est vivant, lui qui délivre Israël, que cela eût-il été fait par mon fils Jonathan, certainement il mourrait! Mais de tout le peuple nul ne lui répondit.
40 Tsono Sauli anawuza Aisraeli onse kuti, “Inu mukhale mbali imodzi. Ine ndi mwana wanga Yonatani tikhala mbali inayo.” “Chitani chilichonse chimene chikukomerani.”
Puis il dit à tout Israël: Mettez-vous d'un côté, et nous serons de l'autre, moi et Jonathan, mon fils. Le peuple répondit à Saül: Fais ce qui te semble bon.
41 Ndipo Sauli anapemphera kwa Yehova Mulungu wa Israeli kuti, “Chifukwa chiyani simunandiyankhe ine mtumiki wanu lero lino? Ngati tchimoli lipezeka ndi ine kapena ndi Yonatani mwana wanga, Inu Mulungu wa Israeli, aoneke ndi Urimu. Koma ngati wochimwa ndi anthu anu, Aisraeli aoneke Tamimu.” Maere anagwera Sauli ndi Yonatani ndipo anthu anapezeka osalakwa.
Et Saül dit à l'Éternel: Dieu d'Israël! fais connaître la vérité. Et Jonathan et Saül furent désignés, et le peuple échappa.
42 Sauli anati, “Chitani maere pakati pa ine ndi Yonatani mwana wanga.” Ndipo maere anagwera Yonatani.
Et Saül dit: Jetez le sort entre moi et Jonathan, mon fils. Et Jonathan fut désigné.
43 Kenaka Sauli anati kwa Yonatani, “Ndiwuze chimene wachita.” Ndipo Yonatani anamuwuza kuti, “Ine ndinangolawa uchi pangʼono ndi ndodo yangayi. Ndiye ine ndili wokonzeka kufa.”
Alors Saül dit à Jonathan: Déclare-moi ce que tu as fait. Et Jonathan le lui déclara, et dit: J'ai goûté, avec le bout du bâton que j'avais à la main, un peu de miel; me voici, je mourrai.
44 Sauli anati, “Mulungu andilange ngakhale kufa kumene, ngati sufa iwe Yonatani.”
Et Saül dit: Que Dieu me traite dans toute sa rigueur; certainement tu mourras, Jonathan!
45 Koma anthuwo anafunsa Saulo kuti, “Kodi Yonatani afe, iye amene wagwira ntchito iyi yayikulu yopulumutsa Aisraeli? Osatheka! Pali Yehova ngakhale tsitsi ndi limodzi lomwe lapamutu pake silidzathothoka, pakuti wachita zimenezi lero ndi thandizo la Mulungu.” Choncho anthuwo anamupulumutsa Yonatani, ndipo sanaphedwe.
Mais le peuple dit à Saül: Jonathan, qui a opéré cette grande délivrance en Israël, mourrait-il? Cela ne sera point! L'Éternel est vivant! il ne tombera pas à terre un seul des cheveux de sa tête; car c'est avec Dieu qu'il a agi en ce jour. Ainsi le peuple délivra Jonathan, et il ne mourut point.
46 Pambuyo pake Sauli analeka kulondola Afilisti, kenaka anabwerera ku dziko lawo.
Puis Saül s'en retourna de la poursuite des Philistins, et les Philistins s'en allèrent dans leur pays.
47 Sauli ali mtsogoleri wa Israeli, anachita nkhondo ndi adani awa omuzungulira: Mowabu, Amoni, Edomu mafumu a ku Zoba ndi Afilisti. Kulikonse kumene ankapita ankawagonjetsa.
Saül régna donc sur Israël, et fit la guerre de tous côtés contre ses ennemis, contre Moab et contre les Ammonites, contre Édom, contre les rois de Tsoba, et contre les Philistins; partout où il se tournait il portait la terreur.
48 Anachita nkhondo mwamphamvu ndi kugonjetsa Aamaleki. Choncho anapulumutsa Aisraeli mʼmanja mwa anthu amene ankawalanda zinthu zawo.
Il déploya de la vaillance, et battit Amalek, et délivra Israël de la main de ceux qui le pillaient.
49 Ana aamuna a Sauli anali Yonatani, Isivi ndi Maliki-Suwa. Analinso ndi ana aakazi awiri, dzina la mwana wake wamkulu wamkazi linali Merabi ndipo la mwana wake wamngʼono wamkazi linali Mikala.
Or, les fils de Saül étaient Jonathan, Jishui et Malkishua; et quant aux noms de ses deux filles, le nom de l'aînée était Mérab, et le nom de la cadette Mical;
50 Dzina la mkazi wake linali Ahinoamu. Iyeyu anali mwana wa Ahimaazi. Dzina la mkulu wa ankhondo a Sauli linali Abineri mwana wa Neri, mʼbale wa abambo a Sauli.
Et le nom de la femme de Saül était Achinoam, fille d'Achimaats. Et le nom du chef de son armée était Abner, fils de Ner, oncle de Saül.
51 Kisi abambo a Sauli ndi Neri abambo a Abineri anali ana a Abieli.
Et Kis, père de Saül, et Ner, père d'Abner, étaient fils d'Abiel.
52 Pa moyo wake wonse, Sauli ankakhalira kuchita nkhondo pakati pa Israeli ndi Afilisti. Ndipo Sauli ankati akaona munthu aliyense wamphamvu kapena wolimba mtima ankamulemba ntchito mu gulu lake lankhondo.
Et pendant tout le temps de Saül il y eut une guerre violente contre les Philistins; et dès que Saül voyait quelque homme fort, et quelque homme vaillant, il le prenait auprès de lui.

< 1 Samueli 14 >