< 1 Samueli 14 >

1 Tsiku lina Yonatani mwana wa Sauli anawuza mnyamata wake womunyamulira zida zake za nkhondo kuti, “Tiye tiwoloke tipite ku kaboma ka Afilisti tsidya ilo.” Koma iye sanawuze abambo ake.
Un jour, Jonathan, fils de Saül, dit au serviteur qui portait ses armes: "Viens, nous allons attaquer le poste des Philistins qui est là, de l’autre côté"; mais il n’en dit rien à son père.
2 Sauli ankakhala mʼmalire a Gibeya pa tsinde pa mtengo wamakangadza ku Migironi. Anthu amene anali naye analipo 600.
Saül était alors à l’extrémité de la colline, sous le grenadier qui s’élève à Migron, et la troupe sous ses ordres était d’environ six cents hommes.
3 Pakati pawo panalinso Ahiya amene ankavala efodi. Iye anali mwana wa Ahitubi, mʼbale wake wa Ikabodi mwana wa Finehasi, mwana wa Eli, wansembe wa Yehova wa ku Silo. Koma palibe amene anadziwa kuti Yonatani wachoka.
Ahiya, fils d’Ahitoub, frère d’Ikabod, fils de Phinéas, fils d’Héli, était alors prêtre du Seigneur à Silo, et revêtu de l’éphod. Le peuple ignorait également l’entreprise de Jonathan.
4 Pa mpata pamene Yonatani ankafuna kudutsa kukafika ku kaboma ka nkhondo ka Afilisti kunali thanthwe lotsetsereka mbali ina ndi lina lotsetsereka mbali inayo. Thanthwe limodzi linkatchedwa Bozezi ndipo linalo linkatchedwa Seni.
Or, entre les passages par où Jonathan voulait surprendre le poste des Philistins, une pointe de rocher s’élevait d’un côté, et une pointe de rocher de l’autre, l’une appelée Bocêç, l’autre Séné;
5 Thanthwe limodzi linali chakumpoto kuyangʼanana ndi Mikimasi, ndipo thanthwe linalo linali chakummwera kuyangʼanana ndi Geba.
l’une était située vers Mikhmach, au nord, l’autre au midi vers Ghéba.
6 Yonatani anawuza mnyamata wake womunyamulira zida uja kuti, “Tiye tiwoloke tipite ku kaboma ka anthu osachita mdulidwewo. Mwina Yehova adzatigwirira ntchito. Palibe chomuletsa Yehova kutipulumutsa, ngakhale tikhale ambiri kapena ochepa.”
Jonathan donc dit à son écuyer: "Viens, nous allons attaquer le poste de ces incirconcis, peut-être le Seigneur nous fera-t-il réussir; car pour lui point d’obstacle, il peut donner la victoire au petit nombre comme au grand."
7 Mnyamata uja anati, “Chitani chilichonse chimene mtima wanu ukhumba. Ine ndili nanu pamodzi. Chimene mtima wanu ukhumba ndi chomwenso ine ndikhumba.”
L’Écuyer lui répondit: "Agis absolument à ton gré, va où tu veux, je suis prêt à te suivre."
8 Yonatani anati, “Tiye tsono tiwoloke kupita kumene kuli anthuwo ndi kukadzionetsa kwa iwo.
"Ecoute, reprit Jonathan: nous allons nous glisser vers ces hommes, puis nous nous ferons voir à eux.
9 Akatiwuza kuti, ‘Imani pomwepo mpaka tikupezeni,’ ife tikangoyima pomwepo osapita kumene kuli iwoko.
Si alors ils nous disent: "Halte! Nous allons vous joindre", nous resterons en place et ne monterons pas vers eux.
10 Koma akadzati, ‘Bwerani kuno,’ ndiye ife tikapitedi, chifukwa ichi chidzakhala chizindikiro chakuti Yehova wapereka mʼmanja mwathu.”
Mais s’ils disent: "Montez vers nous", nous irons, car l’Eternel nous les aura livrés, et ce mot en sera pour nous le pronostic."
11 Choncho awiriwa anadzionetsa ku kaboma ka nkhondo ka Afilisti. Tsono Afilistiwo anati, “Taonani! Aheberi akutuluka mʼmaenje mʼmene anabisala.”
Lorsqu’ils furent aperçus tous deux par les hommes du poste, les Philistins dirent: "Voilà des Hébreux qui sortent des trous où ils s’étaient cachés."
12 Anthu a ku kaboma kaja anafuwula kwa Yonatani ndi mnyamata wake uja kuti, “Bwerani kuno ndipo tikuphunzitsani phunziro.” Ndipo Yonatani anati kwa mnyamata wake. “Nditsate pakuti Yehova wapereka Afilistiwa mʼmanja mwa Aisraeli.”
Et les hommes du poste, interpellant Jonathan et son écuyer: "Montez ici, dirent-ils, nous avons quelque chose à vous apprendre." Alors Jonathan dit à son écuyer: "Suis-moi là-haut, l’Eternel les livre au pouvoir d’Israël!"
13 Choncho Yonatani anakwera mokwawa, ndipo mnyamata wake uja ankamutsata. Tsono Yonatani anathira nkhondo Afilisti aja namawagwetsa, ndipo mnyamata wake uja ankawapha pambuyo pa iyeyo.
Et Jonathan monta, en s’aidant des mains et des pieds, et son écuyer le suivit; ils tombèrent sous les coups de Jonathan, tandis que l’écuyer donnait la mort à sa suite.
14 Nthawi yoyambayo Yonatani ndi mnyamata wake uja anapha anthu makumi awiri ndipo anawaphera pa malo ochepa okwanira ngati theka la ekala.
Cette première défaite, où Jonathan et son serviteur tuèrent une vingtaine d’hommes, eut lieu dans l’espace d’un demi-arpent de terre environ.
15 Tsono gulu lonse la ankhondo, ndiye kuti iwo amene anali mʼmisasa ndi mʼminda ndiponso iwo amene anali ku kaboma ka ankhondo kaja, onse anagwidwa ndi mantha aakulu. Dzikonso linagwedezeka, choncho anthu anachita mantha koopsa.
L’Effroi fut au camp, dans la campagne, dans toute l’armée; les avant-postes et le corps d’invasion tremblèrent à leur tour; la contrée fut en émoi, et cela devint une terreur de Dieu.
16 Alonda a Sauli a ku Gibeya dziko la Benjamini atangomwaza maso anangoona chigulu cha asilikali chikumwazikana uku ndi uku.
Les sentinelles postées par Saül à Ghibea-de-Benjamin signalèrent cette multitude en désordre, qui courait éperdue.
17 Kenaka Sauli anawawuza anthu amene anali naye kuti, “Awerengeni asilikali kuti muona amene wachoka.” Atawawerenga anapeza kuti Yonatani ndi mnyamata wake womunyamulira zida zake za nkhondo palibe.
Saül dit alors à sa troupe: "Comptez-vous, et voyez qui nous a quittés." On fit l’appel et on constata l’absence de Jonathan et de son écuyer.
18 Tsono Sauli anawuza Ahiya kuti, “Bwera nalo Bokosi la Mulungulo.” (Nthawi imeneyo nʼkuti efodiyo ili ndi Ahiya pamaso pa Aisraeli).
Saül dit à Ahiya: "Fais avancer l’arche du Seigneur!" car l’arche du Seigneur, ce jour-là, était auprès des enfants d’Israël.
19 Pamene Sauli amayankhula ndi wansembe, phokoso limanka likulirakulira mu msasa wa Afilisti, Kotero Sauli anati kwa wansembe, “Leka kuwombeza.”
Mais pendant que Saül parlait au prêtre, la confusion allait croissant dans le camp des Philistins… Alors Saül dit au prêtre: "Retire ta main."
20 Ndipo Sauli ndi asilikali onse amene anali naye anasonkhana kupita kukamenya nkhondo, ndipo anangoona chisokonezo chachikulu kwambiri. Afilisti akuphana okhaokha.
Et Saül se mit en mouvement avec tout son monde, et, arrivés sur le terrain de la lutte, ils les virent s’entre-tuant de leurs glaives dans une effroyable mêlée.
21 Aheberi ena amene kale anali ndi Afilisti mpaka kukakhala ku misasa yawo, iwonso anatembenuka nakhala pamodzi ndi Aisraeli amene ankatsata Sauli ndi Yonatani.
Les Hébreux qui, antérieurement, avaient passé aux Philistins, et qui, répandus dans leur armée, avaient pris part à leur expédition, firent cause commune avec les Israélites rangés sous les ordres de Saül et de Jonathan.
22 Ngakhale Aisraeli amene ankabisala ku dziko lamapiri la Efereimu atamva kuti Afilisti akuthawa, nawonso anawathamangitsa Afilistiwo nawathira nkhondo.
Pareillement, tous les Israélites cachés dans la montagne d’Ephraïm, apprenant la déroute des Philistins, reprirent l’offensive en les poursuivant.
23 Nkhondo inapitirira mpaka kufika ku Beti-Aveni. Choncho Yehova anapulumutsa Aisraeli tsiku limenelo.
L’Eternel donna, en cette occurrence, la victoire à Israël; la lutte s’était étendue jusqu’à Beth-Avên.
24 Koma asilikali a Israeli anavutika tsiku limenelo, chifukwa Sauli anawalumbirira Aisraeli kuti, “Wotembereredwa munthu aliyense amene adzadya kusanade, ine ndisanalipsire adani anga!” Kotero palibe wankhondo aliyense amene analawa chakudya.
Or, les Israélites avaient été surmenés ce jour-là, et Saül avait adjuré le peuple en disant: "Malheur à celui qui prendrait de la nourriture avant le soir, avant que j’aie fait justice de mes ennemis!" Et le peuple entier ne goûta quoi que ce fût.
25 Gulu lonse la ankhondo linalowa mʼnkhalango mmene munali uchi.
Toute l’armée était arrivée à un bois, où la surface du sol était couverte de miel.
26 Atalowa mʼnkhalango, anaona uchi ukukha, koma palibe amene anadya, pakuti ankaopa lumbiro lija.
En arrivant dans le bois, le peuple vit ce miel ruisselant; mais, craignant les effets de l’adjuration, personne n’y porta la main pour en goûter.
27 Koma Yonatani sanamve kuti abambo ake anawalumbirira anthu aja choncho anatenga ndodo yake imene inali mʼdzanja lake ndipo anayipisa mu chisa cha njuchi. Choncho iye anadya uchiwo ndipo mʼmaso mwake munayera.
Toutefois Jonathan, ignorant que son père avait adjuré le peuple, étendit la baguette qu’il tenait à la main, en trempa l’extrémité dans un rayon de miel, et, avec la main, le porta à sa bouche, ce qui lui éclaircit la vue.
28 Kenaka mmodzi mwa Asilikali anamuwuza kuti, “Abambo ako alumbirira anthu nati, ‘Wotembereredwa munthu aliyense amene adye chakudya lero.’ Nʼchifukwa chake anthu alefuka.”
Quelqu’un du peuple s’écria: "Ton père a adjuré le peuple en disant: Malheur à qui prendra de la nourriture aujourd’hui! Et le peuple est exténué."
29 Yonatani anati, “Abambo anga achita chinthu choyipira dziko. Taonani mʼmaso mwanga mwayera chifukwa ndalawa uchiwu pangʼono.
Jonathan répondit "Mon père a fait tort au pays: voyez donc comme mes yeux se sont éclaircis, pour avoir goûté un peu de ce miel!
30 Zikanakhala zabwino kwambiri anthuwa akanadya lero zofunkha za adani awo. Zikanatero tikanapha Afilisti ochuluka.”
Et certes, si le peuple s’était restauré aujourd’hui du butin fait sur les ennemis, combien la défaite des Philistins ne serait-elle pas plus considérable!"
31 Tsiku limenelo Aisraeli anapha Afilisti kuchokera ku Mikimasi mpaka ku Ayaloni. Koma Aisraeliwo analefuka kwambiri ndi njala.
Ce jour-là on tailla en pièces les Philistins, depuis Mikhmach jusqu’à Ayyalôn; mais le peuple était bien harassé.
32 Choncho iwo anathamangira pa zofunkha ndipo anatenga nkhosa, ngʼombe ndi ana angʼombe. Iwo anazipha zonsezi nazidya pamodzi ndi magazi omwe.
Aussi se rua-t-il sur le butin: brebis, bœufs, veaux, ils s’en saisirent, les égorgèrent à même le sol, en mangèrent la chair avec le sang.
33 Koma anthu ena anawuza Sauli kuti, “Taona anthu akuchimwira Yehova pakudya nyama yomwe ili ndi magazi.” Ndipo Sauli anati, “Mwaonetsa kusakhulupirika. Tsopano gubuduzirani mwala waukulu pano.”
On le rapporta à Saül en disant: "Le peuple offense le Seigneur, en mangeant la chair avec le sang!" Et il dit: "Vous agissez en infidèles! Roulez-moi ici sur l’heure une grosse pierre.
34 Kenaka Sauli anati, “Mwazikanani pakati pa anthu ndi kukawawuza kuti aliyense abwere ndi ngʼombe yake kapena nkhosa yake, ndipo adzayiphe pomwe pano ndi kuyidya. Musachimwire Yehova pakudya nyama imene ili ndi magazi.” Kotero aliyense anabwera ndi ngʼombe yake usiku womwewo ndi kuyipha pomwepo.
Répandez-vous dans l’armée, continua Saül, et dites-leur de m’amener chacun son bœuf ou sa menue bête, de l’égorger ici et de la manger; de la sorte, vous ne commettrez pas envers Dieu le péché de manger avec le sang." Et chacun parmi le peuple amena ses bêtes cette même nuit, et on les tua là.
35 Ndipo Sauli anamangira Yehova guwa. Ili linali guwa loyamba limene Sauli anamangira Yehova.
Saül bâtit un autel au Seigneur: ce fut le premier autel qu’il éleva en son honneur.
36 Sauli anati, “Tiyeni titsatire Afilisti usikuwu ndi kulanda zinthu zawo mpaka mmawa. Tisasiyepo wamoyo ndi mmodzi yemwe.” Ankhondowo anayankha kuti, “Chitani chilichonse chimene chikukomerani.” Koma wansembe anati, “Tipemphe uphungu kwa Mulungu poyamba.”
Et Saül dit: "Courons cette nuit à la poursuite des Philistins, accablons-les jusqu’au matin, n’en laissons pas survivre un seul!" On lui répondit: "Fais comme il te plaira…" Mais le prêtre dit: "Approchons-nous d’abord du Seigneur."
37 Choncho Sauli anafunsa Mulungu kuti, “Kodi ndiwatsatire Afilisti? Kodi mukawapereka mʼmanja mwathu?” Koma Mulungu sanamuyankhe tsiku limenelo.
Saül consulta donc le Seigneur: "Dois-je, dit-il, me mettre à la poursuite des Philistins? Les livreras-tu au pouvoir d’Israël?" Mais il ne lui fut pas répondu cette fois.
38 Choncho Sauli anati, “Bwerani kuno nonse atsogoleri a anthu, ndipo tiyeni tione kuti kodi tchimo limeneli lachitika bwanji lero?
Alors Saül dit: "Avancez ici, tous les rangs du peuple, afin de savoir et de constater quel péché s’est commis en ce jour!
39 Pali Yehova amene amapulumutsa Israeli, ngakhale tchimolo litapezeka ndi mwana wanga Yonatani, iye afe ndithu.” Koma palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthuwo amene anamuyankha.
Oui, par le Dieu vivant qui protège Israël, quand il s’agirait de Jonathan mon fils, il devra mourir!" Personne du peuple ne lui répondit.
40 Tsono Sauli anawuza Aisraeli onse kuti, “Inu mukhale mbali imodzi. Ine ndi mwana wanga Yonatani tikhala mbali inayo.” “Chitani chilichonse chimene chikukomerani.”
Et il dit à tout Israël: "Vous, mettez-vous d’un côté; moi et mon fils Jonathan, nous serons de l’autre." Le peuple répondit à Saül: "Agis à ton gré."
41 Ndipo Sauli anapemphera kwa Yehova Mulungu wa Israeli kuti, “Chifukwa chiyani simunandiyankhe ine mtumiki wanu lero lino? Ngati tchimoli lipezeka ndi ine kapena ndi Yonatani mwana wanga, Inu Mulungu wa Israeli, aoneke ndi Urimu. Koma ngati wochimwa ndi anthu anu, Aisraeli aoneke Tamimu.” Maere anagwera Sauli ndi Yonatani ndipo anthu anapezeka osalakwa.
Et Saül, s’adressant à l’Eternel, dit "Dieu d’Israël, fais connaître la vérité!" Le sort atteignit Jonathan et Saül, et écarta le peuple.
42 Sauli anati, “Chitani maere pakati pa ine ndi Yonatani mwana wanga.” Ndipo maere anagwera Yonatani.
Saül dit alors: "Faites l’épreuve entre moi et mon fils Jonathan." Et le sort tomba sur Jonathan.
43 Kenaka Sauli anati kwa Yonatani, “Ndiwuze chimene wachita.” Ndipo Yonatani anamuwuza kuti, “Ine ndinangolawa uchi pangʼono ndi ndodo yangayi. Ndiye ine ndili wokonzeka kufa.”
"Déclare-moi ce que tu as fait!" dit Saül à Jonathan. Celui-ci l’avoua en disant: "J’Ai goûté un peu de miel avec le bout de la baguette que je tenais à la main. Je suis prêt à mourir."
44 Sauli anati, “Mulungu andilange ngakhale kufa kumene, ngati sufa iwe Yonatani.”
Saül répondit: "Dieu me soit toujours en aide aussi vrai que tu vas mourir, Jonathan!"
45 Koma anthuwo anafunsa Saulo kuti, “Kodi Yonatani afe, iye amene wagwira ntchito iyi yayikulu yopulumutsa Aisraeli? Osatheka! Pali Yehova ngakhale tsitsi ndi limodzi lomwe lapamutu pake silidzathothoka, pakuti wachita zimenezi lero ndi thandizo la Mulungu.” Choncho anthuwo anamupulumutsa Yonatani, ndipo sanaphedwe.
Mais le peuple dit à Saül "Quoi! Jonathan mourrait, lui qui a procuré une si grande victoire à Israël! Garde-toi bien, vive Dieu! de faire tomber un cheveu de sa tête, car c’est avec Dieu qu’il a agi en ce jour!" L’Intervention du peuple sauva Jonathan de la mort.
46 Pambuyo pake Sauli analeka kulondola Afilisti, kenaka anabwerera ku dziko lawo.
Saül renonça à poursuivre les Philistins, lesquels regagnèrent leur pays.
47 Sauli ali mtsogoleri wa Israeli, anachita nkhondo ndi adani awa omuzungulira: Mowabu, Amoni, Edomu mafumu a ku Zoba ndi Afilisti. Kulikonse kumene ankapita ankawagonjetsa.
Saül s’assura la royauté d’Israël en combattant tous ses ennemis d’alentour, Moab, les Ammonites, Edom, les rois de Çoba et les Philistins, et sortant vainqueur de toutes ses entreprises.
48 Anachita nkhondo mwamphamvu ndi kugonjetsa Aamaleki. Choncho anapulumutsa Aisraeli mʼmanja mwa anthu amene ankawalanda zinthu zawo.
Il signala sa bravoure en battant Amalec, et délivra Israël de ses déprédateurs.
49 Ana aamuna a Sauli anali Yonatani, Isivi ndi Maliki-Suwa. Analinso ndi ana aakazi awiri, dzina la mwana wake wamkulu wamkazi linali Merabi ndipo la mwana wake wamngʼono wamkazi linali Mikala.
Les fils de Saül étaient: Jonathan, Yichvi et Malkichoua; et ses deux filles avaient nom, l’aînée Mérab, la plus jeune Mikhal.
50 Dzina la mkazi wake linali Ahinoamu. Iyeyu anali mwana wa Ahimaazi. Dzina la mkulu wa ankhondo a Sauli linali Abineri mwana wa Neri, mʼbale wa abambo a Sauli.
Pour la femme de Saül, elle se nommait Ahinoam, fille d’Ahimaaç; et son général d’armée était Abiner, fils de Ner et cousin de Saül:
51 Kisi abambo a Sauli ndi Neri abambo a Abineri anali ana a Abieli.
car Kich, père de Saül, et Ner, père d’Abner, étaient fils d’Abïel.
52 Pa moyo wake wonse, Sauli ankakhalira kuchita nkhondo pakati pa Israeli ndi Afilisti. Ndipo Sauli ankati akaona munthu aliyense wamphamvu kapena wolimba mtima ankamulemba ntchito mu gulu lake lankhondo.
La guerre se continua violente avec les Philistins, tant que vécut Saül; et toutes les fois que Saül remarquait un homme fort, un vaillant combattant, il le faisait entrer dans sa milice.

< 1 Samueli 14 >