< 1 Samueli 14 >

1 Tsiku lina Yonatani mwana wa Sauli anawuza mnyamata wake womunyamulira zida zake za nkhondo kuti, “Tiye tiwoloke tipite ku kaboma ka Afilisti tsidya ilo.” Koma iye sanawuze abambo ake.
Now it happened one day that Jonathan, the son of Saul, said to the young man who carried his armor, "Come, let's go over to the Philistine garrison on the other side." But he did not tell his father.
2 Sauli ankakhala mʼmalire a Gibeya pa tsinde pa mtengo wamakangadza ku Migironi. Anthu amene anali naye analipo 600.
Now Saul stayed in the outskirts of Gibeah under the pomegranate tree by the threshing floor, and the people who were with him were about six hundred men.
3 Pakati pawo panalinso Ahiya amene ankavala efodi. Iye anali mwana wa Ahitubi, mʼbale wake wa Ikabodi mwana wa Finehasi, mwana wa Eli, wansembe wa Yehova wa ku Silo. Koma palibe amene anadziwa kuti Yonatani wachoka.
Now Ahijah was wearing an ephod. He was the son of Ahitub, the brother of Ichabod, the son of Phinehas, the son of Eli, the priest of the LORD in Shiloh. And the people did not know that Jonathan was gone.
4 Pa mpata pamene Yonatani ankafuna kudutsa kukafika ku kaboma ka nkhondo ka Afilisti kunali thanthwe lotsetsereka mbali ina ndi lina lotsetsereka mbali inayo. Thanthwe limodzi linkatchedwa Bozezi ndipo linalo linkatchedwa Seni.
Now on each side of the pass through which Jonathan intended to cross to the Philistine garrison there was a steep cliff on one side and a steep cliff on the other side. And the name of the one was Bozez, and the name of the other Seneh.
5 Thanthwe limodzi linali chakumpoto kuyangʼanana ndi Mikimasi, ndipo thanthwe linalo linali chakummwera kuyangʼanana ndi Geba.
The one cliff was to north in front of Michmash, and the other on the south in front of Geba.
6 Yonatani anawuza mnyamata wake womunyamulira zida uja kuti, “Tiye tiwoloke tipite ku kaboma ka anthu osachita mdulidwewo. Mwina Yehova adzatigwirira ntchito. Palibe chomuletsa Yehova kutipulumutsa, ngakhale tikhale ambiri kapena ochepa.”
Then Jonathan said to the young man who carried his armor, "Come, let's go over to the garrison of these uncircumcised. It may be that the LORD will work for us, for nothing can prevent the LORD from saving by many or by a few."
7 Mnyamata uja anati, “Chitani chilichonse chimene mtima wanu ukhumba. Ine ndili nanu pamodzi. Chimene mtima wanu ukhumba ndi chomwenso ine ndikhumba.”
His armor bearer said to him, "Do all that your heart inclines toward. Look, I am with you, my heart is as your heart."
8 Yonatani anati, “Tiye tsono tiwoloke kupita kumene kuli anthuwo ndi kukadzionetsa kwa iwo.
Then Jonathan said, "Look, we will pass over to the men, and we will reveal ourselves to them.
9 Akatiwuza kuti, ‘Imani pomwepo mpaka tikupezeni,’ ife tikangoyima pomwepo osapita kumene kuli iwoko.
If they say thus to us, 'Wait until we come to you,' then we will stop where we are, and will not go up to them.
10 Koma akadzati, ‘Bwerani kuno,’ ndiye ife tikapitedi, chifukwa ichi chidzakhala chizindikiro chakuti Yehova wapereka mʼmanja mwathu.”
But if they say this, 'Come up to us,' then we will go up; for the LORD has delivered them into our hand. This shall be the sign to us."
11 Choncho awiriwa anadzionetsa ku kaboma ka nkhondo ka Afilisti. Tsono Afilistiwo anati, “Taonani! Aheberi akutuluka mʼmaenje mʼmene anabisala.”
Both of them revealed themselves to the garrison of the Philistines: and the Philistines said, "Look, the Hebrews are coming out of the holes where they had hidden themselves."
12 Anthu a ku kaboma kaja anafuwula kwa Yonatani ndi mnyamata wake uja kuti, “Bwerani kuno ndipo tikuphunzitsani phunziro.” Ndipo Yonatani anati kwa mnyamata wake. “Nditsate pakuti Yehova wapereka Afilistiwa mʼmanja mwa Aisraeli.”
The men of the garrison answered Jonathan and his armor bearer, and said, "Come up to us, and we will show you something." Jonathan said to his armor bearer, "Come up after me; for the LORD has delivered them into the hand of Israel."
13 Choncho Yonatani anakwera mokwawa, ndipo mnyamata wake uja ankamutsata. Tsono Yonatani anathira nkhondo Afilisti aja namawagwetsa, ndipo mnyamata wake uja ankawapha pambuyo pa iyeyo.
Jonathan climbed up on his hands and on his feet, and his armor bearer after him. And they fell before Jonathan; and his armor bearer killed them after him.
14 Nthawi yoyambayo Yonatani ndi mnyamata wake uja anapha anthu makumi awiri ndipo anawaphera pa malo ochepa okwanira ngati theka la ekala.
That first slaughter which Jonathan and his armor bearer made was about twenty men, with arrows and with weapons from flints of the field.
15 Tsono gulu lonse la ankhondo, ndiye kuti iwo amene anali mʼmisasa ndi mʼminda ndiponso iwo amene anali ku kaboma ka ankhondo kaja, onse anagwidwa ndi mantha aakulu. Dzikonso linagwedezeka, choncho anthu anachita mantha koopsa.
And there was a terror in the camp, and in the field, and among all the people. The garrison and even the raiders were terrified. And the earth quaked, and it became a terror of God.
16 Alonda a Sauli a ku Gibeya dziko la Benjamini atangomwaza maso anangoona chigulu cha asilikali chikumwazikana uku ndi uku.
And the watchmen of Saul in Gibeah of Benjamin saw, and look, the multitude was scattering here and there.
17 Kenaka Sauli anawawuza anthu amene anali naye kuti, “Awerengeni asilikali kuti muona amene wachoka.” Atawawerenga anapeza kuti Yonatani ndi mnyamata wake womunyamulira zida zake za nkhondo palibe.
Then Saul said to the people who were with him, "Count now, and see who is missing from us." When they had counted, look, Jonathan and his armor bearer were not there.
18 Tsono Sauli anawuza Ahiya kuti, “Bwera nalo Bokosi la Mulungulo.” (Nthawi imeneyo nʼkuti efodiyo ili ndi Ahiya pamaso pa Aisraeli).
And Saul said to Ahijah, "Bring near the ephod," for he wore the ephod at that time before Israel.
19 Pamene Sauli amayankhula ndi wansembe, phokoso limanka likulirakulira mu msasa wa Afilisti, Kotero Sauli anati kwa wansembe, “Leka kuwombeza.”
And it happened, while Saul was speaking to the priest, that the tumult that was in the camp of the Philistines went on and increased: and Saul said to the priest, "Withdraw your hand."
20 Ndipo Sauli ndi asilikali onse amene anali naye anasonkhana kupita kukamenya nkhondo, ndipo anangoona chisokonezo chachikulu kwambiri. Afilisti akuphana okhaokha.
Saul and all the people who were with him were gathered together, and came to the battle: and look, every man's sword was against his fellow: a very great confusion.
21 Aheberi ena amene kale anali ndi Afilisti mpaka kukakhala ku misasa yawo, iwonso anatembenuka nakhala pamodzi ndi Aisraeli amene ankatsata Sauli ndi Yonatani.
Now the Hebrews who were with the Philistines previously when they went up with them to the camp, they too turned to be with the Israelites who were with Saul and Jonathan.
22 Ngakhale Aisraeli amene ankabisala ku dziko lamapiri la Efereimu atamva kuti Afilisti akuthawa, nawonso anawathamangitsa Afilistiwo nawathira nkhondo.
Likewise all the men of Israel who had hidden themselves in the hill country of Ephraim, when they heard that the Philistines fled, even they also followed closely after them in the battle.
23 Nkhondo inapitirira mpaka kufika ku Beti-Aveni. Choncho Yehova anapulumutsa Aisraeli tsiku limenelo.
So the LORD saved Israel that day, and the battle passed over by Beth Aven. And all the people with Saul were about ten thousand men. And the battle extended itself into every city in the hill country of Ephraim.
24 Koma asilikali a Israeli anavutika tsiku limenelo, chifukwa Sauli anawalumbirira Aisraeli kuti, “Wotembereredwa munthu aliyense amene adzadya kusanade, ine ndisanalipsire adani anga!” Kotero palibe wankhondo aliyense amene analawa chakudya.
And Saul committed a great blunder that day, for he had placed the people under an oath, saying, "Cursed is the man who eats any food until it is evening, and I am avenged of my enemies." So none of the people tasted food.
25 Gulu lonse la ankhondo linalowa mʼnkhalango mmene munali uchi.
Now all the people came upon a honeycomb, and there was honey on the ground.
26 Atalowa mʼnkhalango, anaona uchi ukukha, koma palibe amene anadya, pakuti ankaopa lumbiro lija.
And when the people came upon the honeycomb, look, its bees had left, but no man would raise his hand to his mouth, for the people feared the oath.
27 Koma Yonatani sanamve kuti abambo ake anawalumbirira anthu aja choncho anatenga ndodo yake imene inali mʼdzanja lake ndipo anayipisa mu chisa cha njuchi. Choncho iye anadya uchiwo ndipo mʼmaso mwake munayera.
But Jonathan did not hear when his father commanded the people with the oath, so he put forth the end of the staff that was in his hand, and dipped it in the honeycomb, and raised his hand to his mouth, and his eyes brightened.
28 Kenaka mmodzi mwa Asilikali anamuwuza kuti, “Abambo ako alumbirira anthu nati, ‘Wotembereredwa munthu aliyense amene adye chakudya lero.’ Nʼchifukwa chake anthu alefuka.”
Then one of the people answered, and said, "Your father directly commanded the people with an oath, saying, 'Cursed is the man who eats food this day.'" The people were faint.
29 Yonatani anati, “Abambo anga achita chinthu choyipira dziko. Taonani mʼmaso mwanga mwayera chifukwa ndalawa uchiwu pangʼono.
Then Jonathan said, "My father has troubled the land. Please look how my eyes have been enlightened, because I tasted a little of this honey.
30 Zikanakhala zabwino kwambiri anthuwa akanadya lero zofunkha za adani awo. Zikanatero tikanapha Afilisti ochuluka.”
How much better if the people had eaten freely today of the spoil of their enemies when they found it, for the slaughter among the Philistines would have been greater."
31 Tsiku limenelo Aisraeli anapha Afilisti kuchokera ku Mikimasi mpaka ku Ayaloni. Koma Aisraeliwo analefuka kwambiri ndi njala.
They struck of the Philistines that day from Michmash to Aijalon. The people were very faint;
32 Choncho iwo anathamangira pa zofunkha ndipo anatenga nkhosa, ngʼombe ndi ana angʼombe. Iwo anazipha zonsezi nazidya pamodzi ndi magazi omwe.
and the people pounced upon the spoil, and took sheep, and cattle, and calves, and killed them on the ground; and the people ate them with the blood.
33 Koma anthu ena anawuza Sauli kuti, “Taona anthu akuchimwira Yehova pakudya nyama yomwe ili ndi magazi.” Ndipo Sauli anati, “Mwaonetsa kusakhulupirika. Tsopano gubuduzirani mwala waukulu pano.”
Then they told Saul, saying, "Look, the people are sinning against the LORD, in that they eat meat with the blood." He said, "You have dealt treacherously. Roll a large stone to me this day."
34 Kenaka Sauli anati, “Mwazikanani pakati pa anthu ndi kukawawuza kuti aliyense abwere ndi ngʼombe yake kapena nkhosa yake, ndipo adzayiphe pomwe pano ndi kuyidya. Musachimwire Yehova pakudya nyama imene ili ndi magazi.” Kotero aliyense anabwera ndi ngʼombe yake usiku womwewo ndi kuyipha pomwepo.
And Saul said, "Disperse yourselves among the people, and say to them, 'Each one of you bring to me his ox or his sheep, and slaughter them here and eat, and do not sin against the LORD by eating with the blood.'" So everyone of the people brought whatever he had at hand with him, and slaughtered it there.
35 Ndipo Sauli anamangira Yehova guwa. Ili linali guwa loyamba limene Sauli anamangira Yehova.
Saul built an altar to the LORD. This was the first altar that he built to the LORD.
36 Sauli anati, “Tiyeni titsatire Afilisti usikuwu ndi kulanda zinthu zawo mpaka mmawa. Tisasiyepo wamoyo ndi mmodzi yemwe.” Ankhondowo anayankha kuti, “Chitani chilichonse chimene chikukomerani.” Koma wansembe anati, “Tipemphe uphungu kwa Mulungu poyamba.”
Saul said, "Let us go down after the Philistines by night, and take spoil among them until the morning light, and let us not leave a man of them." They said, "Do whatever seems good to you." Then the priest said, "Let us draw near here to God."
37 Choncho Sauli anafunsa Mulungu kuti, “Kodi ndiwatsatire Afilisti? Kodi mukawapereka mʼmanja mwathu?” Koma Mulungu sanamuyankhe tsiku limenelo.
Saul asked counsel of God, "Shall I go down after the Philistines? Will you deliver them into the hand of Israel?" But he did not answer him that day.
38 Choncho Sauli anati, “Bwerani kuno nonse atsogoleri a anthu, ndipo tiyeni tione kuti kodi tchimo limeneli lachitika bwanji lero?
And Saul said, "Come here, all you leaders of the people; and investigate and see how this sin has arisen today.
39 Pali Yehova amene amapulumutsa Israeli, ngakhale tchimolo litapezeka ndi mwana wanga Yonatani, iye afe ndithu.” Koma palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthuwo amene anamuyankha.
For, as the LORD lives, who saves Israel, though it is in Jonathan my son, he shall surely die." But there was not a man among all the people who answered him.
40 Tsono Sauli anawuza Aisraeli onse kuti, “Inu mukhale mbali imodzi. Ine ndi mwana wanga Yonatani tikhala mbali inayo.” “Chitani chilichonse chimene chikukomerani.”
Then he said to all Israel, "You be on one side, and I and Jonathan my son will be on the other side." The people said to Saul, "Do what seems good to you."
41 Ndipo Sauli anapemphera kwa Yehova Mulungu wa Israeli kuti, “Chifukwa chiyani simunandiyankhe ine mtumiki wanu lero lino? Ngati tchimoli lipezeka ndi ine kapena ndi Yonatani mwana wanga, Inu Mulungu wa Israeli, aoneke ndi Urimu. Koma ngati wochimwa ndi anthu anu, Aisraeli aoneke Tamimu.” Maere anagwera Sauli ndi Yonatani ndipo anthu anapezeka osalakwa.
Therefore Saul said, "LORD, God of Israel, why have you not answered your servant this day? If this sin is mine or in Jonathan my son, LORD, God of Israel, give Urim. But if this sin is in your people Israel, give Thummim." And Jonathan and Saul were chosen, but the people were cleared.
42 Sauli anati, “Chitani maere pakati pa ine ndi Yonatani mwana wanga.” Ndipo maere anagwera Yonatani.
And Saul said, "Cast lots between me and Jonathan my son. Whomever the LORD shall indicate to be taken by lot, let him die." And the people said to Saul, "This thing is not to be." And Saul prevailed over the people, and they cast lots between him and Jonathan his son. And Jonathan was selected.
43 Kenaka Sauli anati kwa Yonatani, “Ndiwuze chimene wachita.” Ndipo Yonatani anamuwuza kuti, “Ine ndinangolawa uchi pangʼono ndi ndodo yangayi. Ndiye ine ndili wokonzeka kufa.”
Then Saul said to Jonathan, "Tell me what you have done." And Jonathan told him, and said, "I certainly did taste a little honey with the end of the staff that was in my hand; and look, I must die."
44 Sauli anati, “Mulungu andilange ngakhale kufa kumene, ngati sufa iwe Yonatani.”
And Saul said, "God do the same to me and more also if you are not put to death this day."
45 Koma anthuwo anafunsa Saulo kuti, “Kodi Yonatani afe, iye amene wagwira ntchito iyi yayikulu yopulumutsa Aisraeli? Osatheka! Pali Yehova ngakhale tsitsi ndi limodzi lomwe lapamutu pake silidzathothoka, pakuti wachita zimenezi lero ndi thandizo la Mulungu.” Choncho anthuwo anamupulumutsa Yonatani, ndipo sanaphedwe.
The people said to Saul, "Shall he who has worked this great salvation in Israel die today? As the LORD lives, there shall not one hair of his head fall to the ground; for he has worked with God this day." So the people rescued Jonathan, and he did not die.
46 Pambuyo pake Sauli analeka kulondola Afilisti, kenaka anabwerera ku dziko lawo.
Then Saul went up from following the Philistines; and the Philistines went to their own place.
47 Sauli ali mtsogoleri wa Israeli, anachita nkhondo ndi adani awa omuzungulira: Mowabu, Amoni, Edomu mafumu a ku Zoba ndi Afilisti. Kulikonse kumene ankapita ankawagonjetsa.
Now when Saul had taken the kingdom over Israel, he fought against all his enemies on every side, against Moab, and against the people of Ammon, and against Edom, and against Beth Rehob, and against the king of Zobah, and against the Philistines; and wherever he turned, he was victorious.
48 Anachita nkhondo mwamphamvu ndi kugonjetsa Aamaleki. Choncho anapulumutsa Aisraeli mʼmanja mwa anthu amene ankawalanda zinthu zawo.
And he did valiantly, and struck Amalek, and delivered Israel out of the hand of its plunderers.
49 Ana aamuna a Sauli anali Yonatani, Isivi ndi Maliki-Suwa. Analinso ndi ana aakazi awiri, dzina la mwana wake wamkulu wamkazi linali Merabi ndipo la mwana wake wamngʼono wamkazi linali Mikala.
Now the sons of Saul were Jonathan, and Jishvi, and Malkishua; and the names of his two daughters were these: the name of the firstborn Merob, and the name of the younger Mikal:
50 Dzina la mkazi wake linali Ahinoamu. Iyeyu anali mwana wa Ahimaazi. Dzina la mkulu wa ankhondo a Sauli linali Abineri mwana wa Neri, mʼbale wa abambo a Sauli.
and the name of Saul's wife was Ahinoam the daughter of Ahimaaz. The name of the commander of his army was Abiner the son of Ner, Saul's uncle.
51 Kisi abambo a Sauli ndi Neri abambo a Abineri anali ana a Abieli.
Kish was the father of Saul; and Ner the father of Abner was the son of Abiel.
52 Pa moyo wake wonse, Sauli ankakhalira kuchita nkhondo pakati pa Israeli ndi Afilisti. Ndipo Sauli ankati akaona munthu aliyense wamphamvu kapena wolimba mtima ankamulemba ntchito mu gulu lake lankhondo.
There was severe war against the Philistines all the days of Saul: and when Saul saw any mighty man, or any valiant man, he took him to him.

< 1 Samueli 14 >