< 1 Samueli 14 >

1 Tsiku lina Yonatani mwana wa Sauli anawuza mnyamata wake womunyamulira zida zake za nkhondo kuti, “Tiye tiwoloke tipite ku kaboma ka Afilisti tsidya ilo.” Koma iye sanawuze abambo ake.
Now it fell upon a day that Jonathan the son of Saul said to the young man who bore his armor, Come, and let us go over to the Philistines' garrison that is on yonder side. But he did not tell his father.
2 Sauli ankakhala mʼmalire a Gibeya pa tsinde pa mtengo wamakangadza ku Migironi. Anthu amene anali naye analipo 600.
And Saul abode in the outermost part of Gibeah under the pomegranate tree which is in Migron. And the people who were with him were about six hundred men,
3 Pakati pawo panalinso Ahiya amene ankavala efodi. Iye anali mwana wa Ahitubi, mʼbale wake wa Ikabodi mwana wa Finehasi, mwana wa Eli, wansembe wa Yehova wa ku Silo. Koma palibe amene anadziwa kuti Yonatani wachoka.
and Ahijah, the son of Ahitub, Ichabod's brother, the son of Phinehas, the son of Eli, the priest of Jehovah in Shiloh, wearing an ephod. And the people did not know that Jonathan was gone.
4 Pa mpata pamene Yonatani ankafuna kudutsa kukafika ku kaboma ka nkhondo ka Afilisti kunali thanthwe lotsetsereka mbali ina ndi lina lotsetsereka mbali inayo. Thanthwe limodzi linkatchedwa Bozezi ndipo linalo linkatchedwa Seni.
And between the passes by which Jonathan sought to go over to the Philistines' garrison, there was a rocky crag on the one side, and a rocky crag on the other side. And the name of the one was Bozez, and the name of the other Seneh.
5 Thanthwe limodzi linali chakumpoto kuyangʼanana ndi Mikimasi, ndipo thanthwe linalo linali chakummwera kuyangʼanana ndi Geba.
The one crag rose up on the north in front of Michmash, and the other on the south in front of Geba.
6 Yonatani anawuza mnyamata wake womunyamulira zida uja kuti, “Tiye tiwoloke tipite ku kaboma ka anthu osachita mdulidwewo. Mwina Yehova adzatigwirira ntchito. Palibe chomuletsa Yehova kutipulumutsa, ngakhale tikhale ambiri kapena ochepa.”
And Jonathan said to the young man who bore his armor, Come, and let us go over to the garrison of these uncircumcised. It may be that Jehovah will work for us, for there is no limitation to Jehovah to save by many or by few.
7 Mnyamata uja anati, “Chitani chilichonse chimene mtima wanu ukhumba. Ine ndili nanu pamodzi. Chimene mtima wanu ukhumba ndi chomwenso ine ndikhumba.”
And his armor bearer said to him, Do all that is in thy heart. Turn thee, behold, I am with thee according to thy heart.
8 Yonatani anati, “Tiye tsono tiwoloke kupita kumene kuli anthuwo ndi kukadzionetsa kwa iwo.
Then Jonathan said, Behold, we will pass over to the men, and we will disclose ourselves to them.
9 Akatiwuza kuti, ‘Imani pomwepo mpaka tikupezeni,’ ife tikangoyima pomwepo osapita kumene kuli iwoko.
If they say thus to us, Tarry until we come to you, then we will stand still in our place, and will not go up to them.
10 Koma akadzati, ‘Bwerani kuno,’ ndiye ife tikapitedi, chifukwa ichi chidzakhala chizindikiro chakuti Yehova wapereka mʼmanja mwathu.”
But if they say thus, Come up to us, then we will go up, for Jehovah has delivered them into our hand, and this shall be the sign to us.
11 Choncho awiriwa anadzionetsa ku kaboma ka nkhondo ka Afilisti. Tsono Afilistiwo anati, “Taonani! Aheberi akutuluka mʼmaenje mʼmene anabisala.”
And both of them disclosed themselves to the garrison of the Philistines. And the Philistines said, Behold, the Hebrews come forth out of the holes where they had hid themselves.
12 Anthu a ku kaboma kaja anafuwula kwa Yonatani ndi mnyamata wake uja kuti, “Bwerani kuno ndipo tikuphunzitsani phunziro.” Ndipo Yonatani anati kwa mnyamata wake. “Nditsate pakuti Yehova wapereka Afilistiwa mʼmanja mwa Aisraeli.”
And the men of the garrison answered Jonathan and his armor bearer, and said, Come up to us, and we will show you a thing. And Jonathan said to his armor bearer, Come up after me, for Jehovah has delivered them into the hand of Israel.
13 Choncho Yonatani anakwera mokwawa, ndipo mnyamata wake uja ankamutsata. Tsono Yonatani anathira nkhondo Afilisti aja namawagwetsa, ndipo mnyamata wake uja ankawapha pambuyo pa iyeyo.
And Jonathan climbed up upon his hands and upon his feet, and his armor bearer after him. And they fell before Jonathan, and his armor bearer killed them after him.
14 Nthawi yoyambayo Yonatani ndi mnyamata wake uja anapha anthu makumi awiri ndipo anawaphera pa malo ochepa okwanira ngati theka la ekala.
And that first slaughter, which Jonathan and his armor bearer made, was about twenty men, within as it were half a furrow's length in an acre of land.
15 Tsono gulu lonse la ankhondo, ndiye kuti iwo amene anali mʼmisasa ndi mʼminda ndiponso iwo amene anali ku kaboma ka ankhondo kaja, onse anagwidwa ndi mantha aakulu. Dzikonso linagwedezeka, choncho anthu anachita mantha koopsa.
And there was a trembling in the camp, in the field, and among all the people. The garrison, and the spoilers, they also trembled. And the earth quaked, so there was an exceedingly great trembling.
16 Alonda a Sauli a ku Gibeya dziko la Benjamini atangomwaza maso anangoona chigulu cha asilikali chikumwazikana uku ndi uku.
And the watchmen of Saul in Gibeah of Benjamin looked, and, behold, the multitude melted away, and they went here and there.
17 Kenaka Sauli anawawuza anthu amene anali naye kuti, “Awerengeni asilikali kuti muona amene wachoka.” Atawawerenga anapeza kuti Yonatani ndi mnyamata wake womunyamulira zida zake za nkhondo palibe.
Then Saul said to the people who were with him, Number now, and see who has gone from us. And when they had numbered, behold, Jonathan and his armor bearer were not there.
18 Tsono Sauli anawuza Ahiya kuti, “Bwera nalo Bokosi la Mulungulo.” (Nthawi imeneyo nʼkuti efodiyo ili ndi Ahiya pamaso pa Aisraeli).
And Saul said to Ahijah, Bring here the ark of God. For the ark of God was there at that time with the sons of Israel.
19 Pamene Sauli amayankhula ndi wansembe, phokoso limanka likulirakulira mu msasa wa Afilisti, Kotero Sauli anati kwa wansembe, “Leka kuwombeza.”
And it came to pass, while Saul talked to the priest, that the tumult that was in the camp of the Philistines went on and increased. And Saul said to the priest, Withdraw thy hand.
20 Ndipo Sauli ndi asilikali onse amene anali naye anasonkhana kupita kukamenya nkhondo, ndipo anangoona chisokonezo chachikulu kwambiri. Afilisti akuphana okhaokha.
And Saul and all the people who were with him were gathered together, and came to the battle. And, behold, every man's sword was against his fellow, and there was a very great discomfiture.
21 Aheberi ena amene kale anali ndi Afilisti mpaka kukakhala ku misasa yawo, iwonso anatembenuka nakhala pamodzi ndi Aisraeli amene ankatsata Sauli ndi Yonatani.
Now the Hebrews who were with the Philistines as formerly, and who went up with them into the camp, from the country round about, even they also turned to be with the Israelites who were with Saul and Jonathan.
22 Ngakhale Aisraeli amene ankabisala ku dziko lamapiri la Efereimu atamva kuti Afilisti akuthawa, nawonso anawathamangitsa Afilistiwo nawathira nkhondo.
Likewise all the men of Israel who had hid themselves in the hill-country of Ephraim, when they heard that the Philistines fled, even they also followed close after them in the battle.
23 Nkhondo inapitirira mpaka kufika ku Beti-Aveni. Choncho Yehova anapulumutsa Aisraeli tsiku limenelo.
So Jehovah saved Israel that day, and the battle passed over by Beth-aven.
24 Koma asilikali a Israeli anavutika tsiku limenelo, chifukwa Sauli anawalumbirira Aisraeli kuti, “Wotembereredwa munthu aliyense amene adzadya kusanade, ine ndisanalipsire adani anga!” Kotero palibe wankhondo aliyense amene analawa chakudya.
And the men of Israel were distressed that day, for Saul had adjured the people, saying, Cursed be the man who eats any food until it be evening, and I be avenged on my enemies. So none of the people tasted food.
25 Gulu lonse la ankhondo linalowa mʼnkhalango mmene munali uchi.
And all the people came into the forest, and there was honey upon the ground.
26 Atalowa mʼnkhalango, anaona uchi ukukha, koma palibe amene anadya, pakuti ankaopa lumbiro lija.
And when the people came to the forest, behold, the honey dropped, but no man put his hand to his mouth, for the people feared the oath.
27 Koma Yonatani sanamve kuti abambo ake anawalumbirira anthu aja choncho anatenga ndodo yake imene inali mʼdzanja lake ndipo anayipisa mu chisa cha njuchi. Choncho iye anadya uchiwo ndipo mʼmaso mwake munayera.
But Jonathan heard not when his father charged the people with the oath, therefore he put forth the end of the rod that was in his hand, and dipped it in the honeycomb, and put his hand to his mouth, and his eyes were enlightened.
28 Kenaka mmodzi mwa Asilikali anamuwuza kuti, “Abambo ako alumbirira anthu nati, ‘Wotembereredwa munthu aliyense amene adye chakudya lero.’ Nʼchifukwa chake anthu alefuka.”
Then one of the people answered, and said, Thy father strictly charged the people with an oath, saying, Cursed be the man who eats food this day, and the people were faint.
29 Yonatani anati, “Abambo anga achita chinthu choyipira dziko. Taonani mʼmaso mwanga mwayera chifukwa ndalawa uchiwu pangʼono.
Then Jonathan said, My father has troubled the land. See, I pray you, how my eyes have been enlightened because I tasted a little of this honey.
30 Zikanakhala zabwino kwambiri anthuwa akanadya lero zofunkha za adani awo. Zikanatero tikanapha Afilisti ochuluka.”
How much more, if haply the people had eaten freely today of the spoil of their enemies which they found? For now there has been no great slaughter among the Philistines.
31 Tsiku limenelo Aisraeli anapha Afilisti kuchokera ku Mikimasi mpaka ku Ayaloni. Koma Aisraeliwo analefuka kwambiri ndi njala.
And they smote of the Philistines that day from Michmash to Aijalon. And the people were very faint,
32 Choncho iwo anathamangira pa zofunkha ndipo anatenga nkhosa, ngʼombe ndi ana angʼombe. Iwo anazipha zonsezi nazidya pamodzi ndi magazi omwe.
and the people flew upon the spoil, and took sheep, and oxen, and calves, and killed them on the ground. And the people ate them with the blood.
33 Koma anthu ena anawuza Sauli kuti, “Taona anthu akuchimwira Yehova pakudya nyama yomwe ili ndi magazi.” Ndipo Sauli anati, “Mwaonetsa kusakhulupirika. Tsopano gubuduzirani mwala waukulu pano.”
Then they told Saul, saying, Behold, the people sin against Jehovah, in that they eat with the blood. And he said, ye have dealt treacherously. Roll a great stone to me this day.
34 Kenaka Sauli anati, “Mwazikanani pakati pa anthu ndi kukawawuza kuti aliyense abwere ndi ngʼombe yake kapena nkhosa yake, ndipo adzayiphe pomwe pano ndi kuyidya. Musachimwire Yehova pakudya nyama imene ili ndi magazi.” Kotero aliyense anabwera ndi ngʼombe yake usiku womwewo ndi kuyipha pomwepo.
And Saul said, Disperse yourselves among the people, and say to them, Bring me here every man his ox, and every man his sheep, and kill them here, and eat. And sin not against Jehovah in eating with the blood. And all the people brought every man his ox with him that night, and killed them there.
35 Ndipo Sauli anamangira Yehova guwa. Ili linali guwa loyamba limene Sauli anamangira Yehova.
And Saul built an altar to Jehovah; the same was the first altar that he built to Jehovah.
36 Sauli anati, “Tiyeni titsatire Afilisti usikuwu ndi kulanda zinthu zawo mpaka mmawa. Tisasiyepo wamoyo ndi mmodzi yemwe.” Ankhondowo anayankha kuti, “Chitani chilichonse chimene chikukomerani.” Koma wansembe anati, “Tipemphe uphungu kwa Mulungu poyamba.”
And Saul said, Let us go down after the Philistines by night, and take spoil among them until the morning light, and let us not leave a man of them. And they said, Do whatever seems good to thee. Then the priest said, Let us draw near here to God.
37 Choncho Sauli anafunsa Mulungu kuti, “Kodi ndiwatsatire Afilisti? Kodi mukawapereka mʼmanja mwathu?” Koma Mulungu sanamuyankhe tsiku limenelo.
And Saul asked counsel of God, Shall I go down after the Philistines? Will thou deliver them into the hand of Israel? But he did not answer him that day.
38 Choncho Sauli anati, “Bwerani kuno nonse atsogoleri a anthu, ndipo tiyeni tione kuti kodi tchimo limeneli lachitika bwanji lero?
And Saul said, Draw near here, all ye chiefs of the people, and know and see how this sin has been this day.
39 Pali Yehova amene amapulumutsa Israeli, ngakhale tchimolo litapezeka ndi mwana wanga Yonatani, iye afe ndithu.” Koma palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthuwo amene anamuyankha.
For, as Jehovah lives, who saves Israel, though it be in Jonathan my son, he shall surely die. But there was not a man among all the people who answered him.
40 Tsono Sauli anawuza Aisraeli onse kuti, “Inu mukhale mbali imodzi. Ine ndi mwana wanga Yonatani tikhala mbali inayo.” “Chitani chilichonse chimene chikukomerani.”
Then he said to all Israel, Be ye on one side, and I and Jonathan my son will be on the other side. And the people said to Saul, Do what seems good to thee.
41 Ndipo Sauli anapemphera kwa Yehova Mulungu wa Israeli kuti, “Chifukwa chiyani simunandiyankhe ine mtumiki wanu lero lino? Ngati tchimoli lipezeka ndi ine kapena ndi Yonatani mwana wanga, Inu Mulungu wa Israeli, aoneke ndi Urimu. Koma ngati wochimwa ndi anthu anu, Aisraeli aoneke Tamimu.” Maere anagwera Sauli ndi Yonatani ndipo anthu anapezeka osalakwa.
Therefore Saul said to Jehovah, the God of Israel, Show the right. And Jonathan and Saul were taken by lot, but the people escaped.
42 Sauli anati, “Chitani maere pakati pa ine ndi Yonatani mwana wanga.” Ndipo maere anagwera Yonatani.
And Saul said, Cast lots between me and Jonathan my son. And Jonathan was taken.
43 Kenaka Sauli anati kwa Yonatani, “Ndiwuze chimene wachita.” Ndipo Yonatani anamuwuza kuti, “Ine ndinangolawa uchi pangʼono ndi ndodo yangayi. Ndiye ine ndili wokonzeka kufa.”
Then Saul said to Jonathan, Tell me what thou have done. And Jonathan told him, and said, I did certainly taste a little honey with the end of the rod that was in my hand. And, lo, I must die.
44 Sauli anati, “Mulungu andilange ngakhale kufa kumene, ngati sufa iwe Yonatani.”
And Saul said, God do so and more also, for thou shall surely die, Jonathan.
45 Koma anthuwo anafunsa Saulo kuti, “Kodi Yonatani afe, iye amene wagwira ntchito iyi yayikulu yopulumutsa Aisraeli? Osatheka! Pali Yehova ngakhale tsitsi ndi limodzi lomwe lapamutu pake silidzathothoka, pakuti wachita zimenezi lero ndi thandizo la Mulungu.” Choncho anthuwo anamupulumutsa Yonatani, ndipo sanaphedwe.
And the people said to Saul, Shall Jonathan die, who has wrought this great salvation in Israel? Far from it. As Jehovah lives, there shall not one hair of his head fall to the ground, for he has wrought with God this day. So the people rescued Jonathan, that he did not die.
46 Pambuyo pake Sauli analeka kulondola Afilisti, kenaka anabwerera ku dziko lawo.
Then Saul went up from following the Philistines, and the Philistines went to their own place.
47 Sauli ali mtsogoleri wa Israeli, anachita nkhondo ndi adani awa omuzungulira: Mowabu, Amoni, Edomu mafumu a ku Zoba ndi Afilisti. Kulikonse kumene ankapita ankawagonjetsa.
Now when Saul had taken the kingdom over Israel, he fought against all his enemies on every side, against Moab, and against the sons of Ammon, and against Edom, and against the kings of Zobah, and against the Philistines. And wherever he turned himself, he put them to the worse.
48 Anachita nkhondo mwamphamvu ndi kugonjetsa Aamaleki. Choncho anapulumutsa Aisraeli mʼmanja mwa anthu amene ankawalanda zinthu zawo.
And he did valiantly, and smote the Amalekites, and delivered Israel out of the hands of those who despoiled them.
49 Ana aamuna a Sauli anali Yonatani, Isivi ndi Maliki-Suwa. Analinso ndi ana aakazi awiri, dzina la mwana wake wamkulu wamkazi linali Merabi ndipo la mwana wake wamngʼono wamkazi linali Mikala.
Now the sons of Saul were Jonathan, and Ishvi, and Malchishua. And the names of his two daughters were these: the name of the firstborn Merab, and the name of the younger Michal.
50 Dzina la mkazi wake linali Ahinoamu. Iyeyu anali mwana wa Ahimaazi. Dzina la mkulu wa ankhondo a Sauli linali Abineri mwana wa Neri, mʼbale wa abambo a Sauli.
And the name of Saul's wife was Ahinoam the daughter of Ahimaaz. And the name of the captain of his army was Abner the son of Ner, Saul's uncle.
51 Kisi abambo a Sauli ndi Neri abambo a Abineri anali ana a Abieli.
And Kish was the father of Saul, and Ner the father of Abner was the son of Abiel.
52 Pa moyo wake wonse, Sauli ankakhalira kuchita nkhondo pakati pa Israeli ndi Afilisti. Ndipo Sauli ankati akaona munthu aliyense wamphamvu kapena wolimba mtima ankamulemba ntchito mu gulu lake lankhondo.
And there was great war against the Philistines all the days of Saul. And when Saul saw any mighty man, or any valiant man, he took him to him.

< 1 Samueli 14 >