< 1 Samueli 13 >

1 Sauli analowa ufumu ali ndi zaka makumi atatu, ndipo analamulira Israeli kwa zaka 42.
When he began to reign, Saul was the son of one year, and he reigned over Israel for two years.
2 Nthawi ina Sauli anasankha Aisraeli 3,000. Mwa iwowa, 2,000 anali ndi Sauliyo ku Mikimasi ndi ku dziko la mapiri ku Beteli, ndipo 1,000 anali ndi Yonatani ku Gibeya ku Benjamini. Anthu ena onse otsala anawabweza kwawo.
And Saul chose for himself three thousand men of Israel. And two thousand were with Saul at Michmash and at mount Bethel. Then one thousand were with Jonathan at Gibeah of Benjamin. But the remainder of the people, he sent back, each one to his own tent.
3 Yonatani anakantha mkulu wa ankhondo wa Afilisti ku Geba, ndipo Afilisti anamva kuti Aheberi awukira. Tsono Sauli anawuza amithenga kuti alize lipenga mʼdziko lonse la Israeli.
And Jonathan struck the garrison of the Philistines, which was in Gibeah. And when the Philistines had heard about it, Saul sounded the trumpet over all the land, saying, “Let the Hebrews listen.”
4 Choncho Aisraeli onse anamva kuti Sauli wakantha mkulu wa ankhondo Wachifilisiti ndi kuti Afilisti anayipidwa nawo Aisraeli. Ndiye anthu anayitanidwa kuti abwere kwa Sauli ku Giligala.
And all of Israel heard this report, that Saul had struck the garrison of the Philistines. And Israel raised himself up against the Philistines. Then the people cried out to Saul at Gilgal.
5 Tsono Afilisti anasonkhana kuti amenyane ndi Aisraeli. Iwo anali ndi magaleta 3,000, okwera pa akavalo 2,000 ndiponso asilikali kuchuluka kwake ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja. Iwo anapita ndi kukamanga misasa yawo ku Mikimasi, kummawa kwa Beti-Aveni.
And the Philistines gathered to do battle against Israel, thirty thousand chariots, and six thousand horsemen, and the remainder of the common people, who were very many, like the sand that is on the shore of the sea. And ascending, they encamped at Michmash, toward the east of Bethaven.
6 Pamene Aisraeli anaona kuti anali pamavuto akulu, poti anali atapanikizidwa kwambiri, anabisala mʼmapanga, mʼmaenje, mʼmatanthwe, mʼmakwalala ndi mʼzitsime.
And when the men of Israel had seen themselves to be in a narrowed position, they hid themselves in caves, and in out of the way places, and in rocks, and in hollows, and in pits (for the people were distressed).
7 Ahebri ena anawoloka Yorodani mpaka kukafika ku dziko la Gadi ndi ku Giliyadi. Koma Sauli anakhalabe ku Giligala ndipo ankhondo onse amene anali naye anali njenjenje ndi mantha.
Then some of the Hebrews crossed over the Jordan, into the land of Gad and Gilead. And while Saul was still at Gilgal, the entire people who followed him were terrified.
8 Saulo anadikirira masiku asanu ndi awiri, monga mwa nthawi imene ananena Samueli. Koma Samueli sanabwere ku Giligala, ndipo anthu anayamba kumuthawa Sauli uja.
But he waited for seven days, in accord with what was agreed with Samuel. But Samuel did not arrive at Gilgal, for the people were scattering away from him.
9 Kotero iye anati, “Bwera nayoni nsembe yopsereza ndi nsembe ya chiyanjano.” Ndipo Sauli anapereka nsembe yopsereza.
Therefore, Saul said, “Bring me the holocaust and the peace offerings.” And he offered the holocaust.
10 Atangomaliza kupereka nsembe, anangoona Samueli watulukira ndipo Sauli anapita kukamulonjera.
And when he had completed the offering of the holocaust, behold, Samuel arrived. And Saul went out to meet him, so that he might greet him.
11 Samueli anafunsa kuti, “Nʼchiyani chimene wachita?” Sauli anayankha kuti, “Nditaona kuti anthu ayamba kundithawa, ndi kuti inu simunabwere pa nthawi munanena ija, ndiponso kuti Afilisti akusonkhana ku Mikimasi,
And Samuel said to him, “What have you done?” Saul responded: “Since I saw that the people were scattering away from me, and you had not arrived after the agreed upon days, and yet the Philistines had gathered together at Michmash,
12 ndinati, ‘Tsopano Afilisti abwera kudzandithira nkhondo ku Giligala kuno, chonsecho sindinapemphe Yehova kuti andikomere mtima.’ Motero ndinakakamizika kupereka nsembe yopsereza.”
I said: ‘Now the Philistines will descend to me at Gilgal. And I have not appeased the face of the Lord.’ Compelled by necessity, I offered the holocaust.
13 Samueli anati, “Mwachita zopusa. Simunatsate zimene Yehova Mulungu wanu anakulamulani kuti muchite. Mukanazitsata, Yehova akanawukhazikitsa ufumu wanu mu Israeli mpaka kalekale.
And Samuel said to Saul: “You have acted foolishly. You have not kept the commandments of the Lord your God, which he instructed to you. And if you had not acted in this way, the Lord would, here and now, have prepared your kingdom over Israel forever.
14 Koma tsopano ufumu wanu sudzakhalitsa. Yehova wapeza munthu wapamtima pake ndipo wamusankha kukhala mtsogoleri wa anthu ake chifukwa inu simunasunge malamulo a Yehova.”
But by no means shall your kingdom rise up any more. The Lord has sought for himself a man according to his own heart. And him the Lord has instructed to be the leader over his people, because you have not kept what the Lord has instructed.”
15 Kenaka Samueli anachoka ku Giligala ndi kupita ku Gibeyati ku dziko la Benjamini. Saulo anawerenga anthu amene anali naye ndipo analipo 600.
Then Samuel rose up and ascended from Gilgal to Gibeah of Benjamin. And the remainder of the people ascended after Saul, to meet the people who were fighting against them, going from Gilgal into Gibeah, to the hill of Benjamin. And Saul took a census of the people, who had been found to be with him, about six hundred men.
16 Sauli ndi mwana wake Yonatani pamodzi ndi asilikali amene anali naye aja amakhala ku Geba ku dziko la Benjamini. Koma Afilisti anamanga misasa yawo ku Mikimasi.
And Saul, and his son Jonathan, and the people who had been found to be with them, were at Gibeah of Benjamin. But the Philistines had settled in at Michmash.
17 Ankhondo a Afilisti anatuluka mʼmisasa yawo mʼmagulu atatu. Gulu lina linapita ku Ofiri ku dziko la Suwala.
And three companies went out from the camp of the Philistines, in order to plunder. One company was traveling toward the way of Ophrah, to the land of Shual.
18 Gulu lina linalunjika ku Beti-Horoni, ndipo gulu lachitatu linalunjika ku malire oyangʼanana ndi chigwa cha Zeboimu cha ku chipululu.
Then another entered along the way of Beth-horon. But the third turned itself to the way of the border, overhanging the valley of Zeboim, opposite the desert.
19 Nthawi imeneyo nʼkuti mulibe osula zitsulo mʼdziko lonse la Israeli, pakuti Afilisti anati, “Tisawalole Aheberi kudzipangira okha malupanga kapena mikondo!”
Now there was no worker of iron to be found in all the land of Israel. For the Philistines had been cautious, lest perhaps the Hebrews might make swords or spears.
20 Kotero Aisraeli onse amapita kwa Afilisti kukanoletsa mapulawo, makasu, nkhwangwa ndi zikwakwa zawo.
Therefore, all of Israel descended to the Philistines, so that each man could sharpen his plowshare, or pick axe, or hatchet, or hoe.
21 Mtengo wonolera mapulawo ndi makasu unali zigawo ziwiri za sekeli, mtengo wonolera zisonga ndi nkhwangwa unali gawo limodzi la Sekeli.
For their plow blades, and pick axes, and pitch forks, and axes had become blunt, and even the handles needed to be repaired.
22 Motero tsiku la nkhondolo panalibe lupanga kapena mkondo mʼdzanja la aliyense amene anatsatira Saulo ndi Yonatani. Koma Saulo ndi Yonatani, iwo okha ndiwo anali ndi zida.
And when the day of battle had arrived, there was found neither sword nor spear in the hand of the entire people who were with Saul and Jonathan, except for Saul and his son Jonathan.
23 Tsono gulu lina lankhondo la Chifilisti linapita kukalonda mpata wa Mikimasi.
Then the army of the Philistines went out in order to go across Michmash.

< 1 Samueli 13 >