< 1 Samueli 13 >

1 Sauli analowa ufumu ali ndi zaka makumi atatu, ndipo analamulira Israeli kwa zaka 42.
Saul var. . Aar, da han blev Konge, og han regerede paa andet Aar over Israel.
2 Nthawi ina Sauli anasankha Aisraeli 3,000. Mwa iwowa, 2,000 anali ndi Sauliyo ku Mikimasi ndi ku dziko la mapiri ku Beteli, ndipo 1,000 anali ndi Yonatani ku Gibeya ku Benjamini. Anthu ena onse otsala anawabweza kwawo.
Da udvalgte Saul sig tre Tusinde af Israel, og to Tusinde vare med Saul i Mikmas og paa Bethels Bjerg, og tusinde vare med Jonathan i Benjamins Gibea; men de øvrige Folk lod han fare, hver til sine Telte.
3 Yonatani anakantha mkulu wa ankhondo wa Afilisti ku Geba, ndipo Afilisti anamva kuti Aheberi awukira. Tsono Sauli anawuza amithenga kuti alize lipenga mʼdziko lonse la Israeli.
Og Jonathan slog Filisternes Besætning, som var paa Højen, og Filisterne hørte det; derfor lod Saul blæse i Trompeten i hele Landet og sige: Lad Hebræerne høre det!
4 Choncho Aisraeli onse anamva kuti Sauli wakantha mkulu wa ankhondo Wachifilisiti ndi kuti Afilisti anayipidwa nawo Aisraeli. Ndiye anthu anayitanidwa kuti abwere kwa Sauli ku Giligala.
Og al Israel hørte, at der sagdes: Saul har slaget Filisternes Besætning, og Israel har gjort sig forhadt hos Filisterne; da blev Folket sammenkaldt efter Saul til Gilgal.
5 Tsono Afilisti anasonkhana kuti amenyane ndi Aisraeli. Iwo anali ndi magaleta 3,000, okwera pa akavalo 2,000 ndiponso asilikali kuchuluka kwake ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja. Iwo anapita ndi kukamanga misasa yawo ku Mikimasi, kummawa kwa Beti-Aveni.
Og Filisterne samledes til at stride med Israel, tredive Tusinde Vogne og seks Tusinde Ryttere og Folk som Sand, der er ved Havbredden i Mangfoldighed; og de droge op og lejrede sig i Mikmas, Østen for Beth-Aven.
6 Pamene Aisraeli anaona kuti anali pamavuto akulu, poti anali atapanikizidwa kwambiri, anabisala mʼmapanga, mʼmaenje, mʼmatanthwe, mʼmakwalala ndi mʼzitsime.
Der Israels Mænd saa sig i Nød (thi Folket blev trængt), da skjulte Folket sig i Hulerne og i Tornebuskene og i Klipperne og i de faste Taarne og i Grøfterne.
7 Ahebri ena anawoloka Yorodani mpaka kukafika ku dziko la Gadi ndi ku Giliyadi. Koma Sauli anakhalabe ku Giligala ndipo ankhondo onse amene anali naye anali njenjenje ndi mantha.
Og Hebræere gik over Jordanen til Gads Land og til Gilead; og Saul var endnu i Gilgal, og alt Folket var forskrækket og fulgte efter ham.
8 Saulo anadikirira masiku asanu ndi awiri, monga mwa nthawi imene ananena Samueli. Koma Samueli sanabwere ku Giligala, ndipo anthu anayamba kumuthawa Sauli uja.
Og han tøvede i syv Dage til den Tid, som var bestemt af Samuel, men Samuel kom ikke til Gilgal; da adspredtes Folket fra ham.
9 Kotero iye anati, “Bwera nayoni nsembe yopsereza ndi nsembe ya chiyanjano.” Ndipo Sauli anapereka nsembe yopsereza.
Da sagde Saul: Fører hid til mig Brændofret og Takofrene; og han ofrede Brændofret.
10 Atangomaliza kupereka nsembe, anangoona Samueli watulukira ndipo Sauli anapita kukamulonjera.
Og det skete, der han var færdig med at ofre Brændofret, se, da kom Samuel! og Saul gik ud imod ham at hilse paa ham.
11 Samueli anafunsa kuti, “Nʼchiyani chimene wachita?” Sauli anayankha kuti, “Nditaona kuti anthu ayamba kundithawa, ndi kuti inu simunabwere pa nthawi munanena ija, ndiponso kuti Afilisti akusonkhana ku Mikimasi,
Da sagde Samuel: Hvad har du gjort? og Saul sagde: Da jeg saa, at Folket adspredtes fra mig, og du kom ikke til den bestemte Tid, og Filisterne vare samlede udi Mikmas,
12 ndinati, ‘Tsopano Afilisti abwera kudzandithira nkhondo ku Giligala kuno, chonsecho sindinapemphe Yehova kuti andikomere mtima.’ Motero ndinakakamizika kupereka nsembe yopsereza.”
da sagde jeg: Nu komme Filisterne ned mod mig i Gilgal, og jeg har ikke bedet for Herrens Ansigt; da tog jeg Mod til mig og ofrede Brændofret.
13 Samueli anati, “Mwachita zopusa. Simunatsate zimene Yehova Mulungu wanu anakulamulani kuti muchite. Mukanazitsata, Yehova akanawukhazikitsa ufumu wanu mu Israeli mpaka kalekale.
Da sagde Samuel til Saul: Du har handlet daarligen; du har ikke holdt Herren din Guds Bud, som han bød dig; saa havde Herren nu stadfæstet dit Kongedømme over Israel evindelig.
14 Koma tsopano ufumu wanu sudzakhalitsa. Yehova wapeza munthu wapamtima pake ndipo wamusankha kukhala mtsogoleri wa anthu ake chifukwa inu simunasunge malamulo a Yehova.”
Men nu skal dit Kongedømme ikke bestaa; Herren har opsøgt sig en Mand efter sit Hjerte, og ham har Herren budet at være en Fyrste over sit Folk, fordi du ikke har holdt det, som Herren har befalet dig.
15 Kenaka Samueli anachoka ku Giligala ndi kupita ku Gibeyati ku dziko la Benjamini. Saulo anawerenga anthu amene anali naye ndipo analipo 600.
Og Samuel gjorde sig rede og gik op fra Gilgal til Gibea i Benjamin; og Saul talte det Folk, som fandtes hos ham, ved seks Hundrede Mand.
16 Sauli ndi mwana wake Yonatani pamodzi ndi asilikali amene anali naye aja amakhala ku Geba ku dziko la Benjamini. Koma Afilisti anamanga misasa yawo ku Mikimasi.
Og Saul og Jonathan, hans Søn, og det Folk, som fandtes hos dem, bleve i Gibea i Benjamin; men Filisterne havde lejret sig i Mikmas.
17 Ankhondo a Afilisti anatuluka mʼmisasa yawo mʼmagulu atatu. Gulu lina linapita ku Ofiri ku dziko la Suwala.
Og der uddrog en ødelæggende Skare af Filisternes Lejr i tre Hobe; den ene Hob vendte sig ad Vejen imod Ofra, til Landet Sual;
18 Gulu lina linalunjika ku Beti-Horoni, ndipo gulu lachitatu linalunjika ku malire oyangʼanana ndi chigwa cha Zeboimu cha ku chipululu.
og den anden Hob vendte sig ad Vejen til Beth-Horon; og den tredje Hob vendte sig mod Vejen ved Skellet, der rager frem over Zeboims Dal, ad Ørken til.
19 Nthawi imeneyo nʼkuti mulibe osula zitsulo mʼdziko lonse la Israeli, pakuti Afilisti anati, “Tisawalole Aheberi kudzipangira okha malupanga kapena mikondo!”
Og der blev ingen Smed funden i al Israels Land; thi Filisterne sagde: At Hebræerne ikke skulde gøre Sværd eller Spyd.
20 Kotero Aisraeli onse amapita kwa Afilisti kukanoletsa mapulawo, makasu, nkhwangwa ndi zikwakwa zawo.
Derfor maatte al Israel fare ned til Filisterne, at hver kunde faa sit Plovjern og sin Hakke og sin Økse og sin Spade skærpet;
21 Mtengo wonolera mapulawo ndi makasu unali zigawo ziwiri za sekeli, mtengo wonolera zisonga ndi nkhwangwa unali gawo limodzi la Sekeli.
og de havde skarpe File til Spader og Hakker og Treforke og Økser, og saa ofte Æggen var sløvet paa Spader, og naar de skulde have en Braad sat ind.
22 Motero tsiku la nkhondolo panalibe lupanga kapena mkondo mʼdzanja la aliyense amene anatsatira Saulo ndi Yonatani. Koma Saulo ndi Yonatani, iwo okha ndiwo anali ndi zida.
Og det skete paa Stridens Dag, at der ikke blev funden Sværd eller Spyd i nogen af Folkets Haand, som var med Saul og med Jonathan; dog fandtes der hos Saul og hos Jonathan, hans Søn.
23 Tsono gulu lina lankhondo la Chifilisti linapita kukalonda mpata wa Mikimasi.
Og Filisternes Besætning drog ud til Kløftvejen ved Mikmas.

< 1 Samueli 13 >