< 1 Samueli 12 >
1 Pambuyo pake Samueli anawuza Aisraeli onse kuti, “Ine ndamvera zonse zimene munandiwuza ndipo ndakupatsani mfumu kuti izikulamulirani.
Bundan sonra Samuel İsrail halkına şöyle dedi: “Bana söylediğiniz her şeye kulak verdim: Size bir kral atadım.
2 Tsopano muli ndi mfumu imene izikutsogolerani, koma ine ndakalamba, kumutu kwanga kuli imvi zokhazokha ndipo ana anga ali pamodzi ndi inu. Ndakhala ndili mtsogoleri wanu kuyambira ndili mnyamata mpaka lero.
Şimdi size önderlik yapan bir kralınız var. Bense yaşlandım, saçım ağardı. Oğullarım da sizlerle birlikte. Gençliğimden bu güne dek size önderlik yaptım.
3 Ine ndili pano. Ngati ndinalakwa chilichonse nditsutseni pamaso pa Yehova ndi wodzozedwa wake. Kodi ndinalanda ngʼombe ya yani? Kodi ndinalanda bulu wa yani? Kodi ndani amene ndinamudyera masuku pa mutu? Kodi ndinazunza yani? Kodi ndinalandira kwa yani chiphuphu choti nʼkundidetsa mʼmaso? Ngati ndinachita chilichonse cha izi, ine ndidzakubwezerani.”
İşte karşınızda duruyorum. Hanginizin öküzünü aldım? Kimin eşeğine el koydum? Kimi dolandırdım? Kime baskı yaptım? Göz yummak için kimden rüşvet aldım? RAB'bin ve O'nun meshettiğinin önünde bana karşı tanıklık edin de size karşılığını vereyim.”
4 Iwo anayankha kuti, “Inu simunatidyere masuku pamutu kapena kutizunza. Simunalande kanthu kalikonse ka munthu.”
Halk, “Bizi dolandırmadın” diye karşılık verdi, “Bize baskı da yapmadın. Kimsenin elinden hiçbir şey almadın.”
5 Samueli anawawuza kuti, “Yehova ndiye mboni pakati pa inu ndi ine, ndiponso wodzozedwa wake ndi mboni kuti lero simunapeze chilichonse mʼdzanja langa.” Iwo anati, “Inde, Yehova ndiye mboni.”
Samuel, “Bana karşı bir şey bulamadığınıza bugün hem RAB, hem de O'nun meshettiği kral tanıktır” dedi. “Evet, tanıktır” dediler.
6 Samueli anawawuzanso kuti, “Yehova ndiye amene anasankha Mose ndi Aaroni kuti atulutse makolo anu mʼdziko la Igupto.
Samuel konuşmasını şöyle sürdürdü: “Musa ile Harun'u görevlendiren, atalarınızı Mısır'dan çıkaran RAB'dir.
7 Nʼchifukwa chake tsopano imani pomwepa kuti ndikufotokozereni pamaso pa Yehova, za ntchito za chipulumutso zimene Yehova anachitira inu ndi makolo anu.
Şimdi burada durun, RAB'bin önünde, O'nun sizi ve atalarınızı tekrar tekrar nasıl kurtardığına dair kanıtlar göstereyim size.
8 “Yakobo atapita ku dziko la Igupto, Aiguptowo akuwazunza, iwo analirira kwa Yehova kuti awathandize, ndipo Yehova anatumiza Mose ndi Aaroni, amene anatulutsa makolo anu mʼdziko la Igupto ndi kudzawakhazika pa malo ano.
“Yakup Mısır'a gittikten sonra, atalarınız RAB'be yakardı. O da atalarınızı Mısır'dan çıkarıp burada yerleşmelerini sağlayan Musa ile Harun'u gönderdi.
9 “Koma iwo anayiwala Yehova Mulungu wawo, choncho Yehova anawapereka mʼdzanja la Sisera mkulu wa ankhondo wa mzinda wa Hazori, ndiponso mʼmanja mwa Afilisti ndi mfumu ya Mowabu. Mafumu onsewa anathira nkhondo makolo anu.
Ama atalarınız Tanrıları RAB'bi unuttular. Bu yüzden RAB onları Hasor ordusunun komutanı Sisera'nın, Filistliler'in ve Moav Kralı'nın eline teslim etti. Bunlar atalarınıza karşı savaştılar.
10 Tsono iwo analira kwa Yehova nati, ‘Ife tachimwa, chifukwa tamusiya Yehova ndi kumatumikira mafano a Baala ndi Asiteroti. Koma tsopano tilanditseni mʼmanja mwa adani athu ndipo tidzakutumikirani.’
Atalarınız RAB'be, ‘Günah işledik; RAB'bi bırakıp Baal'ın ve Aştoret'in putlarına kulluk ettik. Ama şimdi bizi düşmanlarımızın elinden kurtar, sana kulluk edeceğiz’ diye seslendiler.
11 Choncho Yehova anatumiza Yeru-Baala, Bedani, Yefita ndi Samueli ndipo anakulanditsani mʼmanja mwa adani anu amene anakuzungulirani, kotero munakhala mwamtendere.
RAB de Yerubbaal'ı, Bedan'ı, Yiftah'ı ve ben Samuel'i gönderdi. Güvenlik içinde yaşamanız için sizi saran düşmanlarınızın elinden kurtardı.
12 “Koma mutaona kuti Nahasi mfumu ya Amoni inkabwera kudzamenyana nanu, inu munandiwuza kuti, ‘Ayi, ife tikufuna mfumu kuti itilamulire,’ ngakhale kuti Yehova Mulungu wanu ndiye anali mfumu yanu.
“Ama siz Ammon Kralı Nahaş'ın üzerinize yürüdüğünü görünce, Tanrınız RAB kralınız olduğu halde bana, ‘Hayır, bize bir kral önderlik yapacak’ dediniz.
13 Tsopano nayi mfumu imene mwayisankha, imene munayipempha. Onani, Yehova wakupatsani mfumu.
İşte seçtiğiniz, dilediğiniz kral! Evet, RAB size bir kral verdi.
14 Ngati muziopa Yehova ndi kumamutumikira ndi kumamumvera, osamupandukira ndiponso ngati inu pamodzi ndi mfumu yanu mudzatsata Yehova Mulungu wanu, ndiye zinthu zonse zidzakuyenderani bwino.
Eğer RAB'den korkar, O'na kulluk ederseniz, O'nun sözünü dinleyip buyruklarına karşı gelmezseniz, hem siz hem de önderiniz olacak kral Tanrınız RAB'bin ardınca giderseniz, ne âlâ!
15 Koma mukapanda kumvera Yehova ndi kumupandukira, ndiye adzakulangani pamodzi ndi mfumu yanu yomwe.
Ama RAB'bin sözünü dinlemez, buyruklarına karşı gelirseniz, RAB kralınızı cezalandırdığı gibi sizi de cezalandıracaktır.
16 “Tsono imani pomwepa kuti muone chinthu chachikulu chimene Yehova ali pafupi kuchita pamaso panu!
“Şimdi olduğunuz yerde durun ve RAB'bin gözlerinizin önünde yapacağı şu olağanüstü olayı görün.
17 Kodi ino si nthawi yokolola tirigu? Komabe ndipemphera kwa Yehova kuti agwetse mvula ya mabingu. Zikatero mudzadziwa kuti tchimo lanu limene mwachita popempha mfumu kwa Yehova ndi lalikulu.”
Bugün buğday biçme zamanı değil mi? Göğü gürletsin, yağmur yağdırsın diye RAB'be yalvaracağım. Böylece bir kral istemekle yaptığınız kötülüğün RAB'bin gözünde ne denli büyük olduğunu iyice anlayacaksınız.”
18 Choncho Samueli anapemphera, ndipo Yehova anatumiza mvula ya mabingu tsiku lomwelo. Apo anthu aja anaopa kwambiri Yehova ndi Samueli.
Samuel RAB'be yalvardı ve RAB o gün göğü gürletti, yağmur yağdırdı. Halk RAB'den de Samuel'den de çok korktu.
19 Tsono anamupempha Samueli nati, “Chonde mutipempherere kwa Yehova, ife atumiki kuti tingafe pakuti pa machimo athu onse tawonjezapo tchimo lopempha mfumu.”
Bunun üzerine Samuel'e, “Yok olmayalım diye, biz kulların için Tanrın RAB'be yakar” dediler, “Çünkü bütün günahlarımıza kendimize bir kral istemek kötülüğünü de ekledik.”
20 Samueli anayankha kuti, “Musaope, inu mwachitadi tchimo ili, koma musaleke kumutsata Yehova ndi kumutumikira ndi mtima wanu wonse.
Samuel halka, “Korkmayın” dedi, “Siz bu büyük kötülüğü yaptınız, ama yine de RAB'bin ardınca gitmekten vazgeçmeyin; tersine, bütün yüreğinizle RAB'be kulluk edin.
21 Ndipo musatsate mafano achabechabe amene alibe phindu ndipo sangakupulumutseni popeza ndi achabechabe.
Kimseyi kurtaramayan yararsız putların ardınca gitmeyin; çünkü onlar değersizdir.
22 Yehova adzakana anthu ake kuopa kuti dzina lake lamphamvu linganyozeke, pakuti chinamukondweretsa Yehova kuti akusandutseni inu kukhala anthu ake.
RAB görkemli adının hatırına halkını bırakmayacak. Çünkü sizi kendi halkı kılmaktan hoşnut kaldı.
23 Ndiponso kunena za ine, zisachitike kuti ndichimwire Yehova pakulephera kukupemphererani. Ndipo ine ndidzakuphunzitsani njira yabwino ndi yolungama kuti muziyendamo.
Bana gelince, sizin için RAB'be yalvarmaktan vazgeçip O'na karşı günah işlemek benden uzak olsun! Ancak size iyi ve doğru yolu öğreteceğim.
24 Koma onetsetsani kuti mukuopa Yehova ndi kumutumikira mokhulupirika ndi mtima wanu wonse. Nthawi zonse muziganizira zinthu zazikulu wakhala akukuchitirani.
Yalnız RAB'den korkun, O'na bağlılıkla ve bütün yüreğinizle kulluk edin. O'nun sizler için ne görkemli işler yaptığını bir düşünün!
25 Komabe mukapitirira kuchita zoyipa, ndiye kuti inu pamodzi ndi mfumu yanu mudzachotsedwa.”
Ama kötülük yapmayı sürdürürseniz, hem siz yok olacaksınız, hem de kralınız.”