< 1 Samueli 12 >
1 Pambuyo pake Samueli anawuza Aisraeli onse kuti, “Ine ndamvera zonse zimene munandiwuza ndipo ndakupatsani mfumu kuti izikulamulirani.
Forsothe Samuel seide to al Israel, Lo! Y herde youre vois bi alle thingis whiche ye spaken to me, and Y ordeynede a kyng on you;
2 Tsopano muli ndi mfumu imene izikutsogolerani, koma ine ndakalamba, kumutu kwanga kuli imvi zokhazokha ndipo ana anga ali pamodzi ndi inu. Ndakhala ndili mtsogoleri wanu kuyambira ndili mnyamata mpaka lero.
and now the king goith bifor you. Sotheli Y wexide eld and hoor; forsothe my sones ben with you; therfor Y lyuyde bifor you fro my yong wexynge age `til to this dai. And lo!
3 Ine ndili pano. Ngati ndinalakwa chilichonse nditsutseni pamaso pa Yehova ndi wodzozedwa wake. Kodi ndinalanda ngʼombe ya yani? Kodi ndinalanda bulu wa yani? Kodi ndani amene ndinamudyera masuku pa mutu? Kodi ndinazunza yani? Kodi ndinalandira kwa yani chiphuphu choti nʼkundidetsa mʼmaso? Ngati ndinachita chilichonse cha izi, ine ndidzakubwezerani.”
Y am redi; speke ye to me bifor the Lord, and bifor `the crist of hym; whether Y took `the oxe of ony man, ether the asse; if Y falsly chalengide ony mon; yf Y oppresside ony man; if Y took yifte of `the hond of ony man; and Y schal `dispise it to dai, and Y schal restore to you.
4 Iwo anayankha kuti, “Inu simunatidyere masuku pamutu kapena kutizunza. Simunalande kanthu kalikonse ka munthu.”
And thei seiden, Thou hast not falsly chalengid vs, nether hast oppressid vs, nether hast take ony thing of `the hond of ony man.
5 Samueli anawawuza kuti, “Yehova ndiye mboni pakati pa inu ndi ine, ndiponso wodzozedwa wake ndi mboni kuti lero simunapeze chilichonse mʼdzanja langa.” Iwo anati, “Inde, Yehova ndiye mboni.”
And he seide to hem, The Lord is witnesse ayens you, and his crist is witnesse in this day; for ye han not founde ony thing in myn hond. And thei seiden, Witnesse.
6 Samueli anawawuzanso kuti, “Yehova ndiye amene anasankha Mose ndi Aaroni kuti atulutse makolo anu mʼdziko la Igupto.
And Samuel seide to the puple, The Lord, that made Moises and Aaron, and ledde youre fadris out of the lond of Egipt, is present;
7 Nʼchifukwa chake tsopano imani pomwepa kuti ndikufotokozereni pamaso pa Yehova, za ntchito za chipulumutso zimene Yehova anachitira inu ndi makolo anu.
now therfor stonde ye, that Y stryue bi doom ayens you bifor the Lord, of alle the mercyes of the Lord, whiche he dide with you, and with youre fadris.
8 “Yakobo atapita ku dziko la Igupto, Aiguptowo akuwazunza, iwo analirira kwa Yehova kuti awathandize, ndipo Yehova anatumiza Mose ndi Aaroni, amene anatulutsa makolo anu mʼdziko la Igupto ndi kudzawakhazika pa malo ano.
Hou Jacob entride in to Egipt, and youre fadris crieden to the Lord; and the Lord sente Moises and Aaron, and ledde youre fadris out of Egipt, and settide hem in this place.
9 “Koma iwo anayiwala Yehova Mulungu wawo, choncho Yehova anawapereka mʼdzanja la Sisera mkulu wa ankhondo wa mzinda wa Hazori, ndiponso mʼmanja mwa Afilisti ndi mfumu ya Mowabu. Mafumu onsewa anathira nkhondo makolo anu.
Whiche foryaten her Lord God; and he bitook hem in the hond of Sisara, maystir of the chyualrie of Asor, and in the hond of Filisteis, and in the hond of the kyng of Moab; and thei fouyten ayens hem.
10 Tsono iwo analira kwa Yehova nati, ‘Ife tachimwa, chifukwa tamusiya Yehova ndi kumatumikira mafano a Baala ndi Asiteroti. Koma tsopano tilanditseni mʼmanja mwa adani athu ndipo tidzakutumikirani.’
Sotheli afterward thei crieden to the Lord, and seiden, We synneden, for we forsoken the Lord, and seruyden Baalym and Astroth; now therfor delyuere thou vs fro `the hond of oure enemyes, and we schulen serue thee.
11 Choncho Yehova anatumiza Yeru-Baala, Bedani, Yefita ndi Samueli ndipo anakulanditsani mʼmanja mwa adani anu amene anakuzungulirani, kotero munakhala mwamtendere.
And the Lord sente Gerobaal, and `Bedan, that is, Sampson, and Barach, and Jepte, and Samuel, and delyuerede you fro the hond of youre enemyes bi cumpass; and ye dwelliden tristili.
12 “Koma mutaona kuti Nahasi mfumu ya Amoni inkabwera kudzamenyana nanu, inu munandiwuza kuti, ‘Ayi, ife tikufuna mfumu kuti itilamulire,’ ngakhale kuti Yehova Mulungu wanu ndiye anali mfumu yanu.
Forsothe ye sien, that Naas, kyng of the sones of Amon, cam ayens you; and ye seiden to me, counseilynge to axe noon other kyng than God, Nay, but a kyng schal comaunde to vs; whanne `youre Lord God regnede in you.
13 Tsopano nayi mfumu imene mwayisankha, imene munayipempha. Onani, Yehova wakupatsani mfumu.
Now therfor youre kyng is redi, whom ye han chose and axid; lo! the Lord yaf to you a kyng.
14 Ngati muziopa Yehova ndi kumamutumikira ndi kumamumvera, osamupandukira ndiponso ngati inu pamodzi ndi mfumu yanu mudzatsata Yehova Mulungu wanu, ndiye zinthu zonse zidzakuyenderani bwino.
If ye dreden the Lord, and seruen hym, and heren his vois, and wraththen not the `mouth of the Lord; ye and youre kyng, that comaundith to you, schulen sue youre Lord God.
15 Koma mukapanda kumvera Yehova ndi kumupandukira, ndiye adzakulangani pamodzi ndi mfumu yanu yomwe.
Forsothe if ye heren not the vois of `the Lord, but wraththen his word, the hond of the Lord schal be on you, and on youre fadris.
16 “Tsono imani pomwepa kuti muone chinthu chachikulu chimene Yehova ali pafupi kuchita pamaso panu!
But also now stonde ye, and se this gret thing which the Lord schal make in youre siyt.
17 Kodi ino si nthawi yokolola tirigu? Komabe ndipemphera kwa Yehova kuti agwetse mvula ya mabingu. Zikatero mudzadziwa kuti tchimo lanu limene mwachita popempha mfumu kwa Yehova ndi lalikulu.”
Whether heruest of whete is not `to dai? I schal inwardli clepe the Lord, and he schal yyue voices, `that is, thundris, and reynes; and ye schulen wite, and schulen se, for ye axynge a kyng on you han do greuouse yuel to you in the siyt of the Lord.
18 Choncho Samueli anapemphera, ndipo Yehova anatumiza mvula ya mabingu tsiku lomwelo. Apo anthu aja anaopa kwambiri Yehova ndi Samueli.
And Samuel criede to the Lord, and the Lord yaf voices and reynes in that dai.
19 Tsono anamupempha Samueli nati, “Chonde mutipempherere kwa Yehova, ife atumiki kuti tingafe pakuti pa machimo athu onse tawonjezapo tchimo lopempha mfumu.”
And al the puple dredde greetli the Lord and Samuel; and al the puple seide to Samuel, Preye thou for thi seruauntis to thi Lord God, that we die not; for we addiden yuel to alle oure synnes, that we axiden a kyng to vs.
20 Samueli anayankha kuti, “Musaope, inu mwachitadi tchimo ili, koma musaleke kumutsata Yehova ndi kumutumikira ndi mtima wanu wonse.
Forsothe Samuel seide to the puple, `Nyle ye drede; ye han do al this yuel; netheles `nyle ye go awey fro the bak of the Lord, but serue ye the Lord in al youre herte;
21 Ndipo musatsate mafano achabechabe amene alibe phindu ndipo sangakupulumutseni popeza ndi achabechabe.
and nyle ye bowe aftir veyn thingis, that schulen not profite to you, nether schulen delyuere you; for tho ben veyn thingis.
22 Yehova adzakana anthu ake kuopa kuti dzina lake lamphamvu linganyozeke, pakuti chinamukondweretsa Yehova kuti akusandutseni inu kukhala anthu ake.
And the Lord schal not forsake his puple for his grete name; for the Lord swoor to make you a puple to hym silf.
23 Ndiponso kunena za ine, zisachitike kuti ndichimwire Yehova pakulephera kukupemphererani. Ndipo ine ndidzakuphunzitsani njira yabwino ndi yolungama kuti muziyendamo.
Forsothe this synne be fer fro me in the Lord, that Y ceesse to preye for you; and Y schal teche you a riytful weie and good.
24 Koma onetsetsani kuti mukuopa Yehova ndi kumutumikira mokhulupirika ndi mtima wanu wonse. Nthawi zonse muziganizira zinthu zazikulu wakhala akukuchitirani.
Therfor drede ye the Lord, and `serue ye hym in treuthe, and of al youre herte; for ye sien tho grete thingis, whiche he `dide in you;
25 Komabe mukapitirira kuchita zoyipa, ndiye kuti inu pamodzi ndi mfumu yanu mudzachotsedwa.”
that if ye contynuen in malice, bothe ye and youre kyng schulen perische to gidere.