< 1 Samueli 12 >

1 Pambuyo pake Samueli anawuza Aisraeli onse kuti, “Ine ndamvera zonse zimene munandiwuza ndipo ndakupatsani mfumu kuti izikulamulirani.
Then Samuel said to all of Israel, “I have paid attention to everything you asked from me, and I have given you a king to rule over you.
2 Tsopano muli ndi mfumu imene izikutsogolerani, koma ine ndakalamba, kumutu kwanga kuli imvi zokhazokha ndipo ana anga ali pamodzi ndi inu. Ndakhala ndili mtsogoleri wanu kuyambira ndili mnyamata mpaka lero.
Now your king is your leader. I am old and gray, and my sons are here with you. I have led you from the time I was a boy up to today.
3 Ine ndili pano. Ngati ndinalakwa chilichonse nditsutseni pamaso pa Yehova ndi wodzozedwa wake. Kodi ndinalanda ngʼombe ya yani? Kodi ndinalanda bulu wa yani? Kodi ndani amene ndinamudyera masuku pa mutu? Kodi ndinazunza yani? Kodi ndinalandira kwa yani chiphuphu choti nʼkundidetsa mʼmaso? Ngati ndinachita chilichonse cha izi, ine ndidzakubwezerani.”
I stand here before you. Bring any charges you have against me in the presence of the Lord and of his anointed one. Have I taken anyone's ox or donkey? Have I wronged anyone? Have I oppressed anyone? Have I accepted a bribe from anyone to turn a blind eye? Tell me, and I will repay you.”
4 Iwo anayankha kuti, “Inu simunatidyere masuku pamutu kapena kutizunza. Simunalande kanthu kalikonse ka munthu.”
“No, you have never cheated or oppressed us,” they replied, “and you have never taken anything from anyone.”
5 Samueli anawawuza kuti, “Yehova ndiye mboni pakati pa inu ndi ine, ndiponso wodzozedwa wake ndi mboni kuti lero simunapeze chilichonse mʼdzanja langa.” Iwo anati, “Inde, Yehova ndiye mboni.”
Samuel told them, “The Lord is a witness, and his anointed is a witness today, in this case involving you, that you have not found me guilty of anything.” “He is a witness,” they replied.
6 Samueli anawawuzanso kuti, “Yehova ndiye amene anasankha Mose ndi Aaroni kuti atulutse makolo anu mʼdziko la Igupto.
“The Lord is a witness, he who appointed Moses and Aaron,” Samuel went on. “He led your forefathers out of the land of Egypt.
7 Nʼchifukwa chake tsopano imani pomwepa kuti ndikufotokozereni pamaso pa Yehova, za ntchito za chipulumutso zimene Yehova anachitira inu ndi makolo anu.
So stand here as I present to you in the presence of the Lord the evidence of all the good things the Lord has done for you and your forefathers.
8 “Yakobo atapita ku dziko la Igupto, Aiguptowo akuwazunza, iwo analirira kwa Yehova kuti awathandize, ndipo Yehova anatumiza Mose ndi Aaroni, amene anatulutsa makolo anu mʼdziko la Igupto ndi kudzawakhazika pa malo ano.
After Jacob had gone to Egypt, your fathers cried out to the Lord for help, and he sent Moses and Aaron to lead your forefathers out of Egypt and settle them here.
9 “Koma iwo anayiwala Yehova Mulungu wawo, choncho Yehova anawapereka mʼdzanja la Sisera mkulu wa ankhondo wa mzinda wa Hazori, ndiponso mʼmanja mwa Afilisti ndi mfumu ya Mowabu. Mafumu onsewa anathira nkhondo makolo anu.
But they forgot about the Lord their God, so he abandoned them to Sisera, the commander of the army of Hazor, to the Philistines, and to the king of Moab, who attacked them.
10 Tsono iwo analira kwa Yehova nati, ‘Ife tachimwa, chifukwa tamusiya Yehova ndi kumatumikira mafano a Baala ndi Asiteroti. Koma tsopano tilanditseni mʼmanja mwa adani athu ndipo tidzakutumikirani.’
They cried out to the Lord for help and said, ‘We have sinned, for we have rejected the Lord and worshiped the Baals and Ashtoreths. Please save us from the hands of our enemies, and we will worship you.’
11 Choncho Yehova anatumiza Yeru-Baala, Bedani, Yefita ndi Samueli ndipo anakulanditsani mʼmanja mwa adani anu amene anakuzungulirani, kotero munakhala mwamtendere.
Then the Lord sent Gideon, Barak, Jephthah and Samuel, and he saved you from your enemies who surrounded you so you could live in safety.
12 “Koma mutaona kuti Nahasi mfumu ya Amoni inkabwera kudzamenyana nanu, inu munandiwuza kuti, ‘Ayi, ife tikufuna mfumu kuti itilamulire,’ ngakhale kuti Yehova Mulungu wanu ndiye anali mfumu yanu.
But when you saw that Nahash, king of the Ammonites, was coming to attack you, you told me, ‘No, we want our own king,’ even though the Lord your God was your king.
13 Tsopano nayi mfumu imene mwayisankha, imene munayipempha. Onani, Yehova wakupatsani mfumu.
So here's the king you have chosen, the one you asked for. Look—the Lord now gives him to you as your king!
14 Ngati muziopa Yehova ndi kumamutumikira ndi kumamumvera, osamupandukira ndiponso ngati inu pamodzi ndi mfumu yanu mudzatsata Yehova Mulungu wanu, ndiye zinthu zonse zidzakuyenderani bwino.
If you honor the Lord, worship him, do what he tells you, and don't rebel against the Lord's instructions, and if both you and your king follow the Lord your God, then good!
15 Koma mukapanda kumvera Yehova ndi kumupandukira, ndiye adzakulangani pamodzi ndi mfumu yanu yomwe.
However, if you refuse to do what he tells you, and rebel against the Lord's instructions, then the Lord will be against you as he was against your forefathers.
16 “Tsono imani pomwepa kuti muone chinthu chachikulu chimene Yehova ali pafupi kuchita pamaso panu!
Now stand still and watch what the Lord is going to do, right before your very eyes.
17 Kodi ino si nthawi yokolola tirigu? Komabe ndipemphera kwa Yehova kuti agwetse mvula ya mabingu. Zikatero mudzadziwa kuti tchimo lanu limene mwachita popempha mfumu kwa Yehova ndi lalikulu.”
Isn't it the time of wheat harvest? Well, I will ask the Lord to send thunder and rain. Then you will realize how very evil you were in the Lord's sight when you demanded your own king.”
18 Choncho Samueli anapemphera, ndipo Yehova anatumiza mvula ya mabingu tsiku lomwelo. Apo anthu aja anaopa kwambiri Yehova ndi Samueli.
Then Samuel prayed to the Lord, and that very day the Lord sent thunder and rain. Everyone was in absolute awe of the Lord and of Samuel.
19 Tsono anamupempha Samueli nati, “Chonde mutipempherere kwa Yehova, ife atumiki kuti tingafe pakuti pa machimo athu onse tawonjezapo tchimo lopempha mfumu.”
“Please pray to the Lord your God for us your servants, so we will not die!” they begged Samuel. “For we have added to all our sins the evil of asking for our own king.”
20 Samueli anayankha kuti, “Musaope, inu mwachitadi tchimo ili, koma musaleke kumutsata Yehova ndi kumutumikira ndi mtima wanu wonse.
“Don't be afraid,” Samuel replied. “Even though you have indeed done all these evil things, don't give up following the Lord, but dedicate yourselves completely to worshiping him.
21 Ndipo musatsate mafano achabechabe amene alibe phindu ndipo sangakupulumutseni popeza ndi achabechabe.
Don't worship worthless idols that can't help you or save you, for they are nothing.
22 Yehova adzakana anthu ake kuopa kuti dzina lake lamphamvu linganyozeke, pakuti chinamukondweretsa Yehova kuti akusandutseni inu kukhala anthu ake.
The fact is because of the kind of person the Lord is, he won't give up on his people, because he was happy to claim you as his own.
23 Ndiponso kunena za ine, zisachitike kuti ndichimwire Yehova pakulephera kukupemphererani. Ndipo ine ndidzakuphunzitsani njira yabwino ndi yolungama kuti muziyendamo.
As for me, how could I sin against the Lord by no longer praying for you. I will also continue to teach you the way of goodness and right.
24 Koma onetsetsani kuti mukuopa Yehova ndi kumutumikira mokhulupirika ndi mtima wanu wonse. Nthawi zonse muziganizira zinthu zazikulu wakhala akukuchitirani.
Make sure you honor God and worship him faithfully, with complete dedication. Think of all the tremendous things he has done for you.
25 Komabe mukapitirira kuchita zoyipa, ndiye kuti inu pamodzi ndi mfumu yanu mudzachotsedwa.”
But if you continue to do what is evil, you and your king will be wiped out.”

< 1 Samueli 12 >