< 1 Samueli 12 >

1 Pambuyo pake Samueli anawuza Aisraeli onse kuti, “Ine ndamvera zonse zimene munandiwuza ndipo ndakupatsani mfumu kuti izikulamulirani.
And Samuel said to all Israel, Behold, I have hearkened to your voice in all that ye said to me, and have made a king over you.
2 Tsopano muli ndi mfumu imene izikutsogolerani, koma ine ndakalamba, kumutu kwanga kuli imvi zokhazokha ndipo ana anga ali pamodzi ndi inu. Ndakhala ndili mtsogoleri wanu kuyambira ndili mnyamata mpaka lero.
And now behold, the king walks before you; and I am old and grey-headed; and behold, my sons are with you; and I have walked before you from my youth up to this day.
3 Ine ndili pano. Ngati ndinalakwa chilichonse nditsutseni pamaso pa Yehova ndi wodzozedwa wake. Kodi ndinalanda ngʼombe ya yani? Kodi ndinalanda bulu wa yani? Kodi ndani amene ndinamudyera masuku pa mutu? Kodi ndinazunza yani? Kodi ndinalandira kwa yani chiphuphu choti nʼkundidetsa mʼmaso? Ngati ndinachita chilichonse cha izi, ine ndidzakubwezerani.”
Here I am: testify against me before Jehovah, and before his anointed. Whose ox have I taken? or whose ass have I taken? or whom have I defrauded? whom have I injured? or of whose hand have I received any ransom and blinded mine eyes therewith? and I will restore it to you.
4 Iwo anayankha kuti, “Inu simunatidyere masuku pamutu kapena kutizunza. Simunalande kanthu kalikonse ka munthu.”
And they said, Thou hast not defrauded us, and thou hast not injured us, neither hast thou taken aught of any man's hand.
5 Samueli anawawuza kuti, “Yehova ndiye mboni pakati pa inu ndi ine, ndiponso wodzozedwa wake ndi mboni kuti lero simunapeze chilichonse mʼdzanja langa.” Iwo anati, “Inde, Yehova ndiye mboni.”
And he said to them, Jehovah is witness against you, and his anointed is witness this day, that ye have not found aught in my hand! And [the people] said, [He is] witness!
6 Samueli anawawuzanso kuti, “Yehova ndiye amene anasankha Mose ndi Aaroni kuti atulutse makolo anu mʼdziko la Igupto.
And Samuel said to the people, [It is] Jehovah who appointed Moses and Aaron, and who brought your fathers up out of the land of Egypt.
7 Nʼchifukwa chake tsopano imani pomwepa kuti ndikufotokozereni pamaso pa Yehova, za ntchito za chipulumutso zimene Yehova anachitira inu ndi makolo anu.
And now stand still, that I may plead with you before Jehovah of all the righteous acts of Jehovah which he did to you and to your fathers.
8 “Yakobo atapita ku dziko la Igupto, Aiguptowo akuwazunza, iwo analirira kwa Yehova kuti awathandize, ndipo Yehova anatumiza Mose ndi Aaroni, amene anatulutsa makolo anu mʼdziko la Igupto ndi kudzawakhazika pa malo ano.
When Jacob had come into Egypt, and your fathers cried to Jehovah, then Jehovah sent Moses and Aaron, and they brought your fathers forth out of Egypt, and made them dwell in this place.
9 “Koma iwo anayiwala Yehova Mulungu wawo, choncho Yehova anawapereka mʼdzanja la Sisera mkulu wa ankhondo wa mzinda wa Hazori, ndiponso mʼmanja mwa Afilisti ndi mfumu ya Mowabu. Mafumu onsewa anathira nkhondo makolo anu.
And they forgot Jehovah their God, and he sold them into the hand of Sisera, captain of the host of Hazor, and into the hand of the Philistines, and into the hand of the king of Moab, and they fought against them.
10 Tsono iwo analira kwa Yehova nati, ‘Ife tachimwa, chifukwa tamusiya Yehova ndi kumatumikira mafano a Baala ndi Asiteroti. Koma tsopano tilanditseni mʼmanja mwa adani athu ndipo tidzakutumikirani.’
And they cried to Jehovah and said, We have sinned, because we have forsaken Jehovah, and have served the Baals and the Ashtoreths; and now deliver us out of the hand of our enemies, and we will serve thee.
11 Choncho Yehova anatumiza Yeru-Baala, Bedani, Yefita ndi Samueli ndipo anakulanditsani mʼmanja mwa adani anu amene anakuzungulirani, kotero munakhala mwamtendere.
And Jehovah sent Jerubbaal and Bedan and Jephthah and Samuel, and delivered you out of the hand of your enemies round about, so that ye dwelt in safety.
12 “Koma mutaona kuti Nahasi mfumu ya Amoni inkabwera kudzamenyana nanu, inu munandiwuza kuti, ‘Ayi, ife tikufuna mfumu kuti itilamulire,’ ngakhale kuti Yehova Mulungu wanu ndiye anali mfumu yanu.
But when ye saw that Nahash the king of the children of Ammon came against you, ye said to me, Nay, but a king shall reign over us; when Jehovah your God was your king.
13 Tsopano nayi mfumu imene mwayisankha, imene munayipempha. Onani, Yehova wakupatsani mfumu.
And now behold, the king whom ye have chosen, whom ye have asked for! and behold, Jehovah has set a king over you.
14 Ngati muziopa Yehova ndi kumamutumikira ndi kumamumvera, osamupandukira ndiponso ngati inu pamodzi ndi mfumu yanu mudzatsata Yehova Mulungu wanu, ndiye zinthu zonse zidzakuyenderani bwino.
If ye fear Jehovah, and serve him, and hearken to his voice, and rebel not against the commandment of Jehovah, then both ye and the king also that reigns over you shall continue following Jehovah your God.
15 Koma mukapanda kumvera Yehova ndi kumupandukira, ndiye adzakulangani pamodzi ndi mfumu yanu yomwe.
But if ye will not hearken to the voice of Jehovah, and if ye rebel against the commandment of Jehovah, then will the hand of Jehovah be against you, as against your fathers.
16 “Tsono imani pomwepa kuti muone chinthu chachikulu chimene Yehova ali pafupi kuchita pamaso panu!
Now therefore stand and see this great thing which Jehovah will do before your eyes.
17 Kodi ino si nthawi yokolola tirigu? Komabe ndipemphera kwa Yehova kuti agwetse mvula ya mabingu. Zikatero mudzadziwa kuti tchimo lanu limene mwachita popempha mfumu kwa Yehova ndi lalikulu.”
Is it not wheat-harvest to-day? I will call unto Jehovah, and he will send thunder and rain; and ye shall perceive and see that your wickedness is great which ye have done in the sight of Jehovah in asking for yourselves a king.
18 Choncho Samueli anapemphera, ndipo Yehova anatumiza mvula ya mabingu tsiku lomwelo. Apo anthu aja anaopa kwambiri Yehova ndi Samueli.
And Samuel called to Jehovah; and Jehovah sent thunder and rain that day. And all the people greatly feared Jehovah and Samuel.
19 Tsono anamupempha Samueli nati, “Chonde mutipempherere kwa Yehova, ife atumiki kuti tingafe pakuti pa machimo athu onse tawonjezapo tchimo lopempha mfumu.”
And all the people said to Samuel, Pray to Jehovah thy God for thy servants, that we die not; for we have added to all our sins the wickedness to ask for ourselves a king.
20 Samueli anayankha kuti, “Musaope, inu mwachitadi tchimo ili, koma musaleke kumutsata Yehova ndi kumutumikira ndi mtima wanu wonse.
And Samuel said to the people, Fear not: ye have done all this wickedness; yet turn not aside from following Jehovah, and serve Jehovah with all your heart;
21 Ndipo musatsate mafano achabechabe amene alibe phindu ndipo sangakupulumutseni popeza ndi achabechabe.
and turn ye not aside; for [it would be] after vain things which cannot profit nor deliver; for they are vain.
22 Yehova adzakana anthu ake kuopa kuti dzina lake lamphamvu linganyozeke, pakuti chinamukondweretsa Yehova kuti akusandutseni inu kukhala anthu ake.
For Jehovah will not cast away his people for his great name's sake; because it has pleased Jehovah to make you his people.
23 Ndiponso kunena za ine, zisachitike kuti ndichimwire Yehova pakulephera kukupemphererani. Ndipo ine ndidzakuphunzitsani njira yabwino ndi yolungama kuti muziyendamo.
Moreover, as for me, far be it from me that I should sin against Jehovah in ceasing to pray for you; and I will teach you the good and right way.
24 Koma onetsetsani kuti mukuopa Yehova ndi kumutumikira mokhulupirika ndi mtima wanu wonse. Nthawi zonse muziganizira zinthu zazikulu wakhala akukuchitirani.
Only, fear Jehovah, and serve him in truth, with all your heart; for see how great things he has done for you.
25 Komabe mukapitirira kuchita zoyipa, ndiye kuti inu pamodzi ndi mfumu yanu mudzachotsedwa.”
But if ye do wickedly, ye shall perish, both ye and your king.

< 1 Samueli 12 >