< 1 Samueli 12 >
1 Pambuyo pake Samueli anawuza Aisraeli onse kuti, “Ine ndamvera zonse zimene munandiwuza ndipo ndakupatsani mfumu kuti izikulamulirani.
Mluvil pak Samuel ke všemu Izraelovi: Aj, uposlechl jsem hlasu vašeho ve všem, což jste mluvili ke mně, a ustanovil jsem nad vámi krále.
2 Tsopano muli ndi mfumu imene izikutsogolerani, koma ine ndakalamba, kumutu kwanga kuli imvi zokhazokha ndipo ana anga ali pamodzi ndi inu. Ndakhala ndili mtsogoleri wanu kuyambira ndili mnyamata mpaka lero.
A nyní aj, král jde před vámi, já pak zstaral jsem se a ošedivěl, a synové moji, aj, mezi vámi jsou. Já také chodil jsem před vámi od své mladosti až do dnešního dne.
3 Ine ndili pano. Ngati ndinalakwa chilichonse nditsutseni pamaso pa Yehova ndi wodzozedwa wake. Kodi ndinalanda ngʼombe ya yani? Kodi ndinalanda bulu wa yani? Kodi ndani amene ndinamudyera masuku pa mutu? Kodi ndinazunza yani? Kodi ndinalandira kwa yani chiphuphu choti nʼkundidetsa mʼmaso? Ngati ndinachita chilichonse cha izi, ine ndidzakubwezerani.”
A však aj, teď jsem. Vydejte svědectví proti mně před Hospodinem a před pomazaným jeho, vzal-li jsem čího vola, aneb vzal-li jsem čího osla, utiskl-li jsem koho, ublížil-li jsem komu, aneb vzal-li jsem od koho úplatek, abych na něm přehlédl něco, a navrátím vám.
4 Iwo anayankha kuti, “Inu simunatidyere masuku pamutu kapena kutizunza. Simunalande kanthu kalikonse ka munthu.”
Odpověděli: Neutiskl jsi nás, aniž jsi ublížil nám, aniž jsi co vzal z ruky kterého člověka.
5 Samueli anawawuza kuti, “Yehova ndiye mboni pakati pa inu ndi ine, ndiponso wodzozedwa wake ndi mboni kuti lero simunapeze chilichonse mʼdzanja langa.” Iwo anati, “Inde, Yehova ndiye mboni.”
Řekl ještě jim: Svědek jest Hospodin proti vám, svědek jest i pomazaný jeho v tento den, že jste nenalezli při mně ničehož. I řekl lid: Svědek jest.
6 Samueli anawawuzanso kuti, “Yehova ndiye amene anasankha Mose ndi Aaroni kuti atulutse makolo anu mʼdziko la Igupto.
Tedy řekl Samuel lidu: Hospodin jest svědek, kterýž učinil Mojžíše a Arona, a kterýž vyvedl otce vaše z země Egyptské.
7 Nʼchifukwa chake tsopano imani pomwepa kuti ndikufotokozereni pamaso pa Yehova, za ntchito za chipulumutso zimene Yehova anachitira inu ndi makolo anu.
Protož nyní postavte se, ať s vámi v soud vejdu před Hospodinem o všecky spravedlivé skutky Hospodinovy, kteréž učinil s vámi i s otci vašimi.
8 “Yakobo atapita ku dziko la Igupto, Aiguptowo akuwazunza, iwo analirira kwa Yehova kuti awathandize, ndipo Yehova anatumiza Mose ndi Aaroni, amene anatulutsa makolo anu mʼdziko la Igupto ndi kudzawakhazika pa malo ano.
Když byl všel Jákob do Egypta, volali otcové vaši k Hospodinu; i poslal Hospodin Mojžíše a Arona, kteříž vyvedli otce vaše z Egypta, a osadili je na tomto místě.
9 “Koma iwo anayiwala Yehova Mulungu wawo, choncho Yehova anawapereka mʼdzanja la Sisera mkulu wa ankhondo wa mzinda wa Hazori, ndiponso mʼmanja mwa Afilisti ndi mfumu ya Mowabu. Mafumu onsewa anathira nkhondo makolo anu.
A když se zapomenuli na Hospodina Boha svého, vydal je v ruku Zizary, knížete vojska Azor, a v ruku Filistinských, též v ruku krále Moábského, kteříž bojovali proti nim.
10 Tsono iwo analira kwa Yehova nati, ‘Ife tachimwa, chifukwa tamusiya Yehova ndi kumatumikira mafano a Baala ndi Asiteroti. Koma tsopano tilanditseni mʼmanja mwa adani athu ndipo tidzakutumikirani.’
Ale když volali k Hospodinu a řekli: Zhřešili jsme, nebo jsme opustili Hospodina, a sloužili jsme Bálim a Astarot, protož nyní vysvoboď nás z ruky nepřátel našich, a sloužiti budeme tobě:
11 Choncho Yehova anatumiza Yeru-Baala, Bedani, Yefita ndi Samueli ndipo anakulanditsani mʼmanja mwa adani anu amene anakuzungulirani, kotero munakhala mwamtendere.
I poslal Hospodin Jerobále a Bedana a Jefte a Samuele, a vytrhl vás z ruky nepřátel vašich okolních, a bydlili jste bezpečně.
12 “Koma mutaona kuti Nahasi mfumu ya Amoni inkabwera kudzamenyana nanu, inu munandiwuza kuti, ‘Ayi, ife tikufuna mfumu kuti itilamulire,’ ngakhale kuti Yehova Mulungu wanu ndiye anali mfumu yanu.
Potom vidouce, že Náhas král synů Ammon přitáhl proti vám, řekli jste mi: Nikoli, ale král bude kralovati nad námi; ješto Hospodin Bůh váš jest králem vaším.
13 Tsopano nayi mfumu imene mwayisankha, imene munayipempha. Onani, Yehova wakupatsani mfumu.
Nyní tedy, aj, král, kteréhož jste zvolili, za něhož jste žádali, a aj, Hospodin ustanovil ho nad vámi králem.
14 Ngati muziopa Yehova ndi kumamutumikira ndi kumamumvera, osamupandukira ndiponso ngati inu pamodzi ndi mfumu yanu mudzatsata Yehova Mulungu wanu, ndiye zinthu zonse zidzakuyenderani bwino.
Budete-li se báti Hospodina, a jemu sloužiti a poslouchati hlasu jeho, a nebudete-li se zpěčovati řeči Hospodinově, tak i vy i král, kterýž kraluje nad vámi, ostojíte, jdouce za Hospodinem Bohem vaším.
15 Koma mukapanda kumvera Yehova ndi kumupandukira, ndiye adzakulangani pamodzi ndi mfumu yanu yomwe.
Pakli nebudete poslouchati hlasu Hospodinova, ale odporni budete řeči jeho, bude ruka Hospodinova proti vám, jako i proti otcům vašim.
16 “Tsono imani pomwepa kuti muone chinthu chachikulu chimene Yehova ali pafupi kuchita pamaso panu!
Ještě se teď pozastavte, a vizte věc tuto velikou, kterouž učiní Hospodin před očima vašima.
17 Kodi ino si nthawi yokolola tirigu? Komabe ndipemphera kwa Yehova kuti agwetse mvula ya mabingu. Zikatero mudzadziwa kuti tchimo lanu limene mwachita popempha mfumu kwa Yehova ndi lalikulu.”
Zdaliž není dnes žeň pšeničná? Volati budu k Hospodinu, i vydá hřímání a déšť, tak že poznati a viděti musíte, jak jest to velmi zlá věc, kteréž jste se dopustili před očima Hospodinovýma, žádavše sobě krále.
18 Choncho Samueli anapemphera, ndipo Yehova anatumiza mvula ya mabingu tsiku lomwelo. Apo anthu aja anaopa kwambiri Yehova ndi Samueli.
Protož volal Samuel k Hospodinu, a vydal Hospodin hřímání a déšť v ten den. I bál se všecken lid Hospodina velmi i Samuele.
19 Tsono anamupempha Samueli nati, “Chonde mutipempherere kwa Yehova, ife atumiki kuti tingafe pakuti pa machimo athu onse tawonjezapo tchimo lopempha mfumu.”
A řekl všecken lid Samuelovi: Modl se za služebníky své Hospodinu Bohu svému, abychom nezemřeli; nebo jsme přidali ke všem hříchům našim i toto zlé, že jsme sobě žádali krále.
20 Samueli anayankha kuti, “Musaope, inu mwachitadi tchimo ili, koma musaleke kumutsata Yehova ndi kumutumikira ndi mtima wanu wonse.
I řekl Samuel lidu: Nebojte se. Učiniliť jste sic všecko to zlé, však proto neodstupujte zpět od Hospodina, ale služte Hospodinu celým srdcem svým.
21 Ndipo musatsate mafano achabechabe amene alibe phindu ndipo sangakupulumutseni popeza ndi achabechabe.
Neodstupujte, pravím, následujíce marnosti, totiž cizích bohů, kteříž nic neprospívají, aniž vysvobozují, nebo jsou marnost.
22 Yehova adzakana anthu ake kuopa kuti dzina lake lamphamvu linganyozeke, pakuti chinamukondweretsa Yehova kuti akusandutseni inu kukhala anthu ake.
Neopustíť zajisté Hospodin lidu svého pro jméno své veliké; nebo zalíbilo se Hospodinu, aby vás sobě vzdělal v lid.
23 Ndiponso kunena za ine, zisachitike kuti ndichimwire Yehova pakulephera kukupemphererani. Ndipo ine ndidzakuphunzitsani njira yabwino ndi yolungama kuti muziyendamo.
Ode mne také odstup to, abych měl hřešiti proti Hospodinu, a přestávati modliti se za vás, nýbrž navoditi vás budu na cestu dobrou a přímou.
24 Koma onetsetsani kuti mukuopa Yehova ndi kumutumikira mokhulupirika ndi mtima wanu wonse. Nthawi zonse muziganizira zinthu zazikulu wakhala akukuchitirani.
A však bojte se Hospodina a služte jemu v pravdě celým srdcem svým; nebo vidíte, jak veliké věci učinil s vámi.
25 Komabe mukapitirira kuchita zoyipa, ndiye kuti inu pamodzi ndi mfumu yanu mudzachotsedwa.”
Jestliže pak předce zle činiti budete, i vy i král váš zahynete.