< 1 Samueli 11 >

1 Nahasi, Mwamoni anapita ndi kuzungulira mzinda wa Yabesi Giliyadi. Tsono anthu onse a ku Yabesi anapempha Nahasiyo kuti, “Muchite nafe pangano, ndipo tidzakutumikirani.”
Нахаш, Амонитул, а венит ши а ымпресурат Иабесул дин Галаад. Тоць локуиторий дин Иабес ау зис луй Нахаш: „Фэ легэмынт ку ной, ши-ць вом фи супушь.”
2 Koma Nahasi Mwamoni uja anayankha kuti, “Ndidzachita nanu pangano pokhapokha nditakolowola diso lakumanja la aliyense wa inu kuti ndichititse manyazi Aisraeli onse.”
Дар Нахаш, Амонитул, ле-а рэспунс: „Вой фаче легэмынт ку вой дакэ мэ лэсаць сэ вэ скот ла тоць окюл дрепт ши сэ арунк астфел о окарэ асупра ынтрегулуй Исраел.”
3 Akuluakulu a mzinda wa Yabesi anati kwa iye, “Utipatse masiku asanu ndi awiri kuti titumize uthenga mu Israeli monse. Ngati sipapezeka wodzatipulumutsa, ndiye ife tidzadzipereka kwa iwe.”
Бэтрыний дин Иабес й-ау зис: „Дэ-не ун рэгаз де шапте зиле ка сэ тримитем соль ын тот цинутул луй Исраел; ши дакэ ну ва фи нимень сэ не ажуте, не вом супуне цие.”
4 Amithenga aja atafika kwawo kwa Sauli ku Gibeya ndi kufotokoza nkhaniyi kwa anthu onse, iwo analira motaya mtima.
Солий ау ажунс ла Гибея, четатя луй Саул, ши ау спус ачесте лукрурь ын аузул попорулуй. Ши тот попорул а ридикат гласул ши а плынс.
5 Pa nthawiyo nʼkuti Sauli akubwera kuchokera ku munda, ali pambuyo pa ngʼombe zake za ntchito ndipo anafunsa. “Nʼchiyani chawavuta anthuwa kuti azilira motere?” Ndipo anamufotokozera zomwe anthu a mu mzinda wa Yabesi ananena.
Саул токмай се ынторчя де ла кымп, ын урма боилор, ши а ынтребат: „Че аре попорул де плынӂе?” Й-ау историсит че спусесерэ чей дин Иабес.
6 Sauli atamva mawu awo, Mzimu wa Mulungu unabwera pa iye mwa mphamvu ndipo anakwiya kwambiri.
Кум а аузит Саул ачесте лукрурь, Духул луй Думнезеу а венит песте ел ши с-а мыният фоарте таре.
7 Tsono anatenga ngʼombe ziwiri za ntchito, nazidula nthulinthuli. Ndipo anatumiza amithenga ndi nthulizo dziko lonse la Israeli ndi mawu akuti, “Umo ndi mmene adzachite ndi ngʼombe ya aliyense amene satsata Sauli ndi Samueli.” Ndipo anthu anachita mantha aakulu motero kuti onse ananyamuka ndi mtima umodzi.
А луат о переке де бой, й-а тэят ын букэць ши ле-а тримис прин соль ын тот цинутул луй Исраел, зикынд: „Орьчине ну ва мерӂе дупэ Саул ши Самуел ышь ва ведя боий тэяць ла фел.” Гроаза Домнулуй а апукат пе попор, каре а порнит ка ун сингур ом.
8 Pamenepo Sauli anawasonkhanitsa ku Bezeki nawawerenga, ndipo Aisraeli analipo 300,000, Ayuda analipo 30,000.
Саул ле-а фэкут нумэрэтоаря ла Безек; копиий луй Исраел ерау трей суте де мий ши бэрбаций луй Иуда, трейзечь де мий.
9 Tsono Sauli anawuza amithenga ochokera ku Yabesi aja kuti, “Mukawawuze anthu a ku Yabesi Giliyadi kuti mawa nthawi ya masana adzapulumutsidwa.” Pamene amithengawo anapita ndi kukafotokoza nkhani imeneyi kwa anthu a ku Yabesi, iwo anasangalala kwambiri.
Ей ау зис солилор каре венисерэ: „Аша сэ ворбиць локуиторилор Иабесулуй дин Галаад: ‘Мыне, кынд ва догори соареле, вець авя ажутор.’” Солий ау дус вестя ачаста челор дин Иабес, каре с-ау умплут де букурие
10 Choncho anthu a ku Yabesi anawuza Nahasi kuti, “Mawa tidzadzipereka kwa inu ndipo inu mudzachite nafe chilichonse chokukomerani.”
ши ау зис амоницилор: „Мыне не вом супуне воуэ ши не вець фаче че вэ ва плэчя.”
11 Tsono mmawa mwake Sauli anagawa anthuwo mʼmagulu atatu. Mmamawa kusanache iwo analowa mʼmisasa ya Aamoni ndi kuwapha mpaka masana. Amene anapulumuka anabalalika, aliyense kwakekwake.
А доуа зи, Саул а ымпэрцит попорул ын трей чете. Ау пэтрунс ын табэра амоницилор ын стража диминеций ши й-ау бэтут пынэ ла кэлдура зилей. Чей че ау скэпат ау фост рисипиць ши н-ау май рэмас дой лаолалтэ динтре ей.
12 Kenaka anthu anafunsa Samueli kuti, “Kodi ndani aja ankanena kuti, ‘Kodi Sauli nʼkutilamulira ife?’ Bwera nawoni kuno kuti tidzawaphe.”
Попорул а зис луй Самуел: „Чине зичя: ‘Саул сэ домняскэ песте ной?’ Даць ынкоаче пе оамений ачея, ка сэ-й оморым.”
13 Koma Sauli anati, “Palibe amene ati aphedwe lero, pakuti lero lino Yehova wagwira ntchito yopulumutsa Israeli.”
Дар Саул а зис: „Нимень ну ва фи оморыт ын зиуа ачаста, кэч астэзь Домнул а дат о избэвире луй Исраел.”
14 Ndipo Samueli anati kwa anthuwo, “Tiyeni tipite ku Giligala kuti tikatsimikizenso kuti Sauli ndi mfumu yathu.”
Ши Самуел а зис попорулуй: „Вениць ши сэ мерӂем ла Гилгал, ка сэ ынтэрим аколо ымпэрэция.”
15 Choncho anthu onse anapita ku Giligala ndipo kumeneko Samueli anakalonga Sauli ufumu pamaso pa Yehova. Pambuyo pake anthu anapereka nsembe zachiyanjano pamaso pa Yehova, ndipo Sauli ndi Aisraeli onse anachita chikondwerero chachikulu.
Тот попорул с-а дус ла Гилгал ши ау пус пе Саул ымпэрат, ынаинтя Домнулуй, ла Гилгал. Аколо, ау адус жертфе де мулцумире ынаинтя Домнулуй ши Саул ши тоць оамений луй Исраел с-ау веселит фоарте мулт аколо.

< 1 Samueli 11 >