< 1 Samueli 11 >

1 Nahasi, Mwamoni anapita ndi kuzungulira mzinda wa Yabesi Giliyadi. Tsono anthu onse a ku Yabesi anapempha Nahasiyo kuti, “Muchite nafe pangano, ndipo tidzakutumikirani.”
Så drog ammonitten Nahas op og kringsatte Jabes i Gilead, og alle Jabes' menn sa til Nahas: Gjør fred med oss, så vil vi tjene dig.
2 Koma Nahasi Mwamoni uja anayankha kuti, “Ndidzachita nanu pangano pokhapokha nditakolowola diso lakumanja la aliyense wa inu kuti ndichititse manyazi Aisraeli onse.”
Men ammonitten Nahas svarte dem: På det vilkår vil jeg gjøre fred med eder at det høire øie stikkes ut på eder alle; den skjensel vil jeg legge på hele Israel.
3 Akuluakulu a mzinda wa Yabesi anati kwa iye, “Utipatse masiku asanu ndi awiri kuti titumize uthenga mu Israeli monse. Ngati sipapezeka wodzatipulumutsa, ndiye ife tidzadzipereka kwa iwe.”
Da sa Jabes eldste til ham: Gi oss frist i syv dager, så vi kan sende bud rundt om i hele Israels land! Er det da ingen som hjelper oss, så vil vi overgi oss til dig.
4 Amithenga aja atafika kwawo kwa Sauli ku Gibeya ndi kufotokoza nkhaniyi kwa anthu onse, iwo analira motaya mtima.
Da sendebudene kom til Sauls Gibea og bar frem sitt ærend for folket, brast alt folket i gråt.
5 Pa nthawiyo nʼkuti Sauli akubwera kuchokera ku munda, ali pambuyo pa ngʼombe zake za ntchito ndipo anafunsa. “Nʼchiyani chawavuta anthuwa kuti azilira motere?” Ndipo anamufotokozera zomwe anthu a mu mzinda wa Yabesi ananena.
I samme stund kom Saul gående hjem fra marken bakefter sine okser. Og Saul sa: Hvad er det i veien med folket siden de gråter? Og de fortalte ham hvad mennene fra Jabes hadde sagt.
6 Sauli atamva mawu awo, Mzimu wa Mulungu unabwera pa iye mwa mphamvu ndipo anakwiya kwambiri.
Da Saul hørte dette, kom Guds Ånd over ham, og hans vrede optendtes høilig.
7 Tsono anatenga ngʼombe ziwiri za ntchito, nazidula nthulinthuli. Ndipo anatumiza amithenga ndi nthulizo dziko lonse la Israeli ndi mawu akuti, “Umo ndi mmene adzachite ndi ngʼombe ya aliyense amene satsata Sauli ndi Samueli.” Ndipo anthu anachita mantha aakulu motero kuti onse ananyamuka ndi mtima umodzi.
Og han tok et par okser og hugg dem i stykker og sendte stykkene om i hele Israels land med sendebudene og lot si: Den som ikke drar ut efter Saul og Samuel, med hans okser skal det gjøres likedan. Da falt det en redsel fra Herren over folket, og de drog ut som en mann.
8 Pamenepo Sauli anawasonkhanitsa ku Bezeki nawawerenga, ndipo Aisraeli analipo 300,000, Ayuda analipo 30,000.
Han mønstret dem i Besek, og Israels barn var tre hundre tusen, og Judas menn tretti tusen.
9 Tsono Sauli anawuza amithenga ochokera ku Yabesi aja kuti, “Mukawawuze anthu a ku Yabesi Giliyadi kuti mawa nthawi ya masana adzapulumutsidwa.” Pamene amithengawo anapita ndi kukafotokoza nkhani imeneyi kwa anthu a ku Yabesi, iwo anasangalala kwambiri.
Og de sa til sendebudene som var kommet: Så skal I si til mennene i Jabes i Gilead: Imorgen, når solen brenner hett, skal det komme hjelp til eder. Da sendebudene kom og meldte dette til mennene i Jabes, blev de glade,
10 Choncho anthu a ku Yabesi anawuza Nahasi kuti, “Mawa tidzadzipereka kwa inu ndipo inu mudzachite nafe chilichonse chokukomerani.”
og de sa til ammonittene: Imorgen vil vi overgi oss til eder, så kan I gjøre med oss aldeles som I finner for godt!
11 Tsono mmawa mwake Sauli anagawa anthuwo mʼmagulu atatu. Mmamawa kusanache iwo analowa mʼmisasa ya Aamoni ndi kuwapha mpaka masana. Amene anapulumuka anabalalika, aliyense kwakekwake.
Dagen efter stilte Saul folket op i tre hoper, og i morgenvakten trengte de midt inn i leiren og hugg ammonittene ned, til dagen blev het; og de som blev tilbake, spredtes, så det ikke blev to sammen tilbake av dem.
12 Kenaka anthu anafunsa Samueli kuti, “Kodi ndani aja ankanena kuti, ‘Kodi Sauli nʼkutilamulira ife?’ Bwera nawoni kuno kuti tidzawaphe.”
Da sa folket til Samuel: Hvem var det som sa: Skal Saul være konge over oss? La oss få fatt i disse menn, så vi kan drepe dem.
13 Koma Sauli anati, “Palibe amene ati aphedwe lero, pakuti lero lino Yehova wagwira ntchito yopulumutsa Israeli.”
Da sa Saul: På denne dag skal ingen drepes; for idag har Gud hjulpet Israel til seier.
14 Ndipo Samueli anati kwa anthuwo, “Tiyeni tipite ku Giligala kuti tikatsimikizenso kuti Sauli ndi mfumu yathu.”
Og Samuel sa til folket: Kom, la oss gå til Gilgal for å stadfeste kongedømmet der!
15 Choncho anthu onse anapita ku Giligala ndipo kumeneko Samueli anakalonga Sauli ufumu pamaso pa Yehova. Pambuyo pake anthu anapereka nsembe zachiyanjano pamaso pa Yehova, ndipo Sauli ndi Aisraeli onse anachita chikondwerero chachikulu.
Da gikk alt folket til Gilgal, og der i Gilgal gjorde de Saul til konge for Herrens åsyn; og de ofret der takkoffer for Herrens åsyn. Og Saul og alle Israels menn gledet sig der storlig.

< 1 Samueli 11 >