< 1 Samueli 11 >
1 Nahasi, Mwamoni anapita ndi kuzungulira mzinda wa Yabesi Giliyadi. Tsono anthu onse a ku Yabesi anapempha Nahasiyo kuti, “Muchite nafe pangano, ndipo tidzakutumikirani.”
Nionjoñe mb’eo amy zao t’i Nakase nte-Amone, nitobe am-piatrefañe Iabese-Gilade eo: le nanao ty hoe amy Nakase iaby o nte-Iabeseo: Mifañinà ama’ay vaho hitoroña’ay.
2 Koma Nahasi Mwamoni uja anayankha kuti, “Ndidzachita nanu pangano pokhapokha nditakolowola diso lakumanja la aliyense wa inu kuti ndichititse manyazi Aisraeli onse.”
Le hoe t’i Nakase nte-Amone am’ iereo: Inao arè ty fepètse hanoeko ama’ areo, te songa hakatrake o fihaino’ areo ankavanao ho fañinjeañe am’ Israele iaby.
3 Akuluakulu a mzinda wa Yabesi anati kwa iye, “Utipatse masiku asanu ndi awiri kuti titumize uthenga mu Israeli monse. Ngati sipapezeka wodzatipulumutsa, ndiye ife tidzadzipereka kwa iwe.”
Le hoe o mpiaolo’ Iabeseo ama’e: Toloro fito androm-panintsiñan-jahay hañitrifa’ay mb’an-tane’ Israele iaby; ie amy zay naho tsy eo ty handrombak’ anay le hiakatse mb’ama’o mb’eo.
4 Amithenga aja atafika kwawo kwa Sauli ku Gibeya ndi kufotokoza nkhaniyi kwa anthu onse, iwo analira motaya mtima.
Nivotrake e Gibàn-tSaole ao o ìrakeo le nisaontsie’e an-dravembia’ondatio i entañe zay vaho fonga nipoñake ty rovetse ondatio.
5 Pa nthawiyo nʼkuti Sauli akubwera kuchokera ku munda, ali pambuyo pa ngʼombe zake za ntchito ndipo anafunsa. “Nʼchiyani chawavuta anthuwa kuti azilira motere?” Ndipo anamufotokozera zomwe anthu a mu mzinda wa Yabesi ananena.
Nañorike mpirai-troke boak’ an-tetek’ ao t’i Saole, le hoe t’i Saole: Ino ty mañore ondatio t’ie mirovetse? Aa le nitalilia’ iareo ty saontsi’ o nte-Iabeseo.
6 Sauli atamva mawu awo, Mzimu wa Mulungu unabwera pa iye mwa mphamvu ndipo anakwiya kwambiri.
Ie nahajanjiñe i entañe zay t’i Saole le nentoe’ ty Arofon’ Añahare, vaho nisolebotse ty haviñera’e.
7 Tsono anatenga ngʼombe ziwiri za ntchito, nazidula nthulinthuli. Ndipo anatumiza amithenga ndi nthulizo dziko lonse la Israeli ndi mawu akuti, “Umo ndi mmene adzachite ndi ngʼombe ya aliyense amene satsata Sauli ndi Samueli.” Ndipo anthu anachita mantha aakulu motero kuti onse ananyamuka ndi mtima umodzi.
Rinambe’e i katràka mpirai-joka rey, le linili-lili’e, naho nahitri’e mb’an-tane’ Israele mb’eo mb’eo am-pitàn’ ìrake, ami’ty hoe: Ze tsy mionjoñe mb’eo am-panonjohizañe i Saole naho am-pañorihañe i Samoele, le zao ka ty hanoañe o katràka’eo. Aa le nifetsak’ am’ondatio ty fañeveñañe am’ Iehovà, vaho niakatse mb’eo hoe ondaty raike.
8 Pamenepo Sauli anawasonkhanitsa ku Bezeki nawawerenga, ndipo Aisraeli analipo 300,000, Ayuda analipo 30,000.
Niahe’e e Betseke ao: telo hetse ty ana’ Israele vaho telo-ale o nte-Iehodao.
9 Tsono Sauli anawuza amithenga ochokera ku Yabesi aja kuti, “Mukawawuze anthu a ku Yabesi Giliyadi kuti mawa nthawi ya masana adzapulumutsidwa.” Pamene amithengawo anapita ndi kukafotokoza nkhani imeneyi kwa anthu a ku Yabesi, iwo anasangalala kwambiri.
Aa le hoe ty asa’ iareo amo ìrake nivotrakeo: Zao ty ho enta’ areo amo nte-Iabese-giladeo: hamaray aolo’ ty mafana-voho t’ie hitendreke rombake. Nibalike naho nitalily amo nte-Iabeseo o irakeo le niehake,
10 Choncho anthu a ku Yabesi anawuza Nahasi kuti, “Mawa tidzadzipereka kwa inu ndipo inu mudzachite nafe chilichonse chokukomerani.”
vaho hoe o nte-Iabeseo: Hamaray ty hiakara’ay mb’ ama’ areo vaho hanoe’ areo ama’ay ze satrin’ arofo’ areo.
11 Tsono mmawa mwake Sauli anagawa anthuwo mʼmagulu atatu. Mmamawa kusanache iwo analowa mʼmisasa ya Aamoni ndi kuwapha mpaka masana. Amene anapulumuka anabalalika, aliyense kwakekwake.
Aa ie maraiñe, zinara’ i Saole an-dia-rai’e telo ondatio le nimoak’ an-tobe ao am-pijilovañe maraindraiñey vaho zinevo’ iereo o nte-Amoneo am-para’ te mafana-voho; niparaitake iaby ze nisisa kanao tsy nahaisahañe roe miharo lia.
12 Kenaka anthu anafunsa Samueli kuti, “Kodi ndani aja ankanena kuti, ‘Kodi Sauli nʼkutilamulira ife?’ Bwera nawoni kuno kuti tidzawaphe.”
Le hoe ondatio amy Samoele; Ia o nivolañe ty hoe: Hahafehe antika hao t’i Saoleo? Aseseo mb’atoa indaty rezay hañohofan-doza.
13 Koma Sauli anati, “Palibe amene ati aphedwe lero, pakuti lero lino Yehova wagwira ntchito yopulumutsa Israeli.”
Fe hoe t’i Saole: Leo raik’ am’ondatio tsy havetrake te anito, fa nanao fandrombahañe e Israele ao t’Iehovà anindroany.
14 Ndipo Samueli anati kwa anthuwo, “Tiyeni tipite ku Giligala kuti tikatsimikizenso kuti Sauli ndi mfumu yathu.”
Le hoe t’i Samoele am’ondatio, Antao homb’ e Gilgale mb’eo hamentesan-tika ty fifeheañe.
15 Choncho anthu onse anapita ku Giligala ndipo kumeneko Samueli anakalonga Sauli ufumu pamaso pa Yehova. Pambuyo pake anthu anapereka nsembe zachiyanjano pamaso pa Yehova, ndipo Sauli ndi Aisraeli onse anachita chikondwerero chachikulu.
Aa le niheo mb’e Gilgale mb’eo ondaty iabio naho nanoe’ iereo mpanjaka añatrefa’ Iehovà e Gilgale t’i Saole; le nisoroñe engam-panintsiñañe añatrefa’ Iehovà; vaho nandia taroba t’i Saole naho o ana’ Israele iabio.