< 1 Samueli 11 >

1 Nahasi, Mwamoni anapita ndi kuzungulira mzinda wa Yabesi Giliyadi. Tsono anthu onse a ku Yabesi anapempha Nahasiyo kuti, “Muchite nafe pangano, ndipo tidzakutumikirani.”
Then came up Nachash the 'Ammonite, and encamped against Yabesh-gil'ad: and all the men of Yabesh said unto Nachash, Make a covenant with us, and we will serve thee.
2 Koma Nahasi Mwamoni uja anayankha kuti, “Ndidzachita nanu pangano pokhapokha nditakolowola diso lakumanja la aliyense wa inu kuti ndichititse manyazi Aisraeli onse.”
And Nachash the 'Ammonite said unto them, On this condition will I make it with you, that ye all have put out the right eye, that I may lay it as a reproach upon all Israel.
3 Akuluakulu a mzinda wa Yabesi anati kwa iye, “Utipatse masiku asanu ndi awiri kuti titumize uthenga mu Israeli monse. Ngati sipapezeka wodzatipulumutsa, ndiye ife tidzadzipereka kwa iwe.”
And the elders of Yabesh said unto him, Grant us seven days' respite, that we may send messengers throughout all the boundary of Israel; and then, if there be none to save us, will we come out to thee.
4 Amithenga aja atafika kwawo kwa Sauli ku Gibeya ndi kufotokoza nkhaniyi kwa anthu onse, iwo analira motaya mtima.
And the messengers came to Gib'ah of Saul, and spoke the words in the ears of the people; and all the people lifted up their voice, and wept.
5 Pa nthawiyo nʼkuti Sauli akubwera kuchokera ku munda, ali pambuyo pa ngʼombe zake za ntchito ndipo anafunsa. “Nʼchiyani chawavuta anthuwa kuti azilira motere?” Ndipo anamufotokozera zomwe anthu a mu mzinda wa Yabesi ananena.
And, behold, Saul was coming after the herds out of the field; and Saul said, What aileth the people that they weep? And they told him the words of the men of Yabesh.
6 Sauli atamva mawu awo, Mzimu wa Mulungu unabwera pa iye mwa mphamvu ndipo anakwiya kwambiri.
And the spirit of God came suddenly over Saul when he heard these words, and his anger was kindled greatly,
7 Tsono anatenga ngʼombe ziwiri za ntchito, nazidula nthulinthuli. Ndipo anatumiza amithenga ndi nthulizo dziko lonse la Israeli ndi mawu akuti, “Umo ndi mmene adzachite ndi ngʼombe ya aliyense amene satsata Sauli ndi Samueli.” Ndipo anthu anachita mantha aakulu motero kuti onse ananyamuka ndi mtima umodzi.
And he took a yoke of oxen, and cut them in pieces, and sent them about throughout all the boundary of Israel by the hand of the messengers, saying, Whosoever goeth not forth after Saul and after Samuel, shall have his herds thus treated. And the dread of the Lord fell on the people, and they went out as one man.
8 Pamenepo Sauli anawasonkhanitsa ku Bezeki nawawerenga, ndipo Aisraeli analipo 300,000, Ayuda analipo 30,000.
And he numbered them in Bezek; and the children of Israel were three hundred thousand, and the men of Judah thirty thousand.
9 Tsono Sauli anawuza amithenga ochokera ku Yabesi aja kuti, “Mukawawuze anthu a ku Yabesi Giliyadi kuti mawa nthawi ya masana adzapulumutsidwa.” Pamene amithengawo anapita ndi kukafotokoza nkhani imeneyi kwa anthu a ku Yabesi, iwo anasangalala kwambiri.
And they said unto the messengers that were come, Thus shall ye say unto the men of Yabesh-gil'ad, Tomorrow shall ye have help, when the sun shineth hot. And the messengers came and told it to the men of Yabesh; and these were glad.
10 Choncho anthu a ku Yabesi anawuza Nahasi kuti, “Mawa tidzadzipereka kwa inu ndipo inu mudzachite nafe chilichonse chokukomerani.”
And the men of Yabesh said, Tomorrow will we go out unto you, and ye can do unto us in accordance with all that seemeth good in your eyes.
11 Tsono mmawa mwake Sauli anagawa anthuwo mʼmagulu atatu. Mmamawa kusanache iwo analowa mʼmisasa ya Aamoni ndi kuwapha mpaka masana. Amene anapulumuka anabalalika, aliyense kwakekwake.
And it happened on the morrow, that Saul put the people in three companies; and they came into the midst of the camp in the morning watch, and they smote the 'Ammonites until the heat of the day: and it came to pass, that those that remained were scattered, and no two among them were left together.
12 Kenaka anthu anafunsa Samueli kuti, “Kodi ndani aja ankanena kuti, ‘Kodi Sauli nʼkutilamulira ife?’ Bwera nawoni kuno kuti tidzawaphe.”
And the people said unto Samuel, Who is there that saith, Shall Saul reign over us? give up the men, and we will put them to death.
13 Koma Sauli anati, “Palibe amene ati aphedwe lero, pakuti lero lino Yehova wagwira ntchito yopulumutsa Israeli.”
And Saul said, There shall not a man be put to death on this day; for today the Lord hath wrought deliverance in Israel.
14 Ndipo Samueli anati kwa anthuwo, “Tiyeni tipite ku Giligala kuti tikatsimikizenso kuti Sauli ndi mfumu yathu.”
And Samuel said to the people, Come and let us go to Gilgal, and renew there the choice of the king.
15 Choncho anthu onse anapita ku Giligala ndipo kumeneko Samueli anakalonga Sauli ufumu pamaso pa Yehova. Pambuyo pake anthu anapereka nsembe zachiyanjano pamaso pa Yehova, ndipo Sauli ndi Aisraeli onse anachita chikondwerero chachikulu.
And all the people went to Gilgal; and they appointed there Saul as king before the Lord in Gilgal; and they sacrificed there sacrifices of peace-offerings before the Lord; and Saul with all the men of Israel rejoiced there very greatly.

< 1 Samueli 11 >