< 1 Samueli 10 >

1 Ndipo Samueli anatenga botolo la mafuta nathira mafutawo pa mutu wa Sauli ndipo anapsompsona nati, “Yehova wakudzoza kuti ukhale mtsogoleri wa anthu ake, Aisraeli. Iwe udzalamulira anthu a Yehova ndiponso udzawapulumutsa mʼmanja mwa adani awo owazungulira. Chizindikiro chakuti Yehova wakudzoza kuti ukhale mtsogoleri wa anthu ake ndi ichi:
USamuweli wasethatha umfuma wamafutha, wawathela ekhanda lakhe, wamanga, wathi: Angithi kungoba iNkosi ikugcobele ukuthi ube ngumbusi phezu kwelifa layo?
2 Ukachoka pano lero lino, udzakumana ndi amuna awiri kufupi ndi manda a Rakele ku Zeliza mʼmalire mwa dziko la Benjamini ndipo adzakuwuza kuti, ‘Abulu amene munkafunafuna aja apezeka. Ndipo tsopano abambo ako asiya kuganiza za abulu ndipo akudera nkhawa za iwe.’ Iwo akufunsa kuti, ‘Kodi ndidzachita chiyani mmene mwana wanga sakuoneka?’”
Ekusukeni kwakho kimi lamuhla uzafica abantu ababili engcwabeni likaRasheli emngceleni wakoBhenjamini eZeliza; njalo bazakuthi kuwe: Obabhemikazi obuyebadinga sebetholiwe, khangela-ke, uyihlo useyekele udaba labobabhemikazi, usenqinekela lina esithi: Ngizayenzelani indodana yami?
3 “Ndipo udzapyola pamenepo ndi kufika ku mtengo wa thundu wa ku Tabori. Kumeneko udzakumana ndi anthu atatu akupita kukapereka nsembe ku Nyumba ya Mulungu ku Beteli. Mmodzi adzakhala atanyamula ana ambuzi atatu, wina atanyamula malofu atatu a buledi, ndi winayo atanyamula thumba la vinyo.
Nxa usudlule lapho waya phambili, uzafika esihlahleni se-okhi seThabhori; lalapho uzahlangana labantu abathathu besenyuka besiya kuNkulunkulu eBhetheli, omunye ephethe amazinyane amathathu, lomunye ephethe amaqebelengwana ezinkwa amathathu, lomunye ephethe imbodlela yewayini.
4 Adzakupatsa moni ndi kukupatsa malofu awiri a buledi. Iwe udzalandire bulediyo.
Bazakubuza ngempilo, bakunike izinkwa ezimbili, ozazithatha esandleni sabo.
5 “Pambuyo pake, udzafike ku Gibeyati-Elohimu, kumene kuli gulu la ankhondo la Afilisti. Pamene ukuyandikira mzindawo, udzakumana ndi gulu la aneneri akutsika kuchokera ku phiri, akuyimba zeze, ngʼoma, zitoliro ndi pangwe, ndiponso akulosera.
Emva kwalokho uzafika eqaqeni lukaNkulunkulu lapho okuhlala khona ibutho lenqaba yamaFilisti; kuzakuthi-ke, nxa ufika lapho emzini uzahlangana lexuku labaprofethi besehla endaweni ephakemeyo, laphambi kwabo kulogubhu lwezintambo, lesigubhu, lomhlanga, lechacho, beprofetha.
6 Kenaka Mzimu wa Yehova udzabwera pa iwe ndi mphamvu, ndipo udzayamba kulosera nawo pamodzi. Ndipo udzasinthika kukhala munthu wina.
LoMoya kaNkulunkulu uzafika ngamandla phezu kwakho, uprofethe kanye labo, uphendulwe ube ngomunye umuntu.
7 Zizindikiro izi zikakachitika, dzachite chilichonse manja ako angathe kuchita, pakuti Mulungu ali nawe.
Kuzakuthi-ke lapho lezizibonakaliso zikufikela, wena wenze lokho isandla sakho esizakuthola, ngoba uNkulunkulu ulawe.
8 “Tsono tsogola kupita ku Giligala. Ine ndidzabwera ndithu kudzapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Koma ukandidikire masiku asanu ndi awiri mpaka ine nditabwera kuti ndidzakuwuze zomwe udzachite.”
Uzakwehla phambi kwami uye eGiligali; khangela-ke, ngizakwehlela kuwe ukuze nginikele iminikelo yokutshiswa, ngihlabe imihlatshelo yeminikelo yokuthula. Uzalinda insuku eziyisikhombisa ngize ngifike kuwe, ngikutshele lokho ozakwenza.
9 Sauli akutembenuka kusiyana ndi Samueli, Mulungu anasintha mtima wa Sauli, ndipo zinthu zonsezi zinakwaniritsidwa tsiku lomwelo.
Kwasekusithi lapho esefulathele ukuthi asuke kuSamuweli, uNkulunkulu wamnika enye inhliziyo; lazo zonke lezizibonakaliso zeza mhlalokho.
10 Atafika ku Gibeya, anakumana ndi gulu la aneneri. Mzimu wa Mulungu unabwera pa iye mwamphamvu, nayamba kulosa nawo.
Lapho sebefikile khona eqaqeni, khangela, ixuku labaprofethi lamhlangabeza; uMoya kaNkulunkulu wasefika ngamandla phezu kwakhe, waprofetha phakathi kwabo.
11 Pamene onse amene ankamudziwa kale anamuona akulosera pamodzi ndi aneneri, anafunsana wina ndi mnzake. “Kodi nʼchiyani chachitika ndi mwana wa Kisi? Kodi Sauli alinso mʼgulu la aneneri?”
Kwasekusithi bonke ababemazi mandulo bebona ukuthi, khangela, uprofetha labaprofethi, abantu bathi, omunye komunye: Kuyini lokhu okwehlele indodana kaKishi? Kanti uSawuli laye uphakathi kwabaprofethi?
12 Munthu wina wa kumeneko anayankha kuti, “Nanga enawa abambo awo ndani?” Kotero kunayambika mwambi wakuti, “Kodi Saulinso ali mʼgulu la aneneri?”
Kwasekuphendula umuntu owakhona wathi: Kanti ngubani uyise wabo? Ngakho kwasekusiba yisaga ukuthi: Kanti uSawuli laye uphakathi kwabaprofethi?
13 Sauli atasiya kuloserako, anapita ku kachisi ku phiri.
Eseqedile ukuprofetha wafika endaweni ephakemeyo.
14 Tsono amalume ake a Sauli anamufunsa ndi mnyamata wake kuti, “Munapita kuti?” Iye anayakha, “Timakafunafuna abulu koma titaona kuti sakupezeka, tinapita kwa Samueli.”
Uyise omncinyane kaSawuli wathi kuye lencekwini yakhe: Beliye ngaphi? Wasesithi: Ukuyadinga obabhemikazi; lapho sesibona ukuthi kabakho sasesifika kuSamuweli.
15 Amalume ake a Sauli anati, “Chonde, ndifotokozereniko zimene Samueli wakuwuzani.”
Uyise omncinyane kaSawuli wathi: Ake ungitshele ukuthi utheni kini uSamuweli?
16 Sauli anati, “Iye anatitsimikizira kuti abulu anapezeka.” Koma sanawawuze amalume akewo za nkhani ija ya ufumu imene Samueli anamuwuza.
USawuli wasesithi kuyise omncinyane: Usitshelile sibili ukuthi obabhemikazi sebetholakele. Kodwa udaba lombuso akhuluma ngalo uSamuweli kamtshelanga.
17 Samueli anayitana Aisraeli onse kuti asonkhane pamaso pa Yehova ku Mizipa.
USamuweli wasebizela abantu ndawonye eNkosini eMizipa;
18 Ndipo anawuza Aisraeli onse kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi kukupulumutsani mʼdzanja la Igupto ndi mʼdzanja la mafumu onse amene ankakuzunzani.’
wathi kubantwana bakoIsrayeli: Itsho njalo iNkosi uNkulunkulu kaIsrayeli: Mina ngamenyusa uIsrayeli eGibhithe, ngalikhulula esandleni samaGibhithe lesandleni sayo yonke imibuso eyalicindezelayo.
19 Koma lero mwamukana Mulungu wanu amene amakupulumutsani mʼmavuto anu onse ndi mʼzowawa zanu. Ndipo mukuti, ‘Ayi, koma mutipatse mfumu yotilamulira.’ Tsopanotu sonkhanani pamaso pa Yehova mwa mafuko ndi mabanja anu.”
Kodwa lamuhla lina limalile uNkulunkulu wenu, yena ngokwakhe owalisindisayo engozini zonke zenu lensizini zenu; laselisithi kuye: Hatshi, beka inkosi phezu kwethu. Ngakho-ke manini phambi kweNkosi ngezizwe zenu langezinkulungwane zenu.
20 Samueli atasonkhanitsa mafuko onse a Israeli, fuko la Benjamini linasankhidwa.
USamuweli wasesondeza zonke izizwe zakoIsrayeli; njalo isizwe sakoBhenjamini sabanjwa.
21 Anasonkhanitsa fuko la Benjamini banja ndi banja. Pomaliza anasonkhanitsa banja la Matiri mmodzimmodzi ndipo Sauli mwana wa Kisi anasankhidwa. Koma atamufunafuna, sanamupeze.
Wasesondeza isizwe sakoBhenjamini ngensendo zaso, losendo lwakoMatiri lwabanjwa, loSawuli indodana kaKishi wabanjwa. Kuthe bemdinga katholakalanga.
22 Tsono anthu anafunsanso kwa Yehova kuti, “Kodi munthuyu wabwera kale kuno?” Ndipo Yehova anayankha kuti, “Inde wabisala pakati pa katundu.”
Ngakho babuya babuza eNkosini ukuthi lowomuntu usezafika lapha yini? INkosi yasisithi: Khangelani, ucatshile empahleni.
23 Iwo anathamanga ndi kukamutenga kumeneko. Atayimirira pakati pa anthu anapezeka kuti anali wamtali kuposa anthu ena mwakuti ankamulekeza mʼmapewa.
Basebegijima bamlanda khona; lapho esemi phakathi kwabantu, wayemude kulabo bonke abantu kusukela ehlombe lakhe kusiya phezulu.
24 Samueli anafunsa anthu onse kuti, “Kodi mukumuona munthu amene Yehova wasankha? Palibe wofanana naye pakati pa anthu onse.” Kenaka anthu onse anafuwula kuti, “Mfumu ikhale ndi moyo wautali!”
USamuweli wasesithi kubo bonke abantu: Liyambona yini lowo iNkosi emkhethileyo, ukuthi kakho loyedwa onjengaye kubo bonke abantu? Bonke abantu basebememeza bathi: Kayiphile inkosi!
25 Samueli anafotokozera anthu ntchito ndi udindo wa mfumu. Pambuyo pake analemba mʼbuku zonse zokhudza ntchito ndi udindo wa mfumu, ndipo bukulo analiyika pamaso pa Yehova. Kenaka Samueli analola aliyense kuti abwerere kupita kwawo.
USamuweli wasebatshela abantu indlela yombuso, wawubhala egwalweni, walubeka phambi kweNkosi. USamuweli wasebayekela bonke abantu bahamba, wonke waya endlini yakhe.
26 Sauli anapitanso ku mudzi kwawo ku Gibeya, pamodzi ndi anthu amphamvu amene Mulungu anawafewetsa mitima.
USawuli laye wasesiya endlini yakhe eGibeya; kwasekuhamba laye amaqhawe onhliziyo zawo uNkulunkulu wayezithintile.
27 Koma anthu ena achabechabe anati, “Kodi munthu uyu angathe bwanji kutipulumutsa?” Iwo anayamba kumunyoza Sauliyo, ndipo sankamupatsa ngakhale mphatso. Koma iye sanalabadireko.
Kodwa abantwana bakaBheliyali bathi: Uzasisindisa njani lo? Basebemdelela, kabamphathelanga sipho; kodwa wazithulela.

< 1 Samueli 10 >