< 1 Samueli 10 >

1 Ndipo Samueli anatenga botolo la mafuta nathira mafutawo pa mutu wa Sauli ndipo anapsompsona nati, “Yehova wakudzoza kuti ukhale mtsogoleri wa anthu ake, Aisraeli. Iwe udzalamulira anthu a Yehova ndiponso udzawapulumutsa mʼmanja mwa adani awo owazungulira. Chizindikiro chakuti Yehova wakudzoza kuti ukhale mtsogoleri wa anthu ake ndi ichi:
Eka Samuel nokawo tungʼ mar mo mi oolo ewi Saulo eka nonyodhe mowacho niya, “Donge Jehova Nyasaye osewiri mondo ibed jatelo ne joge moyiero.
2 Ukachoka pano lero lino, udzakumana ndi amuna awiri kufupi ndi manda a Rakele ku Zeliza mʼmalire mwa dziko la Benjamini ndipo adzakuwuza kuti, ‘Abulu amene munkafunafuna aja apezeka. Ndipo tsopano abambo ako asiya kuganiza za abulu ndipo akudera nkhawa za iwe.’ Iwo akufunsa kuti, ‘Kodi ndidzachita chiyani mmene mwana wanga sakuoneka?’”
Kawuononi ka iseweya ibiro romo gi ji ariyo machiegni gi liend Rael e gwengʼ Zelza e tongʼ jo-Benjamin. Gibiro wachoni ni, ‘Punde mane iwuok idhi dwaro oseyudi. Kendo wuonu oseweyo parogi koro chunye chandore ni wachne kopenjo niya, “Abiro timo angʼo ne wach wuodani?”’
3 “Ndipo udzapyola pamenepo ndi kufika ku mtengo wa thundu wa ku Tabori. Kumeneko udzakumana ndi anthu atatu akupita kukapereka nsembe ku Nyumba ya Mulungu ku Beteli. Mmodzi adzakhala atanyamula ana ambuzi atatu, wina atanyamula malofu atatu a buledi, ndi winayo atanyamula thumba la vinyo.
“Eka ibiro wuok kanyo midhi nyaka yath maduongʼ man Tabor. Ji adek mawuotho kadhi Bethel ir Nyasaye norom kodi kanyo. Achiel kuomgi biro biro kotingʼo nyidiek adek, to machielo biro tingʼo makati adek, to machielo to otingʼo ndede mar divai.
4 Adzakupatsa moni ndi kukupatsa malofu awiri a buledi. Iwe udzalandire bulediyo.
Gibiro mosi kendo miyi makati ariyo, mibiro kawo kuomgi.
5 “Pambuyo pake, udzafike ku Gibeyati-Elohimu, kumene kuli gulu la ankhondo la Afilisti. Pamene ukuyandikira mzindawo, udzakumana ndi gulu la aneneri akutsika kuchokera ku phiri, akuyimba zeze, ngʼoma, zitoliro ndi pangwe, ndiponso akulosera.
“Bangʼ mano ibiro dhi Gibea miluongo ni Got mar Nyasaye kama nitie kambi mar jo-Filistia. Ka ichopo machiegni gi dala to ibiro romo gi oganda jonabi kalor koa kar lemo kotelnegi gi joma goyo orutu, gi tamborin, asili gi nyatiti, kendo jonabi biro biro ka gikoro wach.
6 Kenaka Mzimu wa Yehova udzabwera pa iwe ndi mphamvu, ndipo udzayamba kulosera nawo pamodzi. Ndipo udzasinthika kukhala munthu wina.
Roho mar Jehova Nyasaye nobi kuomi gi teko, inikor kaachiel kodgi kendo noloki mibed ngʼato mopogore.
7 Zizindikiro izi zikakachitika, dzachite chilichonse manja ako angathe kuchita, pakuti Mulungu ali nawe.
Ka ranyisi otimore to mondo itim atima gima lweti oyudo ni onego tim; nikech Nyasaye ni kodi.
8 “Tsono tsogola kupita ku Giligala. Ine ndidzabwera ndithu kudzapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Koma ukandidikire masiku asanu ndi awiri mpaka ine nditabwera kuti ndidzakuwuze zomwe udzachite.”
“Tel nyima idhi Gilgal. Chutho abiro lor ka abiro iri mondo atim misango miwangʼo pep kod misengini mag lalruok, to nyaka ine ni irita kuom ndalo abiriyo mondo abi anyisi gima onego itim.”
9 Sauli akutembenuka kusiyana ndi Samueli, Mulungu anasintha mtima wa Sauli, ndipo zinthu zonsezi zinakwaniritsidwa tsiku lomwelo.
Kane Saulo oseweyo Samuel, Nyasaye ne oloko chuny Saulo, kendo ranyisi duto nochopo kare chiengʼno.
10 Atafika ku Gibeya, anakumana ndi gulu la aneneri. Mzimu wa Mulungu unabwera pa iye mwamphamvu, nayamba kulosa nawo.
Kane gichopo Gibea, oganda mar jonabi noromone, Roho mar Nyasaye nobiro mopongʼe gi teko eka nochako koro wach kodgi.
11 Pamene onse amene ankamudziwa kale anamuona akulosera pamodzi ndi aneneri, anafunsana wina ndi mnzake. “Kodi nʼchiyani chachitika ndi mwana wa Kisi? Kodi Sauli alinso mʼgulu la aneneri?”
Eka joma ne ongʼeye kane onene ka okoro gi jonabi, negipenjore kendgi niya, “Ma to en angʼo matimore ne wuod Kish? Saulo bende en achiel kuom jonabi?”
12 Munthu wina wa kumeneko anayankha kuti, “Nanga enawa abambo awo ndani?” Kotero kunayambika mwambi wakuti, “Kodi Saulinso ali mʼgulu la aneneri?”
To ngʼat moro modak e gwengʼno nomedo dwoko kopenjo niya, “Wuon-gi to en ngʼa?” Omiyo wachni nolokore ngero niya, “Saulo-ni bende en achiel kuom jonabi?”
13 Sauli atasiya kuloserako, anapita ku kachisi ku phiri.
Kane Saulo osetieko koro noidho mobet e kar lemo.
14 Tsono amalume ake a Sauli anamufunsa ndi mnyamata wake kuti, “Munapita kuti?” Iye anayakha, “Timakafunafuna abulu koma titaona kuti sakupezeka, tinapita kwa Samueli.”
Eka owad gi wuon Saulo nopenjogi niya, “Ne pod un kanye?” Ne odwoko niya, “Ne wadwaro punde, to kane waneno ni gitamowa yudo eka wadhi ir Samuel.”
15 Amalume ake a Sauli anati, “Chonde, ndifotokozereniko zimene Samueli wakuwuzani.”
Owad gi wuon Saulo nowachone niya, “Nyisa gima Samuel nowachonu.”
16 Sauli anati, “Iye anatitsimikizira kuti abulu anapezeka.” Koma sanawawuze amalume akewo za nkhani ija ya ufumu imene Samueli anamuwuza.
Saulo nodwoke niya, “Ne owachonwa malongʼo ni punde ne oseyudo.” To ne ok onyise gima Samuel ne owacho kuom wach bedo ruoth.
17 Samueli anayitana Aisraeli onse kuti asonkhane pamaso pa Yehova ku Mizipa.
Samuel noluongo oganda jo-Israel duto Mizpa e nyim Jehova Nyasaye,
18 Ndipo anawuza Aisraeli onse kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi kukupulumutsani mʼdzanja la Igupto ndi mʼdzanja la mafumu onse amene ankakuzunzani.’
mowachonegi niya, “Ma e gima Jehova Nyasaye ma Nyasach Israel wacho: ‘Ne agolo Israel koa Misri, kendo ne aresou e teko mar loch Misri kod pinjeruodhi duto mane thirou.’
19 Koma lero mwamukana Mulungu wanu amene amakupulumutsani mʼmavuto anu onse ndi mʼzowawa zanu. Ndipo mukuti, ‘Ayi, koma mutipatse mfumu yotilamulira.’ Tsopanotu sonkhanani pamaso pa Yehova mwa mafuko ndi mabanja anu.”
To koro useweyo Nyasachu, ma resou e masicheu gi chandruoku. Ma usewacho ni, ‘Ooyo miwa ruodhwa.’ Omiyo sani suduru e nyim Jehova Nyasaye kuchanoru e ogandau kod e dhoutu.”
20 Samueli atasonkhanitsa mafuko onse a Israeli, fuko la Benjamini linasankhidwa.
Kane Samuel okelo ogendini duto mag Israel machiegni, to oganda mar Benjamin ema ne oyier.
21 Anasonkhanitsa fuko la Benjamini banja ndi banja. Pomaliza anasonkhanitsa banja la Matiri mmodzimmodzi ndipo Sauli mwana wa Kisi anasankhidwa. Koma atamufunafuna, sanamupeze.
Eka nokelo oganda mar Benjamin nyime, kaluwore gi dhoot ka dhoot, mine oyier dhood Matri. Mogik ne oyier Saulo wuod Kish. To kane gidware, to ne ok oyude.
22 Tsono anthu anafunsanso kwa Yehova kuti, “Kodi munthuyu wabwera kale kuno?” Ndipo Yehova anayankha kuti, “Inde wabisala pakati pa katundu.”
Eka negimedo penjo wach kuom Jehova Nyasaye niya, “Ngʼatni bende osebiro ka koso?” Kendo Jehova Nyasaye nodwoko niya, “Ee, osepondo e kind misike.”
23 Iwo anathamanga ndi kukamutenga kumeneko. Atayimirira pakati pa anthu anapezeka kuti anali wamtali kuposa anthu ena mwakuti ankamulekeza mʼmapewa.
Negiringo ma giome, kane ochungʼ e dier oganda to ne obor ma ji moko ne gik mana e goke.
24 Samueli anafunsa anthu onse kuti, “Kodi mukumuona munthu amene Yehova wasankha? Palibe wofanana naye pakati pa anthu onse.” Kenaka anthu onse anafuwula kuti, “Mfumu ikhale ndi moyo wautali!”
Samuel nowachone ji duto niya, “Bende uneno ngʼat ma Jehova Nyasaye oseyiero? Onge ngʼama chalo kode kuom ji duto.” Eka ji nokok niya, “Ruoth mondo odag amingʼa!”
25 Samueli anafotokozera anthu ntchito ndi udindo wa mfumu. Pambuyo pake analemba mʼbuku zonse zokhudza ntchito ndi udindo wa mfumu, ndipo bukulo analiyika pamaso pa Yehova. Kenaka Samueli analola aliyense kuti abwerere kupita kwawo.
Samuel nolero ne ji chike mag bedo ruoth. Nondikogi e kitabu mokano e nyim Jehova Nyasaye. Eka Samuel ne ogonyo ji mondo ngʼato ka ngʼato odog e dalane.
26 Sauli anapitanso ku mudzi kwawo ku Gibeya, pamodzi ndi anthu amphamvu amene Mulungu anawafewetsa mitima.
Saulo bende nodhi dalagi man Gibea, ka en gi joma thuondi mane osemul chunygi gi Nyasaye.
27 Koma anthu ena achabechabe anati, “Kodi munthu uyu angathe bwanji kutipulumutsa?” Iwo anayamba kumunyoza Sauliyo, ndipo sankamupatsa ngakhale mphatso. Koma iye sanalabadireko.
To jomoko ma acheje nowacho niya, “Ere kaka ngʼatni nyalo resowa?” Negi chaye mine ok gikelone mich. To Saulo nolingʼ mos.

< 1 Samueli 10 >