< 1 Samueli 10 >
1 Ndipo Samueli anatenga botolo la mafuta nathira mafutawo pa mutu wa Sauli ndipo anapsompsona nati, “Yehova wakudzoza kuti ukhale mtsogoleri wa anthu ake, Aisraeli. Iwe udzalamulira anthu a Yehova ndiponso udzawapulumutsa mʼmanja mwa adani awo owazungulira. Chizindikiro chakuti Yehova wakudzoza kuti ukhale mtsogoleri wa anthu ake ndi ichi:
Da tog Samuel Olieflasken og udgød Olien over hans Hoved, kyssede ham og sagde: "Har HERREN ikke salvet dig til Fyrste over sit Folk Israel? Du skal herske over HERRENs Folk og frelse det fra dets Fjender. Og dette skal være dig Tegnet på, at HERREN har salvet dig til Fyrste over sin Arv:
2 Ukachoka pano lero lino, udzakumana ndi amuna awiri kufupi ndi manda a Rakele ku Zeliza mʼmalire mwa dziko la Benjamini ndipo adzakuwuza kuti, ‘Abulu amene munkafunafuna aja apezeka. Ndipo tsopano abambo ako asiya kuganiza za abulu ndipo akudera nkhawa za iwe.’ Iwo akufunsa kuti, ‘Kodi ndidzachita chiyani mmene mwana wanga sakuoneka?’”
Når du i Dag går fra mig, skal du træffe to Mænd ved Rakels Grav ved Benjamins Grænse i Zelza, og de skal sige til dig: Æslerne, du gik ud at lede efter, er fundet; dem har din Fader slået af Tanke, men nu er han urolig for eder og siger: Hvad skal jeg gøre for min Søn?
3 “Ndipo udzapyola pamenepo ndi kufika ku mtengo wa thundu wa ku Tabori. Kumeneko udzakumana ndi anthu atatu akupita kukapereka nsembe ku Nyumba ya Mulungu ku Beteli. Mmodzi adzakhala atanyamula ana ambuzi atatu, wina atanyamula malofu atatu a buledi, ndi winayo atanyamula thumba la vinyo.
Og når du er gået et Stykke længere frem og kommer til Taboregen, skal du træffe tre Mænd, som er på Vej op til Gud i Betel; den ene bærer tre Kid, den anden tre Brødkager og den tredje en Dunk Vin;
4 Adzakupatsa moni ndi kukupatsa malofu awiri a buledi. Iwe udzalandire bulediyo.
de skal hilse på dig og give dig to Brødkager, som du skal tage imod.
5 “Pambuyo pake, udzafike ku Gibeyati-Elohimu, kumene kuli gulu la ankhondo la Afilisti. Pamene ukuyandikira mzindawo, udzakumana ndi gulu la aneneri akutsika kuchokera ku phiri, akuyimba zeze, ngʼoma, zitoliro ndi pangwe, ndiponso akulosera.
Derefter kommer du til Guds Gibea, hvor Filisternes Foged bor; og når du kommer hen til Byen, vil du støde på en Flok Profeter, som kommer ned fra Offerhøjen i profetisk Henrykkelse til Harpers, Paukers, Fløjters og Citres Klang;
6 Kenaka Mzimu wa Yehova udzabwera pa iwe ndi mphamvu, ndipo udzayamba kulosera nawo pamodzi. Ndipo udzasinthika kukhala munthu wina.
så vil HERRENs Ånd overvælde dig, så du falder i profetisk Henrykkelse sammen med dem, og du skal blive til et andet Menneske.
7 Zizindikiro izi zikakachitika, dzachite chilichonse manja ako angathe kuchita, pakuti Mulungu ali nawe.
Når disse Tegn indtræffer for dig, kan du trygt gøre, hvad der falder for; thi Gud er med dig.
8 “Tsono tsogola kupita ku Giligala. Ine ndidzabwera ndithu kudzapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Koma ukandidikire masiku asanu ndi awiri mpaka ine nditabwera kuti ndidzakuwuze zomwe udzachite.”
Og du skal gå i Forvejen ned til Gilgal; så kommer jeg ned til dig for at bringe Brændofre og ofre Takofre. Syv Dage skal du vente, til jeg kommer og kundgør dig, hvad du skal gøre!"
9 Sauli akutembenuka kusiyana ndi Samueli, Mulungu anasintha mtima wa Sauli, ndipo zinthu zonsezi zinakwaniritsidwa tsiku lomwelo.
Da han derpå vendte sig for at gå bort fra Samuel, gav Gud ham et helt andet Hjerte, og alle disse Tegn indtraf samme Dag.
10 Atafika ku Gibeya, anakumana ndi gulu la aneneri. Mzimu wa Mulungu unabwera pa iye mwamphamvu, nayamba kulosa nawo.
Da han kom hen til Gibea, se, da kom en Flok Profeter ham i Møde, og Guds Ånd overvældede ham, og han faldt i profetisk Henrykkelse midt iblandt dem.
11 Pamene onse amene ankamudziwa kale anamuona akulosera pamodzi ndi aneneri, anafunsana wina ndi mnzake. “Kodi nʼchiyani chachitika ndi mwana wa Kisi? Kodi Sauli alinso mʼgulu la aneneri?”
Og da alle, som kendte ham fra tidligere Tid, så ham i profetisk Henrykkelse sammen med Profeterne, sagde de til hverandre: "Hvad går der af Kisjs Søn? Er også Saul iblandt Profeterne?"
12 Munthu wina wa kumeneko anayankha kuti, “Nanga enawa abambo awo ndani?” Kotero kunayambika mwambi wakuti, “Kodi Saulinso ali mʼgulu la aneneri?”
Så sagde en der fra Stedet: "Hvem er vel deres Fader?" Derfor blev det et Mundheld: "Er også Saul iblandt Profeterne?"
13 Sauli atasiya kuloserako, anapita ku kachisi ku phiri.
Da hans profetiske Henrykkelse var ovre, gik han til Gibea.
14 Tsono amalume ake a Sauli anamufunsa ndi mnyamata wake kuti, “Munapita kuti?” Iye anayakha, “Timakafunafuna abulu koma titaona kuti sakupezeka, tinapita kwa Samueli.”
Sauls Farbroder spurgte da ham og Karlen: "Hvor har I været henne?" Han svarede: "Ude at lede efter Æslerne; og da vi ikke fandt dem, gik vi hen til Samuel."
15 Amalume ake a Sauli anati, “Chonde, ndifotokozereniko zimene Samueli wakuwuzani.”
Da sagde Sauls Farbroder: "Fortæl mig, hvad Samuel sagde til eder!"
16 Sauli anati, “Iye anatitsimikizira kuti abulu anapezeka.” Koma sanawawuze amalume akewo za nkhani ija ya ufumu imene Samueli anamuwuza.
Saul svarede: "Han fortalte os, at Æslerne var fundet!" Men hvad Samuel havde sagt om Kongedømmet, fortalte han ham ikke.
17 Samueli anayitana Aisraeli onse kuti asonkhane pamaso pa Yehova ku Mizipa.
Derpå stævnede Samuel Folket sammen hos HERREN i Mizpa;
18 Ndipo anawuza Aisraeli onse kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi kukupulumutsani mʼdzanja la Igupto ndi mʼdzanja la mafumu onse amene ankakuzunzani.’
og han sagde til Israeliterne: "Så siger HERREN, Israels Gud: Jeg førte Israel op fra Ægypten og frelste eder af Ægypternes Hånd og fra alle de Riger, som plagede eder.
19 Koma lero mwamukana Mulungu wanu amene amakupulumutsani mʼmavuto anu onse ndi mʼzowawa zanu. Ndipo mukuti, ‘Ayi, koma mutipatse mfumu yotilamulira.’ Tsopanotu sonkhanani pamaso pa Yehova mwa mafuko ndi mabanja anu.”
Men nu vrager I eders Gud, som var eders Frelser i alle eders Ulykker og Trængsler, og siger: Nej, en Konge skal du sætte over os! Så træd nu frem for HERRENs Åsyn Stamme for Stamme og Slægt for Slægt!"
20 Samueli atasonkhanitsa mafuko onse a Israeli, fuko la Benjamini linasankhidwa.
Derpå lod Samuel alle Israels Stammer træde frem, og Loddet ramte Benjamins Stamme.
21 Anasonkhanitsa fuko la Benjamini banja ndi banja. Pomaliza anasonkhanitsa banja la Matiri mmodzimmodzi ndipo Sauli mwana wa Kisi anasankhidwa. Koma atamufunafuna, sanamupeze.
Så lod han Benjamins Stamme træde frem Slægt for Slægt, og Matris Slægt ramtes. Så lod han Matris Slægt træde frem Mand for Mand, og Saul, Kisjs Søn, ramtes. Men da man ledte efter ham, var han ikke til at finde.
22 Tsono anthu anafunsanso kwa Yehova kuti, “Kodi munthuyu wabwera kale kuno?” Ndipo Yehova anayankha kuti, “Inde wabisala pakati pa katundu.”
Da adspurgte de på ny HERREN: "Er Manden her?" Og HERREN svarede: "Se, han holder sig skjult ved Trosset."
23 Iwo anathamanga ndi kukamutenga kumeneko. Atayimirira pakati pa anthu anapezeka kuti anali wamtali kuposa anthu ena mwakuti ankamulekeza mʼmapewa.
Så løb de hen og hentede ham der; og da han trådte ind imellem Folket, var han et Hoved højere end alt Folket.
24 Samueli anafunsa anthu onse kuti, “Kodi mukumuona munthu amene Yehova wasankha? Palibe wofanana naye pakati pa anthu onse.” Kenaka anthu onse anafuwula kuti, “Mfumu ikhale ndi moyo wautali!”
Da sagde Samuel til hele Folket: "Ser I ham, HERREN har udvalgt? Hans Lige findes ikke i alt Folket!" Og hele Folket brød ud i Jubelskrig og råbte: "Kongen leve!"
25 Samueli anafotokozera anthu ntchito ndi udindo wa mfumu. Pambuyo pake analemba mʼbuku zonse zokhudza ntchito ndi udindo wa mfumu, ndipo bukulo analiyika pamaso pa Yehova. Kenaka Samueli analola aliyense kuti abwerere kupita kwawo.
Derpå fremsagde Samuel Kongedømmets Ret for Folket og optegnede den i en Bog, som han lagde hen for HERRENs Åsyn. Så lod Samuel hele Folket gå hver til sit:
26 Sauli anapitanso ku mudzi kwawo ku Gibeya, pamodzi ndi anthu amphamvu amene Mulungu anawafewetsa mitima.
også Saul gik til sit Hjem i Gibea, og de tapre Mænd, hvis Hjerte Gud rørte, gik med ham.
27 Koma anthu ena achabechabe anati, “Kodi munthu uyu angathe bwanji kutipulumutsa?” Iwo anayamba kumunyoza Sauliyo, ndipo sankamupatsa ngakhale mphatso. Koma iye sanalabadireko.
Men nogle Niddinger sagde: "Hvor skulde denne kunne hjælpe os?" Og de ringeagtede ham og bragte ham ingen Hyldingsgave. Men han var, som han var døv.