< 1 Petro 1 >

1 Ndine Petro, mtumwi wa Yesu Khristu. Ndikulemba kalatayi kwa onse osankhidwa ndi Mulungu, alendo mʼdziko lapansi, obalalikira ku Ponto, Galatiya, Kapadokiya, Asiya ndi Bituniya.
O PETERO, kekahi lunaolelo no Iesu Kristo, i ka poe i puehu liilii, a e noho malihini ana hoi ma Poneto, a ma Galatia, a ma Kapadokia, a ma Asia, a ma Bitunia;
2 Mulungu Atate anakusankhani, atakudziwani kuyambira pachiyambi, ndipo Mzimu Woyera wakuyeretsani kuti mumvere Yesu Khristu ndikutsukidwa ndi magazi ake. Chisomo ndi mtendere zikhale ndi inu mochuluka.
Ma ka ike mua ana o ke Akua, ka Makua, ma o ka huikala ana o ka Uhane, ua waeia mai oukou, i poe hoolohe, a i poe e kapipiia i ke koko o Iesu Kristo; i nui ko oukou alohaia mai, a me ka maluhia hoi.
3 Alemekezedwe Mulungu, Atate wa Ambuye athu Yesu Khristu. Mwachifundo chake chachikulu anatibadwitsa kwatsopano, mʼchiyembekezo chamoyo pomuukitsa Yesu Khristu kwa akufa,
E hoomaikaiia'ku ke Akua, ka Makua o ko kakou Haku o Iesu Kristo, no kona lokomaikai nui iho, nana no i hoohanau mai ia kakou, i lana mau loa ai ka manao, ma ke alahouana o Iesu Kristo, mai ka make mai;
4 kuti tidzalandire chuma chomwe sichingawonongeke, kuyipitsidwa kapena kufota. Chuma chimenechi akukusungirani kumwamba.
I loaa mai ia kakou ka hooilina pau ole, pelapela ole, mae ole, ua hoana e ia ma ka lani no kakou;
5 Mwachikhulupiriro, mukusungidwa ndi mphamvu ya Mulungu mpaka chipulumutso chitafika chimene chinakonzedwa kuti adzachionetse nthawi yotsiriza.
Ka poe i malamaia mai e ka mana o ke Akua, ma ka manaoio, i loaa mai ke ola i hoomakaukauia no ka hoikeia mai i ka wa mahope.
6 Zimenezi zikukondweretseni kwambiri, ngakhale tsopano, kwa kanthawi kochepa, mukumva zowawa mʼmayesero osiyanasiyana.
Malaila no oukou e hauoli nui nei, oiai nae ua kaumaha oukou i keia wa pokole, no ka hoao pinepine ia mai, i mea e pono ai;
7 Mayeserowa abwera nʼcholinga chakuti chikhulupiriro chanu, chimene ndi chamtengo woposa wa golide, amene amawonongeka ngakhale amayengedwa ndi moto, chitsimikizike kuti ndi chenicheni. Pamenepo ndiye mudzalandire mayamiko, ulemerero ndi ulemu pamene Yesu Khristu adzaoneka.
I lilo hoi ka hoao ana o ko oukou manaoio, ka mea i oi aku ka maikai mamua o ke gula pau wale, i hoaoia i ke ahi, i mea e mahaloia'i, a e hoomaikaiia'i, a e hoonani ia'i i ka wa e ikea mai ai o Iesu Kristo:
8 Ngakhale kuti simunamuone, mumamukonda; ndipo ngakhale kuti simukumuona tsopano, mumamukhulupirira ndipo mumakondwera ndi chimwemwe chachikulu ndi chosaneneka.
Ka mea a oukou i ike maka ole ai, a ua makemake no nae; a, me ka ike ole aku ia ia, ua manaoio aku no nae oukou ia ia me ka hauoli i ka olioli nani pau ole i ka haiia aku;
9 Motero mukulandira mphotho ya chikhulupiriro chanu, ndiyo chipulumutso cha moyo wanu.
E loaa mai ana ka hope o ko oukou manaoio, o ke ola o ko oukou poe uhane.
10 Kunena za chipulumutso chimenechi, aneneri amene ananeneratu za chisomo chimene chimabwera kwa inu, anafunafuna mofufuzafufuza za chipulumutsochi,
Oia ke ola a na kaula i huli ai, me ka imi ikaika, o ka poe i wanana mai i ka pono e hiki mai ana io oukou nei.
11 kufuna kudziwa nthawi ndi momwe zidzachitikire zinthu zimene Mzimu wa Khristu amene ali mwa iwo ankanenera za kuvutika kwa Khristu, ndi ulemerero umene adzakhale nawo pambuyo pake.
Ua imi nui no lakou i ka mea a me ka manawa a ka Uhane o Kristo i hai mai ai iloko o lakou, i kona hoike mua ana mai i ka hoinoia o Kristo, a me ka hoonaniia, mahope o keia mau mea.
12 Mulungu anawawululira kuti ntchito yawoyo sankayigwira chifukwa cha iwo eni, koma chifukwa inu, pamene iwo ankayankhula zinthu zimene mwamva tsopano kuchokera kwa amene amalalikira Uthenga Wabwino mwamphamvu ya Mzimu Woyera wotumidwa kuchokera kumwamba. Ngakhale angelo amalakalaka kuona nawo zinthuzi.
Ua hoikeia mai ia lakou, aole nae na lakou, na kakou, na mea a lakou i ao mai ai; oia hoi na mea i haiia'ku nei ia oukou, e ka poe hai aku i ka euanelio ia oukou, me ka Uhane Hemolele i hoounaia mai, mai ka lani mai: oia ka na anela i makemake ai e ike iho.
13 Choncho konzani mtima wanu, khalani odziretsa; khazikitsani chiyembekezo chanu kotheratu pa chisomo chimene mudzapatsidwe pamene Yesu Khristu adzaonekera.
No ia mea, e kaei oukou i ka puhaka o ko oukou naau, e kuoo, a e hoomau i ka lana ana o ka manao, no ke alohaia mai i ka wa e hoikea mai ai o Iesu Kristo;
14 Monga ana omvera, musatsatenso zilakolako zoyipa zomwe munali nazo pamene munali osadziwa.
I like hoi oukou me na keiki hoolohe, aole e hoolike ana ia oukou iho me na kuko kahiko, i ko oukou wa e naaupo ana.
15 Koma monga amene anakuyitanani ndi woyera, inunso khalani oyera mtima mʼmakhalidwe anu wonse.
Aka, e like me ka hemolele o ka mea nana oukou i koho mai, pela oukou e hemolele ai, i ko oukou noho ana a pau:
16 Pakuti, kwalembedwa kuti, “Khalani oyera mtima, chifukwa Ine ndine Woyera.”
No ka mea, na palapalaia mai, E hemolele oukou; no ka mea, owau ka hemolele.
17 Popeza mumapemphera kwa Atate amene amaweruza munthu aliyense mopanda tsankho molingana ndi zochita zake, pa nthawi imene muli alendo pa dziko lapansi khalani moopa Mulungu.
Ina oukou e hea aku i ka Makua, i ka mea i hoomaopopo me ka ewaewa ole, i kela kanaka, i keia kanaka, ma ke ano o kana hana ana, e noho oukou me ka makau, i ko oukou noho malihini ana.
18 Pakuti mukudziwa kuti simunawomboledwe ndi zinthu zimene zimawonongeka monga siliva kapena golide, kuchoka ku khalidwe lanu lachabe limene munalandira kwa makolo anu.
Ua ike no hoi oukou, aole me na mea popo wale e like me ke kala a me ke gula, ua kuaiia oukou mai ko oukou noho lapuwale ana, mamuli o na mooolelo a ko oukou kupuna mai;
19 Koma munawomboledwa ndi magazi a mtengowapatali a Khristu, Mwana Wankhosa wopanda banga kapena chilema.
Aka, me ke koko waiwai io o Kristo, me ko ke keikihipa kina ole a me ka hala ole:
20 Iye anasankhidwa lisanalengedwe dziko lapansi, koma waonetsedwa chifukwa cha inu pa nthawi ino yotsiriza.
Ua boonohoia oia mamua o ka hookumu ana o ke ao nei; aka, ua hoikeia mai i keia wa hope no oukou,
21 Kudzera mwa Iye mumakhulupirira Mulungu, amene anamuukitsa kwa akufa namupatsa ulemerero. Nʼchifukwa chake chikhulupiriro ndi chiyembekezo chanu chili mwa Mulungu.
Ma ona la oukou i manaoio aku ai i ke Akua, nana i hoala mai ia ia mai ka make mai, a i hoonani aku ia ia; i manaoio ai, a i lana ai hoi ko oukou manao i ke Akua.
22 Tsopano mwayeretsa mitima yanu pomvera choonadi, kuti muzikondana ndi abale anu, kukondana kwenikweni kochokera pansi pa mtima.
I ka malama ana i ka oiaio, ua hoomaemae oukou i ko oukou naau, na ka Uhane mai, i ke aloha hookamani ole i na hoahanau; nolaila, ea, e aloha ikaika loa aku oukou i kekahi i kekahi me ka naau maemae.
23 Popeza mwabadwanso, osati ndi mbewu imene imawonongeka, koma imene siwonongeka, ndiye kuti ndi Mawu a Mulungu amoyo ndi okhalitsa. (aiōn g165)
Ua hanau hou ia mai oukou, aole hoi na ka hua e pala wale ana, aka, na ka hua pala ole, ma ka olelo a ke Akua ola, ka mea e mau loa ana. (aiōn g165)
24 Pakuti, “Anthu onse ali ngati udzu, ndipo ulemerero wawo uli ngati duwa la kuthengo. Udzu umafota ndipo duwa limathothoka,
No ka mea, ua like wale no me ka mauu na kanaka a pau, a o kona nani a pau, ua like me ka pua o ka mauu. E maloo ana no ka mauu. a haule wale iho no hoi kona pua;
25 koma mawu a Ambuye adzakhala mpaka muyaya.” Ndipo awa ndi mawu amene tinalalikira kwa inu. (aiōn g165)
Aka, e mau loa aku no ka olelo a ke Akua; oia hoi ka olelo i aoia'ku nei ia oukou ma ka euaneho. (aiōn g165)

< 1 Petro 1 >