< 1 Petro 5 >

1 Ine ndikupempha akulu a mpingo amene ali pakati panu, monga inenso mkulu mnzawo, mboni ya zowawa za Khristu ndiponso amene ndidzalandira nawo ulemerero umene uti udzaonetsedwe.
Starszych, którzy są między wami, proszę ja spółstarszy i świadek ucierpienia Chrystusowego, i uczestnik chwały, która ma być objawiona:
2 Wetani gulu la Mulungu limene lili mʼmanja mwanu, muziliyangʼanira. Muzichita osati mowumirizidwa, koma mwakufuna kwanu, monga momwe Mulungu akufunira kuti mutero. Musachite chifukwa chadyera la ndalama, koma ndi mtima ofuna kutumikira.
Paście trzodę Bożą, która jest między wami, doglądając jej nie poniewolnie, ale dobrowolnie; nie dla sprośnego zysku, ale ochotnym umysłem:
3 Musakhale ngati mafumu pa amene mukuwayangʼanira, koma mukhale chitsanzo kwa gululo.
Ani jako panując nad dziedzictwem Pańskiem, ale wzorami będąc trzody.
4 Ndipo Mʼbusa wamkulu akadzaonekera, mudzalandira chipewa cha ulemerero chosafota.
A gdy się okaże on książę pasterzy, odniesiecie niezwiędłą koronę chwały.
5 Momwemonso, inu anyamata gonjerani amene ndi akulu. Inu nonse mukhale odzichepetsa kuti mutumikirane, chifukwa, “Mulungu amatsutsana nawo odzikuza, koma amapereka chisomo kwa odzichepetsa.”
Także, młodsi! bądźcie poddani starszym, a wszyscy jedni drugim bądźcie poddani. Pokorą bądźcie wewnątrz ozdobieni, gdyż Bóg pysznym się sprzeciwia, a pokornym łaskę daje.
6 Choncho, mudzichepetse pamaso pa Mulungu wamphamvu, kuti pa nthawi yake adzakukwezeni.
Uniżajcież się tedy pod mocną ręką Bożą, aby was wywyższył czasu swego;
7 Tayani pa Iye nkhawa zanu zonse chifukwa ndiye amakusamalani.
Wszystko staranie wasze wrzuciwszy na niego, gdyż on ma pieczę o was.
8 Khalani odziretsa ndi atcheru. Mdani wanu mdierekezi amayendayenda monga mkango wobangula kufunafuna wina kuti amumeze.
Trzeźwymi bądźcie, czujcie; albowiem przeciwnik wasz dyjabeł, jako lew ryczący obchodzi, szukając kogo by pożarł.
9 Mukaneni iye, ndipo mukhazikike mʼchikhulupiriro, chifukwa mukudziwa kuti abale anzanu pa dziko lonse lapansi nawonso akumva zowawa zomwezi.
Któremu dawajcie odpór, mocni będąc w wierze, wiedząc, iż się takoweż ucierpienia nad braterstwem waszem, które jest na świecie, wykonywają.
10 Ndipo Mulungu wachisomo chonse, amene anakuyitanani ku ulemerero wake wamuyaya mwa Khristu, mutamva zowawa pa kanthawi, adzakukonzaninso ndi kukulimbitsani pa maziko olimba. (aiōnios g166)
A Bóg wszelkiej łaski, który nas powołał do wiecznej chwały swojej w Chrystusie Jezusie, gdy maluczko ucierpicie, ten niech was doskonałymi uczyni, utwierdzi, umocni i ugruntuje; (aiōnios g166)
11 Kwa Iye kukhale mphamvu mpaka muyaya, Ameni. (aiōn g165)
Jemu niech będzie chwała i panowanie na wieki wieków. Amen. (aiōn g165)
12 Mothandizidwa ndi Sila, amene ndi mʼbale wokhulupirika, ndakulemberani mwachidule kukulimbikitsani ndi kuchita umboni kuti ichi ndi chisomo choona cha Mulungu.
Przez Sylwana wam wiernego brata, jako rozumiem, krótkom pisał, napominając i świadcząc, iż ta jest prawdziwa łaska Boża, w której stoicie.
13 Imani mwamphamvu mʼchisomochi. Mlongo wanu amene ali ku Babuloni, wosankhidwa pamodzi nanu akupereka moni, nayenso Marko, mwana wanga, akupereka moni.
Pozdrawia was spółwybrany zbór, ten, który jest w Babilonie i Marek, syn mój
14 Mupatsane moni ndi mpsopsono wachikondi. Mtendere ukhale ndi inu nonse amene muli mwa Khristu.
Pozdrówcie jedni drugich w pocałowaniu miłości. Pokój niech będzie wam wszystkim, którzyście w Chrystusie Jezusie. Amen.

< 1 Petro 5 >