< 1 Petro 5 >
1 Ine ndikupempha akulu a mpingo amene ali pakati panu, monga inenso mkulu mnzawo, mboni ya zowawa za Khristu ndiponso amene ndidzalandira nawo ulemerero umene uti udzaonetsedwe.
The elders that are among you I exhort, who am also an elder and a witness of the sufferings of Christ, and a partaker of the glory which shall be revealed; feed the flock of God that is among you,
2 Wetani gulu la Mulungu limene lili mʼmanja mwanu, muziliyangʼanira. Muzichita osati mowumirizidwa, koma mwakufuna kwanu, monga momwe Mulungu akufunira kuti mutero. Musachite chifukwa chadyera la ndalama, koma ndi mtima ofuna kutumikira.
taking the episcopal charge of it, not by constraint, but willingly; not for shameful lucre, but with a ready mind:
3 Musakhale ngati mafumu pa amene mukuwayangʼanira, koma mukhale chitsanzo kwa gululo.
nor as lording it over the people, but being examples to the flock.
4 Ndipo Mʼbusa wamkulu akadzaonekera, mudzalandira chipewa cha ulemerero chosafota.
And when the sovereign Shepherd shall appear, ye shall receive an unfading crown of glory.
5 Momwemonso, inu anyamata gonjerani amene ndi akulu. Inu nonse mukhale odzichepetsa kuti mutumikirane, chifukwa, “Mulungu amatsutsana nawo odzikuza, koma amapereka chisomo kwa odzichepetsa.”
Likewise ye younger, be subject to the elder; and all of you behaving with due submission one to another, be clothed with humility: for God resisteth the proud, but sheweth favor to the humble.
6 Choncho, mudzichepetse pamaso pa Mulungu wamphamvu, kuti pa nthawi yake adzakukwezeni.
Humble yourselves therefore under the mighty hand of God, that He may exalt you in due time;
7 Tayani pa Iye nkhawa zanu zonse chifukwa ndiye amakusamalani.
casting all your care upon Him, for He careth for you.
8 Khalani odziretsa ndi atcheru. Mdani wanu mdierekezi amayendayenda monga mkango wobangula kufunafuna wina kuti amumeze.
Be sober, be vigilant; for your adversary the devil, like a roaring lion, walketh about, seeking whom he may devour:
9 Mukaneni iye, ndipo mukhazikike mʼchikhulupiriro, chifukwa mukudziwa kuti abale anzanu pa dziko lonse lapansi nawonso akumva zowawa zomwezi.
whom resist, stedfast in the faith, knowing that the same sufferings are endured by your brethren in the world.
10 Ndipo Mulungu wachisomo chonse, amene anakuyitanani ku ulemerero wake wamuyaya mwa Khristu, mutamva zowawa pa kanthawi, adzakukonzaninso ndi kukulimbitsani pa maziko olimba. (aiōnios )
But may the God of all grace, who hath called us to his eternal glory in Christ Jesus, after ye have suffered a little while, make you perfect, confirm, strengthen, and establish you. (aiōnios )
11 Kwa Iye kukhale mphamvu mpaka muyaya, Ameni. (aiōn )
To Him be glory and dominion for ever and ever. Amen. (aiōn )
12 Mothandizidwa ndi Sila, amene ndi mʼbale wokhulupirika, ndakulemberani mwachidule kukulimbikitsani ndi kuchita umboni kuti ichi ndi chisomo choona cha Mulungu.
Thus I have written briefly by Silvanus, a faithful brother to you (as I judge) exhorting and testifying, that this is the true grace of God wherein ye stand.
13 Imani mwamphamvu mʼchisomochi. Mlongo wanu amene ali ku Babuloni, wosankhidwa pamodzi nanu akupereka moni, nayenso Marko, mwana wanga, akupereka moni.
The church in Babylon, chosen together with you saluteth you, and so doth Marcus my son.
14 Mupatsane moni ndi mpsopsono wachikondi. Mtendere ukhale ndi inu nonse amene muli mwa Khristu.
Salute one another with a kiss of charity. Peace be with you all who are in Christ Jesus. Amen.