< 1 Petro 5 >
1 Ine ndikupempha akulu a mpingo amene ali pakati panu, monga inenso mkulu mnzawo, mboni ya zowawa za Khristu ndiponso amene ndidzalandira nawo ulemerero umene uti udzaonetsedwe.
The elders who are among you I exhort, who am also an elder, and a witness of the sufferings of Christ, and also a partaker of the glory that shall be revealed:
2 Wetani gulu la Mulungu limene lili mʼmanja mwanu, muziliyangʼanira. Muzichita osati mowumirizidwa, koma mwakufuna kwanu, monga momwe Mulungu akufunira kuti mutero. Musachite chifukwa chadyera la ndalama, koma ndi mtima ofuna kutumikira.
Feed the flock of God which is among you, taking the oversight [of it], not by constraint, but willingly; not for filthy lucre, but from a ready mind;
3 Musakhale ngati mafumu pa amene mukuwayangʼanira, koma mukhale chitsanzo kwa gululo.
Neither as being lords over [God's] heritage, but being examples to the flock.
4 Ndipo Mʼbusa wamkulu akadzaonekera, mudzalandira chipewa cha ulemerero chosafota.
And when the chief Shepherd shall appear, ye shall receive a crown of glory that fadeth not away.
5 Momwemonso, inu anyamata gonjerani amene ndi akulu. Inu nonse mukhale odzichepetsa kuti mutumikirane, chifukwa, “Mulungu amatsutsana nawo odzikuza, koma amapereka chisomo kwa odzichepetsa.”
Likewise, ye younger, submit yourselves to the elder. Yes, all [of you] be subject one to another, and be clothed with humility: for God resisteth the proud, and giveth grace to the humble.
6 Choncho, mudzichepetse pamaso pa Mulungu wamphamvu, kuti pa nthawi yake adzakukwezeni.
Humble yourselves therefore under the mighty hand of God, that he may exalt you in due time:
7 Tayani pa Iye nkhawa zanu zonse chifukwa ndiye amakusamalani.
Casting all your care upon him; for he careth for you.
8 Khalani odziretsa ndi atcheru. Mdani wanu mdierekezi amayendayenda monga mkango wobangula kufunafuna wina kuti amumeze.
Be sober, be vigilant; because your adversary the devil, as a roaring lion, walketh about, seeking whom he may devour:
9 Mukaneni iye, ndipo mukhazikike mʼchikhulupiriro, chifukwa mukudziwa kuti abale anzanu pa dziko lonse lapansi nawonso akumva zowawa zomwezi.
Whom resist steadfast in the faith, knowing that the same afflictions are accomplished in your brethren that are in the world.
10 Ndipo Mulungu wachisomo chonse, amene anakuyitanani ku ulemerero wake wamuyaya mwa Khristu, mutamva zowawa pa kanthawi, adzakukonzaninso ndi kukulimbitsani pa maziko olimba. (aiōnios )
But the God of all grace, who hath called us to his eternal glory by Christ Jesus, after ye have suffered a while, make you perfect, establish, strengthen, settle [you]. (aiōnios )
11 Kwa Iye kukhale mphamvu mpaka muyaya, Ameni. (aiōn )
To him [be] glory and dominion for ever and ever. Amen. (aiōn )
12 Mothandizidwa ndi Sila, amene ndi mʼbale wokhulupirika, ndakulemberani mwachidule kukulimbikitsani ndi kuchita umboni kuti ichi ndi chisomo choona cha Mulungu.
By Silvanus, a faithful brother to you, as I suppose, I have written briefly, exhorting, and testifying that this is the true grace of God in which ye stand.
13 Imani mwamphamvu mʼchisomochi. Mlongo wanu amene ali ku Babuloni, wosankhidwa pamodzi nanu akupereka moni, nayenso Marko, mwana wanga, akupereka moni.
The [church that is] at Babylon, elected together with [you], saluteth you; and [so doth] Mark my son.
14 Mupatsane moni ndi mpsopsono wachikondi. Mtendere ukhale ndi inu nonse amene muli mwa Khristu.
Greet ye one another with a kiss of charity. Peace [be] with you all that are in Christ Jesus. Amen.