< 1 Petro 5 >

1 Ine ndikupempha akulu a mpingo amene ali pakati panu, monga inenso mkulu mnzawo, mboni ya zowawa za Khristu ndiponso amene ndidzalandira nawo ulemerero umene uti udzaonetsedwe.
The seniors who are among you, I exhort, who am also a senior, and a witness of the sufferings of Christ, and also a partaker of the glory which is to be revealed.
2 Wetani gulu la Mulungu limene lili mʼmanja mwanu, muziliyangʼanira. Muzichita osati mowumirizidwa, koma mwakufuna kwanu, monga momwe Mulungu akufunira kuti mutero. Musachite chifukwa chadyera la ndalama, koma ndi mtima ofuna kutumikira.
Feed the flock of God, which is with you; exercising the overseer's office, not by constraint, but willingly; neither for the sake of sordid gain, but from good disposition;
3 Musakhale ngati mafumu pa amene mukuwayangʼanira, koma mukhale chitsanzo kwa gululo.
neither as lording it over the heritage of God, but, being patterns to the flock:
4 Ndipo Mʼbusa wamkulu akadzaonekera, mudzalandira chipewa cha ulemerero chosafota.
and when the Chief Shepherd shall appear, you shall receive the crown of glory which fades not away.
5 Momwemonso, inu anyamata gonjerani amene ndi akulu. Inu nonse mukhale odzichepetsa kuti mutumikirane, chifukwa, “Mulungu amatsutsana nawo odzikuza, koma amapereka chisomo kwa odzichepetsa.”
For the like reason, you younger persons subject yourselves to the seniors. Yes, all be subject to one another, and be clothed with humility, for God resists the proud but gives favor to the humble.
6 Choncho, mudzichepetse pamaso pa Mulungu wamphamvu, kuti pa nthawi yake adzakukwezeni.
Be humbled, therefore, under the mighty hand of God, that he may exalt you in due time.
7 Tayani pa Iye nkhawa zanu zonse chifukwa ndiye amakusamalani.
Cast all your anxious care on him, because he cares for you.
8 Khalani odziretsa ndi atcheru. Mdani wanu mdierekezi amayendayenda monga mkango wobangula kufunafuna wina kuti amumeze.
Be sober, be vigilant: your adversary, the devil, is walking about as a roaring lion, seeking whom he may devour:
9 Mukaneni iye, ndipo mukhazikike mʼchikhulupiriro, chifukwa mukudziwa kuti abale anzanu pa dziko lonse lapansi nawonso akumva zowawa zomwezi.
whom resist, steadfast in the faith, knowing that the very same sufferings are accomplished in your brethren, who are in the world.
10 Ndipo Mulungu wachisomo chonse, amene anakuyitanani ku ulemerero wake wamuyaya mwa Khristu, mutamva zowawa pa kanthawi, adzakukonzaninso ndi kukulimbitsani pa maziko olimba. (aiōnios g166)
And may the God of all favor, who has called us to his eternal glory, by Christ Jesus, after you have suffered a little, himself make you complete; support, strengthen, establish you: (aiōnios g166)
11 Kwa Iye kukhale mphamvu mpaka muyaya, Ameni. (aiōn g165)
to him be the glory and dominion for ever and ever. Amen. (aiōn g165)
12 Mothandizidwa ndi Sila, amene ndi mʼbale wokhulupirika, ndakulemberani mwachidule kukulimbikitsani ndi kuchita umboni kuti ichi ndi chisomo choona cha Mulungu.
By Sylvanus, a faithful brother, (as I conclude, ) I have written to you in in few words, exhorting you, and strongly testifying that this is the true favor of God, in which you stand.
13 Imani mwamphamvu mʼchisomochi. Mlongo wanu amene ali ku Babuloni, wosankhidwa pamodzi nanu akupereka moni, nayenso Marko, mwana wanga, akupereka moni.
They at Babylon, elected jointly with you, and Mark, my son, salute you.
14 Mupatsane moni ndi mpsopsono wachikondi. Mtendere ukhale ndi inu nonse amene muli mwa Khristu.
Salute one another with a kiss of love. Peace to you all, who are in Christ Jesus.

< 1 Petro 5 >