< 1 Petro 5 >
1 Ine ndikupempha akulu a mpingo amene ali pakati panu, monga inenso mkulu mnzawo, mboni ya zowawa za Khristu ndiponso amene ndidzalandira nawo ulemerero umene uti udzaonetsedwe.
De Ældste iblandt eder formaner jeg som Medældste og Vidne til Kristi Lidelser, som den, der ogsaa har Del i Herligheden, der skal aabenbares:
2 Wetani gulu la Mulungu limene lili mʼmanja mwanu, muziliyangʼanira. Muzichita osati mowumirizidwa, koma mwakufuna kwanu, monga momwe Mulungu akufunira kuti mutero. Musachite chifukwa chadyera la ndalama, koma ndi mtima ofuna kutumikira.
Vogter Guds Hjord hos eder, og fører Tilsyn med den, ikke tvungne, men frivilligt, ikke for slet Vindings Skyld, men med Redebonhed;
3 Musakhale ngati mafumu pa amene mukuwayangʼanira, koma mukhale chitsanzo kwa gululo.
ikke heller som de, der ville herske over Menighederne, men som Mønstre for Hjorden;
4 Ndipo Mʼbusa wamkulu akadzaonekera, mudzalandira chipewa cha ulemerero chosafota.
og naar da Overhyrden aabenbares, skulle I faa Herlighedens uvisnelige Krans.
5 Momwemonso, inu anyamata gonjerani amene ndi akulu. Inu nonse mukhale odzichepetsa kuti mutumikirane, chifukwa, “Mulungu amatsutsana nawo odzikuza, koma amapereka chisomo kwa odzichepetsa.”
Ligesaa, I unge! underordner eder under de ældre; og ifører eder alle Ydmyghed imod hverandre; thi „Gud staar de hoffærdige imod, men de ydmyge giver han Naade.‟
6 Choncho, mudzichepetse pamaso pa Mulungu wamphamvu, kuti pa nthawi yake adzakukwezeni.
Derfor ydmyger eder under Guds vældige Haand, for at han i sin Tid maa ophøje eder.
7 Tayani pa Iye nkhawa zanu zonse chifukwa ndiye amakusamalani.
Kaster al eders Sorg paa ham, thi han har Omsorg for eder.
8 Khalani odziretsa ndi atcheru. Mdani wanu mdierekezi amayendayenda monga mkango wobangula kufunafuna wina kuti amumeze.
Værer ædrue, vaager; eders Modstander, Djævelen, gaar omkring som en brølende Løve, søgende, hvem han kan opsluge.
9 Mukaneni iye, ndipo mukhazikike mʼchikhulupiriro, chifukwa mukudziwa kuti abale anzanu pa dziko lonse lapansi nawonso akumva zowawa zomwezi.
Staar ham imod, faste i Troen, vidende, at de samme Lidelser fuldbyrdes paa eders Brødre i Verden.
10 Ndipo Mulungu wachisomo chonse, amene anakuyitanani ku ulemerero wake wamuyaya mwa Khristu, mutamva zowawa pa kanthawi, adzakukonzaninso ndi kukulimbitsani pa maziko olimba. (aiōnios )
Men al Naades Gud, som kaldte eder til sin evige Herlighed i Kristus Jesus efter en kort Tids Lidelse, han vil selv fuldelig berede eder, styrke, bekræfte, grundfæste eder! (aiōnios )
11 Kwa Iye kukhale mphamvu mpaka muyaya, Ameni. (aiōn )
Ham tilhører Magten i Evighedernes Evigheder! Amen. (aiōn )
12 Mothandizidwa ndi Sila, amene ndi mʼbale wokhulupirika, ndakulemberani mwachidule kukulimbikitsani ndi kuchita umboni kuti ichi ndi chisomo choona cha Mulungu.
Med Silvanus, den trofaste Broder (thi det holder jeg ham for), har jeg i Korthed skrevet eder til for at formane og bevidne, at dette er Guds sande Naade, hvori I staa.
13 Imani mwamphamvu mʼchisomochi. Mlongo wanu amene ali ku Babuloni, wosankhidwa pamodzi nanu akupereka moni, nayenso Marko, mwana wanga, akupereka moni.
Den medudvalgte i Babylon og min Søn, Markus, hilser eder.
14 Mupatsane moni ndi mpsopsono wachikondi. Mtendere ukhale ndi inu nonse amene muli mwa Khristu.
Hilser hverandre med Kærligheds Kys! Fred være med eder alle, som ere i Kristus!