< 1 Petro 4 >
1 Popeza kuti Khristu anamva zowawa mʼthupi lake, mukhale nawonso mtima omwewo, chifukwa iye amene wamva zowawa mʼthupi lake walekana nawo uchimo.
Njengoba uKristu wasihluphekela enyameni, hlomani lani ngengqondo efananayo, ngoba ohlupheke enyameni, useyekele isono,
2 Chifukwa cha ichi, iwo sakhalanso moyo wawo akuchita zofuna za matupi awo, koma amachita chifuniro cha Mulungu.
ukuze isikhathi esiseleyo enyameni lingabe lisaphilela inkanuko zabantu, kodwa intando kaNkulunkulu.
3 Pakuti mwataya kale nthawi yambiri mʼmbuyomu pochita zimene anthu osapembedza amachita, moyo wokhumba zonyansa, zilakolako zoyipa kuledzera, zochitika zoyipa za pa phwando, mapokoso ndi kupembedza mafano onyansa.
Ngoba kwanele kithi ukuthi isikhathi sempilo esedlulileyo siqhube intando yabezizwe, lapho sasihamba emanyaleni, ezinkanukweni, ekudakweni, ekuminzeni, ekunatheni, lekukhonzeni izithombe okuyangisayo;
4 Anthu osapembedza amadabwa pamene simuthamangira nawo kuchita zoyipitsitsazi, nʼchifukwa chake amakuchitani chipongwe.
abamangala kukho, nxa lingagijimi ndawonye kulokhukuthululeka kwamanyala, belihlambaza;
5 Koma adzafotokoza okha mlandu wawo kwa Mulungu amene wakonzeka kuweruza amoyo ndi akufa.
abazaziphendulela kulowo olungele ukwahlulela abaphilayo labafileyo.
6 Pa chifukwa chimenechi, Uthenga Wabwino unalalikidwa ngakhale kwa iwo amene tsopano ndi akufa, kuti adzaweruzidwe monga anthu ku thupi, koma adzakhale ndi moyo monga mwa Mulungu mu mzimu.
Ngoba ngenxa yalokhu ivangeli latshunyayelwa lakwabafileyo, ukuze bahlulelwe ngokwabantu enyameni, kodwa baphile ngokukaNkulunkulu emoyeni.
7 Chimaliziro cha zinthu zonse chili pafupi. Choncho khalani maso ndi odziletsa kuti muthe kupemphera.
Kodwa ukuphela kwezinto zonke sekusondele; ngakho qondani lilinde lisemikhulekweni;
8 Koposa zonse muzikondana wina ndi mnzake kwambiri, chifukwa chikondi chimaphimba machimo ambiri.
kodwa phambi kwakho konke banini lothando oluvuthayo omunye komunye, ngoba uthando luzasibekela inkithinkithi yezono;
9 Muzisamalirana wina ndi mnzake osamanyinyirika.
phathanani kuhle ekwethekelaneni, ngaphandle kokusola;
10 Aliyense agwiritse ntchito mokhulupirika mphatso iliyonse imene anayilandira potumikira ena ngati adindo ogwiritsa bwino ntchito mphatso za Mulungu za mitundumitundu.
ngulowo lalowo njengesiphiwo asemukeleyo, kasisebenze omunye komunye, njengabaphathi abalungileyo bomusa kaNkulunkulu ozinhlobonhlobo;
11 Ngati wina ayankhula, ayankhuledi mawu enieni a Mulungu. Ngati wina atumikira, atumikire ndi mphamvu imene Mulungu amapereka, kuti pa zonse Mulungu alemekezedwe mwa Yesu Khristu. Kwa Iye kukhale ulemerero ndi mphamvu mpaka muyaya, Ameni. (aiōn )
uba umuntu ekhuluma, kakhulume njengamazwi kaNkulunkulu; uba umuntu esebenza, kasebenze njengokuvela emandleni uNkulunkulu awanikayo; ukuze uNkulunkulu adunyiswe kuzo zonke izinto ngoJesu Kristu, okukuye ubukhosi lamandla kuze kube nini lanini. Ameni. (aiōn )
12 Abale okondedwa musadabwe ndi mayesero owawa amene mukukumana nawo ngati kuti china chake chachilendo chakuchitikirani.
Bathandekayo, lingamangali ngesilingo esitshisayo esiphezu kwenu esilihlolayo, ngokungathi lehlelwe yinto engaziwayo;
13 Koma kondwerani popeza mukumva zowawa pamodzi ndi Khristu, kuti mudzakondwere kwakukulu pamene ulemerero wake udzaonekera.
kodwa njengoba lihlanganyela inhlupheko zikaKristu, thokozani, ukuze kuthi lekwembulweni kwenkazimulo yakhe lithokoze lijabule kakhulu.
14 Ngati akuchitani chipongwe chifukwa cha dzina la Khristu, ndinu odala, ndiye kuti Mzimu waulemerero wa Mulungu uli pa inu.
Uba lithukwa ngenxa yebizo likaKristu, libusisiwe; ngoba uMoya wenkazimulo lokaNkulunkulu uhlezi phezu kwenu; ngabo-ke uyathukwa, kodwa ngani uyadunyiswa.
15 Ngati mumva zowawa, zisakhale chifukwa cha kupha munthu, kapena kuba, kapena kuchita choyipa, kapena kulowerera za anthu ena,
Kodwa kakungabi khona owakini ohlupheka njengombulali, loba isela, loba umenzi wokubi, loba njengozigaxa endabeni zabanye;
16 koma ngati mumva zowawa chifukwa ndinu Mkhristu, musachite manyazi, koma muyamike Mulungu chifukwa cha dzinalo.
kodwa uba ehlupheka njengomKristu, kangabi lanhloni, kodwa kadumise uNkulunkulu ngenxa yalokhu.
17 Pakuti nthawi yafika kuti chiweruzo chiyambe mʼnyumba ya Mulungu, ndipo ngati chiyamba ndi ife nanga podzafika kwa osamvera Uthenga Wabwino wa Mulungu, chidzakhala chotani?
Ngoba sekuyisikhathi sokuthi ukwahlulela kuqale endlini kaNkulunkulu; njalo uba kuqala kithi, kuzakuba yini ukuphela kwalabo abangalalelanga ivangeli likaNkulunkulu?
18 Monga Malemba akuti, “Ngati kuli kovuta kuti olungama apulumuke, nanga munthu wochimwa, wosasamala za Mulungu adzatani?”
Uba-ke olungileyo esindiswa ngobulukhuni, oweyisa uNkulunkulu lesoni uzabonakala ngaphi?
19 Nʼchifukwa chake, iwo amene akumva zowawa monga mwa chifuniro cha Mulungu, adzipereke okha mʼmanja mwa Mlengi wawo wokhulupirika ndi kumapitiriza kuchita zabwino.
Ngakho-ke labo abahluphekayo ngokwentando kaNkulunkulu, njengakuMdali othembekileyo kabanikele eyabo imiphefumulo ekwenzeni okuhle.