< 1 Petro 4 >

1 Popeza kuti Khristu anamva zowawa mʼthupi lake, mukhale nawonso mtima omwewo, chifukwa iye amene wamva zowawa mʼthupi lake walekana nawo uchimo.
Ainsi donc, puisque Christ a souffert pour nous dans la chair, armez-vous aussi du même esprit; car celui qui a souffert dans la chair a cessé de pécher,
2 Chifukwa cha ichi, iwo sakhalanso moyo wawo akuchita zofuna za matupi awo, koma amachita chifuniro cha Mulungu.
afin que vous ne viviez plus le reste de votre temps dans la chair selon les convoitises des hommes, mais selon la volonté de Dieu.
3 Pakuti mwataya kale nthawi yambiri mʼmbuyomu pochita zimene anthu osapembedza amachita, moyo wokhumba zonyansa, zilakolako zoyipa kuledzera, zochitika zoyipa za pa phwando, mapokoso ndi kupembedza mafano onyansa.
Car nous avons assez passé notre temps à satisfaire les désirs des païens, et à marcher dans l'impudicité, les convoitises, les ivrogneries, les orgies, les carrousels, et les idolâtries abominables.
4 Anthu osapembedza amadabwa pamene simuthamangira nawo kuchita zoyipitsitsazi, nʼchifukwa chake amakuchitani chipongwe.
Ils trouvent étrange que vous ne couriez pas avec eux dans les mêmes excès d'émeute, et ils parlent mal de vous.
5 Koma adzafotokoza okha mlandu wawo kwa Mulungu amene wakonzeka kuweruza amoyo ndi akufa.
Ils rendront compte à celui qui est prêt à juger les vivants et les morts.
6 Pa chifukwa chimenechi, Uthenga Wabwino unalalikidwa ngakhale kwa iwo amene tsopano ndi akufa, kuti adzaweruzidwe monga anthu ku thupi, koma adzakhale ndi moyo monga mwa Mulungu mu mzimu.
Car c'est dans ce but que la Bonne Nouvelle a été annoncée même aux morts, afin qu'ils soient jugés comme des hommes dans la chair, mais qu'ils vivent comme devant Dieu dans l'esprit.
7 Chimaliziro cha zinthu zonse chili pafupi. Choncho khalani maso ndi odziletsa kuti muthe kupemphera.
Mais la fin de toutes choses est proche. C'est pourquoi, soyez sains d'esprit, maîtres de vous-mêmes, et sobres dans la prière.
8 Koposa zonse muzikondana wina ndi mnzake kwambiri, chifukwa chikondi chimaphimba machimo ambiri.
Et surtout, soyez sérieux dans votre amour entre vous, car l'amour couvre une multitude de péchés.
9 Muzisamalirana wina ndi mnzake osamanyinyirika.
Soyez accueillants les uns envers les autres, sans vous plaindre.
10 Aliyense agwiritse ntchito mokhulupirika mphatso iliyonse imene anayilandira potumikira ena ngati adindo ogwiritsa bwino ntchito mphatso za Mulungu za mitundumitundu.
Comme chacun a reçu un don, employez-vous à vous servir les uns les autres, comme de bons gestionnaires de la grâce de Dieu sous ses diverses formes.
11 Ngati wina ayankhula, ayankhuledi mawu enieni a Mulungu. Ngati wina atumikira, atumikire ndi mphamvu imene Mulungu amapereka, kuti pa zonse Mulungu alemekezedwe mwa Yesu Khristu. Kwa Iye kukhale ulemerero ndi mphamvu mpaka muyaya, Ameni. (aiōn g165)
Si quelqu'un parle, que ce soit comme si c'était les paroles mêmes de Dieu. Si quelqu'un sert, que ce soit avec la force que Dieu fournit, afin qu'en toutes choses Dieu soit glorifié par Jésus-Christ, à qui appartiennent la gloire et la domination dans les siècles des siècles. Amen. (aiōn g165)
12 Abale okondedwa musadabwe ndi mayesero owawa amene mukukumana nawo ngati kuti china chake chachilendo chakuchitikirani.
Bien-aimés, ne vous étonnez pas de l'épreuve ardente qui vous a été imposée pour vous éprouver, comme si une chose étrange vous arrivait.
13 Koma kondwerani popeza mukumva zowawa pamodzi ndi Khristu, kuti mudzakondwere kwakukulu pamene ulemerero wake udzaonekera.
Mais parce que vous participez aux souffrances de Christ, réjouissez-vous, afin qu'à la révélation de sa gloire vous vous réjouissiez aussi d'une joie extrême.
14 Ngati akuchitani chipongwe chifukwa cha dzina la Khristu, ndinu odala, ndiye kuti Mzimu waulemerero wa Mulungu uli pa inu.
Si l'on vous insulte pour le nom du Christ, vous êtes heureux, car l'Esprit de gloire et de Dieu repose sur vous. De leur côté, il est blasphémé, mais de votre côté, il est glorifié.
15 Ngati mumva zowawa, zisakhale chifukwa cha kupha munthu, kapena kuba, kapena kuchita choyipa, kapena kulowerera za anthu ena,
Que nul de vous ne souffre comme meurtrier, ou voleur, ou malfaiteur, ou comme se mêlant des affaires des autres.
16 koma ngati mumva zowawa chifukwa ndinu Mkhristu, musachite manyazi, koma muyamike Mulungu chifukwa cha dzinalo.
Mais si l'un de vous souffre parce qu'il est chrétien, qu'il n'ait pas honte, mais qu'il glorifie Dieu à ce sujet.
17 Pakuti nthawi yafika kuti chiweruzo chiyambe mʼnyumba ya Mulungu, ndipo ngati chiyamba ndi ife nanga podzafika kwa osamvera Uthenga Wabwino wa Mulungu, chidzakhala chotani?
Car le temps est venu où le jugement doit commencer par la maison de Dieu. S'il commence d'abord par nous, qu'arrivera-t-il à ceux qui n'obéissent pas à la Bonne Nouvelle de Dieu?
18 Monga Malemba akuti, “Ngati kuli kovuta kuti olungama apulumuke, nanga munthu wochimwa, wosasamala za Mulungu adzatani?”
« S'il est difficile pour le juste d'être sauvé, qu'arrivera-t-il à l'impie et au pécheur? »
19 Nʼchifukwa chake, iwo amene akumva zowawa monga mwa chifuniro cha Mulungu, adzipereke okha mʼmanja mwa Mlengi wawo wokhulupirika ndi kumapitiriza kuchita zabwino.
Que ceux-là aussi qui souffrent selon la volonté de Dieu en faisant le bien lui confient leurs âmes, comme à un Créateur fidèle.

< 1 Petro 4 >