< 1 Petro 4 >

1 Popeza kuti Khristu anamva zowawa mʼthupi lake, mukhale nawonso mtima omwewo, chifukwa iye amene wamva zowawa mʼthupi lake walekana nawo uchimo.
Therefore of Christ having suffered in flesh for us, arm ye yourselves also with the same mentality, because he who has suffered in flesh has ceased from sin,
2 Chifukwa cha ichi, iwo sakhalanso moyo wawo akuchita zofuna za matupi awo, koma amachita chifuniro cha Mulungu.
in order to live the remaining time in flesh, no longer by lusts of men, but by the will of God.
3 Pakuti mwataya kale nthawi yambiri mʼmbuyomu pochita zimene anthu osapembedza amachita, moyo wokhumba zonyansa, zilakolako zoyipa kuledzera, zochitika zoyipa za pa phwando, mapokoso ndi kupembedza mafano onyansa.
For enough time of life has past for you to accomplish the will of the Gentiles, having gone in debaucheries, lusts, excesses of wine, revelings, drinking parties, and lawless idolatries.
4 Anthu osapembedza amadabwa pamene simuthamangira nawo kuchita zoyipitsitsazi, nʼchifukwa chake amakuchitani chipongwe.
During which they think it strange of you not running together into the same pouring out of debauchery, while they slander.
5 Koma adzafotokoza okha mlandu wawo kwa Mulungu amene wakonzeka kuweruza amoyo ndi akufa.
Men who will give back an accounting to him who fares readily to judge the living and the dead.
6 Pa chifukwa chimenechi, Uthenga Wabwino unalalikidwa ngakhale kwa iwo amene tsopano ndi akufa, kuti adzaweruzidwe monga anthu ku thupi, koma adzakhale ndi moyo monga mwa Mulungu mu mzimu.
For good news was preached even to the dead for this, so that they might indeed be judged according to men in flesh, but live according to God in spirit.
7 Chimaliziro cha zinthu zonse chili pafupi. Choncho khalani maso ndi odziletsa kuti muthe kupemphera.
But the end of all things has approached. Therefore be serious, and be sober for the prayers.
8 Koposa zonse muzikondana wina ndi mnzake kwambiri, chifukwa chikondi chimaphimba machimo ambiri.
And above all having fervent love for yourselves, because love will cover a multitude of sins,
9 Muzisamalirana wina ndi mnzake osamanyinyirika.
stranger-loving toward each other without complaints.
10 Aliyense agwiritse ntchito mokhulupirika mphatso iliyonse imene anayilandira potumikira ena ngati adindo ogwiritsa bwino ntchito mphatso za Mulungu za mitundumitundu.
As each has received a gift, serving it for yourselves, as good stewards of the manifold grace of God.
11 Ngati wina ayankhula, ayankhuledi mawu enieni a Mulungu. Ngati wina atumikira, atumikire ndi mphamvu imene Mulungu amapereka, kuti pa zonse Mulungu alemekezedwe mwa Yesu Khristu. Kwa Iye kukhale ulemerero ndi mphamvu mpaka muyaya, Ameni. (aiōn g165)
If any man speaks, as oracles of God. If any man serves, as of ability as God supplies. So that God may be glorified in all things through Jesus Christ, to whom is the glory and the dominion into the ages of the ages. Truly. (aiōn g165)
12 Abale okondedwa musadabwe ndi mayesero owawa amene mukukumana nawo ngati kuti china chake chachilendo chakuchitikirani.
Beloved, ye should not be surprised at the fieriness in you, which occurs for a trial to you, like a strange thing happening to you.
13 Koma kondwerani popeza mukumva zowawa pamodzi ndi Khristu, kuti mudzakondwere kwakukulu pamene ulemerero wake udzaonekera.
But rejoice in so far as ye are partakers in the sufferings of the Christ, so that also at the revealing of his glory ye may rejoice, having exceeding joy.
14 Ngati akuchitani chipongwe chifukwa cha dzina la Khristu, ndinu odala, ndiye kuti Mzimu waulemerero wa Mulungu uli pa inu.
Blessed are ye if ye are reviled for the name of Christ, because the Spirit of glory and of God rests upon you. From them he is indeed blasphemed, but from you he is glorified.
15 Ngati mumva zowawa, zisakhale chifukwa cha kupha munthu, kapena kuba, kapena kuchita choyipa, kapena kulowerera za anthu ena,
For let not any man of you suffer as a murderer, or a thief, or an evildoer, or as a busybody.
16 koma ngati mumva zowawa chifukwa ndinu Mkhristu, musachite manyazi, koma muyamike Mulungu chifukwa cha dzinalo.
But if as a Christian, let him not be ashamed, but let him glorify God in this regard.
17 Pakuti nthawi yafika kuti chiweruzo chiyambe mʼnyumba ya Mulungu, ndipo ngati chiyamba ndi ife nanga podzafika kwa osamvera Uthenga Wabwino wa Mulungu, chidzakhala chotani?
Because the time to begin judgment is from the house of God, and if first from us, what is the end of those who disobey the good news of God?
18 Monga Malemba akuti, “Ngati kuli kovuta kuti olungama apulumuke, nanga munthu wochimwa, wosasamala za Mulungu adzatani?”
And if the righteous man is scarcely saved, where will the irreverent and sinful man appear?
19 Nʼchifukwa chake, iwo amene akumva zowawa monga mwa chifuniro cha Mulungu, adzipereke okha mʼmanja mwa Mlengi wawo wokhulupirika ndi kumapitiriza kuchita zabwino.
Therefore also let those who suffer according to the will of God entrust their souls as to a faithful Creator by well-doing.

< 1 Petro 4 >