< 1 Mafumu 1 >

1 Mfumu Davide atakalamba sankamva kufunda ngakhale akamufunditsa mabulangeti.
Now king David was old, stricken in years; and they covered him with clothes, but he could not become warm.
2 Choncho nduna zake zinamuwuza kuti, “Tiloleni tifune namwali woti azikhala nanu ndi kumakusamalirani. Namwaliyo azigona pafupi nanu kuti mbuye wathu mfumu muzimva kufundira.”
Wherefore his servants said unto him, Let them seek out for my lord the king a young virgin, and let her stand before the king, and let her be an attendant on him; and let her lie in thy bosom, that my lord the king may become warm.
3 Kotero anafunafuna mʼdziko lonse la Israeli mtsikana wokongola ndipo anapeza Abisagi wa ku Sunemu, nabwera naye kwa mfumu.
So they sought for a fair maiden throughout all the territory of Israel; and they found Abishag the Shunammite, and brought her to the king.
4 Mtsikanayo anali wokongola kwambiri ndipo ankasamalira mfumu ndi kumayitumikira, koma mfumuyo sinakhale naye malo amodzi.
And the maiden was exceedingly fair; and she became an attendant on the king, and ministered to him; but the king knew her not.
5 Nthawi imeneyi Adoniya, mwana wa Hagiti, anayamba kudzitukumula ndipo anati, “Ndidzakhala mfumu ndine.” Choncho anadzikonzera galeta ndi akavalo, pamodzi ndi anthu 50 woti azithamanga patsogolo pake.
And Adoniyah the son of Chaggith exalted himself, saying, I shall be king: and he procured himself a chariot and horsemen, and fifty men who ran before him.
6 (Abambo ake sanalowererepo nʼkamodzi komwe ndipo sanafunsepo kuti, “Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?” Adoniyayo anali wokongola kwambiri ndipo anali wopondana ndi Abisalomu).
And his father had never grieved him in all his life by saying, Why hast thou done so? and he also was of a very goodly form; and his mother had born him after Abshalom.
7 Adoniya anagwirizana ndi Yowabu mwana wa Zeruya ndiponso Abiatara wansembe, ndipo iwowa anamuthandiza.
And he had conferences with Joab the son of Zeruyah, and with Ebyathar the priest: and they, following Adoniyah, helped him.
8 Koma Zadoki wansembe, Benaya mwana wa Yehoyada, mneneri Natani, Simei ndi Rei ndiponso asilikali amphamvu a Davide sanamutsate Adoniya uja.
But Zadok the priest, and Benayahu the son of Yehoyada', and Nathan the prophet, and Shim'i, and Re'i, and the mighty men that belonged to David, were not with Adoniyah.
9 Kenaka Adoniya anapereka nsembe za nkhosa ndi ngʼombe ndiponso ana angʼombe onenepa ku Mwala wa Zohereti kufupi ndi Eni Rogeli. Iye anayitana abale ake onse, ana aamuna a mfumu ndiponso akuluakulu onse a ku Yuda,
And Adoniyah slaughtered sheep and oxen and fatted cattle by the stone Zocheleth, which is by 'En-rogel; and he invited all his brothers the king's sons, and all the men of Judah the king's servants;
10 koma sanayitane mneneri Natani kapena Benaya kapenanso asilikali amphamvu a Davide ngakhalenso mʼbale wake Solomoni.
But Nathan the prophet, and Benayahu, and the mighty men, and Solomon his brother, he invited not.
11 Pamenepo Natani anafunsa Batiseba, amayi ake a Solomoni, kuti, “Kodi simunamve kuti Adoniya, mwana wa Hagiti, walowa ufumu popanda Davide mbuye wathu kudziwa?
And Nathan spoke unto Bath-sheba' the mother of Solomon, saying, Hast thou not heard that Adoniyah the son of Chaggith is become king, and [that] David our lord knoweth it not?
12 Tsopano ine ndikulangizeni inu mmene mungapulumutsire moyo wanu ndi moyo wa mwana wanu Solomoni.
And now come, let me, I pray thee, give thee counsel, that thou mayest save thy own life, and the life of thy son Solomon.
13 Pitani msanga kwa Mfumu Davide ndipo mukanene kuti, ‘Mbuye wanga mfumu, kodi simunalumbire kwa ine mdzakazi wanu kuti, ‘Ndithu mwana wako Solomoni ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwanga, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu?’ Nanga nʼchifukwa chiyani Adoniya walowa ufumu?’
Go and get thee in unto king David, and say unto him, Didst not thou, my lord, O king, swear unto thy hand-maid, saying, Assuredly, Solomon thy son shall reign after me, and only he shall sit upon my throne? why then is Adoniyah become king?
14 Pamene inu muzikayankhula ndi mfumu, ine ndidzalowa ndi kuchitira umboni mawu anuwo.”
And, lo, while thou shalt be yet speaking there with the king, I myself will come in after thee, and confirm thy words.
15 Choncho Batiseba anapita nakalowa ku chipinda kukaonana ndi mfumu imene inali itakalamba kwambiri, kumene Abisagi wa ku Sunemu uja ankayisamalira.
And Bath-sheba' went in unto the king into the chamber, and the king was very old; and Abishag the Shunammite was ministering unto the king.
16 Batiseba anagwada nalambira mfumu. Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi nʼchiyani chimene ukufuna?”
And Bath-sheba' bowed, and prostrated herself unto the king: and the king said, What wouldst thou?
17 Iye anayankha kuti, “Mbuye wanga, inu mwini munalumbira kwa ine mdzakazi wanu mʼdzina la Yehova Mulungu wanu kuti, ‘Solomoni mwana wako ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwa ine, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.’
And she said unto him, My lord, thou thyself didst swear by the Lord thy God unto thy hand-maid, Assuredly, Solomon thy son shall reign after me, and only he shall sit upon my throne.
18 Koma tsopano Adoniya ndiye walowa ufumu, ndipo inu mbuye wanga mfumu, simukuzidziwa zimenezi.
And now, behold, Adoniyah is become king; and now, my lord, O king, thou knowest it not:
19 Ndipo wapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndi nkhosa ndi mbuzi ndipo wayitana ana anu onse, wansembe Abiatara ndiponso Yowabu mkulu wa ankhondo, koma sanayitane kapolo wanu Solomoni.
And he hath slaughtered oxen and fatted cattle and sheep in abundance, and hath invited all the sons of the king, and Ebyathar the priest, and Joab the captain of the army; but Solomon thy servant hath he not invited.
20 Mbuye wanga mfumu, maso a Aisraeli onse ali pa inu, kuti adziwe kuchokera kwa inu amene adzakhala pa mpando waufumu wa mbuye wanga mʼmalo mwanu.
And as for thee, my lord, O king, the eyes of all Israel are upon thee, to tell them, who shall sit on the throne of my lord the king after him.
21 Mukapanda kutero, mbuye wanga, mukadzangotisiya nʼkulondola kumene kunapita makolo anu, ine pamodzi ndi mwana wangayu Solomoni adzatiyesa owukira.”
Otherwise it would come to pass, when my lord the king sleepeth with his fathers, that I and my son Solomon may be counted offenders.
22 Pamene Batiseba amayankhula ndi mfumu, mneneri Natani analowa.
And, lo, while she was yet speaking with the king, Nathan the prophet also came in.
23 Ndipo anthu anawuza mfumu kuti, “Kwabwera mneneri Natani.” Kotero iye anafika pamaso pa mfumu ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.
And they told the king, saying, Behold, here is Nathan the prophet: and when he was come in before the king, he prostrated himself before the king with his face to the ground.
24 Natani anafunsa kuti, “Mbuye wanga mfumu, kodi mwalengeza kuti Adoniya adzakhala mfumu mʼmalo mwanu, ndi kuti adzakhala pa mpando wanu waufumu?
And Nathan said, My lord, O king, hast thou then said, Adoniyah shall reign after me, and he shall sit upon my throne?
25 Lero lomwe lino wakapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndiponso nkhosa ndi mbuzi. Iye wayitana ana anu onse, atsogoleri a nkhondo, ndiponso wansembe Abiatara. Panopa onsewa akudya ndi kumwa naye ndipo akunena kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Adoniya!’
For he is gone down this day, and hath slaughtered oxen and fatted cattle and sheep in abundance, and hath invited all the king's sons, and the captains of the army, and Ebyathar the priest: and, behold, they are eating and drinking before him, and they say, Long live king Adoniyah.
26 Koma ine kapolo wanu, wansembe Zadoki ndi Benaya mwana wa Yehoyada, ndiponso kapolo wanu Solomoni sanatiyitane.
But as for me, me thy servant, and Zadok the priest, and Benayahu the son of Yehoyada', and thy servant Solomon, hath he not invited.
27 Kodi zimenezi mbuye wanga mfumu mwazichita ndinu, osawawuza atumiki anu kuti adziwe amene adzakhale pa mpando waufumu mʼmalo mwanu?”
Can it be that this hath been done by order of my lord the king, and thou hast not informed thy servant, who should sit on the throne of my lord the king after him?
28 Pamenepo mfumu Davide anati, “Muyitaneni Batiseba.” Kotero Batiseba analowa ndipo anayimirira pamaso pa mfumu.
Then answered king David, and said, Call me Bath-sheba'; and she came into the king's presence, and stood before the king.
29 Tsono mfumu inalumbira kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene anandipulumutsa ine ku mavuto onse,
And the king swore and said, As the Lord liveth, that hath redeemed my soul out of all distress,
30 ndithu ine lero ndichita zonse zimene ndinalumbira kwa Yehova Mulungu wa Israeli kuti, mwana wako Solomoni adzakhala mfumu mʼmalo mwanga ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.”
Even as I have sworn unto thee by the Lord the God of Israel, saying, Assuredly Solomon thy son shall reign after me, and only he shall sit upon my throne in my stead: even so will I certainly do this day.
31 Pamenepo Batiseba anawerama, nagunditsa mutu wake pansi nalambira mfumu, ndipo anati, “Mbuye wanga Mfumu Davide mukhale ndi moyo wautali!”
Then did Bath-sheba' bow herself with her face to the earth, and prostrate herself unto the king; and she said, May my lord, the king David, live for ever!
32 Mfumu Davide anati, “Ndiyitanireni wansembe Zadoki, mneneri Natani ndi Benaya mwana wa Yehoyada.” Atafika pamaso pa mfumu,
And king David said, Call unto me Zadok the priest, and Nathan the prophet, and Benayahu the son of Yehoyada'. And they came before the king.
33 mfumuyo inati kwa iwo, “Tengani atumiki anga ndipo mukweze mwana wanga Solomoni pa bulu wanga ndipo mupite naye ku Gihoni. Mukalize lipenga ndi kufuwula kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Solomoni!’
And the king said unto them, Take with you the servants of your lord, and cause Solomon my son to ride upon my own mule, and conduct him down to Gichon:
34 Kumeneko Zadoki wansembe ndi mneneri Natani akamudzoze kuti akhale mfumu ya Israeli. Kenaka mukalize lipenga ndi kumanena kuti ‘Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni.’
And let Zadok the priest with Nathan the prophet anoint him there as king over Israel; and blow ye with the cornet, and say, Long live king Solomon.
35 Ndipo pobwera muzikamutsata pambuyo. Iyeyo akabwere kuno ndi kudzakhala pa mpando wanga waufumu ndi kudzalamulira mʼmalo mwanga. Ndamusankha kukhala wolamulira Israeli ndi Yuda.”
Then shall ye go up after him, and he shall come and sit upon my throne; and he shall be king in my stead: and him have I ordained to be ruler over Israel and over Judah.
36 Benaya mwana wa Yehoyada anayankha mfumu kuti, “Ameni! Yehova Mulungu wa mbuye wanga mfumu akhazikitse kuti zichitike motero.
And Benayahu the son of Yehoyada' answered the king, and said, Amen: May thus say the Eternal the God of my lord the king.
37 Monga momwe Yehova wakhalira ndi inu mbuye wanga mfumu, momwemonso akhale ndi Solomoni ndi kukhazikitsa ufumu wake kuti ukhale waukulu kuposa ufumu wa mbuye wanga Mfumu Davide!”
As the Eternal hath been with my lord the king, even so may he be with Solomon, and may he make his throne greater than the throne of my lord the king David.
38 Kotero Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndiponso Apeleti, anthu oteteza mfumu, anapita kukamukweza Solomoni pa bulu wa Mfumu Davide ndi kupita naye ku Gihoni.
Thereupon Zadok the priest, and Nathan the prophet, and Benayahu the son of Yehoyada', and the Kerethites, and the Pelethites, went down, and caused Solomon to ride upon king David's mule, and conducted him to Gichon.
39 Wansembe Zadoki anatenga nyanga ya mafuta yochokera ku malo opatulika ndi kumudzoza Solomoni. Kenaka analiza lipenga ndipo anthu onse anafuwula kuti, “Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni!”
And Zadok the priest took the horn of oil out of the tabernacle, and anointed Solomon. And they blew with the cornet; and all the people said, Long live king Solomon.
40 Ndipo anthu onsewo anapita namutsatira pambuyo akuyimba zitoliro ndi kukondwerera kwambiri, kotero nthaka inagwedezeka chifukwa cha phokoso lawo.
And all the people went up after him, and the people blew on flutes, and rejoiced with great joy, so that the earth was rent at their noise.
41 Adoniya pamodzi ndi anthu onse oyitanidwa amene anali naye anamva zimenezi pamene ankamaliza madyerero awo. Atamva kulira kwa malipenga, Yowabu anafunsa kuti, “Kodi phokoso lonselo mu mzindamo likutanthauza chiyani?”
And Adoniyah and all the guests that were with him heard it as they had just finished eating: and when Joab heard the sound of the cornet, he said, Wherefore is this noise of the city in an uproar?
42 Iye akuyankhula, Yonatani mwana wa wansembe Abiatara anafika. Adoniya anati, “Lowa. Munthu wabwino ngati iwe ayenera kubweretsa nkhani yabwino.”
And while he was yet speaking, behold, Jonathan the son of Ebyathar the priest came in: and Adoniyah said [unto him], Come in; for thou art a worthy man, and must bring good tidings.
43 Yonatani anayankha Adoniya kuti, “Ayi ndithu, zinthu sizili bwino! Mbuye wathu Mfumu Davide walonga Solomoni ufumu.
And Jonathan answered and said to Adoniyah, Alas, no; our lord king David hath made Solomon king;
44 Mfumu yatuma Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndi Apeleti ku Gihoni ndipo iwo amukweza pa bulu wa mfumu,
And the king hath sent with him Zadok the priest, and Nathan the prophet, and Benayahu the son of Yehoyada', and the Kerethites, and the Pelethites, and they have caused him to ride upon the king's mule;
45 ndipo Zadoki wansembe ndi mneneri Natani adzoza Solomoni ku Gihoni kuti akhale mfumu. Ndipo kuchokera kumeneko akhala akululutira, kotero kuti mu mzinda monse muli phokoso lokhalokha. Ndiyetu phokoso limene mukulimvalo.
And Zadok the priest and Nathan the prophet have anointed him as king on the Gichon; and they are come up from there rejoicing, and the city hath been set in commotion. This is the noise that ye have heard.
46 Ndipo Solomoni wakhala kale pa mpando wake waufumu.
And Solomon hath also sat on the kingly throne.
47 Kuwonjezera pamenepo, nduna za mfumu zabwera kale kudzayamika mbuye wathu Mfumu Davide, pomanena kuti, ‘Mulungu wanu atchukitse dzina la Solomoni kuposa dzina lanu ndipo ufumu wake ukule kupambana ufumu wanu!’ Ndipo mfumu inawerama niyamba kupembedza pa bedi lake,
And also the king's servants are come to bless our lord king David, saying, May God make the name of Solomon more famous than thy name, and make his throne greater than thy throne: and the king hath bowed himself upon the bed.
48 inati, ‘Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, amene wasankha wolowa mʼmalo mwanga ine ndikanali ndi moyo lero lino.’”
And also thus hath the king said, Blessed be the Lord the God of Israel, who hath given [me] this day one who sitteth on my throne, while my eyes see it.
49 Anthu onse amene Adoniya anawayitana ananjenjemera ndi mantha, ndipo anayimirira, kenaka anamwazikana.
And all the guests that were with Adoniyah were terrified, and rose up, and went, every man, on his own way.
50 Koma Adoniya, poopa Solomoni, anapita ku Nyumba ya Mulungu nakagwira msonga za guwa lansembe.
And Adoniyah was afraid because of Solomon; and he arose, and went, and caught hold on the horns of the altar.
51 Tsono Solomoni anawuzidwa kuti, “Adoniya akukuopani inu Mfumu Solomoni ndipo wagwira msonga za guwa lansembe. Iye akuti, ‘Mfumu Solomoni alumbire kuti sadzapha kapolo wake ndi lupanga.’”
And it was told unto Solomon, saying, Behold, Adoniyah feareth king Solomon; and, behold, he hath caught hold on the horns of the altar, saying, Let king Solomon swear unto me today that he will not slay his servant with the sword.
52 Solomoni anayankha kuti, “Ngati iyeyo aonetse kuti ndi munthu wakhalidwe labwino, ngakhale tsitsi la mʼmutu mwake silidzathothoka ndi kugwera pansi, koma akapezeka kuti ali ndi khalidwe loyipa, adzafa ndithu.”
And Solomon said, If he will become a worthy man, there shall not a hair of his fall to the earth; but if any wrong shall be found on him, then shall he die.
53 Pamenepo Mfumu Solomoni inatuma anthu ndipo anakamutenga paguwa paja. Adoniya anabwera ndi kudzalambira Mfumu Solomoni, ndipo Solomoni anati, “Pita ku nyumba yako.”
So king Solomon sent, and they brought him down from the altar; and he came and bowed himself to king Solomon; and Solomon said unto him, Go to thy house.

< 1 Mafumu 1 >