< 1 Mafumu 8 >

1 Pamenepo Mfumu Solomoni inasonkhanitsa akuluakulu a Israeli, atsogoleri onse a mafuko ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli mu Yerusalemu, kuti akatenge Bokosi la Chipangano la Yehova ku Ziyoni, Mzinda wa Davide.
Ngakho iNkosi uSolomoni wamema abadala bako-Israyeli ukuthi beze kuye eJerusalema, bonke abazinhloko zezizwana lezinduna zezimuli zako-Israyeli, ukuthi balethe ibhokisi lesivumelwano sikaThixo lisuka eZiyoni, uMuzi kaDavida.
2 Aisraeli onse anasonkhana pamaso pa Mfumu Solomoni nthawi ya chikondwerero cha mwezi wa Etanimu, mwezi wachisanu ndi chiwiri.
Amadoda wonke ako-Israyeli eza ndawonye enkosini uSolomoni ngesikhathi somkhosi ngenyanga ebizwa ngokuthi ngu-Ethanimi, inyanga yesikhombisa.
3 Akuluakulu onse a Israeli atafika, ansembe ananyamula Bokosi la Chipangano,
Kwathi bonke abadala bako-Israyeli sebefikile, abaphristi bathwala ibhokisi lesivumelwano,
4 ndipo anabwera nalo Bokosi la Yehova pamodzi ndi tenti ya msonkhano ndi ziwiya zonse zopatulika zimene zinali mʼmenemo. Ansembe ndi Alevi ndiye anazinyamula,
njalo basebeletha ibhokisi lesivumelwano sikaThixo kanye leThente lokuHlanganela layo yonke imiceciso engcwele iphakathi kwalo. Abaphristi labaLevi bakuthwala lokhu,
5 ndipo Mfumu Solomoni ndi gulu lonse la Aisraeli amene anasonkhana naye anali patsogolo pa Bokosi la Chipangano, akupereka nsembe nkhosa zambiri ndi ngʼombe zambiri zosawerengeka.
njalo inkosi uSolomoni kanye lebandla lonke lako-Israyeli babebuthene ndawonye phambi kwebhokisi lesivumelwano, benikela ngezimvu langenkomo ababengeke bakwazi ukuloba inani lazo loba ukuzibala.
6 Ansembe anafika nalo Bokosi la Chipangano la Yehova mʼchipinda chamʼkati mwenimweni, Malo Opatulika Kwambiri, ndipo analiyika pansi pa mapiko a akerubi.
Abaphristi basebeletha ibhokisi lesivumelwano sikaThixo endaweni yalo engcwele engaphakathi kwethempeli, iNdawo eNgcwelengcwele, basebelifaka ngaphansi kwamaphiko amakherubhi.
7 Akerubiwo anatambalitsa mapiko awo pamwamba pa Bokosi la Chipangano ndipo anaphimba bokosilo pamodzi ndi mitengo yonyamulira.
Amakherubhi elula impiko zawo phezu kwendawo yebhokisi lesivumelwano njalo agubuzela ibhokisi lesivumelwano kanye lezibambo zokulithwala.
8 Mitengoyi inali yayitali kwambiri ndipo inkaonekera kunja kwa chipinda chamʼkati cha Malo Opatulika koma osati kunja kwa Malo Opatulikawo; ndipo mitengoyi ilipo mpaka lero lino.
Izigodo lezi zazizinde zibonakala nxa useNdaweni eNgcwele phambi kwesiphephelo esingaphakathi, kodwa hatshi nxa ungaphandle kweNdawo eNgcwele; lezo zilokhu zimi njalo lalamuhla.
9 Mʼbokosimo munalibe kanthu kena kalikonse kupatula miyala iwiri imene Mose anayikamo ku Horebu, kumene Yehova anachita pangano ndi Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
Kwakungelalutho ebhokisini lesivumelwano ngaphandle kwezibhebhedu ezimbili zamatshe uMosi ayezifake phakathi kwalo eseHorebhi lapho uThixo enza khona isivumelwano labako-Israyeli ngemva kokuphuma kwabo eGibhithe.
10 Ansembe atatuluka mʼMalo Opatulikawo, mtambo unadzaza Nyumba ya Yehova.
Kwathi abaphristi sebesukile eNdaweni eNgcwele, iyezi lagcwala lagubuzela ethempelini likaThixo.
11 Ndipo ansembewo sanathe kugwira ntchito yawo chifukwa cha mtambowo, pakuti ulemerero wa Yehova unadzaza mʼNyumba ya Yehova.
Abaphristi abenzanga inkonzo yabo ngenxa yeyezi, ngoba inkazimulo kaThixo yayigcwele ethempelini lakhe.
12 Pamenepo Solomoni anati, “Yehova anati adzakhala mʼmitambo yakuda;
Ngakho uSolomoni wathi, “UThixo utshilo ukuba uzahlala eyezini elimnyama;
13 taonani ndithu, ine ndakumangirani Nyumba yokongola kwambiri, malo woti muzikhalamo mpaka muyaya.”
ngempela sengikwakhele ithempeli elibukekayo, indawo ozahlala kiyo kuze kube nini lanini.”
14 Aisraeli onse ali chiyimire pomwepo, mfumu inatembenuka ndi kuwadalitsa.
Kwathi ibandla lonke lako-Israyeli lisemi khonapho, inkosi yaphenduka yalibusisa.
15 Ndipo inati: “Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, amene wachita ndi dzanja lake zimene analonjeza ndi pakamwa pake kwa Davide abambo anga. Pakuti Iye anati,
Ngakho yasisithi: “Udumo kuye uThixo, uNkulunkulu ka-Israyeli, yena ngesandla sakhe ophelelise ukwenza lokho akuthembisa ngowakhe umlomo ethembisa ubaba uDavida. Ngoba wathi,
16 ‘Kuyambira tsiku limene ndinatulutsa anthu anga Aisraeli ku Igupto, sindinasankhe mzinda wina uliwonse pa fuko lina lililonse la Aisraeli kuti kumeneko andimangire Nyumba, koma ndasankha Davide kuti alamulire anthu anga Aisraeli.’
‘Kusukela mhla ngikhupha abantu bami abako-Israyeli eGibhithe, bengingakaze ngikhethe idolobho loba kukusiphi isizwana sako-Israyeli ukuthi ngakhelwe ithempeli leBizo lami khona, kodwa ngimkhethile uDavida ukuthi abuse abantu bami bako-Israyeli.’
17 “Abambo anga Davide anali ndi maganizo mu mtima mwawo oti amangire nyumba Yehova, Mulungu wa Israeli.
Ubaba uDavida wayelakho enhliziyweni yakhe ukuthi akhe ithempeli leBizo likaThixo, uNkulunkulu ka-Israyeli.
18 Koma Yehova ananena kwa abambo anga, Davide, kuti, ‘Popeza zinali mu mtima mwako kumangira nyumba Dzina langa, unachita bwino kukhala ndi maganizo amenewa mu mtima mwakomo.
Kodwa uThixo wathi kubaba uDavida, ‘Wenza kuhle ngokuba lesifiso sokungakhela ithempeli leBizo lami enhliziyweni yakho.
19 Komatu, si iwe amene udzamanga Nyumba ya Mulungu, koma mwana wako, mwana amene iwe udzabereke. Iyeyo ndiye adzandimangire Nyumba.’
Lanxa kunjalo, kakusuwe ozalakha lelothempeli, kodwa lizakwakhiwa yindodana yakho, eyinyama legazi lakho, yiyo ezakwakha ithempeli leBizo lami.’
20 “Yehova wasunga zimene analonjeza: ine ndalowa mʼmalo mwa abambo anga Davide ndipo tsopano ndili pa mpando waufumu wa Israeli, monga momwe Yehova analonjezera, ndipo ndamangira nyumba Dzina la Yehova, Mulungu wa Israeli.
UThixo usigcinile isithembiso asenzayo: Sengiyinkosi esikhundleni sikababa uDavida njalo khathesi sengihlezi esihlalweni sobukhosi sika-Israyeli njengokuthembisa kukaThixo, njalo sengakhele iBizo likaThixo, uNkulunkulu ka-Israyeli ithempeli.
21 Ndalikonzera malo Bokosi la Chipangano mmene muli pangano la Yehova limene anapangana ndi makolo athu pamene anawatulutsa mʼdziko la Igupto.”
Ngilungisile indawo khonaphana eyebhokisi lesivumelwano, kulapho okulesivumelwano sikaThixo asenza labokhokho ekubakhupheni kwakhe kwelamaGibhithe.”
22 Pamenepo Solomoni anayimirira patsogolo pa guwa lansembe la Yehova pamaso pa gulu lonse la Aisraeli ndipo anakweza manja ake kumwamba,
Ngalokho uSolomoni wema e-alithareni likaThixo phambi kwebandla lonke lako-Israyeli, welula izandla zakhe waziphakamisela ezulwini
23 nati: “Inu Yehova, Mulungu wa Israeli, palibe Mulungu wofanana nanu kumwamba kapena pansi pa dziko, inu amene mumasunga pangano ndi kuonetsa chikondi chosasinthika kwa atumiki anu amene amayenda pamaso panu ndi mtima wawo wonse.
wasesithi: Oh “Thixo, Nkulunkulu ka-Israyeli, kakho uNkulunkulu onjengawe ezulwini phezulu loba emhlabeni ngaphansi, wena ogcina isivumelwano sakho sothando lezinceku zakho, wena oqhubeka ngenhliziyo yonke endleleni yakho.
24 Inu mwasunga lonjezo lanu kwa abambo anga Davide, mtumiki wanu. Inde zimene munalonjeza ndi pakamwa panu, mwazikwaniritsa ndi manja anu, monga mmene tikuonera lero lino.
Usigcinile isithembiso sakho encekwini yakho uDavida ongubaba; ngomlomo wakho uthembisile njalo ngesandla sakho ukugcwalisile lokho njengoba kunjalo lamuhla.
25 “Ndipo tsopano, Inu Yehova Mulungu wa Israeli, sungani zimene munalonjeza kwa abambo anga Davide, mtumiki wanu, pamene munati, ‘Sudzasowa munthu wokhala pamaso panga pa mpando waufumu wa Israeli, ngati ana ako adzasamalira mayendedwe awo mokhulupirika monga iwe wachitira.’
Khathesi Thixo, Nkulunkulu ka-Israyeli, gcinela inceku yakho uDavida ubaba lezozithembiso owazenzayo lapho wathi, ‘Awuyikwehluleka loba sekutheni ukuzuza indoda ezahlala esihlalweni sami sobukhosi ko-Israyeli, nxa amadodana akho ezananzelela ukuhamba phambi kwami njengalokhu okwenzileyo wena.’
26 Ndipo tsopano, Inu Mulungu wa Israeli, lolani kuti mawu anu akwaniritsidwe amene munalonjeza mtumiki wanu Davide abambo anga.
Ngakho khathesi, Nkulunkulu ka-Israyeli, kaligcwaliseke ilizwi lesithembiso owalikhuluma kubaba uDavida inceku yakho.
27 “Kodi Mulungu angakhaledi pa dziko lapansi? Mlengalenga ngakhale kumwamba kwenikweni, sikungakukwaneni. Nanga kuli bwanji ndi Nyumba iyi imene ndamanga!
Kambe uNkulunkulu uzahlala emhlabeni na? Amazulu, kanye lezulu eliphakemeyo, alikulingani. Pho ithempeli leli engilakhileyo lingabe liyini kuwe na!
28 Koma Inu Yehova Mulungu wanga, imvani pemphero ndi pembedzero la mtumiki wanu. Imvani kulira ndi pemphero la mtumiki wanu limene ndikupempha pamaso panu lero lino.
Kodwa-ke akuzwe umkhuleko wenceku yakho lokucela kwayo umusa, Oh Thixo Nkulunkulu wami. Zwana ukukhala lokukhuleka kwenceku yakho phambi kwakho ngalolusuku.
29 Maso anu azikhala otsekuka kuyangʼana Nyumba ino usiku ndi usana, malo ano amene Inu munanena kuti, ‘Dzina langa lidzakhala mʼmenemo,’ choncho imvani pemphero limene mtumiki wanu akupemphera akuyangʼana malo ano.
Sengathi amehlo akho angahlala phezu kwalelithempeli ebusuku lemini, yonale indawo owathi wena, ‘IBizo lami lizakuba khonapha,’ ukuze uzwe umkhuleko wenceku yakho ngale indawo.
30 Imvani pembedzero la mtumiki wanu ndi la anthu anu Aisraeli pamene akupemphera akuyangʼana malo ano. Imvani kumwambako, malo anu amene mumakhala; ndipo mukamva muzitikhululukira.
Zwana isikhalazo senceku yakho lesabantu bakho bako-Israyeli nxa bekhuleka bekhangele kule indawo. Zwana usezulwini okuyindawo yakho yokuhlala, njalo nxa usizwa, uthethelele.
31 “Munthu akalakwira mnzake, nawuzidwa kuti alumbire, akabwera kudzalumbira patsogolo pa guwa lansembe la Nyumba ino,
Nxa umuntu angonela umakhelwane wakhe, afungiswe, abesefunga isifungo phambi kwe-alithari lakho kulelithempeli,
32 imvani kumwambako ndi kuchitapo kanthu. Weruzani atumiki anuwo, wochimwa mugamule kuti ndi wolakwa ndipo alangidwe chifukwa cha zimene wachita. Wosachimwa mugamule kuti ndi wosalakwa, ndipo muonetse kusalakwa kwakeko.
zwana usezulwini wenze. Yahlulela phakathi kwezinceku zakho, umlahle olecala, wehlisele ekhanda lakhe lokho akwenzileyo. Tshono ukuthi ongonanga kalacala ukuze uveze ukuba msulwa kwakhe.
33 “Anthu anu Aisraeli akagonja kwa adani awo chifukwa akuchimwirani, ndipo akatembenukira kwa Inu ndi kuvomereza Dzina lanu, kupemphera ndi kupembedzera kwa Inu mʼNyumba ino,
Nxa abantu bakho abako-Israyeli behlulwe yisitha ngenxa yokona kwabo phambi kwakho, kuthi nxa sebephendukela ngakuwe bebiza ibizo lakho, bekhuleka njalo becela intethelelo kuwe kulelithempeli,
34 pamenepo imvani kumwambako ndi kukhululukira tchimo la anthu anu Aisraeli ndi kuwabweretsa ku dziko limene munawapatsa makolo awo.
lapho-ke zwana usezulwini uthethelele izono zabantu bakho bako-Israyeli njalo ubabuyisele elizweni owalinika okhokho babo.
35 “Pamene kumwamba kwatsekeka ndipo mvula sikugwa chifukwa anthu anu akuchimwirani, ndipo pamene apemphera akuyangʼana malo ano ndi kuvomereza Dzina lanu, ndi kutembenuka kuchoka ku machimo awo chifukwa inu mwawalanga,
Nxa amazulu evaleka njalo kungaselazulu ngenxa yokuthi abantu bakho bonile phambi kwakho, njalo nxa bekhuleka bekhangele kule indawo bavume ibizo lakho batshiye izono zabo ngoba ubatshayile,
36 pamenepo imvani kumwambako ndipo muwakhululukire atumiki anu, anthu anu Aisraeli. Aphunzitseni makhalidwe oyenera ndipo gwetsani mvula mʼdziko limene munapereka kwa anthu anu monga cholowa chawo.
lapho-ke zwana usezulwini uthethelele izinceku zakho izono zazo, abantu bakho bako-Israyeli. Bafundise indlela yokuphila eqondileyo, uthumele izulu elizweni owalinika abantu bakho ukuba libe yilifa labo.
37 “Pamene mʼdziko mwagwa njala kapena mliri, chinoni kapena chiwawu, dzombe kapena kapuchi, kapena pamene mdani wazungulira mzinda wawo wina uliwonse, kaya mavuto kapena matenda abwera,
Nxa kufika indlala kumbe isifo elizweni, ukukhunta lengumane, isikhongwane lemihogoyi, loba behanqwa yizitha kwelinye lamadolobho abo, loba yincithakalo enganani loba ngumkhuhlane onjani ongeza,
38 ndipo wina aliyense mwa Aisraeli akapemphera kapena kukudandaulirani, aliyense wa iwo akadziwa masautso a mu mtima mwake ndi kukweza manja awo kuloza Nyumba ino,
kuthi lanxa kusenziwa umkhuleko kumbe isicelo ngomunye wabantu bakho bako-Israyeli, ngulowo lalowo ezazela inhlupheko ezinhliziyweni yakhe njalo ephakamisele izandla zakhe kulelithempeli,
39 pamenepo imvani kumwambako, malo anu wokhalamo. Khululukani ndipo chitanipo kanthu. Muchitire aliyense molingana ndi zonse zimene anachita, popeza inu mumadziwa mtima wake (pakuti ndinu nokha amene mumadziwa mitima ya anthu onse),
lalela usezulwini, okuyindawo yakho yokuhlala. Thethelela njalo wenzele umuntu munye ngamunye okuhambelana lezenzo zakhe ngoba wena uyazazi inhliziyo zabo (futhi nguwe wedwa owazi inhliziyo zabantu),
40 motero iwo adzakuopani masiku onse amene adzakhale mʼdziko limene munalipereka kwa makolo athu.
yikho bezakwesaba imihla yabo yonke yokuphila beselizweni owalinika okhokho bethu.
41 “Ndipo kunena za mlendo amene si mmodzi wa anthu anu Aisraeli, koma wabwera kuchokera ku dziko lakutali chifukwa cha dzina lanu,
Owezizweni ongasuye omunye wabantu bakho bako-Israyeli kodwa evela kude ngenxa yodumo lwebizo lakho
42 pakuti anthu adzamva za dzina lanu lotchukali ndiponso za dzanja lanu lamphamvu ndi lochita zazikulu, kudzapemphera akuyangʼana Nyumba ino,
ngoba abantu bazakuzwa ngelakho ibizo eliqakathekileyo lesandla sakho esilamandla lengalo yakho eyeluliweyo, nxa esiza akhuleke ekhangele kulelithempeli,
43 pamenepo imvani kumwambako, malo anu okhalamo, ndipo muchite zonse zimene mlendoyo akukupemphani, kotero kuti anthu onse a dziko lapansi adziwe dzina lanu ndi kukuopani monga amachitira anthu anu Aisraeli, ndipo adziwe kuti Nyumba ino imene ndakumangirani imadziwika ndi Dzina lanu.
lapho-ke zwana usezulwini, indawo elilikhaya lakho, wenze loba yini owezizweni ayicela kuwe, ukuze bonke abantu bomhlaba balazi ibizo lakho njalo bakwesabe, njengoba abantu bakho abako-Israyeli bekwenza, baze bazi ukuthi indlu le engiyakhileyo ithwele iBizo lakho.
44 “Pamene anthu anu apita ku nkhondo kukamenyana ndi adani awo, kulikonse kumene mungawatume, ndipo pamene apemphera kwa Yehova moyangʼana mzinda umene mwausankha ndi Nyumba imene ine ndamangira Dzina lanu,
Nxa abantu bakho bephuma besiya empini ukuyakulwa lezitha zabo, loba kungaphi obathuma khona, njalo kuthi nxa bekhuleka kuThixo bekhangele edolobheni olikhethileyo wena kanye lethempelini engalakhela iBizo lakho,
45 imvani kumwambako pemphero lawo ndi kudandaula kwawo, ndipo apambanitseni.
lapho-ke zwana usezulwini umkhuleko wabo lokuncenga kwabo, ubaphathise kulokho.
46 “Pamene akuchimwirani, popeza palibe munthu amene sachimwa, ndipo Inu nʼkuwakwiyira ndi kuwapereka kwa mdani, amene adzawatenga ukapolo kupita ku dziko lake, kutali kapena pafupi;
Nxa bonile phambi kwakho, ngoba kakho ongoniyo njalo uze ubathukuthelele ubanikele ezitheni zabo ezibathumba zibase ezizweni zazo, ezikhatshana leziseduze;
47 ndipo ngati asintha maganizo ali ku dziko la ukapololo ndi kulapa ndi kukudandaulirani mʼdziko la owagonjetsa ndi kunena kuti, ‘Ife tachimwa, tachita zolakwa, tachita zinthu zoyipa,’
kuthi nxa bengaguquka ezinhliziyweni zabo besemazweni abayabe bethunjelwe kuwo, baphenduke bakuncenge besemazweni abathunjelwa khona bathi, ‘Sonile, senza okungalunganga lokubi,’
48 ndipo ngati abwerera kwa Inu ndi mtima wawo wonse ndi moyo wawo wonse mʼdziko la adani awo amene anawatenga ukapolo, ndi kupemphera kwa Inu moyangʼana dziko limene munapereka kwa makolo awo, moyangʼana mzinda umene munawusankha ndiponso Nyumba imene ine ndamangira Dzina lanu,
njalo nxa bephendukela kuwe ngezinhliziyo zabo zonke langemiphefumulo yabo elizweni lezitha zabo ezabathumbayo, bakhuleke kuwe bekhangele elizweni owalinika oyise, lasedolobheni owalikhethayo lethempeli engilakhele iBizo lakho,
49 imvani kumwambako, malo anu wokhalamo, imvani pemphero lawo ndi kudandaula kwawo, ndipo muwachitire zabwino.
ngakho usezulwini, ikhaya lakho zwana imikhuleko yabo lokuncenga kwabo, ubenzele khona lokho.
50 Ndipo khululukirani anthu anu amene akuchimwirani. Khululukirani zolakwa zonse akuchitirani ndipo mufewetse mitima ya amene anawagonjetsawo kuti awachitire chifundo;
Ubathethelele abantu bakho, abakonileyo wena, bathethelele kukho konke ukona kwabo kuwe, wenze izitha zabo zibe lomusa kubo;
51 popeza ndi anthu anu ndiponso cholowa chanu, anthu omwe munawatulutsa ku Igupto, kuwachotsa mʼngʼanjo yamoto yosungunula zitsulo.
ngoba bangabantu bakho njalo bayilifa lakho, bona owabakhipha eGibhithe, esihogweni esivuthayo esincibilikisa insimbi. (questioned)
52 “Maso anu atsekuke kuti aone dandawulo la mtumiki wanu ndiponso madandawulo a anthu anu Aisraeli, ndipo mutchere khutu nthawi iliyonse pamene akulirirani.
Sengathi amehlo akho angaba phezu kwenceku yakho ukukhala kwayo lokuncengela kwabantu bakho bako-Israyeli, sengathi ungalalela ukukhala kwabo bekhalaza kuwe.
53 Pakuti Inu munawasiyanitsa ndi anthu a mitundu ina yonse ya dziko lonse kuti akhale cholowa chanu, monga momwe munanenera kudzera mwa mtumiki wanu Mose pamene Inu, Ambuye Yehova, munatulutsa makolo athu ku Igupto.”
Ngoba wabakhetha phakathi kwezizwe zonke zomhlaba ukuthi babe yilifa lakho, njengoba wakhuluma ngenceku yakho uMosi, lapho wena, Oh Thixo Wobukhosi, wakhipha okhokho bethu eGibhithe.”
54 Solomoni atamaliza mapemphero ndi mapembedzero onsewa kwa Yehova, anayimirira pa guwa lansembe la Yehova, nagwada atakweza manja ake kumwamba.
Kwathi uSolomoni eseqedile imikhuleko le lezikhalazo kuThixo, waphakama wema phambi kwe-alithari likaThixo, lapho ayekade eguqe khona ephakamisele izandla zakhe ezulwini.
55 Anayimirira ndi kudalitsa gulu lonse la Aisraeli ndi mawu okweza, nati:
Waphakama wabusisa ibandla labako-Israyeli ngelizwi eliphezulu wathi:
56 “Atamandike Yehova, amene wapereka mpumulo kwa anthu ake Aisraeli monga momwe analonjezera. Palibe mawu ndi amodzi omwe amene anapita pachabe pa malonjezo ake onse abwino amene anawapereka kudzera mwa mtumiki wake Mose.
“Udumo kalube kuThixo, yena olethele abantu bako-Israyeli ukuphumula njengokwethembisa kwakhe. Akukho lokukodwa okungenzekanga kuzozonke izithembiso ezinhle azenza ngenceku yakhe uMosi.
57 Yehova Mulungu wathu akhale nafe monga momwe anakhalira ndi makolo athu; asatisiye kapena kutitaya.
Sengathi uThixo uNkulunkulu wethu angaba lathi njengoba wayelabokhokho bethu; sengathi angaze asitshiya loba asidele.
58 Atembenuzire mitima yathu kwa Iye, kuti tiyende mʼnjira zake zonse ndi kusunga mawu ake, malamulo ake ndi malangizo ake amene anapereka kwa makolo athu.
Sengathi angaguqulela inhliziyo zethu kuye, sihambe ezindleleni zakhe sigcine lemilayo yakhe, imithetho lezimiso azipha okhokho.
59 Ndipo mawu angawa, amene ndapemphera pamaso pa Yehova, asayiwalike pamaso pa Yehova Mulungu wathu usana ndi usiku, ndipo Iye alimbikitse mtumiki wake ndiponso athandize Aisraeli, anthu ake powapatsa zosowa zawo za tsiku ndi tsiku,
Sengathi amazwi ami la, engikhuleka ngawo kuThixo, angaba seduze kukaThixo uNkulunkulu wethu emini lebusuku, ukuze aqinise izikhalazo zenceku yakhe lezikhalazo zabantu bakhe bako-Israyeli kusiya ngeziswelo zabo zemihla ngemihla,
60 kotero kuti anthu a mitundu yonse pa dziko lapansi adziwe kuti Yehova ndi Mulungu ndipo kuti palibenso wina.
ukuze abantu bonke bomhlaba bakwazi ukuthi uThixo unguNkulunkulu lokuthi kakho omunye.
61 Koma mitima yanu ikhale yodzipereka kwathunthu kwa Yehova Mulungu wanu, kutsatira malamulo ake ndi kumvera malangizo ake, monga lero lino.”
Kodwa inhliziyo zenu azigcwale ukuzinikela kuThixo uNkulunkulu wethu, ukuphila ngezimiso zakhe lokulalela imilayo yakhe, njengakhathesi.”
62 Ndipo mfumu pamodzi ndi Aisraeli onse anapereka nsembe pamaso pa Yehova.
Ngalokho inkosi labo bonke abako-Israyeli banikela imihlatshelo yabo phambi kukaThixo.
63 Solomoni anapereka nsembe zachiyanjano kwa Yehova: ngʼombe 22,000, nkhosa ndi mbuzi 120,000. Motero mfumu pamodzi ndi Aisraeli onse anapatula Nyumba ya Yehova.
USolomoni wanikela ngomhlatshelo weminikelo yobudlelwano kuThixo; inkomo ezizinkulungwane ezingamatshumi amabili lambili, izimvu lembuzi ezizinkulungwane ezilikhulu lamatshumi amabili. Ngokunjalo inkosi labo bonke abako-Israyeli banikela ithempeli likaThixo.
64 Tsiku lomwelo mfumu inapatulanso malo a pakati pa bwalo limene linali kutsogolo kwa Nyumba ya Yehova ndiponso nthuli za mafuta za nsembe yachiyanjano, chifukwa guwa lansembe la mkuwa limene linali pamaso pa Yehova linali lochepa kwambiri ndipo nsembe zonse zopsereza, nsembe zachakudya, ndi nthuli za mafuta a nsembe zachiyanjano sizikanakwanirapo.
Ngalelolanga inkosi yangcwelisa iphakathi leguma phambi kwethempeli likaThixo, njalo kulapho eyanikela khona ngomnikelo wokutshiswa, umnikelo wamabele kanye lamafutha eminikelo yobudlelwano ngoba i-alithari lethusi elaliphambi kukaThixo lalilincinyane kakhulu ukuthi kutshiselwe kilo iminikelo yokutshiswa, leminikelo yamabele leminikelo yamafutha obudlelwano.
65 Choncho nthawi imeneyi, Solomoni anachita chikondwerero pamodzi ndi Aisraeli onse. Unali msonkhano waukulu, kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku Chigwa cha ku Igupto. Anachita chikondwerero chimenechi pamaso pa Yehova Mulungu wathu kwa masiku asanu ndi awiri, anawonjezerapo masiku ena asanu ndi awiri, onse pamodzi ngati masiku 14.
Ngakho uSolomoni wagcina umkhosi ngalesosikhathi ekanye lo-Israyeli wonke, ibandla elikhulu, abantu abavela eLebho Hamathi kusiya eSihotsheni saseGibhithe. Bawuthakazelela phambi kukaThixo uNkulunkulu wethu okwensuku eziyisikhombisa lezinye eziyisikhombisa njalo zaba litshumi lane sezizonke.
66 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu Solomoni anawuza anthu kuti apite kwawo. Anthuwo anathokoza mfumu ndipo kenaka anapita kwawo mokondwa ndi mosangalala mʼmitima mwawo chifukwa cha zinthu zabwino zimene Yehova anachitira mtumiki wake Davide ndi anthu ake Aisraeli.
Ngosuku olulandelayo inkosi yabachitha. Bayibusisa inkosi basuka baya emakhaya abo, belentokozo bejabula ezinhliziyweni zabo ngakho konke okuhle uThixo ayekwenzele inceku yakhe uDavida kanye labantu bakhe bako-Israyeli.

< 1 Mafumu 8 >