< 1 Mafumu 5 >

1 Hiramu mfumu ya ku Turo atamva kuti Solomoni wadzozedwa kukhala mfumu mʼmalo mwa abambo ake Davide, anatumiza akazembe ake kwa Solomoni, chifukwa mfumu Hiramu inali pa ubale wabwino ndi Davide nthawi zonse.
И Хирам, цар тирски посла слуге своје к Соломуну чувши да су га помазали за цара на место оца његовог, јер Хирам љубљаше Давида свагда.
2 Solomoni anabweza mawu awa kwa Hiramu:
А Соломун посла ка Хираму и поручи му:
3 “Inu mukudziwa kuti chifukwa cha nkhondo zimene zinkachokera ku mbali zonse kulimbana ndi abambo anga, iwo sanathe kumangira Nyumba Yehova Mulungu wawo, mpaka Yehova atawayika adani awo pansi pa ulamuliro wawo.
Ти знаш да Давид, отац мој није могао саградити дом имену Господа Бога свог од ратова којима га опколише, докле их Господ не положи под ноге његове.
4 Koma tsopano Yehova Mulungu wanga wandipatsa mtendere mbali zonse za dziko ndipo ndilibe mdani kapena chovuta chilichonse.
А сада Господ Бог мој дао ми је мир од свуда, немам ни једног непријатеља ни злу сметњу.
5 Choncho ine ndikufuna kumangira nyumba Yehova Mulungu wanga, monga momwe Iye anawuzira abambo anga Davide kuti, ‘Mwana wako amene ndidzamukhazike pa mpando waufumu mʼmalo mwako ndiye adzandimangire Nyumba.’
Зато, ево, велим да саградим дом имену Господа Бога свог, као што је рекао Господ Давиду оцу мом говорећи: Син твој, ког ћу посадити место тебе на престо твој, он ће саградити дом имену мом.
6 “Choncho lamulani kuti andidulire mikungudza ya ku Lebanoni. Anthu anga adzagwira ntchito imeneyo pamodzi ndi anthu anuwo, ndipo ine ndidzalipira anthu anuwo malipiro amene inu mungakhazikitse. Inu mukudziwa kuti ife tilibe anthu aluso locheka matabwa monga Asidoni.”
Зато заповеди сада нека ми насеку дрва кедрових на Ливану, а слуге ће моје бити са слугама твојим, а плату слугама твојим даћу ти како год кажеш; јер ти знаш да у нас нема људи који умеју сећи дрва као сидонци.
7 Hiramu anakondwa kwambiri atamva uthenga wa Solomoni ndipo anati, “Lero Yehova atamandike chifukwa wapatsa Davide mwana wanzeru kuti alamulire mtundu waukuluwu.”
И кад Хирам чу речи Соломунове, обрадова се веома и рече: Да је благословен Господ данас, који даде Давиду мудрог сина над овим народом великим.
8 Tsono Hiramu anabweza mawu awa kwa Solomoni: “Ndalandira uthenga umene mwanditumizira ndipo ine ndidzachita zonse zimene mukufuna pokupatsani mitengo ya mkungudza ndi payini.
И посла Хирам Соломуну, и поручи: Чуо сам чега ради си слао к мени; ја ћу учинити сву вољу твоју за дрва кедрова и за дрва јелова.
9 Anthu anga adzatsika nayo kuchokera ku Lebanoni mpaka ku nyanja, ndipo adzayiyandamitsa pa nyanja mpaka ku malo amene munene. Kumeneko ndidzayimasula ndipo mudzayitenga. Ndipo inu mudzakwaniritsa chokhumba changa pondipatsa chakudya cha banja langa laufumu.”
Моје ће слуге снети с Ливана на море, и ја ћу их повезати у сплавове и спустити морем до места које ми кажеш, и онде ћу развезати, па их носи; а ти ћеш учинити моју вољу и дати храну чељади мојој.
10 Motero Hiramu anapereka kwa Solomoni mitengo yonse ya mkungudza ndi payini imene ankayifuna,
И тако даваше Хирам Соломуну дрва кедрова и дрва јелова, колико му беше воља.
11 ndipo Solomoni anamupatsa Hiramu mitanga ya tirigu 20,000 ngati chakudya cha pa nyumba yake, kuwonjezera pa migolo ya mafuta a olivi yokwana 20,000. Solomoni anapitiriza kupereka zimenezi chaka ndi chaka.
А Соломун даваше Хираму двадесет хиљада кора пшенице за храну чељади његовој, и двадесет кора уља цеђеног; толико даваше Соломун Хираму сваке године.
12 Yehova anamupatsa Solomoni nzeru monga momwe analonjezera. Panali ubale wa mtendere pakati pa Solomoni ndi Hiramu, ndipo awiriwa anachita pangano.
И Господ даде мудрост Соломуну како му беше обрекао, и беше мир између Хирама и Соломуна, и ухватише веру међу собом.
13 Mfumu Solomoni inasonkhanitsa anthu ogwira ntchito ya thangata mʼdziko lonse la Israeli ndipo anthu athangatawo analipo 30,000.
И одреди Соломун људе из свега Израиља, и би одређених тридесет хиљада људи.
14 Iye ankatumiza anthu 10,000 ku Lebanoni pa mwezi mosinthanasinthana, kotero kuti ankakhala ku Lebanoniko mwezi umodzi ndipo kwawo ankakhalako miyezi iwiri. Adoniramu ndiye ankayangʼanira ogwira ntchito yathangatayo.
И слаше их на Ливан по десет хиљада сваког месеца наизменце; један месец беху на Ливану а два месеца код кућа својих. А Адонирам беше над овим посланицима.
15 Solomoni anali ndi anthu amtengatenga 70,000, anthu 80,000 osema miyala ku mapiri,
И имаше Соломун седамдесет хиљада носилаца и осамдесет хиљада тесача у планини,
16 ndi akapitawo 33,000 amene ankayangʼanira ntchitoyi ndiponso anthu ogwira ntchito zina.
Осим настојника Соломунових, који беху над тим послом, три хиљаде и триста, који управљаху народом који пословаше тај посао.
17 Molamulidwa ndi mfumu, anakumba ndi kusema miyala ikuluikulu kwambiri yoti akamangire maziko a Nyumba ya Mulungu.
И заповеди цар да сносе велико камење, скупоцено камење за темељ дому, тесано камење.
18 Amisiri a Solomoni ndi a Hiramu ndiponso anthu a ku Gebala anasema miyala ndi kukonza matabwa ndi miyala yomangira Nyumba ya Mulungu.
И тесаху посленици Соломунови и посленици Хирамови и Гивлеји, и приправљаху дрво и камење да се зида дом.

< 1 Mafumu 5 >