< 1 Mafumu 5 >
1 Hiramu mfumu ya ku Turo atamva kuti Solomoni wadzozedwa kukhala mfumu mʼmalo mwa abambo ake Davide, anatumiza akazembe ake kwa Solomoni, chifukwa mfumu Hiramu inali pa ubale wabwino ndi Davide nthawi zonse.
Hiram, roi de Tyr, envoya aussi ses serviteurs vers Salomon; car il apprit qu’on l’avait oint roi, en la place de son père, parce qu’Hiram avait toujours été l’ami de David.
2 Solomoni anabweza mawu awa kwa Hiramu:
Or Salomon envoya vers Hiram, disant:
3 “Inu mukudziwa kuti chifukwa cha nkhondo zimene zinkachokera ku mbali zonse kulimbana ndi abambo anga, iwo sanathe kumangira Nyumba Yehova Mulungu wawo, mpaka Yehova atawayika adani awo pansi pa ulamuliro wawo.
Vous savez le désir de David mon père, et qu’il n’a pu bâtir une maison au nom du Seigneur son Dieu, à cause des guerres qui le menaçaient de toutes parts, jusqu’à ce que le Seigneur eût mis ses ennemis sous la plante de ses pieds.
4 Koma tsopano Yehova Mulungu wanga wandipatsa mtendere mbali zonse za dziko ndipo ndilibe mdani kapena chovuta chilichonse.
Mais maintenant le Seigneur mon Dieu m’a donné la paix alentour; et il n’y a ni adversaire, ni obstacle fâcheux.
5 Choncho ine ndikufuna kumangira nyumba Yehova Mulungu wanga, monga momwe Iye anawuzira abambo anga Davide kuti, ‘Mwana wako amene ndidzamukhazike pa mpando waufumu mʼmalo mwako ndiye adzandimangire Nyumba.’
C’est pourquoi je pense à bâtir un temple au nom du Seigneur mon Dieu, comme a parlé le Seigneur à David, mon père, disant: Ton fils, que je mettrai en ta place sur ton trône, sera celui qui bâtira une maison à mon nom.
6 “Choncho lamulani kuti andidulire mikungudza ya ku Lebanoni. Anthu anga adzagwira ntchito imeneyo pamodzi ndi anthu anuwo, ndipo ine ndidzalipira anthu anuwo malipiro amene inu mungakhazikitse. Inu mukudziwa kuti ife tilibe anthu aluso locheka matabwa monga Asidoni.”
Ordonnez donc que vos serviteurs coupent pour moi des cèdres du Liban, et que mes serviteurs soient avec les vôtres; quant à la récompense de vos serviteurs, je vous la donnerai telle que vous la demanderez; car vous savez que parmi mon peuple, il n’est pas d’homme qui sache couper le bois comme les Sidoniens.
7 Hiramu anakondwa kwambiri atamva uthenga wa Solomoni ndipo anati, “Lero Yehova atamandike chifukwa wapatsa Davide mwana wanzeru kuti alamulire mtundu waukuluwu.”
Lors donc qu’Hiram eut entendu les paroles de Salomon, il se réjouit beaucoup, et dit: Béni aujourd’hui le Seigneur Dieu, qui a donné à David un fils très sage pour gouverner ce très grand peuple!
8 Tsono Hiramu anabweza mawu awa kwa Solomoni: “Ndalandira uthenga umene mwanditumizira ndipo ine ndidzachita zonse zimene mukufuna pokupatsani mitengo ya mkungudza ndi payini.
Et Hiram envoya vers Salomon, disant: J’ai entendu tout ce que vous m’avez mandé; je ferai tout ce que vous désirez pour les bois de cèdre et de sapin.
9 Anthu anga adzatsika nayo kuchokera ku Lebanoni mpaka ku nyanja, ndipo adzayiyandamitsa pa nyanja mpaka ku malo amene munene. Kumeneko ndidzayimasula ndipo mudzayitenga. Ndipo inu mudzakwaniritsa chokhumba changa pondipatsa chakudya cha banja langa laufumu.”
Mes serviteurs les porteront du Liban à la mer, et moi je les ferai mettre en radeaux sur la mer, jusqu’au lieu que vous m’aurez marqué; je les y ferai aborder; vous les enlèverez, et vous me fournirez tout ce qui me sera nécessaire pour nourrir ma maison.
10 Motero Hiramu anapereka kwa Solomoni mitengo yonse ya mkungudza ndi payini imene ankayifuna,
C’est pourquoi Hiram donnait à Salomon des bois de cèdre et de sapin, selon tous ses désirs.
11 ndipo Solomoni anamupatsa Hiramu mitanga ya tirigu 20,000 ngati chakudya cha pa nyumba yake, kuwonjezera pa migolo ya mafuta a olivi yokwana 20,000. Solomoni anapitiriza kupereka zimenezi chaka ndi chaka.
Et Salomon fournissait à Hiram, pour nourrir sa maison, vingt mille cors de froment et vingt cors d’huile très pure: voilà ce que Salomon livrait chaque année à Hiram.
12 Yehova anamupatsa Solomoni nzeru monga momwe analonjezera. Panali ubale wa mtendere pakati pa Solomoni ndi Hiramu, ndipo awiriwa anachita pangano.
Le Seigneur donna aussi la sagesse à Salomon, comme il le lui avait dit: et il y avait paix entre Hiram et Salomon, et ils firent tous deux alliance.
13 Mfumu Solomoni inasonkhanitsa anthu ogwira ntchito ya thangata mʼdziko lonse la Israeli ndipo anthu athangatawo analipo 30,000.
Et le roi Salomon choisit des ouvriers de tout Israël, et la taxation était de trente mille hommes.
14 Iye ankatumiza anthu 10,000 ku Lebanoni pa mwezi mosinthanasinthana, kotero kuti ankakhala ku Lebanoniko mwezi umodzi ndipo kwawo ankakhalako miyezi iwiri. Adoniramu ndiye ankayangʼanira ogwira ntchito yathangatayo.
Et il les envoyait au Liban tour à tour, dix mille chaque mois, de sorte qu’ils étaient deux mois dans leurs maisons; et Adoniram était préposé à cette taxation.
15 Solomoni anali ndi anthu amtengatenga 70,000, anthu 80,000 osema miyala ku mapiri,
Salomon avait soixante-dix mille hommes qui portaient des fardeaux, et quatre-vingt mille qui taillaient des pierres sur la montagne,
16 ndi akapitawo 33,000 amene ankayangʼanira ntchitoyi ndiponso anthu ogwira ntchito zina.
Sans les préposés qui présidaient à chaque ouvrage, au nombre de trois mille trois cents, et qui donnaient les ordres au peuple et à ceux qui faisaient l’ouvrage.
17 Molamulidwa ndi mfumu, anakumba ndi kusema miyala ikuluikulu kwambiri yoti akamangire maziko a Nyumba ya Mulungu.
Et le roi leur ordonna de prendre de grandes pierres, des pierres de prix, pour les fondements du temple, et de les équarrir;
18 Amisiri a Solomoni ndi a Hiramu ndiponso anthu a ku Gebala anasema miyala ndi kukonza matabwa ndi miyala yomangira Nyumba ya Mulungu.
Et les maçons de Salomon et les maçons d’Hiram les taillèrent; or ceux de Giblos préparèrent les bois et les pierres pour bâtir la maison du Seigneur.