< 1 Mafumu 5 >

1 Hiramu mfumu ya ku Turo atamva kuti Solomoni wadzozedwa kukhala mfumu mʼmalo mwa abambo ake Davide, anatumiza akazembe ake kwa Solomoni, chifukwa mfumu Hiramu inali pa ubale wabwino ndi Davide nthawi zonse.
Hiram, roi de Tyr, envoya de ses serviteurs vers Salomon, quand il eut appris qu'on l'avait oint pour roi à la place de son père; car Hiram avait toujours aimé David.
2 Solomoni anabweza mawu awa kwa Hiramu:
Et Salomon envoya vers Hiram, pour lui dire:
3 “Inu mukudziwa kuti chifukwa cha nkhondo zimene zinkachokera ku mbali zonse kulimbana ndi abambo anga, iwo sanathe kumangira Nyumba Yehova Mulungu wawo, mpaka Yehova atawayika adani awo pansi pa ulamuliro wawo.
Tu sais que David, mon père, n'a pu bâtir une maison au nom de l'Éternel son Dieu, à cause de la guerre dont ses ennemis l'environnaient, jusqu'à ce que l'Éternel les eût mis sous ses pieds.
4 Koma tsopano Yehova Mulungu wanga wandipatsa mtendere mbali zonse za dziko ndipo ndilibe mdani kapena chovuta chilichonse.
Et maintenant l'Éternel mon Dieu m'a donné du repos de toutes parts; je n'ai point d'adversaire ni d'affaire fâcheuse.
5 Choncho ine ndikufuna kumangira nyumba Yehova Mulungu wanga, monga momwe Iye anawuzira abambo anga Davide kuti, ‘Mwana wako amene ndidzamukhazike pa mpando waufumu mʼmalo mwako ndiye adzandimangire Nyumba.’
Voici donc, je me propose de bâtir une maison au nom de l'Éternel mon Dieu, selon que l'Éternel en a parlé à David, mon père, en disant: Ton fils, que je mettrai à ta place sur ton trône, sera celui qui bâtira une maison à mon nom.
6 “Choncho lamulani kuti andidulire mikungudza ya ku Lebanoni. Anthu anga adzagwira ntchito imeneyo pamodzi ndi anthu anuwo, ndipo ine ndidzalipira anthu anuwo malipiro amene inu mungakhazikitse. Inu mukudziwa kuti ife tilibe anthu aluso locheka matabwa monga Asidoni.”
Et maintenant, commande qu'on me coupe des cèdres du Liban; mes serviteurs seront avec tes serviteurs; et je te donnerai pour tes serviteurs le salaire que tu demanderas; car tu sais qu'il n'y a personne parmi nous qui s'entende à couper les bois comme les Sidoniens.
7 Hiramu anakondwa kwambiri atamva uthenga wa Solomoni ndipo anati, “Lero Yehova atamandike chifukwa wapatsa Davide mwana wanzeru kuti alamulire mtundu waukuluwu.”
Quand Hiram entendit les paroles de Salomon, il en eut une grande joie, et il dit: Béni soit aujourd'hui l'Éternel, qui a donné à David un fils sage, pour régner sur ce grand peuple!
8 Tsono Hiramu anabweza mawu awa kwa Solomoni: “Ndalandira uthenga umene mwanditumizira ndipo ine ndidzachita zonse zimene mukufuna pokupatsani mitengo ya mkungudza ndi payini.
Et Hiram envoya vers Salomon, pour lui dire: J'ai entendu ce que tu m'as mandé. Je ferai tout ce que tu voudras, quant au bois de cèdre et au bois de cyprès.
9 Anthu anga adzatsika nayo kuchokera ku Lebanoni mpaka ku nyanja, ndipo adzayiyandamitsa pa nyanja mpaka ku malo amene munene. Kumeneko ndidzayimasula ndipo mudzayitenga. Ndipo inu mudzakwaniritsa chokhumba changa pondipatsa chakudya cha banja langa laufumu.”
Mes serviteurs les descendront du Liban à la mer; puis je les ferai mettre sur la mer en radeaux, jusqu'au lieu que tu m'auras marqué, et je les ferai délivrer là; tu les y prendras; mais, de ton côté, tu me satisferas en fournissant de vivres ma maison.
10 Motero Hiramu anapereka kwa Solomoni mitengo yonse ya mkungudza ndi payini imene ankayifuna,
Hiram donc donna du bois de cèdre et du bois de cyprès à Salomon, autant qu'il en voulut.
11 ndipo Solomoni anamupatsa Hiramu mitanga ya tirigu 20,000 ngati chakudya cha pa nyumba yake, kuwonjezera pa migolo ya mafuta a olivi yokwana 20,000. Solomoni anapitiriza kupereka zimenezi chaka ndi chaka.
Et Salomon donnait à Hiram vingt mille cores de froment, pour la nourriture de sa maison, et vingt cores d'huile très pure. Salomon en donnait autant à Hiram chaque année.
12 Yehova anamupatsa Solomoni nzeru monga momwe analonjezera. Panali ubale wa mtendere pakati pa Solomoni ndi Hiramu, ndipo awiriwa anachita pangano.
L'Éternel donna donc de la sagesse à Salomon, comme il lui en avait parlé. Et il y eut paix entre Hiram et Salomon, et ils traitèrent alliance ensemble.
13 Mfumu Solomoni inasonkhanitsa anthu ogwira ntchito ya thangata mʼdziko lonse la Israeli ndipo anthu athangatawo analipo 30,000.
Et le roi Salomon leva des gens de corvée dans tout Israël; et la corvée fut de trente mille hommes.
14 Iye ankatumiza anthu 10,000 ku Lebanoni pa mwezi mosinthanasinthana, kotero kuti ankakhala ku Lebanoniko mwezi umodzi ndipo kwawo ankakhalako miyezi iwiri. Adoniramu ndiye ankayangʼanira ogwira ntchito yathangatayo.
Et il les envoyait au Liban tour à tour, dix mille chaque mois; ils étaient un mois au Liban et deux mois chez eux; et Adoniram était préposé à la corvée.
15 Solomoni anali ndi anthu amtengatenga 70,000, anthu 80,000 osema miyala ku mapiri,
Salomon eut aussi soixante et dix mille hommes qui portaient les fardeaux, et quatre-vingt mille qui taillaient dans la montagne;
16 ndi akapitawo 33,000 amene ankayangʼanira ntchitoyi ndiponso anthu ogwira ntchito zina.
Outre les chefs préposés par Salomon, qui avaient la direction de l'ouvrage, au nombre de trois mille trois cents, et qui commandaient le peuple qui travaillait.
17 Molamulidwa ndi mfumu, anakumba ndi kusema miyala ikuluikulu kwambiri yoti akamangire maziko a Nyumba ya Mulungu.
Et le roi commanda d'extraire de grandes pierres, des pierres de prix, pour faire de pierres de taille les fondements de la maison.
18 Amisiri a Solomoni ndi a Hiramu ndiponso anthu a ku Gebala anasema miyala ndi kukonza matabwa ndi miyala yomangira Nyumba ya Mulungu.
Et les ouvriers de Salomon, et les ouvriers de Hiram, et les Guibliens taillèrent et préparèrent le bois et les pierres pour bâtir la maison.

< 1 Mafumu 5 >