< 1 Mafumu 5 >

1 Hiramu mfumu ya ku Turo atamva kuti Solomoni wadzozedwa kukhala mfumu mʼmalo mwa abambo ake Davide, anatumiza akazembe ake kwa Solomoni, chifukwa mfumu Hiramu inali pa ubale wabwino ndi Davide nthawi zonse.
Hiram, roi de Tyr, envoya ses serviteurs vers Salomon, car il avait appris qu'on l'avait oint comme roi à la place de son père, et Hiram avait toujours aimé David.
2 Solomoni anabweza mawu awa kwa Hiramu:
Salomon envoya dire à Hiram:
3 “Inu mukudziwa kuti chifukwa cha nkhondo zimene zinkachokera ku mbali zonse kulimbana ndi abambo anga, iwo sanathe kumangira Nyumba Yehova Mulungu wawo, mpaka Yehova atawayika adani awo pansi pa ulamuliro wawo.
« Tu sais que David, mon père, n'a pu bâtir une maison au nom de l'Éternel, son Dieu, à cause des guerres qui l'ont entouré de toutes parts, jusqu'à ce que l'Éternel ait mis ses ennemis sous la plante de ses pieds.
4 Koma tsopano Yehova Mulungu wanga wandipatsa mtendere mbali zonse za dziko ndipo ndilibe mdani kapena chovuta chilichonse.
Mais maintenant, l'Éternel, mon Dieu, m'a donné du repos de tous côtés. Il n'y a plus d'ennemi ni d'événement mauvais.
5 Choncho ine ndikufuna kumangira nyumba Yehova Mulungu wanga, monga momwe Iye anawuzira abambo anga Davide kuti, ‘Mwana wako amene ndidzamukhazike pa mpando waufumu mʼmalo mwako ndiye adzandimangire Nyumba.’
Voici, j'ai l'intention de bâtir une maison au nom de l'Éternel, mon Dieu, comme l'Éternel l'a dit à David, mon père: « Ton fils, que je mettrai à ta place sur ton trône, bâtira la maison de mon nom ».
6 “Choncho lamulani kuti andidulire mikungudza ya ku Lebanoni. Anthu anga adzagwira ntchito imeneyo pamodzi ndi anthu anuwo, ndipo ine ndidzalipira anthu anuwo malipiro amene inu mungakhazikitse. Inu mukudziwa kuti ife tilibe anthu aluso locheka matabwa monga Asidoni.”
Maintenant, ordonne que l'on coupe pour moi des cèdres du Liban. Mes serviteurs seront avec tes serviteurs, et je te donnerai un salaire pour tes serviteurs, selon tout ce que tu diras. Car vous savez qu'il n'y a personne parmi nous qui sache couper le bois comme les Sidoniens. »
7 Hiramu anakondwa kwambiri atamva uthenga wa Solomoni ndipo anati, “Lero Yehova atamandike chifukwa wapatsa Davide mwana wanzeru kuti alamulire mtundu waukuluwu.”
Lorsque Hiram entendit les paroles de Salomon, il se réjouit grandement et dit: « Béni soit aujourd'hui Yahvé, qui a donné à David un fils sage pour gouverner ce grand peuple. »
8 Tsono Hiramu anabweza mawu awa kwa Solomoni: “Ndalandira uthenga umene mwanditumizira ndipo ine ndidzachita zonse zimene mukufuna pokupatsani mitengo ya mkungudza ndi payini.
Hiram envoya dire à Salomon: « J'ai entendu le message que tu m'as envoyé. Je ferai tout ce que tu désires en ce qui concerne le bois de cèdre et le bois de cyprès.
9 Anthu anga adzatsika nayo kuchokera ku Lebanoni mpaka ku nyanja, ndipo adzayiyandamitsa pa nyanja mpaka ku malo amene munene. Kumeneko ndidzayimasula ndipo mudzayitenga. Ndipo inu mudzakwaniritsa chokhumba changa pondipatsa chakudya cha banja langa laufumu.”
Mes serviteurs les feront descendre du Liban jusqu'à la mer. Je les transformerai en radeaux pour qu'ils aillent par mer jusqu'au lieu que tu m'auras indiqué, je les ferai briser là et tu les recevras. Tu accompliras mon désir, en donnant de la nourriture à ma famille. »
10 Motero Hiramu anapereka kwa Solomoni mitengo yonse ya mkungudza ndi payini imene ankayifuna,
Hiram donna à Salomon du bois de cèdre et du bois de cyprès, selon tout son désir.
11 ndipo Solomoni anamupatsa Hiramu mitanga ya tirigu 20,000 ngati chakudya cha pa nyumba yake, kuwonjezera pa migolo ya mafuta a olivi yokwana 20,000. Solomoni anapitiriza kupereka zimenezi chaka ndi chaka.
Salomon donna à Hiram vingt mille cors de blé pour la nourriture de sa maison, et vingt cors d'huile pure. Salomon donna cela à Hiram année par année.
12 Yehova anamupatsa Solomoni nzeru monga momwe analonjezera. Panali ubale wa mtendere pakati pa Solomoni ndi Hiramu, ndipo awiriwa anachita pangano.
Yahvé donna à Salomon de la sagesse, comme il le lui avait promis. La paix régna entre Hiram et Salomon, et tous deux conclurent un traité ensemble.
13 Mfumu Solomoni inasonkhanitsa anthu ogwira ntchito ya thangata mʼdziko lonse la Israeli ndipo anthu athangatawo analipo 30,000.
Le roi Salomon leva une levée sur tout Israël, et la levée fut de trente mille hommes.
14 Iye ankatumiza anthu 10,000 ku Lebanoni pa mwezi mosinthanasinthana, kotero kuti ankakhala ku Lebanoniko mwezi umodzi ndipo kwawo ankakhalako miyezi iwiri. Adoniramu ndiye ankayangʼanira ogwira ntchito yathangatayo.
Il les envoya au Liban, à raison de dix mille par mois par cours: un mois ils étaient au Liban, et deux mois à la maison; et Adoniram était à la tête des hommes soumis au travail forcé.
15 Solomoni anali ndi anthu amtengatenga 70,000, anthu 80,000 osema miyala ku mapiri,
Salomon avait soixante-dix mille personnes qui portaient des fardeaux, et quatre-vingt mille qui taillaient des pierres dans les montagnes,
16 ndi akapitawo 33,000 amene ankayangʼanira ntchitoyi ndiponso anthu ogwira ntchito zina.
sans compter les chefs de Salomon qui étaient chargés de l'ouvrage: trois mille trois cents qui dirigeaient le peuple qui travaillait à l'ouvrage.
17 Molamulidwa ndi mfumu, anakumba ndi kusema miyala ikuluikulu kwambiri yoti akamangire maziko a Nyumba ya Mulungu.
Le roi donna des ordres, et l'on tailla de grosses pierres, des pierres de prix, pour poser les fondements de la maison avec des pierres travaillées.
18 Amisiri a Solomoni ndi a Hiramu ndiponso anthu a ku Gebala anasema miyala ndi kukonza matabwa ndi miyala yomangira Nyumba ya Mulungu.
Les bâtisseursde Salomon, les bâtisseurs de Hiram et les Gébalites les taillèrent et préparèrent le bois et les pierres pour construire la maison.

< 1 Mafumu 5 >