< 1 Mafumu 5 >

1 Hiramu mfumu ya ku Turo atamva kuti Solomoni wadzozedwa kukhala mfumu mʼmalo mwa abambo ake Davide, anatumiza akazembe ake kwa Solomoni, chifukwa mfumu Hiramu inali pa ubale wabwino ndi Davide nthawi zonse.
And he sent Hiram [the] king of Tyre servants his to Solomon for he had heard that him people had anointed to king in place of father his for a friend he had been Hiram of David all the days.
2 Solomoni anabweza mawu awa kwa Hiramu:
And he sent Solomon to Hiram saying.
3 “Inu mukudziwa kuti chifukwa cha nkhondo zimene zinkachokera ku mbali zonse kulimbana ndi abambo anga, iwo sanathe kumangira Nyumba Yehova Mulungu wawo, mpaka Yehova atawayika adani awo pansi pa ulamuliro wawo.
You you know David father my that not he was able to build a house for [the] name of Yahweh God his because of the war which they had surrounded him until gave Yahweh them under [the] soles of (feet my. *Q(K)*)
4 Koma tsopano Yehova Mulungu wanga wandipatsa mtendere mbali zonse za dziko ndipo ndilibe mdani kapena chovuta chilichonse.
And now he has given rest Yahweh God my to me from round about there not [is] an adversary and there not [is] an occurrence evil.
5 Choncho ine ndikufuna kumangira nyumba Yehova Mulungu wanga, monga momwe Iye anawuzira abambo anga Davide kuti, ‘Mwana wako amene ndidzamukhazike pa mpando waufumu mʼmalo mwako ndiye adzandimangire Nyumba.’
And here I [am] saying to build a house for [the] name of Yahweh God my just as - he spoke Yahweh to David father my saying son your whom I will put in place of you on throne your he he will build the house for name my.
6 “Choncho lamulani kuti andidulire mikungudza ya ku Lebanoni. Anthu anga adzagwira ntchito imeneyo pamodzi ndi anthu anuwo, ndipo ine ndidzalipira anthu anuwo malipiro amene inu mungakhazikitse. Inu mukudziwa kuti ife tilibe anthu aluso locheka matabwa monga Asidoni.”
And therefore command so they may cut for me cedars from Lebanon and servants my they will be with servants your and [the] wage[s] of servants your I will give to you according to all that you will say for - you you know that there not among us [is] anyone [who] knows to cut wood like the Sidonians.
7 Hiramu anakondwa kwambiri atamva uthenga wa Solomoni ndipo anati, “Lero Yehova atamandike chifukwa wapatsa Davide mwana wanzeru kuti alamulire mtundu waukuluwu.”
And it was when heard Hiram [the] words of Solomon and he rejoiced exceedingly and he said [be] blessed Yahweh this day who he has given to David a son wise over the people great this.
8 Tsono Hiramu anabweza mawu awa kwa Solomoni: “Ndalandira uthenga umene mwanditumizira ndipo ine ndidzachita zonse zimene mukufuna pokupatsani mitengo ya mkungudza ndi payini.
And he sent Hiram to Solomon saying I have heard [that] which you sent to me I I will do all desire your in wood of cedar and in wood of cypress.
9 Anthu anga adzatsika nayo kuchokera ku Lebanoni mpaka ku nyanja, ndipo adzayiyandamitsa pa nyanja mpaka ku malo amene munene. Kumeneko ndidzayimasula ndipo mudzayitenga. Ndipo inu mudzakwaniritsa chokhumba changa pondipatsa chakudya cha banja langa laufumu.”
Servants my they will bring [them] down from Lebanon [the] sea towards and I I will make them rafts on the sea to the place which you will send to me and I will break up them there and you you will carry [them] away and you you will do desire my by giving [the] food of household my.
10 Motero Hiramu anapereka kwa Solomoni mitengo yonse ya mkungudza ndi payini imene ankayifuna,
And he was Hiram giving to Solomon wood of cedar and wood of cypress all desire his.
11 ndipo Solomoni anamupatsa Hiramu mitanga ya tirigu 20,000 ngati chakudya cha pa nyumba yake, kuwonjezera pa migolo ya mafuta a olivi yokwana 20,000. Solomoni anapitiriza kupereka zimenezi chaka ndi chaka.
And Solomon he gave to Hiram twenty thousand cor[s] of wheat food for household his and twenty cor[s] of oil pressed thus he gave Solomon to Hiram a year in a year.
12 Yehova anamupatsa Solomoni nzeru monga momwe analonjezera. Panali ubale wa mtendere pakati pa Solomoni ndi Hiramu, ndipo awiriwa anachita pangano.
And Yahweh he gave wisdom to Solomon just as he had spoken to him and it was peace between Hiram and between Solomon and they made a covenant [the] two of them.
13 Mfumu Solomoni inasonkhanitsa anthu ogwira ntchito ya thangata mʼdziko lonse la Israeli ndipo anthu athangatawo analipo 30,000.
And he raised the king Solomon forced labor from all Israel and it was the forced labor thirty thousand man.
14 Iye ankatumiza anthu 10,000 ku Lebanoni pa mwezi mosinthanasinthana, kotero kuti ankakhala ku Lebanoniko mwezi umodzi ndipo kwawo ankakhalako miyezi iwiri. Adoniramu ndiye ankayangʼanira ogwira ntchito yathangatayo.
And he sent them Lebanon towards ten thousand in the month relays a month they were in Lebanon two months in home his and Adoniram [was] over the forced labor.
15 Solomoni anali ndi anthu amtengatenga 70,000, anthu 80,000 osema miyala ku mapiri,
And it belonged to Solomon seventy thousand carrier[s] burden-bearer[s] and eighty thousand stone-cutter[s] in the hill country.
16 ndi akapitawo 33,000 amene ankayangʼanira ntchitoyi ndiponso anthu ogwira ntchito zina.
Apart from [the] leaders of the overseers of Solomon who [were] over the work three thousand and three hundred who ruled over the people who were doing the work.
17 Molamulidwa ndi mfumu, anakumba ndi kusema miyala ikuluikulu kwambiri yoti akamangire maziko a Nyumba ya Mulungu.
And he commanded the king and they quarried stones large stones costly to found the house stones of hewn [stone].
18 Amisiri a Solomoni ndi a Hiramu ndiponso anthu a ku Gebala anasema miyala ndi kukonza matabwa ndi miyala yomangira Nyumba ya Mulungu.
And they cut [them] to shape [the] builders of Solomon and [the] builders of Hiram and the Gebalites and they prepared the wood and the stones to build the house.

< 1 Mafumu 5 >