< 1 Mafumu 5 >

1 Hiramu mfumu ya ku Turo atamva kuti Solomoni wadzozedwa kukhala mfumu mʼmalo mwa abambo ake Davide, anatumiza akazembe ake kwa Solomoni, chifukwa mfumu Hiramu inali pa ubale wabwino ndi Davide nthawi zonse.
Poslal pak Chíram král Tyrský služebníky své k Šalomounovi, uslyšav, že ho pomazali za krále na místo otce jeho; nebo miloval Chíram Davida po všecky dny.
2 Solomoni anabweza mawu awa kwa Hiramu:
Zase poslal Šalomoun k Chíramovi, řka:
3 “Inu mukudziwa kuti chifukwa cha nkhondo zimene zinkachokera ku mbali zonse kulimbana ndi abambo anga, iwo sanathe kumangira Nyumba Yehova Mulungu wawo, mpaka Yehova atawayika adani awo pansi pa ulamuliro wawo.
Ty víš, že David otec můj nemohl vystavěti domu jménu Hospodina Boha svého pro války, kteréž jej obkličovaly, dokudž Hospodin nepodložil nepřátel pod nohy jeho.
4 Koma tsopano Yehova Mulungu wanga wandipatsa mtendere mbali zonse za dziko ndipo ndilibe mdani kapena chovuta chilichonse.
Ale nyní Hospodin Bůh můj dal mi odpočinutí všudy vůkol, není žádného protivníka, ani outoku nebezpečného.
5 Choncho ine ndikufuna kumangira nyumba Yehova Mulungu wanga, monga momwe Iye anawuzira abambo anga Davide kuti, ‘Mwana wako amene ndidzamukhazike pa mpando waufumu mʼmalo mwako ndiye adzandimangire Nyumba.’
Z té příčiny, aj, úmysl mám stavěti dům jménu Hospodina Boha svého, jakož mluvil Hospodin Davidovi otci mému, řka: Syn tvůj, kteréhož posadím místo tebe na stolici tvé, onť vystaví dům ten jménu mému.
6 “Choncho lamulani kuti andidulire mikungudza ya ku Lebanoni. Anthu anga adzagwira ntchito imeneyo pamodzi ndi anthu anuwo, ndipo ine ndidzalipira anthu anuwo malipiro amene inu mungakhazikitse. Inu mukudziwa kuti ife tilibe anthu aluso locheka matabwa monga Asidoni.”
A protož nyní rozkaž, ať mi nasekají cedrů na Libánu. Budou pak služebníci moji s služebníky tvými, a mzdu služebníků tvých dám tobě, tak jakž díš. Nebo sám víš, že mezi námi není žádného, kdož by uměl sekati dříví, jako jsou Sidonští.
7 Hiramu anakondwa kwambiri atamva uthenga wa Solomoni ndipo anati, “Lero Yehova atamandike chifukwa wapatsa Davide mwana wanzeru kuti alamulire mtundu waukuluwu.”
Stalo se tedy, když uslyšel Chíram ta slova Šalomounova, že se zradoval náramně, a řekl: Požehnaný Hospodin budiž nyní, kterýž dal Davidovi syna moudrého nad tím lidem tak mnohým.
8 Tsono Hiramu anabweza mawu awa kwa Solomoni: “Ndalandira uthenga umene mwanditumizira ndipo ine ndidzachita zonse zimene mukufuna pokupatsani mitengo ya mkungudza ndi payini.
I poslal Chíram k Šalomounovi, řka: Vyrozuměl jsem, oč jsi poslal ke mně; jáť učiním všecku vůli tvou z strany dříví cedrového i jedlového.
9 Anthu anga adzatsika nayo kuchokera ku Lebanoni mpaka ku nyanja, ndipo adzayiyandamitsa pa nyanja mpaka ku malo amene munene. Kumeneko ndidzayimasula ndipo mudzayitenga. Ndipo inu mudzakwaniritsa chokhumba changa pondipatsa chakudya cha banja langa laufumu.”
Služebníci moji svezou je s Libánu až k moři, a dám je v vořích splaviti po moři až k místu tomu, kteréž mi ukážeš, a tu je složím; ty pak pobéřeš je a naplníš také vůli mou, dodávaje potravy čeledi mé.
10 Motero Hiramu anapereka kwa Solomoni mitengo yonse ya mkungudza ndi payini imene ankayifuna,
A tak dával Chíram Šalomounovi dříví cedrového a dříví jedlového, jakkoli mnoho chtěl.
11 ndipo Solomoni anamupatsa Hiramu mitanga ya tirigu 20,000 ngati chakudya cha pa nyumba yake, kuwonjezera pa migolo ya mafuta a olivi yokwana 20,000. Solomoni anapitiriza kupereka zimenezi chaka ndi chaka.
Šalomoun také dával Chíramovi dvadceti tisíc měr pšenice ku pokrmu čeledi jeho, a dvadceti tisíc měr oleje vytlačeného. To dával Šalomoun Chíramovi každého roku.
12 Yehova anamupatsa Solomoni nzeru monga momwe analonjezera. Panali ubale wa mtendere pakati pa Solomoni ndi Hiramu, ndipo awiriwa anachita pangano.
Když tedy dal Hospodin moudrost Šalomounovi, jakož mu byl zaslíbil, a byl pokoj mezi Chíramem a mezi Šalomounem, tak že mezi sebou učinili smlouvu:
13 Mfumu Solomoni inasonkhanitsa anthu ogwira ntchito ya thangata mʼdziko lonse la Israeli ndipo anthu athangatawo analipo 30,000.
Rozkázal král Šalomoun vybírati osoby ze všeho Izraele, a bylo vybraných třidceti tisíc mužů.
14 Iye ankatumiza anthu 10,000 ku Lebanoni pa mwezi mosinthanasinthana, kotero kuti ankakhala ku Lebanoniko mwezi umodzi ndipo kwawo ankakhalako miyezi iwiri. Adoniramu ndiye ankayangʼanira ogwira ntchito yathangatayo.
Z nichž posílal na Libán deset tisíců na každý měsíc, jedny po druhých. Jeden měsíc bývali na Libánu, a dva měsíce doma, Adoniram pak byl ustaven nad těmi vybranými.
15 Solomoni anali ndi anthu amtengatenga 70,000, anthu 80,000 osema miyala ku mapiri,
Měl také Šalomoun sedmdesáte tisíc nosičů, a osmdesáte tisíc těch, kteříž tesali na hoře,
16 ndi akapitawo 33,000 amene ankayangʼanira ntchitoyi ndiponso anthu ogwira ntchito zina.
Kromě předních vládařů Šalomounových, kterýchž bylo nad dílem tři tisíce a tři sta. Ti představeni byli lidem, kteříž dělali.
17 Molamulidwa ndi mfumu, anakumba ndi kusema miyala ikuluikulu kwambiri yoti akamangire maziko a Nyumba ya Mulungu.
I přikázal král, aby navozili kamení velikého, kamení nákladného k založení toho domu, a kamení tesaného,
18 Amisiri a Solomoni ndi a Hiramu ndiponso anthu a ku Gebala anasema miyala ndi kukonza matabwa ndi miyala yomangira Nyumba ya Mulungu.
Kteréž tesali kameníci Šalomounovi a kameníci Chíramovi a Gibličtí. A tak připravovali dříví i kamení k stavení domu toho.

< 1 Mafumu 5 >