< 1 Mafumu 5 >

1 Hiramu mfumu ya ku Turo atamva kuti Solomoni wadzozedwa kukhala mfumu mʼmalo mwa abambo ake Davide, anatumiza akazembe ake kwa Solomoni, chifukwa mfumu Hiramu inali pa ubale wabwino ndi Davide nthawi zonse.
A napa yueng manghai la anih a koelh uh te a yaak vaengah Tyre manghai Khiram loh a sal rhoek te Solomon taengla a tueih. Amah tue khuiah tah Khiram he David kah a lungnah la om.
2 Solomoni anabweza mawu awa kwa Hiramu:
Solomon long khaw Khiram taengla a tueih tih,
3 “Inu mukudziwa kuti chifukwa cha nkhondo zimene zinkachokera ku mbali zonse kulimbana ndi abambo anga, iwo sanathe kumangira Nyumba Yehova Mulungu wawo, mpaka Yehova atawayika adani awo pansi pa ulamuliro wawo.
“A pa David te BOEIPA loh a kho dongkah a kho khopha hmui la a khueh pah hlan hil caemrhal loh a vael dongah a Pathen BOEIPA ming la im thoh ham a coeng pawt te na ming.
4 Koma tsopano Yehova Mulungu wanga wandipatsa mtendere mbali zonse za dziko ndipo ndilibe mdani kapena chovuta chilichonse.
Tedae ka Pathen BOEIPA loh a duem sak coeng dongah kai ham tah kaepvai ah khingkhoekkung khaw om pawt tih yoekam khaw thae pawh.
5 Choncho ine ndikufuna kumangira nyumba Yehova Mulungu wanga, monga momwe Iye anawuzira abambo anga Davide kuti, ‘Mwana wako amene ndidzamukhazike pa mpando waufumu mʼmalo mwako ndiye adzandimangire Nyumba.’
BOEIPA loh a pa David taengah a thui tih, 'Na ngolkhoel dongah nang yueng la na capa te ka khueh ni. Anih loh kai ming la im a thoh bitni,’ a ti nah vanbangla, ka BOEIPA Pathen ming la im sak ham ka cai coeng he.
6 “Choncho lamulani kuti andidulire mikungudza ya ku Lebanoni. Anthu anga adzagwira ntchito imeneyo pamodzi ndi anthu anuwo, ndipo ine ndidzalipira anthu anuwo malipiro amene inu mungakhazikitse. Inu mukudziwa kuti ife tilibe anthu aluso locheka matabwa monga Asidoni.”
Te dongah uen mai lamtah Lebanon lamkah lamphai te kai hamla vung uh mai saeh. Ka sal rhoek khaw na sal rhoek taengah om uh bitni. Na sal rhoek kah thapang khaw na thui bangla namah taengah boeih kam paek bitni. Sidoni bangla thing vung ham aka ming hlang khaw kaimih taengah a om pawt te na ming.
7 Hiramu anakondwa kwambiri atamva uthenga wa Solomoni ndipo anati, “Lero Yehova atamandike chifukwa wapatsa Davide mwana wanzeru kuti alamulire mtundu waukuluwu.”
Solomon ol te Khiram yaak la a pha vaengah tah a kohoe tangkik tih, “David ham he pilnam miping sokah capa hlangcueih aka pae BOEIPA tah tihnin ah a yoethen pai,” a ti.
8 Tsono Hiramu anabweza mawu awa kwa Solomoni: “Ndalandira uthenga umene mwanditumizira ndipo ine ndidzachita zonse zimene mukufuna pokupatsani mitengo ya mkungudza ndi payini.
Te dongah Khiram loh Solomon taengla a tueih tih, “Kai taengla nan tueih te ka yaak coeng. Na ngaih boeih te tah lamphai thing neh, hmaical thing neh kan saii bitni.
9 Anthu anga adzatsika nayo kuchokera ku Lebanoni mpaka ku nyanja, ndipo adzayiyandamitsa pa nyanja mpaka ku malo amene munene. Kumeneko ndidzayimasula ndipo mudzayitenga. Ndipo inu mudzakwaniritsa chokhumba changa pondipatsa chakudya cha banja langa laufumu.”
Lebanon lamkah te ka sal rhoek loh tuipuei la han colh saeh. Te phoeiah kai ham na tueih nah hmuen hil tuipuei longah paan la kan khuen eh. Te te pahoi ka boe phoeiah tah nang loh khuen. Nang lamloh ka im kah caak ham m'pae lamtah ka kongaih te han saii,” a ti nah.
10 Motero Hiramu anapereka kwa Solomoni mitengo yonse ya mkungudza ndi payini imene ankayifuna,
Te dongah Khiram loh Solomon te lamphai thing khaw, hmaical thing khaw a ngaih bangla boeih a paek.
11 ndipo Solomoni anamupatsa Hiramu mitanga ya tirigu 20,000 ngati chakudya cha pa nyumba yake, kuwonjezera pa migolo ya mafuta a olivi yokwana 20,000. Solomoni anapitiriza kupereka zimenezi chaka ndi chaka.
Solomon loh Khiram te a im kah a caak la cang kore thawng kul, a sui situi kore pakul a paek. Te tlam te Solomon loh Khiram ham a kum, kum ah a paek.
12 Yehova anamupatsa Solomoni nzeru monga momwe analonjezera. Panali ubale wa mtendere pakati pa Solomoni ndi Hiramu, ndipo awiriwa anachita pangano.
A taengah a thui bangla BOEIPA loh Solomon te cueihnah a paek. Te dongah Khiram laklo neh Solomon laklo ah rhoepnah om tih a boktlap la moi a boh rhoi.
13 Mfumu Solomoni inasonkhanitsa anthu ogwira ntchito ya thangata mʼdziko lonse la Israeli ndipo anthu athangatawo analipo 30,000.
Israel tom kah saldong te manghai Solomon loh a khuen tih hlang thawng sawmthum te saldong la om.
14 Iye ankatumiza anthu 10,000 ku Lebanoni pa mwezi mosinthanasinthana, kotero kuti ankakhala ku Lebanoniko mwezi umodzi ndipo kwawo ankakhalako miyezi iwiri. Adoniramu ndiye ankayangʼanira ogwira ntchito yathangatayo.
Lebanon la hla khat ah thawng rha te thovaelnah la a tueih. Lebanon ah hla khat, a im ah hla nit tloeptloep om uh. Te vaengah Adoniram loh saldong rhoek a om thil.
15 Solomoni anali ndi anthu amtengatenga 70,000, anthu 80,000 osema miyala ku mapiri,
Solomon taengah hnophueih aka phuei thawng sawmrhih neh tlang ah lungto aka dae he thawng sawmrhet om.
16 ndi akapitawo 33,000 amene ankayangʼanira ntchitoyi ndiponso anthu ogwira ntchito zina.
Solomon taengah bitat aka pai thil mangpa bueng mah thawng thum ya thum lo tih bitat dongah aka tlun pilnam te a taemrhai uh.
17 Molamulidwa ndi mfumu, anakumba ndi kusema miyala ikuluikulu kwambiri yoti akamangire maziko a Nyumba ya Mulungu.
Manghai kah a uen bangla lung len khaw, lung vang khaw, lung rhaih khaw, im a toong nah ham a puen uh.
18 Amisiri a Solomoni ndi a Hiramu ndiponso anthu a ku Gebala anasema miyala ndi kukonza matabwa ndi miyala yomangira Nyumba ya Mulungu.
Solomon kah imsa rhoek neh Khiram kah imsa rhoek long khaw, Ghiblii rhoek long khaw a saek uh. Te dongah im sak nah ham thing neh lungto te a tawn uh.

< 1 Mafumu 5 >