< 1 Mafumu 4 >

1 Ndipo Mfumu Solomoni inakhala mfumu ya Aisraeli onse.
А цар Соломун цароваше над свим Израиљем.
2 Nduna zake zikuluzikulu zinali izi: Azariya mwana wa Zadoki anali wansembe;
А ово беху кнезови његови: Азарија, син Садоков, намесник;
3 Elihorefe ndi Ahiya, ana a Sisa, anali alembi; Yehosafati mwana wa Ahiludi, anali mlembi wa zochitika;
Елиореф и Ахија, синови Сисини, писари; Јосафат, син Ахилудов, паметар;
4 Benaya mwana wa Yehoyada, anali mtsogoleri wa ankhondo; Zadoki ndi Abiatara, anali ansembe;
Венаја, син Јодајев, војвода; а Садок и Авијатар свештеници;
5 Azariya mwana wa Natani, anali woyangʼanira nduna za mʼzigawo; Zabudi mwana wa Natani, anali wansembe ndi bwenzi la mfumu;
А Азарија син Натанов, беше над приставима; а Завуд, син Натанов, први већник, пријатељ царев;
6 Ahisara, anali mkulu woyangʼanira nyumba ya mfumu; Adoniramu mwana wa Abida, anali mkulu woyangʼanira ntchito za thangata.
А Ахисар управитељ дворски; а Адонирам син Авдин над царским посленицима.
7 Solomoni analinso ndi abwanamkubwa khumi ndi awiri amene ankayangʼanira zigawo zonse za dziko la Israeli. Iwo ankapereka chakudya kwa mfumu ndiponso ku banja laufumu. Bwanamkubwa aliyense ankapereka chakudya mwezi umodzi pa chaka.
И имаше Соломун дванаест пристава по свему Израиљу, који храњаху цара и сав дом његов; по месец дана у години сваки беше дужан хранити.
8 Mayina awo ndi awa: Beni-Huri, wa ku dziko la mapiri la Efereimu;
А ово су им имена: Син Уров у гори Јефремовој;
9 Beni-Dekeri, woyangʼanira mizinda ya Makazi, Saalibimu, Beti-Semesi ndi Eloni Beti-Hanani;
Син Декеров у Макасу и у Салвиму и Вет-Семесу и Елону вет-анатском;
10 Beni-Hesedi, woyangʼanira mizinda ya Aruboti (Soko ndi dziko lonse la Heferi);
Син Еседов у Арувоту; под њим беше Сохот и сва земља Еферова;
11 Beni-Abinadabu, woyangʼanira Nafoti Dori (iye anakwatira Tafati mwana wa Solomoni);
Син Авинадавов над свим крајем дорским; жена му беше Тафата, кћи Соломунова;
12 Baana mwana wa Ahiludi, anali woyangʼanira Taanaki ndi Megido, ndi ku Beti Sani konse, kufupi ndi ku Zaretani kumunsi kwa Yezireeli, kuyambira ku Beti-Seani mpaka ku Abeli-Mehola kukafika mpaka ku Yokineamu;
Вана, син Ахилудов над Танахом и Мегидоном и свим Вет-Саном, који је до Сартане под Језраелом, од Вет-Сана до Авел-Меола, до преко Јок-Меама;
13 Beni-Geberi, anali woyangʼanira Ramoti Giliyadi (midzi ya Yairi inali ya mwana wa Manase ku Giliyadi, pamodzinso ndi chigawo cha Arigobu ku Basani ndiponso mizinda yake yayikulu makumi asanu ndi umodzi yokhala ndi malinga ndi mipiringidzo yamkuwa).
Син Геверов у Рамоту галадском; имаше села Јаира сина Манасијиног у Галаду и крај арговски у Васану, шездесет великих градова са зидовима и преворницама бронзаним;
14 Ahinadabu mwana wa Ido, anali woyangʼanira Mahanaimu;
Ахинадав, син Идов у Маханајиму;
15 Ahimaazi anali woyangʼanira Nafutali (iyeyu anakwatira Basemati mwana wa Solomoni);
Ахимас у Нефталиму; и он беше ожењен кћерју Соломуновом Васематом;
16 Baana mwana wa Husai, anali woyangʼanira Aseri ndi Bealoti;
Вана син Хусајев у Асиру и у Алоту;
17 Yehosafati mwana wa Paruwa, anali woyangʼanira Isakara;
Јосафат син Фарујин у Исахару;
18 Simei mwana wa Ela, anali woyangʼanira Benjamini;
Симеј син Илин у Венијамину;
19 Geberi mwana wa Uri, anali woyangʼanira Giliyadi (dziko la Sihoni mfumu ya Aamori ndi dziko la Ogi mfumu ya Basani). Iye ankayangʼanira chigawo chonsechi yekha.
Гевер, син Уријев у земљи галадској, у земљи Сиона цара аморејског и Ога цара васанског; један беше пристав у тој земљи.
20 Anthu a ku Yuda ndi ku Israeli anali ochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja. Ankadya ndi kumwa ndipo ankasangalala.
Јуде и Израиља беше много као песка покрај мора; и јеђаху и пијаху и весељаху се.
21 Ndipo Solomoni analamulira mayiko onse kuyambira ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku dziko la Afilisti, kukafika mpaka ku malire a dziko la Igupto. Mayikowa ankabweretsa mphatso ndipo anali pansi pa ulamuliro wa Solomoni moyo wake wonse.
А Соломун владаше свим царствима од реке до земље филистејске и до међе мисирске, и доношаху даре и служаху Соломуна свега века његовог.
22 Chakudya cha tsiku ndi tsiku cha Solomoni chinali madengu 150 a ufa wosalala ndi madengu 300 a mgayiwa,
А храна Соломунова беше на дан тридесет кора белог брашна, и шездесет кора другог брашна;
23 ngʼombe khumi zonenepa zodyetsera mʼkhola, ngʼombe za ku busa makumi awiri, ndiponso nkhosa ndi mbuzi 100, pamodzinso ndi mbawala, agwape, mphoyo ndi mbalame zoweta zonona.
Двадесет волова угојених и двадесет с паше, и сто оваца, осим јелена и срна и дивокоза и угојених птица.
24 Pakuti ankalamulira dziko lonse la kumadzulo kwa mtsinje wa Yufurate kuyambira ku Tifisa mpaka ku Gaza, mafumu onse a kumadzulo kwa Mtsinje, ndipo anali pa mtendere ndi mayiko onse ozungulira.
Јер он владаше свуда с ове стране реке од Тапсе до Газе, над свим царствима с ове стране реке, и беше миран са свих страна унаоколо.
25 Pa nthawi ya Solomoni, Yuda ndi Israeli anali pa mtendere, kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba. Munthu aliyense ankangodzikhalira pansi pa mpesa wake ndi mtengo wake wa mkuyu.
И живљаху Јуда и Израиљ без страха, сваки под својом лозом и под својом смоквом, од Дана до Вирсавеје, свега века Соломуновог.
26 Solomoni anali ndi zipinda 4,000 zodyeramo akavalo okoka magaleta ake ndi anthu 12,000 oyendetsa magaleta.
И имаше Соломун четрдесет хиљада коња за јаслима за кола своја, и двадесет хиљада коњика.
27 Abwanamkubwa a zigawo aja, aliyense pa mwezi wake, ankapereka chakudya cha Mfumu Solomoni ndi cha anthu onse amene ankadya naye. Iwo ankaonetsetsa kuti pasasowe kalikonse.
И пристави храњаху цара Соломуна и све који долажаху за сто цара Соломуна, сваки свог месеца, и не даваху да чега понестане.
28 Ankabweretsanso ku malo ake ofunikira muyeso wawo wa barele ndi udzu wa akavalo okoka magaleta ndiponso akavalo ena.
А јечам и сламу за коње и за мазге доношаху на место где беху, сваки како му беше одређено.
29 Mulungu anamupatsa Solomoni nzeru ndi luntha losaneneka ndipo nzeru zake zinali zochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
И Бог даде мудрост Соломуну и разум врло велик и срце пространо као песак на брегу морском.
30 Nzeru za Solomoni zinali zoposa nzeru za anthu onse a Kummawa ndiponso nzeru zonse za ku Igupto.
Јер мудрост Соломунова беше већа од мудрости свих источних народа и од све мудрости мисирске.
31 Iye anali wanzeru kuposa munthu wina aliyense, kuposa ngakhale Etani wa banja la Ezara, Hemani, Kalikoli ndi Darida, ana a Maholi. Ndipo mbiri yake inamveka kwa mitundu yonse ya anthu ozungulira.
Мудрији беше од сваког човека, и од Етана Езраита и од Емана и од Халкола и од Дарде, синова Маолових; и разгласи се име његово по свим народима унаоколо.
32 Solomoni anapeka miyambi 3,000 ndi kulemba nyimbo 1,005.
И изговори три хиљаде прича, и беше песама његових хиљаду и пет.
33 Iye ankaphunzitsa za mitengo, kuyambira mtengo wa mkungudza wa ku Lebanoni mpaka kachitsamba ka hisope khomera pa khoma. Iye ankaphunzitsanso za nyama ndi mbalame, zinthu zokwawa pansi ndiponso za nsomba.
Говорио је и о дрвећу, од кедра на Ливану до исопа који ниче из зида; говорио је и о стоци и о птицама и о бубинама и о рибама.
34 Anthu a mitundu yonse ankabwera kudzamva nzeru za Solomoni. Anthu amenewa ankatumizidwa ndi mafumu onse a dziko lapansi amene anamvapo za nzeru zakezo.
И долажаху од свих народа да чују мудрост Соломунову, од свих царстава на земљи, који чуше за мудрост његову.

< 1 Mafumu 4 >