< 1 Mafumu 4 >

1 Ndipo Mfumu Solomoni inakhala mfumu ya Aisraeli onse.
Tak więc król Salomon był królem nad całym Izraelem.
2 Nduna zake zikuluzikulu zinali izi: Azariya mwana wa Zadoki anali wansembe;
A oto jego dostojnicy: Azariasz, syn Sadoka, kapłan.
3 Elihorefe ndi Ahiya, ana a Sisa, anali alembi; Yehosafati mwana wa Ahiludi, anali mlembi wa zochitika;
Elichoref i Achiasz, synowie Sziszy, pisarze; Jehoszafat, syn Achiluda, kronikarz.
4 Benaya mwana wa Yehoyada, anali mtsogoleri wa ankhondo; Zadoki ndi Abiatara, anali ansembe;
Benajasz, syn Jehojady, dowódca wojska; Sadok i Abiatar, kapłani.
5 Azariya mwana wa Natani, anali woyangʼanira nduna za mʼzigawo; Zabudi mwana wa Natani, anali wansembe ndi bwenzi la mfumu;
Azariasz, syn Natana, przełożony namiestników, Zabud, syn Natana, naczelny dostojnik, przyjaciel króla.
6 Ahisara, anali mkulu woyangʼanira nyumba ya mfumu; Adoniramu mwana wa Abida, anali mkulu woyangʼanira ntchito za thangata.
Achiszar, przełożony dworu, i Adoniram, syn Abdy, odpowiedzialny za daninę.
7 Solomoni analinso ndi abwanamkubwa khumi ndi awiri amene ankayangʼanira zigawo zonse za dziko la Israeli. Iwo ankapereka chakudya kwa mfumu ndiponso ku banja laufumu. Bwanamkubwa aliyense ankapereka chakudya mwezi umodzi pa chaka.
Salomon miał też dwunastu namiestników nad całym Izraelem, którzy zaopatrywali króla i cały jego dwór w żywność. Każdy z nich przez jeden miesiąc w roku miał dostarczać żywność.
8 Mayina awo ndi awa: Beni-Huri, wa ku dziko la mapiri la Efereimu;
A oto ich imiona: syn Chura – na górze Efraim;
9 Beni-Dekeri, woyangʼanira mizinda ya Makazi, Saalibimu, Beti-Semesi ndi Eloni Beti-Hanani;
Syn Dekara – w Makas, Szaalbim – w Bet-Szemesz i Elon-Bet-Chanan;
10 Beni-Hesedi, woyangʼanira mizinda ya Aruboti (Soko ndi dziko lonse la Heferi);
Syn Cheseda – w Arubot, do niego [należało] Soko i cała ziemia Chefer;
11 Beni-Abinadabu, woyangʼanira Nafoti Dori (iye anakwatira Tafati mwana wa Solomoni);
Syn Abinadaba – nad całym obszarem Dor; jego żoną była Tafat, córka Salomona.
12 Baana mwana wa Ahiludi, anali woyangʼanira Taanaki ndi Megido, ndi ku Beti Sani konse, kufupi ndi ku Zaretani kumunsi kwa Yezireeli, kuyambira ku Beti-Seani mpaka ku Abeli-Mehola kukafika mpaka ku Yokineamu;
Baana, syn Achiluda, [do którego należały] Tanak i Megiddo oraz całe Bet-Szean, które leży przy Sartan pod Jizreelem, od Bet-Szean aż do Abel-Mechola, aż poza Jokmeam.
13 Beni-Geberi, anali woyangʼanira Ramoti Giliyadi (midzi ya Yairi inali ya mwana wa Manase ku Giliyadi, pamodzinso ndi chigawo cha Arigobu ku Basani ndiponso mizinda yake yayikulu makumi asanu ndi umodzi yokhala ndi malinga ndi mipiringidzo yamkuwa).
Syn Geber – w Ramot-Gilead, do niego należały wsie Jaira, syna Manassesa, które [leżą] w Gileadzie. Do niego też należała kraina Argob, która [jest] w Baszanie – sześćdziesiąt wielkich miast mających mury i brązowe rygle.
14 Ahinadabu mwana wa Ido, anali woyangʼanira Mahanaimu;
Achinadab, syn Iddo – w Machanaim.
15 Ahimaazi anali woyangʼanira Nafutali (iyeyu anakwatira Basemati mwana wa Solomoni);
Achimaas – w Neftalim; on też pojął za żonę Basemat, córkę Salomona.
16 Baana mwana wa Husai, anali woyangʼanira Aseri ndi Bealoti;
Baana, syn Chuszaia – w Aszer i Alot.
17 Yehosafati mwana wa Paruwa, anali woyangʼanira Isakara;
Jehoszafat, syn Paruacha – w Issacharze.
18 Simei mwana wa Ela, anali woyangʼanira Benjamini;
Szimei, syn Eli – w Beniaminie.
19 Geberi mwana wa Uri, anali woyangʼanira Giliyadi (dziko la Sihoni mfumu ya Aamori ndi dziko la Ogi mfumu ya Basani). Iye ankayangʼanira chigawo chonsechi yekha.
Geber, syn Uriego – w ziemi Gilead, ziemi Sichona, króla Amorytów, i Oga, króla Baszanu. Był on jedynym namiestnikiem tej ziemi.
20 Anthu a ku Yuda ndi ku Israeli anali ochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja. Ankadya ndi kumwa ndipo ankasangalala.
A Juda i Izrael [byli] tak liczni jak piasek nad morzem. Jedli, pili i radowali się.
21 Ndipo Solomoni analamulira mayiko onse kuyambira ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku dziko la Afilisti, kukafika mpaka ku malire a dziko la Igupto. Mayikowa ankabweretsa mphatso ndipo anali pansi pa ulamuliro wa Solomoni moyo wake wonse.
A Salomon panował nad wszystkimi królestwami od rzeki aż do ziemi Filistynów, aż do granicy Egiptu. Płaciły one daninę i służyły Salomonowi po wszystkie dni jego życia.
22 Chakudya cha tsiku ndi tsiku cha Solomoni chinali madengu 150 a ufa wosalala ndi madengu 300 a mgayiwa,
Wyżywienie dla Salomona na jeden dzień wynosiło trzydzieści kor najlepszej mąki i sześćdziesiąt kor zwykłej mąki.
23 ngʼombe khumi zonenepa zodyetsera mʼkhola, ngʼombe za ku busa makumi awiri, ndiponso nkhosa ndi mbuzi 100, pamodzinso ndi mbawala, agwape, mphoyo ndi mbalame zoweta zonona.
Dziesięć tucznych wołów, dwadzieścia wołów z pastwiska, sto owiec, nie licząc jeleni, saren, danieli i tucznego drobiu.
24 Pakuti ankalamulira dziko lonse la kumadzulo kwa mtsinje wa Yufurate kuyambira ku Tifisa mpaka ku Gaza, mafumu onse a kumadzulo kwa Mtsinje, ndipo anali pa mtendere ndi mayiko onse ozungulira.
Panował bowiem nad całym obszarem z tej strony rzeki, od Tifsach aż do Gazy, nad wszystkimi królami z tej strony rzeki. I miał pokój ze wszystkich stron dokoła.
25 Pa nthawi ya Solomoni, Yuda ndi Israeli anali pa mtendere, kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba. Munthu aliyense ankangodzikhalira pansi pa mpesa wake ndi mtengo wake wa mkuyu.
Juda i Izrael mieszkali bezpiecznie, każdy pod swoją winoroślą i pod swoim drzewem figowym, od Dan aż do Beer-Szeby, po wszystkie dni Salomona.
26 Solomoni anali ndi zipinda 4,000 zodyeramo akavalo okoka magaleta ake ndi anthu 12,000 oyendetsa magaleta.
Salomon miał też czterdzieści tysięcy koni w stajniach do swoich rydwanów i dwanaście tysięcy jeźdźców.
27 Abwanamkubwa a zigawo aja, aliyense pa mwezi wake, ankapereka chakudya cha Mfumu Solomoni ndi cha anthu onse amene ankadya naye. Iwo ankaonetsetsa kuti pasasowe kalikonse.
Namiestnicy, każdy w swoim miesiącu, zaopatrywali w żywność króla Salomona i wszystkich, którzy przychodzili do stołu króla Salomona, tak że niczego nie brakowało.
28 Ankabweretsanso ku malo ake ofunikira muyeso wawo wa barele ndi udzu wa akavalo okoka magaleta ndiponso akavalo ena.
Także jęczmień i słomę dla koni i mułów sprowadzali na to miejsce, gdzie [one] przebywały, każdy według swojego obowiązku.
29 Mulungu anamupatsa Solomoni nzeru ndi luntha losaneneka ndipo nzeru zake zinali zochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
A Bóg dał Salomonowi mądrość i bardzo wielkie zrozumienie oraz przestronność serca jak piasek, który jest na brzegu morskim.
30 Nzeru za Solomoni zinali zoposa nzeru za anthu onse a Kummawa ndiponso nzeru zonse za ku Igupto.
I mądrość Salomona była większa od mądrości wszystkich narodów wschodnich i od wszelkiej mądrości Egiptu.
31 Iye anali wanzeru kuposa munthu wina aliyense, kuposa ngakhale Etani wa banja la Ezara, Hemani, Kalikoli ndi Darida, ana a Maholi. Ndipo mbiri yake inamveka kwa mitundu yonse ya anthu ozungulira.
Był mądrzejszy niż wszyscy ludzie, niż Etan Ezrachita, Heman, Kalkol i Darda, synowie Machola. Był sławny wśród wszystkich okolicznych narodów.
32 Solomoni anapeka miyambi 3,000 ndi kulemba nyimbo 1,005.
Wypowiedział trzy tysiące przysłów, a jego pieśni było tysiąc pięć.
33 Iye ankaphunzitsa za mitengo, kuyambira mtengo wa mkungudza wa ku Lebanoni mpaka kachitsamba ka hisope khomera pa khoma. Iye ankaphunzitsanso za nyama ndi mbalame, zinthu zokwawa pansi ndiponso za nsomba.
Wypowiadał się też o drzewach, [poczynając] od cedru na Libanie aż do hizopu, który wyrasta z muru. Mówił też o zwierzętach, ptakach, płazach i rybach.
34 Anthu a mitundu yonse ankabwera kudzamva nzeru za Solomoni. Anthu amenewa ankatumizidwa ndi mafumu onse a dziko lapansi amene anamvapo za nzeru zakezo.
Przychodzili więc [ludzie] ze wszystkich narodów, aby słuchać mądrości Salomona, od wszystkich królów ziemi, którzy słyszeli o jego mądrości.

< 1 Mafumu 4 >