< 1 Mafumu 4 >

1 Ndipo Mfumu Solomoni inakhala mfumu ya Aisraeli onse.
Ngakho inkosi uSolomoni yaba yinkosi phezu kukaIsrayeli wonke.
2 Nduna zake zikuluzikulu zinali izi: Azariya mwana wa Zadoki anali wansembe;
Lalezi yiziphathamandla ayelazo: UAzariya indodana kaZadoki wayengumpristi;
3 Elihorefe ndi Ahiya, ana a Sisa, anali alembi; Yehosafati mwana wa Ahiludi, anali mlembi wa zochitika;
uElihorefi loAhiya amadodana kaShisha babengababhali; uJehoshafathi indodana kaAhiludi wayengumabhalane;
4 Benaya mwana wa Yehoyada, anali mtsogoleri wa ankhondo; Zadoki ndi Abiatara, anali ansembe;
loBhenaya indodana kaJehoyada wayephezu kwebutho; loZadoki loAbhiyatha babengabapristi;
5 Azariya mwana wa Natani, anali woyangʼanira nduna za mʼzigawo; Zabudi mwana wa Natani, anali wansembe ndi bwenzi la mfumu;
loAzariya indodana kaNathani wayephezu kwabaphathi; uZabudi indodana kaNathani wayengumphathi omkhulu, umngane wenkosi;
6 Ahisara, anali mkulu woyangʼanira nyumba ya mfumu; Adoniramu mwana wa Abida, anali mkulu woyangʼanira ntchito za thangata.
loAhishari wayengumlawuli wendlu; loAdoniramu indodana kaAbida wayephezu kwemithelo.
7 Solomoni analinso ndi abwanamkubwa khumi ndi awiri amene ankayangʼanira zigawo zonse za dziko la Israeli. Iwo ankapereka chakudya kwa mfumu ndiponso ku banja laufumu. Bwanamkubwa aliyense ankapereka chakudya mwezi umodzi pa chaka.
USolomoni wayelabaphathi abalitshumi lambili phezu kukaIsrayeli wonke, ababedingela inkosi lendlu yayo ukudla, ngulowo lalowo ngenyanga yakhe ngomnyaka wadinga ukudla.
8 Mayina awo ndi awa: Beni-Huri, wa ku dziko la mapiri la Efereimu;
Lala ngamabizo abo: UBeni-Huri entabeni zakoEfrayimi.
9 Beni-Dekeri, woyangʼanira mizinda ya Makazi, Saalibimu, Beti-Semesi ndi Eloni Beti-Hanani;
UBeni-Dekeri eMakazi leShahalibimi leBeti-Shemeshi leEloni-Beti-Hanani.
10 Beni-Hesedi, woyangʼanira mizinda ya Aruboti (Soko ndi dziko lonse la Heferi);
UBeni-Hesedi eArubothi, eleSoko lelizwe lonke leHeferi.
11 Beni-Abinadabu, woyangʼanira Nafoti Dori (iye anakwatira Tafati mwana wa Solomoni);
UBeni-Abinadaba wayelelizwe lonke leDori; uTafathi indodakazi kaSolomoni wayengumkakhe.
12 Baana mwana wa Ahiludi, anali woyangʼanira Taanaki ndi Megido, ndi ku Beti Sani konse, kufupi ndi ku Zaretani kumunsi kwa Yezireeli, kuyambira ku Beti-Seani mpaka ku Abeli-Mehola kukafika mpaka ku Yokineamu;
UBahana indodana kaAhiludi wayeleThahanakhi leMegido layo yonke iBeti-Sheyani, eseceleni kweZarethani ngaphansi kweJizereyeli, kusukela eBeti-Sheyani kuze kube seAbeli-Mehola, kuze kube ngaphetsheya kweJokimeyama.
13 Beni-Geberi, anali woyangʼanira Ramoti Giliyadi (midzi ya Yairi inali ya mwana wa Manase ku Giliyadi, pamodzinso ndi chigawo cha Arigobu ku Basani ndiponso mizinda yake yayikulu makumi asanu ndi umodzi yokhala ndi malinga ndi mipiringidzo yamkuwa).
UBeni-Geberi eRamothi-Gileyadi wayelemizi kaJayiri indodana kaManase, eseGileyadi, wayelelizwe leArigobi, eliseBashani, imizi engamatshumi ayisithupha emikhulu elemiduli lemigoqo yethusi.
14 Ahinadabu mwana wa Ido, anali woyangʼanira Mahanaimu;
UAhinadaba indodana kaIdo eMahanayimi.
15 Ahimaazi anali woyangʼanira Nafutali (iyeyu anakwatira Basemati mwana wa Solomoni);
UAhimahazi wayekoNafithali; laye wathatha uBasemathi indodakazi kaSolomoni abe ngumkakhe.
16 Baana mwana wa Husai, anali woyangʼanira Aseri ndi Bealoti;
UBahana indodana kaHushayi wayekoAsheri leAlothi.
17 Yehosafati mwana wa Paruwa, anali woyangʼanira Isakara;
UJehoshafathi indodana kaParuwa wayekoIsakari.
18 Simei mwana wa Ela, anali woyangʼanira Benjamini;
UShimeyi indodana kaEla wayekoBhenjamini.
19 Geberi mwana wa Uri, anali woyangʼanira Giliyadi (dziko la Sihoni mfumu ya Aamori ndi dziko la Ogi mfumu ya Basani). Iye ankayangʼanira chigawo chonsechi yekha.
UGeberi indodana kaUri wayeselizweni leGileyadi, ilizwe likaSihoni inkosi yamaAmori, lelikaOgi inkosi yeBashani. Njalo wayenguye yedwa umphathi kulelolizwe.
20 Anthu a ku Yuda ndi ku Israeli anali ochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja. Ankadya ndi kumwa ndipo ankasangalala.
UJuda loIsrayeli babebanengi njengetshebetshebe elingaselwandle ngobunengi, besidla, benatha, bethokoza.
21 Ndipo Solomoni analamulira mayiko onse kuyambira ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku dziko la Afilisti, kukafika mpaka ku malire a dziko la Igupto. Mayikowa ankabweretsa mphatso ndipo anali pansi pa ulamuliro wa Solomoni moyo wake wonse.
USolomoni wayesebusa phezu kwayo yonke imibuso kusukela emfuleni kuze kufike elizweni lamaFilisti kuze kufike emngceleni weGibhithe; babeletha izipho, babemsebenzela uSolomoni zonke izinsuku zempilo yakhe.
22 Chakudya cha tsiku ndi tsiku cha Solomoni chinali madengu 150 a ufa wosalala ndi madengu 300 a mgayiwa,
Njalo ukudla kukaSolomoni ngosuku olulodwa kwakungamakhori angamatshumi amathathu empuphu ecolekileyo, lamakori angamatshumi ayisithupha empuphu,
23 ngʼombe khumi zonenepa zodyetsera mʼkhola, ngʼombe za ku busa makumi awiri, ndiponso nkhosa ndi mbuzi 100, pamodzinso ndi mbawala, agwape, mphoyo ndi mbalame zoweta zonona.
inkabi ezilitshumi ezinonisiweyo, lenkabi ezingamatshumi amabili zemadlelweni, lezimvu ezilikhulu, ngaphandle kwendluzele, lemiziki, lemiziki elempondo ezilembaxambaxa, lenyoni ezinonisiweyo.
24 Pakuti ankalamulira dziko lonse la kumadzulo kwa mtsinje wa Yufurate kuyambira ku Tifisa mpaka ku Gaza, mafumu onse a kumadzulo kwa Mtsinje, ndipo anali pa mtendere ndi mayiko onse ozungulira.
Ngoba wayebusa phezu kwalo lonke nganeno komfula, kusukela eTifisa kusiya eGaza, laphezu kwawo wonke amakhosi nganeno komfula, njalo wayelokuthula kuzo zonke inhlangothi zakhe ezizingelezeleyo.
25 Pa nthawi ya Solomoni, Yuda ndi Israeli anali pa mtendere, kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba. Munthu aliyense ankangodzikhalira pansi pa mpesa wake ndi mtengo wake wa mkuyu.
UJuda loIsrayeli bahlala-ke bevikelekile, ngulowo lalowo ngaphansi kwesivini sakhe langaphansi komkhiwa wakhe, kusukela koDani kuze kufike eBherishebha, zonke izinsuku zikaSolomoni.
26 Solomoni anali ndi zipinda 4,000 zodyeramo akavalo okoka magaleta ake ndi anthu 12,000 oyendetsa magaleta.
Njalo uSolomoni wayelezindlwana zamabhiza enqola zakhe ezizinkulungwane ezingamatshumi amane, labagadi bamabhiza abazinkulungwane ezilitshumi lambili.
27 Abwanamkubwa a zigawo aja, aliyense pa mwezi wake, ankapereka chakudya cha Mfumu Solomoni ndi cha anthu onse amene ankadya naye. Iwo ankaonetsetsa kuti pasasowe kalikonse.
Lalabobaphathi badingela inkosi uSolomoni ukudla, laye wonke osondela etafuleni lenkosi uSolomoni, ngulowo lalowo ngenyanga yakhe; kabatshiyanga kusweleke lutho.
28 Ankabweretsanso ku malo ake ofunikira muyeso wawo wa barele ndi udzu wa akavalo okoka magaleta ndiponso akavalo ena.
Lebhali lamahlanga awamabhiza lawamabhiza alejubane bakuletha endaweni lapho eyayifanele kube khona, ngulowo lalowo njengemfanelo yakhe.
29 Mulungu anamupatsa Solomoni nzeru ndi luntha losaneneka ndipo nzeru zake zinali zochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
UNkulunkulu wasemnika uSolomoni inhlakanipho lokuqedisisa okukhulu kakhulu, lobubanzi benhliziyo, njengetshebetshebe elisekhunjini lolwandle.
30 Nzeru za Solomoni zinali zoposa nzeru za anthu onse a Kummawa ndiponso nzeru zonse za ku Igupto.
Lenhlakanipho kaSolomoni yayinkulu kulenhlakanipho yawo wonke amadodana empumalanga, lakulenhlakanipho yonke yeGibhithe.
31 Iye anali wanzeru kuposa munthu wina aliyense, kuposa ngakhale Etani wa banja la Ezara, Hemani, Kalikoli ndi Darida, ana a Maholi. Ndipo mbiri yake inamveka kwa mitundu yonse ya anthu ozungulira.
Ngoba wayehlakaniphile kulabo bonke abantu, okwedlula uEthani umEzira loHemani loKalikoli loDarida amadodana kaMaholi; lebizo lakhe lalisezizweni zonke inhlangothi zonke.
32 Solomoni anapeka miyambi 3,000 ndi kulemba nyimbo 1,005.
Waseqamba izaga ezizinkulungwane ezintathu, lengoma zakhe zaziyinkulungwane lanhlanu.
33 Iye ankaphunzitsa za mitengo, kuyambira mtengo wa mkungudza wa ku Lebanoni mpaka kachitsamba ka hisope khomera pa khoma. Iye ankaphunzitsanso za nyama ndi mbalame, zinthu zokwawa pansi ndiponso za nsomba.
Wasekhuluma ngezihlahla, kusukela esihlahleni somsedari oseLebhanoni kuze kufike kuhisope emila iphuma emdulini; wakhuluma langezinyamazana langezinyoni langezihuquzelayo langezinhlanzi.
34 Anthu a mitundu yonse ankabwera kudzamva nzeru za Solomoni. Anthu amenewa ankatumizidwa ndi mafumu onse a dziko lapansi amene anamvapo za nzeru zakezo.
Kwasekufika abavela ezizweni zonke ukuzwa inhlakanipho kaSolomoni, bevela emakhosini wonke omhlaba ayezwe ngenhlakanipho yakhe.

< 1 Mafumu 4 >