< 1 Mafumu 4 >

1 Ndipo Mfumu Solomoni inakhala mfumu ya Aisraeli onse.
PELA i alii ai o Solomona maluna o ka Iseraela a pau.
2 Nduna zake zikuluzikulu zinali izi: Azariya mwana wa Zadoki anali wansembe;
Eia hoi kona mau luna, o Azaria ke keiki a Zadoka ke kahuna.
3 Elihorefe ndi Ahiya, ana a Sisa, anali alembi; Yehosafati mwana wa Ahiludi, anali mlembi wa zochitika;
O Elihorepa a me Ahia na keiki a Sisa he mau kakauolelo; o Iehosapata ke keiki a Alihuda, ke kakauhana.
4 Benaya mwana wa Yehoyada, anali mtsogoleri wa ankhondo; Zadoki ndi Abiatara, anali ansembe;
A o Benaia ke keiki a Iehoiada, maluna o ka poe koa; a Zadoka a me Abiatara he mau kahuna pule laua.
5 Azariya mwana wa Natani, anali woyangʼanira nduna za mʼzigawo; Zabudi mwana wa Natani, anali wansembe ndi bwenzi la mfumu;
A o Azaria ke keiki a Natana maluna o na luna; a o Zabuda ke keiki a Natana, kekahi luna punahele a ke alii.
6 Ahisara, anali mkulu woyangʼanira nyumba ya mfumu; Adoniramu mwana wa Abida, anali mkulu woyangʼanira ntchito za thangata.
A o Ahisara maluna o ka hale; o Adonirama ke keiki a Abeda maluna o ka waiwai hookupu.
7 Solomoni analinso ndi abwanamkubwa khumi ndi awiri amene ankayangʼanira zigawo zonse za dziko la Israeli. Iwo ankapereka chakudya kwa mfumu ndiponso ku banja laufumu. Bwanamkubwa aliyense ankapereka chakudya mwezi umodzi pa chaka.
A ia Solomona na luna he umikumamalua maluna o ka Iseraela a pau, na mea hoomakaukau i ka ai na ke alii a na ko kona hale, kela kanaka keia kanaka i kona malama o ka makahiki i hoomakaukau ai.
8 Mayina awo ndi awa: Beni-Huri, wa ku dziko la mapiri la Efereimu;
Eia ko lakou mau inoa, o Benehura ma ka mauna o Eperaima;
9 Beni-Dekeri, woyangʼanira mizinda ya Makazi, Saalibimu, Beti-Semesi ndi Eloni Beti-Hanani;
O Benedekera, ma Makaza, a me Salabima, a me Betesemeta, a me Elonabetehanana.
10 Beni-Hesedi, woyangʼanira mizinda ya Aruboti (Soko ndi dziko lonse la Heferi);
O Beneheseda ma Anibota, ia ia o Soko, a me ka aina a pau o Hepera.
11 Beni-Abinadabu, woyangʼanira Nafoti Dori (iye anakwatira Tafati mwana wa Solomoni);
O Benabinadaba ma ka aina a pau o Dora, ia ia o Tapata ke kaikamahine a Solomona i wahine.
12 Baana mwana wa Ahiludi, anali woyangʼanira Taanaki ndi Megido, ndi ku Beti Sani konse, kufupi ndi ku Zaretani kumunsi kwa Yezireeli, kuyambira ku Beti-Seani mpaka ku Abeli-Mehola kukafika mpaka ku Yokineamu;
A o Baana ke keiki a Ahiluda, ia ia Taanaka, a me Megido, a me Beteseana a pau, e pili ana i Zaretana, malalo o Iezereela, mai Beteseana aku a hiki i Abelamahola a ma o aku o Iokeneama.
13 Beni-Geberi, anali woyangʼanira Ramoti Giliyadi (midzi ya Yairi inali ya mwana wa Manase ku Giliyadi, pamodzinso ndi chigawo cha Arigobu ku Basani ndiponso mizinda yake yayikulu makumi asanu ndi umodzi yokhala ndi malinga ndi mipiringidzo yamkuwa).
A o Benegebera ma Ramota Gileada, ia ia na kauhale o Iaira ke keiki a Manase na wahi ma Gileada; ia ia hoi ka aina o Aregoba kahi ma Basana, he kanaono na kulanakauhale nui me na pa, a me na kaola keleawe:
14 Ahinadabu mwana wa Ido, anali woyangʼanira Mahanaimu;
A o Ahinadaba ke keiki a Ido, ia ia Mahanaima:
15 Ahimaazi anali woyangʼanira Nafutali (iyeyu anakwatira Basemati mwana wa Solomoni);
Ahimiaza ma Napetali; ua lawe hoi oia ia Basemata, ke kaikamahine a Solomona i wahine;
16 Baana mwana wa Husai, anali woyangʼanira Aseri ndi Bealoti;
A o Baana ke keiki a Husai ma Asera a me Alota;
17 Yehosafati mwana wa Paruwa, anali woyangʼanira Isakara;
O Iehosapata ke keiki a Parua ma Isakara;
18 Simei mwana wa Ela, anali woyangʼanira Benjamini;
O Simei ke keiki a Ela ma Beniamina;
19 Geberi mwana wa Uri, anali woyangʼanira Giliyadi (dziko la Sihoni mfumu ya Aamori ndi dziko la Ogi mfumu ya Basani). Iye ankayangʼanira chigawo chonsechi yekha.
O Gebera ke keiki a Uri ma ka aina o Gileada, ka aina o Sihona ke alii o ka Amora, a me Oga ke alii o Basana; oia wale no ka luna ma kela aina.
20 Anthu a ku Yuda ndi ku Israeli anali ochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja. Ankadya ndi kumwa ndipo ankasangalala.
He lehulehu ka Iuda, a me ka Iseraela, e like me ka one ma kahakai i ka nui, e ai ana, a e inu ana, a e hoolealea ana.
21 Ndipo Solomoni analamulira mayiko onse kuyambira ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku dziko la Afilisti, kukafika mpaka ku malire a dziko la Igupto. Mayikowa ankabweretsa mphatso ndipo anali pansi pa ulamuliro wa Solomoni moyo wake wonse.
A ua alii ae la o Solomona maluna o na aupuni a pau mai ka muliwai a hiki i ka aina o ko Pilisetia, a i ka mokuna o Aigupita; a lawe mai la i na makana, a malama lakou ia Solomona i na la a pau o kona ola ana.
22 Chakudya cha tsiku ndi tsiku cha Solomoni chinali madengu 150 a ufa wosalala ndi madengu 300 a mgayiwa,
A o ka ai na Solomona i ka la hookahi, he kanakolu kora palaoa maikai, a me na kora huita wali he kanaono:
23 ngʼombe khumi zonenepa zodyetsera mʼkhola, ngʼombe za ku busa makumi awiri, ndiponso nkhosa ndi mbuzi 100, pamodzinso ndi mbawala, agwape, mphoyo ndi mbalame zoweta zonona.
O na bipikauo kupaluia he umi, a me na bipikauo mai ke kula mai he iwakalua, a me na hipa hookahi haneri, a okoa hoi na dia, a me na anetelopa, a me na bufalo, a me na manu momona.
24 Pakuti ankalamulira dziko lonse la kumadzulo kwa mtsinje wa Yufurate kuyambira ku Tifisa mpaka ku Gaza, mafumu onse a kumadzulo kwa Mtsinje, ndipo anali pa mtendere ndi mayiko onse ozungulira.
No ka mea, ia ia ke aupuni ma keia aoao a pau o ka muliwai, mai Tipesa a hiki i Aza, maluna oia o nalii a pau ma keia aoao o ka muliwai: a he malu kona ma na aoao a puni ia.
25 Pa nthawi ya Solomoni, Yuda ndi Israeli anali pa mtendere, kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba. Munthu aliyense ankangodzikhalira pansi pa mpesa wake ndi mtengo wake wa mkuyu.
Noho maluhia ae la o ka Iuda a me ka Iseraela, kela kanaka keia kanaka, malalo o kona kumuwaina iho a malalo o kona laaufiku iho, mai Dana a Bereseba, i na la a pau o Solomona.
26 Solomoni anali ndi zipinda 4,000 zodyeramo akavalo okoka magaleta ake ndi anthu 12,000 oyendetsa magaleta.
Ia Solomona na wahi e ku ai na lio, he kanaha tausani, no kona mau kaa, a me na kanaka hololio he umikumamalua haneri.
27 Abwanamkubwa a zigawo aja, aliyense pa mwezi wake, ankapereka chakudya cha Mfumu Solomoni ndi cha anthu onse amene ankadya naye. Iwo ankaonetsetsa kuti pasasowe kalikonse.
A ua hoomakaukau kela mau luna i ai na Solomona ke alii, a na ka poe a pau i hele mai i ka papaaina o Solomona ke alii, kela kanaka keia kanaka i kona malama, aole nele iki lakou.
28 Ankabweretsanso ku malo ake ofunikira muyeso wawo wa barele ndi udzu wa akavalo okoka magaleta ndiponso akavalo ena.
Ka hua bale hoi a me ka mauu na na lio, me na lio holo, ka lakou i lawe mai ai i kahi o lakou, kela kanaka keia kanaka e like me kana kauoha.
29 Mulungu anamupatsa Solomoni nzeru ndi luntha losaneneka ndipo nzeru zake zinali zochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
A haawi mai la ke Akua i ke akamai ia Solomona, a me ka naauao he nui loa, a me ka nui ana o ka naau, e like me ka one ma kahakai.
30 Nzeru za Solomoni zinali zoposa nzeru za anthu onse a Kummawa ndiponso nzeru zonse za ku Igupto.
A o ko Solomona akamai, ua oi aku ia mamua o ke akamai o na kamaaina a pau o ka hikina, a me ke akamai a pau o Aigupita.
31 Iye anali wanzeru kuposa munthu wina aliyense, kuposa ngakhale Etani wa banja la Ezara, Hemani, Kalikoli ndi Darida, ana a Maholi. Ndipo mbiri yake inamveka kwa mitundu yonse ya anthu ozungulira.
No ka mea, ua oi aku kona akamai mamua o ko na kanaka a pau, mamua o ko Etana o ka Ezera, a me ko Hemana, a me ko Kalekola, a me ko Dareda na keiki a Mahola: a ua kaulana oia ma na lahuikanaka a puni.
32 Solomoni anapeka miyambi 3,000 ndi kulemba nyimbo 1,005.
A ua olelo mai la oia i na olelo akamai ekolu tausani, a o kana mau mele, hookahi tausani ia a me kumamalima.
33 Iye ankaphunzitsa za mitengo, kuyambira mtengo wa mkungudza wa ku Lebanoni mpaka kachitsamba ka hisope khomera pa khoma. Iye ankaphunzitsanso za nyama ndi mbalame, zinthu zokwawa pansi ndiponso za nsomba.
A ua olelo mai oia i na laau, mai ka laau Kedera ma Lebanona a hiki i ka husopa, e kupu ana mailoko ae o ka pa: a olelo mai la hoi oia no na holoholona, a me na manu, a me na mea kolo, a me na ia.
34 Anthu a mitundu yonse ankabwera kudzamva nzeru za Solomoni. Anthu amenewa ankatumizidwa ndi mafumu onse a dziko lapansi amene anamvapo za nzeru zakezo.
Hele mai la hoi ko na lahuikanaka a pau e hoolohe i ke akamai o Solomona, mai na lii a pau o ka honua, i lohe i kona akamai.

< 1 Mafumu 4 >