< 1 Mafumu 4 >

1 Ndipo Mfumu Solomoni inakhala mfumu ya Aisraeli onse.
Le Roi Salomon donc fut Roi sur tout Israël.
2 Nduna zake zikuluzikulu zinali izi: Azariya mwana wa Zadoki anali wansembe;
Et ceux-ci étaient les principaux Seigneurs de sa [cour]; Hazaria fils de Tsadok Sacrificateur;
3 Elihorefe ndi Ahiya, ana a Sisa, anali alembi; Yehosafati mwana wa Ahiludi, anali mlembi wa zochitika;
Elihoreph et Ahija enfants de Sisa, Secrétaires; Jéhosaphat fils d'Ahilud, commis sur les Registres;
4 Benaya mwana wa Yehoyada, anali mtsogoleri wa ankhondo; Zadoki ndi Abiatara, anali ansembe;
Bénaja fils de Jéhojadah avait la charge de l'armée; et Tsadok et Abiathar étaient les Sacrificateurs;
5 Azariya mwana wa Natani, anali woyangʼanira nduna za mʼzigawo; Zabudi mwana wa Natani, anali wansembe ndi bwenzi la mfumu;
Hazaria fils de Nathan avait la charge de ceux qui étaient commis sur les vivres; et Zabul fils de Nathan était le principal officier; [et] le favori du Roi;
6 Ahisara, anali mkulu woyangʼanira nyumba ya mfumu; Adoniramu mwana wa Abida, anali mkulu woyangʼanira ntchito za thangata.
et Ahisar était le grand-maître de la maison; et Adoniram fils de Habda, [était] commis sur les tributs.
7 Solomoni analinso ndi abwanamkubwa khumi ndi awiri amene ankayangʼanira zigawo zonse za dziko la Israeli. Iwo ankapereka chakudya kwa mfumu ndiponso ku banja laufumu. Bwanamkubwa aliyense ankapereka chakudya mwezi umodzi pa chaka.
Or Salomon avait douze commissaires sur tout Israël, qui faisaient les provisions du Roi et de sa maison; et chacun avait un mois de l'année pour le pourvoir de vivres.
8 Mayina awo ndi awa: Beni-Huri, wa ku dziko la mapiri la Efereimu;
Et ce sont ici leurs noms. Le fils de Hur [était commis] sur la montagne d'Ephraïm;
9 Beni-Dekeri, woyangʼanira mizinda ya Makazi, Saalibimu, Beti-Semesi ndi Eloni Beti-Hanani;
Le fils de Déker sur Makath, sur Sahalbim, sur Beth-sémes, sur Elon de Beth-hanan;
10 Beni-Hesedi, woyangʼanira mizinda ya Aruboti (Soko ndi dziko lonse la Heferi);
Le fils de Hésed sur Arubboth, [et] il avait Soco et tout le pays de Hépher;
11 Beni-Abinadabu, woyangʼanira Nafoti Dori (iye anakwatira Tafati mwana wa Solomoni);
Le fils d'Abinadab avait toute la contrée de Dor; il eut Taphath fille de Salomon pour femme;
12 Baana mwana wa Ahiludi, anali woyangʼanira Taanaki ndi Megido, ndi ku Beti Sani konse, kufupi ndi ku Zaretani kumunsi kwa Yezireeli, kuyambira ku Beti-Seani mpaka ku Abeli-Mehola kukafika mpaka ku Yokineamu;
Bahana fils d'Ahilud avait Tahanac et Méguiddo, et tout [le pays] de Beth-séan qui est vers le chemin tirant vers Tsarthan au dessous de Jizréhel, depuis Beth-séan jusqu'à Abelmeholah, [et] jusqu'au delà de Jokmeham;
13 Beni-Geberi, anali woyangʼanira Ramoti Giliyadi (midzi ya Yairi inali ya mwana wa Manase ku Giliyadi, pamodzinso ndi chigawo cha Arigobu ku Basani ndiponso mizinda yake yayikulu makumi asanu ndi umodzi yokhala ndi malinga ndi mipiringidzo yamkuwa).
Le fils de Guéber [était commis] sur Ramoth de Galaad, [et] il avait les bourgs de Jaïr fils de Manassé en Galaad; il avait aussi toute la contrée d'Argob en Basan, soixante grandes villes murées, et [garnies] de barres d'airain;
14 Ahinadabu mwana wa Ido, anali woyangʼanira Mahanaimu;
Ahinadab fils de Hiddo [était commis] sur Mahanajim;
15 Ahimaazi anali woyangʼanira Nafutali (iyeyu anakwatira Basemati mwana wa Solomoni);
Ahimahats, qui avait pour femme Basemath fille de Salomon, [était commis] sur Nephthali;
16 Baana mwana wa Husai, anali woyangʼanira Aseri ndi Bealoti;
Bahana fils de Cusaï [était commis] sur Aser, et sur Haloth;
17 Yehosafati mwana wa Paruwa, anali woyangʼanira Isakara;
Jéhosaphat fils de Paruah, sur Issacar;
18 Simei mwana wa Ela, anali woyangʼanira Benjamini;
Simhi fils d'Ela, sur Benjamin;
19 Geberi mwana wa Uri, anali woyangʼanira Giliyadi (dziko la Sihoni mfumu ya Aamori ndi dziko la Ogi mfumu ya Basani). Iye ankayangʼanira chigawo chonsechi yekha.
Guéber fils d'Uri, sur le pays de Galaad, [qui avait été] du pays de Sihon Roi des Amorrhéens, et de Hog Roi de Basan; et il était seul commis sur ce pays-là.
20 Anthu a ku Yuda ndi ku Israeli anali ochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja. Ankadya ndi kumwa ndipo ankasangalala.
Juda et Israël étaient en grand nombre, comme le sable qui est sur le bord de la mer, tant ils étaient en grand nombre; ils mangeaient et buvaient, et se réjouissaient.
21 Ndipo Solomoni analamulira mayiko onse kuyambira ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku dziko la Afilisti, kukafika mpaka ku malire a dziko la Igupto. Mayikowa ankabweretsa mphatso ndipo anali pansi pa ulamuliro wa Solomoni moyo wake wonse.
Et Salomon dominait sur tous les Royaumes, depuis le fleuve jusqu'au pays des Philistins, et jusqu'à la frontière d'Egypte; et ils lui apportaient des présents, et lui furent [assujettis] tout le temps de sa vie.
22 Chakudya cha tsiku ndi tsiku cha Solomoni chinali madengu 150 a ufa wosalala ndi madengu 300 a mgayiwa,
Or les vivres de Salomon pour chaque jour étaient trente Cores de fine farine, et soixante d'autre farine;
23 ngʼombe khumi zonenepa zodyetsera mʼkhola, ngʼombe za ku busa makumi awiri, ndiponso nkhosa ndi mbuzi 100, pamodzinso ndi mbawala, agwape, mphoyo ndi mbalame zoweta zonona.
Dix bœufs gras, et vingt bœufs des pâturages, et cent moutons; sans les cerfs, les daims, les buffles, et les volailles engraissées.
24 Pakuti ankalamulira dziko lonse la kumadzulo kwa mtsinje wa Yufurate kuyambira ku Tifisa mpaka ku Gaza, mafumu onse a kumadzulo kwa Mtsinje, ndipo anali pa mtendere ndi mayiko onse ozungulira.
Car il dominait sur toutes les contrées de deçà le fleuve, depuis Tiphsah jusqu'à Gaza, sur tous les Rois qui étaient deçà le fleuve, et il était en paix [avec tous les pays] d'alentour, de tous côtés.
25 Pa nthawi ya Solomoni, Yuda ndi Israeli anali pa mtendere, kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba. Munthu aliyense ankangodzikhalira pansi pa mpesa wake ndi mtengo wake wa mkuyu.
Et Juda et Israël habitaient en assurance chacun sous sa vigne et sous son figuier, depuis Dan jusqu'à Beer-sebah, durant tout le temps de Salomon.
26 Solomoni anali ndi zipinda 4,000 zodyeramo akavalo okoka magaleta ake ndi anthu 12,000 oyendetsa magaleta.
Salomon avait aussi quarante mille places à tenir des chevaux, et douze mille hommes de cheval.
27 Abwanamkubwa a zigawo aja, aliyense pa mwezi wake, ankapereka chakudya cha Mfumu Solomoni ndi cha anthu onse amene ankadya naye. Iwo ankaonetsetsa kuti pasasowe kalikonse.
Or ces commis-là pourvoyaient de vivres le Roi Salomon, et tous ceux qui s'approchaient de la table du Roi Salomon, chacun en son mois, et ils ne [les] laissaient manquer de rien.
28 Ankabweretsanso ku malo ake ofunikira muyeso wawo wa barele ndi udzu wa akavalo okoka magaleta ndiponso akavalo ena.
Ils faisaient aussi venir de l'orge et de la paille pour les chevaux et pour les genets, aux lieux où ils étaient, chacun selon la charge qu'il en avait.
29 Mulungu anamupatsa Solomoni nzeru ndi luntha losaneneka ndipo nzeru zake zinali zochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
Et Dieu donna de la sagesse à Salomon; et une fort grande intelligence, et une étendue d'esprit aussi grande que celle du sable qui est sur le bord de la mer.
30 Nzeru za Solomoni zinali zoposa nzeru za anthu onse a Kummawa ndiponso nzeru zonse za ku Igupto.
Et la sagesse de Salomon était plus grande que la sagesse de tous les Orientaux, et que toute la sagesse des Egyptiens.
31 Iye anali wanzeru kuposa munthu wina aliyense, kuposa ngakhale Etani wa banja la Ezara, Hemani, Kalikoli ndi Darida, ana a Maholi. Ndipo mbiri yake inamveka kwa mitundu yonse ya anthu ozungulira.
Il était même plus sage que quelque homme que ce fût, plus qu'Ethan Ezrahite, qu'Héman, que Calcol, et que Dardah, les fils de Mahol; et sa réputation se répandit dans toutes les nations d'alentour.
32 Solomoni anapeka miyambi 3,000 ndi kulemba nyimbo 1,005.
Il prononça trois mille paraboles, et fit cinq mille cantiques.
33 Iye ankaphunzitsa za mitengo, kuyambira mtengo wa mkungudza wa ku Lebanoni mpaka kachitsamba ka hisope khomera pa khoma. Iye ankaphunzitsanso za nyama ndi mbalame, zinthu zokwawa pansi ndiponso za nsomba.
Il a aussi parlé des arbres, depuis le cèdre qui est au Liban, jusqu'à l'hysope qui sort de la muraille; il a aussi parlé des bêtes, des oiseaux, des reptiles, et des poissons.
34 Anthu a mitundu yonse ankabwera kudzamva nzeru za Solomoni. Anthu amenewa ankatumizidwa ndi mafumu onse a dziko lapansi amene anamvapo za nzeru zakezo.
Et il venait des gens d'entre tous les peuples pour entendre la sagesse de Salomon; [et] de la part de tous les Rois de la terre qui avaient entendu parler de sa sagesse.

< 1 Mafumu 4 >