< 1 Mafumu 4 >
1 Ndipo Mfumu Solomoni inakhala mfumu ya Aisraeli onse.
Et le roi Salomon était roi sur tout Israël.
2 Nduna zake zikuluzikulu zinali izi: Azariya mwana wa Zadoki anali wansembe;
Et ce sont ici les princes qu’il avait: Azaria, fils de Tsadok, le sacrificateur;
3 Elihorefe ndi Ahiya, ana a Sisa, anali alembi; Yehosafati mwana wa Ahiludi, anali mlembi wa zochitika;
Élihoreph et Akhija, fils de Shisha, scribes; Josaphat, fils d’Akhilud, rédacteur des chroniques;
4 Benaya mwana wa Yehoyada, anali mtsogoleri wa ankhondo; Zadoki ndi Abiatara, anali ansembe;
et Benaïa, fils de Jehoïada, [préposé] sur l’armée; et Tsadok, et Abiathar, sacrificateurs;
5 Azariya mwana wa Natani, anali woyangʼanira nduna za mʼzigawo; Zabudi mwana wa Natani, anali wansembe ndi bwenzi la mfumu;
et Azaria, fils de Nathan, [préposé] sur les intendants; et Zabud, fils de Nathan, principal officier, ami du roi;
6 Ahisara, anali mkulu woyangʼanira nyumba ya mfumu; Adoniramu mwana wa Abida, anali mkulu woyangʼanira ntchito za thangata.
et Akhishar, [préposé] sur la maison, et Adoniram, fils d’Abda, sur les levées.
7 Solomoni analinso ndi abwanamkubwa khumi ndi awiri amene ankayangʼanira zigawo zonse za dziko la Israeli. Iwo ankapereka chakudya kwa mfumu ndiponso ku banja laufumu. Bwanamkubwa aliyense ankapereka chakudya mwezi umodzi pa chaka.
Et Salomon avait douze intendants sur tout Israël, et ils pourvoyaient à l’entretien du roi et de sa maison; chacun était tenu de pourvoir à cet entretien un mois dans l’année.
8 Mayina awo ndi awa: Beni-Huri, wa ku dziko la mapiri la Efereimu;
Et ce sont ici leurs noms: le fils de Hur, dans la montagne d’Éphraïm;
9 Beni-Dekeri, woyangʼanira mizinda ya Makazi, Saalibimu, Beti-Semesi ndi Eloni Beti-Hanani;
le fils de Déker, à Makats, et à Shaalbim, et à Beth-Shémesh, et à Élon-Beth-Hanan;
10 Beni-Hesedi, woyangʼanira mizinda ya Aruboti (Soko ndi dziko lonse la Heferi);
le fils de Hésed, à Arubboth: il avait Soco et tout le pays de Hépher.
11 Beni-Abinadabu, woyangʼanira Nafoti Dori (iye anakwatira Tafati mwana wa Solomoni);
Le fils d’Abinadab avait toutes les hauteurs de Dor; il avait Taphath, fille de Salomon, pour femme.
12 Baana mwana wa Ahiludi, anali woyangʼanira Taanaki ndi Megido, ndi ku Beti Sani konse, kufupi ndi ku Zaretani kumunsi kwa Yezireeli, kuyambira ku Beti-Seani mpaka ku Abeli-Mehola kukafika mpaka ku Yokineamu;
Baana, fils d’Akhilud, avait Thaanac et Meguiddo, et tout Beth-Shean, qui est à côté de Tsarthan, sous Jizreël, depuis Beth-Shean jusqu’à Abel-Mehola, jusqu’au-delà de Jokmeam.
13 Beni-Geberi, anali woyangʼanira Ramoti Giliyadi (midzi ya Yairi inali ya mwana wa Manase ku Giliyadi, pamodzinso ndi chigawo cha Arigobu ku Basani ndiponso mizinda yake yayikulu makumi asanu ndi umodzi yokhala ndi malinga ndi mipiringidzo yamkuwa).
Le fils de Guéber était à Ramoth de Galaad: il avait les bourgs de Jaïr, fils de Manassé, qui sont en Galaad, la région d’Argob, qui est en Basan, 60 grandes villes avec des murailles et des barres d’airain.
14 Ahinadabu mwana wa Ido, anali woyangʼanira Mahanaimu;
Akhinadab, fils d’Iddo, était à Mahanaïm;
15 Ahimaazi anali woyangʼanira Nafutali (iyeyu anakwatira Basemati mwana wa Solomoni);
Akhimaats, en Nephthali: lui aussi avait pris Basmath, fille de Salomon, pour femme;
16 Baana mwana wa Husai, anali woyangʼanira Aseri ndi Bealoti;
Baana, fils de Hushaï, en Aser et en Aloth;
17 Yehosafati mwana wa Paruwa, anali woyangʼanira Isakara;
Josaphat, fils de Paruakh, en Issacar;
18 Simei mwana wa Ela, anali woyangʼanira Benjamini;
Shimhi, fils d’Éla, en Benjamin;
19 Geberi mwana wa Uri, anali woyangʼanira Giliyadi (dziko la Sihoni mfumu ya Aamori ndi dziko la Ogi mfumu ya Basani). Iye ankayangʼanira chigawo chonsechi yekha.
Guéber, fils d’Uri, dans le pays de Galaad, le pays de Sihon, roi des Amoréens, et d’Og, roi de Basan: il était le seul intendant qui soit dans le pays.
20 Anthu a ku Yuda ndi ku Israeli anali ochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja. Ankadya ndi kumwa ndipo ankasangalala.
Juda et Israël étaient nombreux, comme le sable qui est près de la mer, en multitude, – mangeant et buvant, et se réjouissant.
21 Ndipo Solomoni analamulira mayiko onse kuyambira ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku dziko la Afilisti, kukafika mpaka ku malire a dziko la Igupto. Mayikowa ankabweretsa mphatso ndipo anali pansi pa ulamuliro wa Solomoni moyo wake wonse.
Et Salomon domina sur tous les royaumes, depuis le fleuve jusqu’au pays des Philistins, et jusqu’à la frontière d’Égypte: ils apportèrent des présents et servirent Salomon tous les jours de sa vie.
22 Chakudya cha tsiku ndi tsiku cha Solomoni chinali madengu 150 a ufa wosalala ndi madengu 300 a mgayiwa,
Et l’ordinaire de Salomon, pour un jour, était: 30 cors de fleur de farine, et 60 cors de farine,
23 ngʼombe khumi zonenepa zodyetsera mʼkhola, ngʼombe za ku busa makumi awiri, ndiponso nkhosa ndi mbuzi 100, pamodzinso ndi mbawala, agwape, mphoyo ndi mbalame zoweta zonona.
dix bœufs gras, et 20 bœufs de pâturages, et 100 moutons, outre les cerfs, et les gazelles, et les daims, et la volaille engraissée.
24 Pakuti ankalamulira dziko lonse la kumadzulo kwa mtsinje wa Yufurate kuyambira ku Tifisa mpaka ku Gaza, mafumu onse a kumadzulo kwa Mtsinje, ndipo anali pa mtendere ndi mayiko onse ozungulira.
Car il dominait sur tout [ce qui était] en deçà du fleuve, depuis Thiphsakh jusqu’à Gaza, sur tous les rois en deçà du fleuve; et il était en paix avec tous ses alentours, de tous côtés.
25 Pa nthawi ya Solomoni, Yuda ndi Israeli anali pa mtendere, kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba. Munthu aliyense ankangodzikhalira pansi pa mpesa wake ndi mtengo wake wa mkuyu.
Et Juda et Israël habitèrent en sécurité, chacun sous sa vigne et sous son figuier, depuis Dan jusqu’à Beër-Shéba, tous les jours de Salomon.
26 Solomoni anali ndi zipinda 4,000 zodyeramo akavalo okoka magaleta ake ndi anthu 12,000 oyendetsa magaleta.
Et Salomon avait 40 000 stalles pour les chevaux de ses chars, et 12 000 cavaliers.
27 Abwanamkubwa a zigawo aja, aliyense pa mwezi wake, ankapereka chakudya cha Mfumu Solomoni ndi cha anthu onse amene ankadya naye. Iwo ankaonetsetsa kuti pasasowe kalikonse.
Et ces intendants pourvoyaient à l’entretien du roi Salomon et de tous ceux qui venaient à la table du roi Salomon, chacun en son mois; ils ne laissaient rien manquer.
28 Ankabweretsanso ku malo ake ofunikira muyeso wawo wa barele ndi udzu wa akavalo okoka magaleta ndiponso akavalo ena.
Et ils faisaient venir l’orge et la paille pour les chevaux et les coursiers au lieu où était [l’intendant], chacun selon sa règle.
29 Mulungu anamupatsa Solomoni nzeru ndi luntha losaneneka ndipo nzeru zake zinali zochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
Et Dieu donna à Salomon de la sagesse et une très grande intelligence, et un cœur large comme le sable qui est sur le bord de la mer.
30 Nzeru za Solomoni zinali zoposa nzeru za anthu onse a Kummawa ndiponso nzeru zonse za ku Igupto.
Et la sagesse de Salomon était plus grande que la sagesse de tous les fils de l’orient et toute la sagesse de l’Égypte.
31 Iye anali wanzeru kuposa munthu wina aliyense, kuposa ngakhale Etani wa banja la Ezara, Hemani, Kalikoli ndi Darida, ana a Maholi. Ndipo mbiri yake inamveka kwa mitundu yonse ya anthu ozungulira.
Et il était plus sage qu’aucun homme, plus qu’Éthan, l’Ezrakhite, et qu’Héman, et Calcol, et Darda, les fils de Makhol. Et sa renommée était [répandue] parmi toutes les nations, à l’entour.
32 Solomoni anapeka miyambi 3,000 ndi kulemba nyimbo 1,005.
Et il proféra 3 000 proverbes, et ses cantiques furent [au nombre] de 1 005.
33 Iye ankaphunzitsa za mitengo, kuyambira mtengo wa mkungudza wa ku Lebanoni mpaka kachitsamba ka hisope khomera pa khoma. Iye ankaphunzitsanso za nyama ndi mbalame, zinthu zokwawa pansi ndiponso za nsomba.
Et il parla sur les arbres, depuis le cèdre qui est sur le Liban, jusqu’à l’hysope qui sort du mur; et il parla sur les bêtes, et sur les oiseaux, et sur les reptiles, et sur les poissons.
34 Anthu a mitundu yonse ankabwera kudzamva nzeru za Solomoni. Anthu amenewa ankatumizidwa ndi mafumu onse a dziko lapansi amene anamvapo za nzeru zakezo.
Et de tous les peuples on venait pour entendre la sagesse de Salomon, de la part de tous les rois de la terre qui avaient entendu parler de sa sagesse.