< 1 Mafumu 3 >
1 Solomoni anachita ubale ndi Farao mfumu ya ku Igupto ndipo anakwatira mwana wake wamkazi. Mkaziyo anabwera naye mu Mzinda wa Davide mpaka anatsiriza kumanga nyumba yaufumu ndi Nyumba ya Yehova ndiponso khoma lozungulira Yerusalemu.
I spowinowacił się Salomon z Faraonem, królem Egipskim; bo pojął córkę Faraonową, i przyprowadził ją do miasta Dawidowego, ażby dobudował domu swego, i domu Pańskiego, i muru Jeruzalemskiego w około.
2 Koma anthu ankaperekabe nsembe ku malo achipembedzo osiyanasiyana chifukwa chakuti mpaka pa nthawi imeneyo Dzina la Yehova anali asanalimangire nyumba.
Wszakże lud ofiarował po górach, przeto, że nie był jeszcze zbudowany dom imieniowi Pańskiemu aż do onych dni.
3 Solomoni anaonetsa chikondi chake pa Yehova poyenda motsatira malamulo a abambo ake Davide, kupatula kuti ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani ku malo osiyanasiyana achipembedzo.
I miłował Salomon Pana, chodząc w przykazaniach Dawida, ojca swego; tylko że na górach ofiarował i kadził.
4 Mfumu inapita ku Gibiyoni kukapereka nsembe popeza kumeneko ndiye kunali malo oposa malo ofunika kwambiri pachipembedzo. Kumeneko Solomoni anapereka nsembe zopsereza 1,000 pa guwa lansembe.
Szedł tedy król do Gabaon, aby tam ofiarował; bo tam była góra największa; tysiąc ofiar całopalonych ofiarował Salomon na onym ołtarzu.
5 Ku Gibiyoniko Yehova anaonekera kwa Solomoni mʼmaloto usiku, ndipo Mulungu anati, “Pempha chilichonse chimene ukufuna ndipo ndidzakupatsa.”
I ukazał się Pan w Gabaon Salomonowi przez sen w nocy, i rzekł Bóg: Proś czego chcesz, a dam ci.
6 Solomoni anayankha kuti, “Inu munaonetsa kukoma mtima kwanu kwakukulu kwa kapolo wanu, abambo anga Davide, chifukwa anali wokhulupirika pamaso panu, wolungama mtima ndiponso wa mtima wangwiro. Inu mukupitirizabe kukoma mtima kwanu kwakukulu kwa iye ndipo mwamupatsa mwana kuti akhale pa mpando wake waufumu lero lino.
Tedy rzekł Salomon: Tyś uczynił z sługą twoim Dawidem, ojcem moim, miłosierdzie wielkie, gdyż chodził przed tobą w prawdzie i w sprawiedliwości, i w prostości serca stał przy tobie; i zachowałeś mu to miłosierdzie wielkie, iżeś mu dał syna, który by siedział na stolicy jego, jako się to dziś okazuje.
7 “Tsopano Inu Yehova Mulungu wanga, mtumiki wanune mwandiyika kukhala mfumu mʼmalo mwa abambo anga Davide. Komatu ndine mwana wamngʼono ndipo sindidziwa kagwiridwe kake ka ntchito yangayi.
A teraz, o Panie Boże mój, tyś postanowił królem sługę twego miasto Dawida, ojca mego, a jam jest dziecię małe, i nie umiem wychodzić ani wchodzić.
8 Mtumiki wanu ali pakati pa anthu amene munawasankha, mtundu waukulu, anthu ochuluka kwambiri osatheka kuwawerenga.
A sługa twój jest w pośrodku ludu twego, któryś obrał, ludu wielkiego, który nie może zliczony ani porachowany być przez mnóstwo.
9 Choncho mupatseni mtumiki wanu nzeru zolamulira anthu anu ndi kuti azitha kusiyanitsa pakati pa chabwino ndi choyipa. Pakuti ndani amene angathe kulamulira anthu anu ochulukawa?”
Przetoż daj słudze twemu serce rozumne, aby sądził lud twój, i aby rozeznawał między dobrem i złem; albowiem któż może sądzić ten lud twój tak wielki?
10 Ambuye anakondwera kuti Solomoni anapempha zimenezi.
I podobało się to Panu, że żądał Salomon tej rzeczy.
11 Tsono Mulungu anati kwa Solomoni, “Popeza wapempha zinthu zimenezi osati moyo wautali kapena chuma chako kapena imfa ya adani ako koma nzeru zolamulira anthu mwachilungamo,
Tedy rzekł Bóg do niego: Dla tego, żeś o to prosił, a nieżądałeś sobie długich dni, aniś żądał sobie bogactw, aniś prosił o wytracenie nieprzyjaciół twoich, aleś sobie prosił o rozum dla rozeznania sądu:
12 Ine ndidzakuchitira zimene wapempha. Ndidzakupatsa mtima wanzeru ndi wozindikira zinthu, kotero kuti sipanakhalepo wina wofanana nawe ndipo sipadzapezekanso wina wonga iwe pambuyo pako.
Otożem uczynił według słów twoich; otom ci dał serce mądre i rozumne, tak, iż żaden równy tobie nie był przed tobą, ani po tobie powstanie równy tobie.
13 Kuwonjeza apo, ndidzakupatsa zimene sunazipemphe: chuma ndi ulemu, kotero kuti pa masiku onse a moyo wako sipadzakhala mfumu yofanana nawe.
Do tego i to, czegoś nie żądał, dałem ci, to jest bogactwa i sławę, tak aby nie było żadnego tobie równego między królmi po wszystkie dni twoje.
14 Ndipo ngati udzayenda mʼnjira zanga ndi kumvera malamulo anga ndiponso malangizo anga monga abambo ako Davide anachitira, ndidzakupatsa moyo wautali.”
A będzieszli chodził drogami mojemi, strzegąc wyroków moich, i rozkazania mego, jako chodził Dawid, ojciec twój, tedy przedłużę dni twoje.
15 Kotero Solomoni anadzuka ndipo anazindikira kuti anali maloto. Iye anabwerera ku Yerusalemu nakayimirira patsogolo pa Bokosi la Chipangano la Ambuye ndipo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Kenaka anakonzera phwando atumiki ake onse.
A gdy się ocucił Salomon, zrozumiał, że to był sen. I przyszedł do Jeruzalemu, a stanąwszy przed skrzynią przymierza Pańskiego, sprawował całopalenia, i ofiarował ofiary spokojne, sprawił też ucztę na wszystkie sługi swoje.
16 Nthawi ina amayi awiri adama anabwera kwa mfumu ndipo anayima pamaso pake.
Tedy przyszły dwie niewiasty wszetecznice do króla, i stanęły przed nim.
17 Mmodzi mwa amayiwo anati, “Mbuye wanga, mayi uyu ndi ine timakhala nyumba imodzi. Ine ndinabala mwana tili limodzi ndi mnzangayu.
I rzekła jedna z onych niewiast: Proszę panie mój, ja i ta niewiasta mieszkamy w jednym domu, i porodziłam u niej w tymże domu.
18 Tsiku lachitatu ine nditabala mwana, mnzangayunso anabereka mwana wake. Tinalipo awiriwiri mʼnyumbamo ndipo munalibe wina aliyense.
I stało się dnia trzeciego po porodzeniu mojem, że porodziła i ta niewiasta; i byłyśmy pospołu, a nie było nikogo obcego z nami w domu, oprócz nas dwóch w tymże domu.
19 “Nthawi ya usiku mwana wa mnzangayu anafa chifukwa anamugonera.
I umarł syn tej niewiasty w nocy, przeto, iż go była przyległa.
20 Tsono iyeyu anadzuka pakati pa usiku, natenga mwana wanga ku mimba kwanga pamene ine mdzakazi wanu ndinali mʼtulo. Anamuyika mwanayo ku mimba kwake ndi kuyika mwana wake wakufayo ku mimba kwanga.
A wstawszy o północy, wzięła syna mego odemnie, gdy służebnica twoja spała, i położyła go na łonie swojem, a syna swego umarłego położyła na łonie mojem.
21 Mmawa nditadzuka kuti ndiyamwitse mwana wanga ndinapeza kuti ndi wakufa! Koma kutacha nditamuyangʼanitsitsa ndinaona kuti si mwana amene ine ndinabala.”
A gdym wstała rano, chcąc dać ssać synowi memu, otom znalazła umarłego; któremu gdym się rano przypatrzyła, a oto nie był syn mój, któregom porodziła.
22 Koma mayi winayo anati, “Ayi! Mwana wamoyoyu ndi wanga, mwana wakufayu ndi wako.” Koma mayi woyambayo analimbikira kuti. “Ayi! Mwana wakufayu ndi wako; wamoyoyu ndi wanga.” Motero akaziwa anatsutsana pamaso pa mfumu.
I rzekła ona druga niewiasta: Nie tak; ale syn mój jest ten żywy, a syn twój ten umarły. Ale ona rzekła: Nie; ale syn twój jest ten umarły, a syn mój ten żywy. I tak się spierały przed królem.
23 Pamenepo mfumu inati, “Wina akuti, ‘Mwana wanga ndi wamoyoyu ndipo mwana wako ndi wakufayu,’ pamene winanso akuti, ‘Ayi! Mwana wako ndi wakufayu wanga ndi wamoyoyu.’”
I rzekł król: Ta mówi: Ten żywy jest syn mój, a syn twój ten umarły; a ta zasię mówi: Nie tak; ale syn twój ten umarły, a syn mój ten żywy.
24 Pamenepo mfumu inati, “Patseni lupanga.” Ndipo anabwera nalo lupanga kwa mfumu.
Przetoż rzekł król: Przynieście mi miecz. I przyniesiono miecz przed króla.
25 Tsono mfumu inagamula kuti, “Muduleni pakati mwana wamoyoyu ndipo wina mumupatse gawo limodzi, gawo linalo mumupatse winayo.”
Tedy rzekł król: Rozetnijcie to żywe dziecię na dwoje, a dajcie połowę jednej, a połowę drugiej.
26 Mayi amene mwana wake anali moyo anagwidwa ndi chisoni chifukwa cha mwana wakeyo ndipo anawuza mfumu kuti, “Chonde mbuye wanga, mupatseni mnzangayu mwana wamoyoyu! Musamuphe!” Koma winayo anati, “Ayi, asandipatse ine kapena iwe. Muduleni pakati!”
Ale niewiasta, której był ten syn żywy, mówiła do króla, (bo się były poruszyły wnętrzności jej nad synem jej, ) i rzekła: Proszę, panie mój, dajcie jej to dziecię żywe, a żadnym sposobem nie zabijajcie go. Ale druga rzekła: Niech nie będzie ani mnie, ani tobie, rozetnijcie je.
27 Choncho mfumu inagamula kuti, “Perekani mwana wamoyoyu kwa mayi woyambayu. Musamuphe, iyeyu ndiye mayi wake wa mwanayu.”
Tedy odpowiedział król, i rzekł: Dajcież tej dziecię żywe, a żadną miarą nie zabijajcie go; tać jest matka jego.
28 Pamene Aisraeli onse anamva za chigamulo chimene mfumu inapereka, anaopa mfumuyo kwambiri, chifukwa anaona kuti mfumu inali ndi nzeru zochokera kwa Mulungu zoweruzira mwachilungamo.
A usłyszawszy wszystek lud Izraelski ten sąd, który osądził król, bali się króla: albowiem wiedzieli, że mądrość Boża była w sercu jego ku czynieniu sądu.