< 1 Mafumu 22 >
1 Kwa zaka zitatu panalibe nkhondo pakati pa Aramu ndi Israeli.
Trois ans se passèrent donc sans guerre entre la Syrie et Israël.
2 Koma pa chaka chachitatu, Yehosafati mfumu ya ku Yuda anapita kukacheza ndi mfumu ya ku Israeli.
Mais, en la troisième année, Josaphat, roi de Juda, descendit vers le roi d’Israël.
3 Mfumu ya ku Israeli nʼkuti itawuza atumiki ake kuti, “Kodi inu simukudziwa kuti Ramoti Giliyadi ndi dera lathu ndipo ife palibe chimene tikuchita kuti tilitenge deralo mʼmanja mwa mfumu ya Aramu?”
(Et le roi d’Israël dit à ses serviteurs: Ignorez-vous que la ville de Ramoth en Galaad est à nous, et nous négligeons de l’enlever de la main du roi de Syrie?)
4 Tsono iye anafunsa Yehosafati kuti, “Kodi udzapita nane ku nkhondo ku Ramoti Giliyadi?” Yehosafati anayankha mfumu ya ku Israeli kuti, “Ine ndili monga inu, anthu anga monga anthu anu, akavalo anga monga akavalo anu.”
Et il demanda à Josaphat: Viendrez-vous avec moi pour combattre contre Ramoth-Galaad?
5 Koma Yehosafati anawuzanso mfumu ya ku Israeli kuti, “Poyamba mupemphe nzeru kwa Yehova.”
Et Josaphat répondit au roi d’Israël: Comme je suis, ainsi vous êtes vous-même: mon peuple et votre peuple sont une seule chose, et ma cavalerie est votre cavalerie. Il dit encore au roi d’Israël: Consultez, je vous prie, aujourd’hui la parole du Seigneur.
6 Choncho mfumu ya Israeli inasonkhanitsa pamodzi aneneri okwanira 400, ndipo inawafunsa kuti, “Kodi ndipite kukathira nkhondo Ramoti Giliyadi, kapena ndileke?” Iwo anayankha kuti, “Pitani, pakuti Ambuye waupereka mzindawo mʼmanja mwa mfumu.”
Le roi d’Israël assembla donc les prophètes, environ quatre cents hommes, et il leur dit: Dois-je aller combattre contre Ramoth-Galaad, ou me tenir en repos? Ceux-ci lui répondirent: Montez, et le Seigneur la mettra dans la main du roi.
7 Koma Yehosafati anafunsa kuti, “Kodi kuno kulibenso mneneri wina wa Yehova kumene ife tingakafunsireko nzeru?”
Mais Josaphat lui demanda: N’y a-t-il pas ici quelque prophète du Seigneur, afin que nous le consultions par lui?
8 Mfumu ya ku Israeli inayankha Yehosafati kuti, “Alipo munthu mmodzi amene ife tingakafunsire kwa Yehova, koma ndimadana naye chifukwa iyeyo samanenera kanthu kalikonse kabwino ka ine, koma zoyipa nthawi zonse. Dzina lake ndi Mikaya mwana wa Imula.” Yehosafati anayankha kuti, “Mfumu musatero.”
Et le roi d’Israël répondit à Josaphat: Il est demeuré un homme par qui nous pouvons consulter le Seigneur; mais, moi, je le hais, parce qu’il ne me prophétise point du bien, mais du mal: c’est Michée, fils de Jemla. Josaphat lui dit: Ne parlez pas ainsi, ô roi.
9 Choncho mfumu ya Israeli inayitana mmodzi mwa atumiki ake ndipo inati, “Kayitane Mikaya mwana wa Imula msangamsanga.”
Le roi d’Israël appela donc un certain eunuque, et lui dit: Hâte-toi d’amener Michée, fils de Jemla.
10 Atavala mikanjo yawo yaufumu, mfumu ya ku Israeli ndi Yehosafati mfumu ya ku Yuda anakhala pa mipando yawo yaufumu pabwalo lopondera tirigu pafupi ndi chipata cha Samariya, pamodzi ndi aneneri onse akunenera pamaso pawo.
Mais le roi d’Israël et Josaphat, roi de Juda, étaient assis chacun sur leur trône, vêtus avec une magnificence royale, dans une aire près de la porte de Samarie, et tous les prophètes prophétisaient en leur présence.
11 Tsono Zedekiya mwana wa Kenaana nʼkuti atapanga nyanga zachitsulo ndipo iye ananenera kuti, “Yehova akuti, ‘Ndi nyanga izi, inu mudzagunda nazo Aaramu mpaka iwo atawonongeka.’”
Sédécias, fils de Chanaana se fit aussi des cornes de fer, et dit: Voici ce que dit le Seigneur: Tu agiteras la Syrie avec ces cornes, jusqu’à ce que tu l’aies détruite.
12 Aneneri ena onse ananenera zomwezonso. Iwo anati, “Kathireni nkhondo Ramoti Giliyadi ndipo mukapambana, pakuti Yehova adzawupereka mzindawo mʼdzanja la mfumu.”
Et tous les prophètes prophétisaient de même, disant: Montez contre Ramoth-Galaad, et marchez heureusement, et le Seigneur la mettra dans la main du roi.
13 Wamthenga amene anapita kukayitana Mikaya anamuwuza kuti, “Taonani, aneneri onse monga munthu mmodzi akunenera za kupambana kwa mfumu. Mawu anunso akhale ogwirizana ndi mawu awo, ndipo mukayankhule zabwino.”
Or le messager qui était allé pour appeler Michée, lui parla, disant: Voilà que les paroles des prophètes prédisent unanimement au roi de bonnes choses: que votre parole soit donc semblable à la leur, et dites de bonnes choses.
14 Koma Mikaya anati, “Pali Yehova wamoyo, ine ndikawawuza zokhazo zimene Yehova akandiwuze.”
Michée lui répondit: Le Seigneur vit! tout ce que m’aura dit le Seigneur, c’est ce que je dirai.
15 Atafika, Ahabu anamufunsa kuti, “Mikaya, kodi tipite kukathira nkhondo Ramoti Giliyadi, kapena tileke?” Iye anayankha kuti, “Pitani ndipo mukapambana, pakuti Yehova adzawupereka mzindawo mʼdzanja la mfumu.”
Michée vint donc vers le roi, et le roi lui dit: Michée, devons-nous aller contre Ramoth-Galaad pour combattre, ou nous reposer? Celui-ci lui répondit: Montez, marchez heureusement, et le Seigneur la mettra dans la main du roi.
16 Ahabu anati kwa iye, “Kodi ndikulumbiritse kangati kuti undiwuze zoona zokhazokha mʼdzina la Yehova?”
Mais le roi lui dit: Je t’adjure de nouveau et encore de nouveau de ne me dire que ce qui est vrai, au nom du Seigneur.
17 Pamenepo Mikaya anayankha kuti, “Ndinaona Aisraeli onse atamwazikana pa mapiri ngati nkhosa zopanda mʼbusa, ndipo Yehova anati, ‘Anthu awa alibe mbuye wawo. Aliyense apite kwawo mwamtendere.’”
Alors il lui dit: J’ai vu tout Israël dispersé dans les montagnes, comme des brebis qui n’ont point de pasteur; et le Seigneur a dit: Ceux-ci n’ont pas de maître; que chacun retourne dans sa maison en paix.
18 Mfumu ya ku Israeli inati kwa Yehosafati, “Kodi ine sindinakuwuzeni kuti ameneyu samanenera kanthu kalikonse kabwino ka ine, koma zoyipa zokhazokha?”
(Le roi d’Israël dit donc à Josaphat: Ne vous ai-je pas dit qu’il ne me prophétise point du bien, mais du mal?)
19 Mikaya anapitiriza kuyankhula nati, “Tsono imvani mawu a Yehova: Ine ndinaona Yehova atakhala pa mpando wake waufumu, gulu lonse la kumwamba litayima ku dzanja lake lamanja ndi ku dzanja lake lamanzere.
Mais Michée continuant, dit: C’est pourquoi écoutez la parole du Seigneur: J’ai vu le Seigneur assis sur son trône, et toute l’armée du ciel se tenant près de lui à droite et à gauche;
20 Ndipo Yehova anati, ‘Kodi ndani amene akamukope Ahabu kuti akathire nkhondo Ramoti Giliyadi, nʼkukafera komweko?’” “Wina anapereka maganizo ena ndipo winanso maganizo ena.
Et le Seigneur a dit: Qui trompera Achab, roi d’Israël, afin qu’il monte et qu’il succombe à Ramoth-Galaad? Et l’un dit de telles choses, et l’autre autrement.
21 Potsirizira, mzimu wina unabwera ndi kuyima pamaso pa Yehova ndipo unati, ‘Ine ndidzamukopa.’”
Mais l’esprit malin sortit, et se tint devant le Seigneur, et dit: C’est moi qui le tromperai. Le Seigneur lui dit: En quoi?
22 Yehova anafunsa kuti, “Ukamukopa bwanji?” Mzimuwo unati, “Ndidzapita ndi kukakhala mzimu wabodza pakamwa pa aneneri ake onse.” Yehova anati, “‘Iwe udzamukopadi. Pita kachite zomwezo.’
Et il répondit: Je sortirai, et je serai un esprit menteur dans la bouche de tous ses prophètes. Et le Seigneur dit: Tu le tromperas et tu prévaudras. Sors, et fais ainsi.
23 “Ndipo tsopano taonani, Yehova wayika mzimu wabodza mʼkamwa mwa aneneri anu onsewa. Yehova waneneratu kuti mukaona mavuto.”
Maintenant donc, voilà que le Seigneur a mis un esprit de mensonge dans la bouche de tous vos prophètes qui sont ici, et le Seigneur a prononcé contre vous malheur.
24 Pamenepo Zedekiya mwana wa Kenaana anapita pafupi namenya Mikaya patsaya. Iye anafunsa Mikaya kuti, “Kodi mzimu wa Yehova unadzera njira iti pamene umatuluka mwa ine kuti uziyankhula ndi iwe?”
Or Sédécias, fils de Chanaana, s’approcha et frappa Michée sur la joue, et dit: Est-ce donc moi que l’esprit du Seigneur a quitté, et t’a-t-il parlé à toi?
25 Mikaya anayankha kuti, “Udzaona pa tsiku limene uzikalowa mʼchipinda chamʼkati kuti ukabisale.”
Et Michée dit: Vous le verrez au jour même où vous entrerez dans une chambre, qui est dans une chambre, pour vous cacher.
26 Pamenepo mfumu ya ku Israeli inalamula kuti, “Mugwireni Mikaya ndipo mubwerere naye kwa Amoni mkulu wa mzinda, ndi kwa Yowasi mwana wa mfumu
Alors le roi d’Israël dit: Prenez Michée, et qu’il demeure chez Amon, gouverneur de la ville, et chez Joas, fils d’Amélech,
27 ndipo mukanene kuti, ‘Chimene mfumu ikunena ndi ichi; Muyikeni mʼndende munthu uyu ndipo musamupatse chakudya china koma buledi ndi madzi pangʼono mpaka nditabwerera mwamtendere.’”
Et dites-leur: Voici ce que dit le roi: Envoyez cet homme dans la prison, et sustentez-le d’un pain de tribulation et d’une eau d’angoisse, jusqu’à ce que je revienne en paix.
28 Mikaya ananena kuti, “Ngati mudzabwerera mwamtendere, Yehova sanayankhule kudzera mwa ine.” Ndipo iye anapitiriza kunena kuti, “Gwiritsitsani mawu angawa, anthu inu nonse!”
Et Michée dit: Si vous revenez en paix, le Seigneur n’a point parlé par moi. Et il ajouta: Peuples, tous tant que vous êtes, écoutez.
29 Choncho mfumu ya ku Israeli ndi Yehosafati mfumu ya ku Yuda anapita ku Ramoti Giliyadi.
Le roi d’Israël monta donc, et Josaphat, roi de Juda, contre Ramoth-Galaad.
30 Mfumu ya ku Israeli inawuza Yehosafati kuti, “Ine ndidzalowa mu nkhondoyi modzibisa, koma inu muvale zovala zanu zaufumu.” Choncho mfumu ya ku Israeli inadzibisa ndi kupita ku nkhondo.
C’est pourquoi le roi d’Israël dit à Josaphat: Prenez vos armes, entrez au combat, et revêtez-vous de vos vêtements. Mais le roi d’Israël changea ses vêtements, puis entra au combat.
31 Tsono mfumu ya ku Aramu nʼkuti italamulira anthu ake 32 olamulira magaleta kuti, “Musamenyane ndi wina aliyense, wamngʼono kapena wamkulu, koma mfumu ya ku Israeli.”
Or le roi de Syrie avait ordonné aux trente-deux commandants de ses chariots, disant: Ne combattez point contre un petit et un grand, quel qu’il soit, si ce n’est contre le roi d’Israël seul.
32 Olamulira magaleta ataona Yehosafati, ankaganiza kuti, “Ndithu iyi ndiye mfumu ya ku Israeli.” Choncho anabwerera kukamenyana naye, koma Yehosafati atafuwula,
Lors donc que les commandants des chariots eurent vu Josaphat, ils supposèrent que c’était le roi d’Israël; et, se précipitant, ils combattaient contre lui; alors Josaphat jeta un grand cri;
33 olamulira akavalo anaona kuti sanali mfumu ya ku Israeli ndipo analeka kumuthamangitsa.
Et les commandants des chariots reconnurent que ce n’était pas le roi d’Israël, et ils le laissèrent.
34 Koma munthu wina anaponya muvi wake mwachiponyeponye ndi kulasa mfumu ya ku Israeli polumikizira malaya ake odzitetezera. Mfumu inawuza woyendetsa galeta lake kuti, “Tembenuka ndipo undichotse pa nkhondo pano pakuti ndalasidwa.”
Mais un certain homme tendit son arc, tirant une flèche à l’aventure, et par hasard, il frappa le roi d’Israël entre le poumon et l’estomac. Mais le roi dit au conducteur de son char: Tourne ta main, et retire-moi de l’armée, parce que je suis grièvement blessé.
35 Nkhondo inakula kwambiri tsiku limenelo, ndipo mfumu inakhala tsonga mʼgaleta lake moyangʼanana ndi Aaramu. Magazi ake ankayenderera pansi kuchokera mʼgaleta, ndipo pa nthawi ya madzulo inamwalira.
Le combat fut donc engagé ce jour-là, et le roi d’Israël se tenait sur son char en face des Syriens, et il mourut vers le soir; or le sang de la plaie coulait dans l’intérieur du char.
36 Pamene dzuwa linkalowa, kunamveka mfuwu wa nkhondo kuti, “Munthu aliyense apite ku mzinda wa kwawo, aliyense apite ku dziko la kwawo!”
Et le héraut, avant que le soleil fût couché; sonna de la trompette dans toute l’armée, disant: Que chacun retourne en sa ville et en sa terre.
37 Ndipo mfumu ija inafa, nabwera nayo ku Samariya, ndipo anayika mʼmanda kumeneko.
Le roi mourut donc, et il fut porté à Samarie; ainsi, on ensevelit le roi à Samarie.
38 Anatsuka galeta lija pa dziwe la ku Samariya (pamene ankasamba akazi achiwerewere) ndipo agalu ananyambita magazi a mfumuyo, monga momwe Yehova ananenera.
Et on lava son char dans la piscine de Samarie, et les chiens léchèrent son sang, et on lava les rênes, selon la parole que le Seigneur avait dite.
39 Tsono ntchito zina za Ahabu, kuphatikiza zonse anazichita, nyumba yaufumu imene anamanga yokutidwa ndi minyanga ya njovu, mizinda yotetezedwa, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?
Mais le reste des actions d’Achab, et tout ce qu’il fit, la maison d’ivoire qu’il bâtit, et toutes les villes qu’il construisit, n’est-ce pas écrit dans le Livre des actions des jours des rois d’Israël?
40 Ahabu anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Ahaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Achab dormit donc avec ses pères, et Ochozias, son fils, régna en sa place.
41 Yehosafati, mwana wa Asa anakhala mfumu ya ku Yuda chaka chachinayi cha Ahabu mfumu ya ku Israeli.
Or Josaphat, fils d’Asa, avait commencé à régner sur Juda la quatrième année d’Achab, roi d’Israël.
42 Yehosafati anali wa zaka 35 pamene analowa ufumu, ndipo analamulira ku Yerusalemu zaka 25. Amayi ake anali Azuba mwana wa Silihi.
Il avait trente-cinq ans lorsqu’il commença à régner, et il régna vingt-cinq ans dans Jérusalem. Le nom de sa mère était Azuba, fille de Salaï.
43 Pa zinthu zonse, Yehosafati anayenda mʼnjira za Asa abambo ake ndipo sanachite zotsutsana ndi machitidwe a abambo ake. Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova. Komabe, malo azipembedzo sanawawononge, ndipo anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
Et il marcha dans toute la voie d’Aza son père, et il ne s’en détourna point, et il fit ce qui était droit en la présence du Seigneur. Cependant il ne détruisit pas les hauts lieux; car le peuple sacrifiait encore et brûlait de l’encens sur les hauts lieux.
44 Yehosafati anakhala mwamtendere ndi mfumu ya ku Israeli.
Et Josaphat eut la paix avec le roi d’Israël.
45 Ntchito zake zina za Yehosafati, zinthu zimene anachita ndi zamphamvu zimene anaonetsa, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Yuda?
Mais le reste des actions de Josaphat, et ses œuvres qu’il fit, et ses combats, n’est-ce pas écrit dans le Livre des actions des jours des rois de Juda?
46 Iye anachotsa mʼdzikomo amuna onse ochita zachiwerewere mwa chipembedzo amene anatsalira pa nthawi ya ulamuliro wa Asa, abambo ake.
Mais aussi les restes des efféminés qui étaient demeurés dans les jours d’Asa son père, il les enleva de la terre.
47 Nthawi imeneyo kunalibe mfumu ku Edomu, amene ankalamulira anali munthu woyikidwa ndi mfumu ya ku Yuda.
Et il n’y avait point alors de roi établi dans Edom.
48 Yehosafati anapanga sitima zapamadzi zopita ku Ofiri kukatenga golide, koma sitimazo sizinayende chifukwa zinawonongeka ku Ezioni Geberi.
Or le roi Josaphat avait construit des flottes sur la mer, lesquelles firent voile vers Ophir, pour en apporter l’or; et elles ne purent pas y aller, parce qu’elles furent brisées à Asiongaber.
49 Nthawi imeneyo Ahaziya mwana wa Ahabu anawuza Yehosafati kuti, “Anthu anga ayende pa madzi pamodzi ndi anthu anu,” koma Yehosafati anakana.
Alors Ochozias, fils d’Achab, dit à Josaphat: Que mes serviteurs aillent sur les vaisseaux avec les vôtres. Mais Josaphat ne voulut pas.
50 Ndipo Yehosafati anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Ndipo Yoramu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Et Josaphat dormit avec ses pères, et il fut enseveli avec eux dans la cité de David, son père; et Joram, son fils, régna en sa place.
51 Ahaziya mwana wa Ahabu anakhala mfumu ya ku Israeli ku Samariya mʼchaka cha 17 cha Yehosafati mfumu ya ku Yuda, ndipo analamulira Israeli zaka ziwiri.
Or Ochozias, fils d’Achab, avait commencé à régner sur Israël dans Samarie la dix-septième année de Josaphat, roi de Juda, et il régna deux ans sur Israël.
52 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, chifukwa anayenda mʼnjira za abambo ndi amayi ake komanso mʼnjira za Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa Israeli.
Et il fit le mal en la présence du Seigneur; il marcha dans la voie de son père et de sa mère, et dans la voie de Jéroboam, fils de Nabath, qui fit pécher Israël.
53 Potumikira ndi kupembedza Baala, iye anakwiyitsa Yehova Mulungu wa Israeli, monga momwe anachitira abambo ake.
Il servit aussi Baal et l’adora, et il irrita le Seigneur Dieu d’Israël, selon tout ce que son père avait fait.