< 1 Mafumu 22 >
1 Kwa zaka zitatu panalibe nkhondo pakati pa Aramu ndi Israeli.
And they remained [at rest] three years, there being no war between Syria and Israel.
2 Koma pa chaka chachitatu, Yehosafati mfumu ya ku Yuda anapita kukacheza ndi mfumu ya ku Israeli.
And it came to pass in the third year that Jehoshaphat the king of Judah came down to the king of Israel.
3 Mfumu ya ku Israeli nʼkuti itawuza atumiki ake kuti, “Kodi inu simukudziwa kuti Ramoti Giliyadi ndi dera lathu ndipo ife palibe chimene tikuchita kuti tilitenge deralo mʼmanja mwa mfumu ya Aramu?”
And the king of Israel said unto his servants, Know ye that Ramoth in Gil'ad is ours, and we remain idle, without taking it out of the hand of the king of Syria?
4 Tsono iye anafunsa Yehosafati kuti, “Kodi udzapita nane ku nkhondo ku Ramoti Giliyadi?” Yehosafati anayankha mfumu ya ku Israeli kuti, “Ine ndili monga inu, anthu anga monga anthu anu, akavalo anga monga akavalo anu.”
And he said unto Jehoshaphat, Wilt thou go with me to the battle against Ramoth-gil'ad? And Jehoshaphat said to the king of Israel, I [will be] like thee, my people like thy people, my horses like thy horses.
5 Koma Yehosafati anawuzanso mfumu ya ku Israeli kuti, “Poyamba mupemphe nzeru kwa Yehova.”
And Jehoshaphat said unto the king of Israel, Inquire, I pray thee, today [first] of the word of the Lord.
6 Choncho mfumu ya Israeli inasonkhanitsa pamodzi aneneri okwanira 400, ndipo inawafunsa kuti, “Kodi ndipite kukathira nkhondo Ramoti Giliyadi, kapena ndileke?” Iwo anayankha kuti, “Pitani, pakuti Ambuye waupereka mzindawo mʼmanja mwa mfumu.”
Then assembled the king of Israel the prophets, about four hundred men, and said unto them, shall I go against Ramoth-gil'ad to battle, or shall I forbear? And they said, Go up; and the Lord will deliver [it] into the hand of the king.
7 Koma Yehosafati anafunsa kuti, “Kodi kuno kulibenso mneneri wina wa Yehova kumene ife tingakafunsireko nzeru?”
And Jehoshaphat said, Is there not here a prophet of the Eternal besides, that we might inquire of him?
8 Mfumu ya ku Israeli inayankha Yehosafati kuti, “Alipo munthu mmodzi amene ife tingakafunsire kwa Yehova, koma ndimadana naye chifukwa iyeyo samanenera kanthu kalikonse kabwino ka ine, koma zoyipa nthawi zonse. Dzina lake ndi Mikaya mwana wa Imula.” Yehosafati anayankha kuti, “Mfumu musatero.”
And the king of Israel said unto Jehoshaphat, There is yet one man, by whom we might inquire of the Lord; but I hate him; for he will never prophesy good concerning me, but evil: [it is] Michayhu the son of Yimlah. And Jehoshaphat said, Let not the king say so.
9 Choncho mfumu ya Israeli inayitana mmodzi mwa atumiki ake ndipo inati, “Kayitane Mikaya mwana wa Imula msangamsanga.”
Then called the king of Israel a certain officer, and said, Hasten hither Michayhu the son of Yimlah.
10 Atavala mikanjo yawo yaufumu, mfumu ya ku Israeli ndi Yehosafati mfumu ya ku Yuda anakhala pa mipando yawo yaufumu pabwalo lopondera tirigu pafupi ndi chipata cha Samariya, pamodzi ndi aneneri onse akunenera pamaso pawo.
And the king of Israel and Jehoshaphat the king of Judah were sitting each on his throne, dressed in their regal garments, in a threshing-floor at the entrance of the gate of Samaria; and all the prophets prophesied before them.
11 Tsono Zedekiya mwana wa Kenaana nʼkuti atapanga nyanga zachitsulo ndipo iye ananenera kuti, “Yehova akuti, ‘Ndi nyanga izi, inu mudzagunda nazo Aaramu mpaka iwo atawonongeka.’”
And Zedekiah the son of Kena'anah had made himself horns of iron; and he said, Thus hath said the Lord, With these shalt thou push the Syrians, until thou have made an end of them.
12 Aneneri ena onse ananenera zomwezonso. Iwo anati, “Kathireni nkhondo Ramoti Giliyadi ndipo mukapambana, pakuti Yehova adzawupereka mzindawo mʼdzanja la mfumu.”
And all the prophets prophesied so, saying, Go up to Ramoth-gil'ad, and prosper; and the Lord will deliver it into the king's hand.
13 Wamthenga amene anapita kukayitana Mikaya anamuwuza kuti, “Taonani, aneneri onse monga munthu mmodzi akunenera za kupambana kwa mfumu. Mawu anunso akhale ogwirizana ndi mawu awo, ndipo mukayankhule zabwino.”
And the messenger that went to call Michayhu spoke unto him, saying, Behold now, the words of the prophets are with one voice good for the king: do let thy word, I pray thee, be like the word of any one of them, and speak something good.
14 Koma Mikaya anati, “Pali Yehova wamoyo, ine ndikawawuza zokhazo zimene Yehova akandiwuze.”
And Michayhu said, As the Lord liveth, truly, what the Lord may say unto me, that will I speak.
15 Atafika, Ahabu anamufunsa kuti, “Mikaya, kodi tipite kukathira nkhondo Ramoti Giliyadi, kapena tileke?” Iye anayankha kuti, “Pitani ndipo mukapambana, pakuti Yehova adzawupereka mzindawo mʼdzanja la mfumu.”
And when he was come to the king, the king said unto him, Michayhu, shall we go against Ramoth-gil'ad to battle, or shall we forbear? And he answered him, Go up, and prosper; and may the Lord deliver it into the hand of the king.
16 Ahabu anati kwa iye, “Kodi ndikulumbiritse kangati kuti undiwuze zoona zokhazokha mʼdzina la Yehova?”
And the king said unto him, How many times yet must I adjure thee that thou shalt not speak to me anything but the truth in the name of the Lord?
17 Pamenepo Mikaya anayankha kuti, “Ndinaona Aisraeli onse atamwazikana pa mapiri ngati nkhosa zopanda mʼbusa, ndipo Yehova anati, ‘Anthu awa alibe mbuye wawo. Aliyense apite kwawo mwamtendere.’”
And he said, I saw all Israel scattered over the mountains, as flocks that have not a shepherd: and the Lord said, These have no master; let them return every man to his house in peace.
18 Mfumu ya ku Israeli inati kwa Yehosafati, “Kodi ine sindinakuwuzeni kuti ameneyu samanenera kanthu kalikonse kabwino ka ine, koma zoyipa zokhazokha?”
And the king of Israel said unto Jehoshaphat, Did I not say unto thee that he would not prophesy concerning me any good, but [only] evil?
19 Mikaya anapitiriza kuyankhula nati, “Tsono imvani mawu a Yehova: Ine ndinaona Yehova atakhala pa mpando wake waufumu, gulu lonse la kumwamba litayima ku dzanja lake lamanja ndi ku dzanja lake lamanzere.
And he said, Therefore hear thou the word of the Lord, I saw the Lord sitting on his throne, and all the host of heaven standing by him on his right and on his left.
20 Ndipo Yehova anati, ‘Kodi ndani amene akamukope Ahabu kuti akathire nkhondo Ramoti Giliyadi, nʼkukafera komweko?’” “Wina anapereka maganizo ena ndipo winanso maganizo ena.
And the Lord said, Who will persuade Achab, that he may go up and fall at Ramoth-gil'ad! And one said, In this manner, and another said, In that manner.
21 Potsirizira, mzimu wina unabwera ndi kuyima pamaso pa Yehova ndipo unati, ‘Ine ndidzamukopa.’”
And there came forth a spirit, and placed himself before the Lord, and said, I will persuade him. And the Lord said unto him, Wherewith?
22 Yehova anafunsa kuti, “Ukamukopa bwanji?” Mzimuwo unati, “Ndidzapita ndi kukakhala mzimu wabodza pakamwa pa aneneri ake onse.” Yehova anati, “‘Iwe udzamukopadi. Pita kachite zomwezo.’
And he said, I will go forth, and I will be a lying spirit in the mouth of all his prophets. And he said, Thou wilt persuade him, and also prevail: go forth, and do so.
23 “Ndipo tsopano taonani, Yehova wayika mzimu wabodza mʼkamwa mwa aneneri anu onsewa. Yehova waneneratu kuti mukaona mavuto.”
And now, behold, the Lord hath put a lying spirit in the mouth of all these thy prophets; but the Lord hath spoken evil concerning thee.
24 Pamenepo Zedekiya mwana wa Kenaana anapita pafupi namenya Mikaya patsaya. Iye anafunsa Mikaya kuti, “Kodi mzimu wa Yehova unadzera njira iti pamene umatuluka mwa ine kuti uziyankhula ndi iwe?”
And Zedekiah, the son of Kena'anah, went near, and struck Michayhu on the cheek, and said, Which way passed the Spirit of the Lord away from me to speak with thee!
25 Mikaya anayankha kuti, “Udzaona pa tsiku limene uzikalowa mʼchipinda chamʼkati kuti ukabisale.”
And Michayhu said, Behold, thou shalt see it on that day, when thou shalt go into the innermost chamber to hide thyself.
26 Pamenepo mfumu ya ku Israeli inalamula kuti, “Mugwireni Mikaya ndipo mubwerere naye kwa Amoni mkulu wa mzinda, ndi kwa Yowasi mwana wa mfumu
And the king of Israel said, Take Michayhu, and carry him back unto Amon the governor of the city, and unto Joash the king's son;
27 ndipo mukanene kuti, ‘Chimene mfumu ikunena ndi ichi; Muyikeni mʼndende munthu uyu ndipo musamupatse chakudya china koma buledi ndi madzi pangʼono mpaka nditabwerera mwamtendere.’”
And say, Thus hath said the king, Put this man in the prison, and feed him with sparing bread and with sparing water, until I come home in peace.
28 Mikaya ananena kuti, “Ngati mudzabwerera mwamtendere, Yehova sanayankhule kudzera mwa ine.” Ndipo iye anapitiriza kunena kuti, “Gwiritsitsani mawu angawa, anthu inu nonse!”
And Michayhu said, If thou return at all in peace, then hath the Lord not spoken through me. And he said, Hear it, O all ye nations!
29 Choncho mfumu ya ku Israeli ndi Yehosafati mfumu ya ku Yuda anapita ku Ramoti Giliyadi.
So the king of Israel went up with Jehoshaphat the king of Judah to Ramoth-gil'ad.
30 Mfumu ya ku Israeli inawuza Yehosafati kuti, “Ine ndidzalowa mu nkhondoyi modzibisa, koma inu muvale zovala zanu zaufumu.” Choncho mfumu ya ku Israeli inadzibisa ndi kupita ku nkhondo.
And the king of Israel said unto Jehoshaphat, I will disguise myself, and enter into the battle; but do thou put on thy regal garments. And the king of Israel disguised himself, and went into the battle.
31 Tsono mfumu ya ku Aramu nʼkuti italamulira anthu ake 32 olamulira magaleta kuti, “Musamenyane ndi wina aliyense, wamngʼono kapena wamkulu, koma mfumu ya ku Israeli.”
And the king of Syria had commanded the captains over his chariots, thirty-two [in number], saying, Fight neither with a small nor a great one, save only with the king of Israel alone.
32 Olamulira magaleta ataona Yehosafati, ankaganiza kuti, “Ndithu iyi ndiye mfumu ya ku Israeli.” Choncho anabwerera kukamenyana naye, koma Yehosafati atafuwula,
And it came to pass, when the captains of the chariots saw Jehoshaphat, that they said, Surely this is the king of Israel. And they turned aside against him to fight: and Jehoshaphat cried out.
33 olamulira akavalo anaona kuti sanali mfumu ya ku Israeli ndipo analeka kumuthamangitsa.
And it came to pass, when the captains of the chariots perceived that it was not the king of Israel, that they turned back from following him.
34 Koma munthu wina anaponya muvi wake mwachiponyeponye ndi kulasa mfumu ya ku Israeli polumikizira malaya ake odzitetezera. Mfumu inawuza woyendetsa galeta lake kuti, “Tembenuka ndipo undichotse pa nkhondo pano pakuti ndalasidwa.”
But a man drew his bow at a venture, and struck the king of Israel between the joints and the armor; wherefore he said unto his chariot-driver. Turn about, and carry me out of the camp; for I am wounded.
35 Nkhondo inakula kwambiri tsiku limenelo, ndipo mfumu inakhala tsonga mʼgaleta lake moyangʼanana ndi Aaramu. Magazi ake ankayenderera pansi kuchokera mʼgaleta, ndipo pa nthawi ya madzulo inamwalira.
And the battle increased on that day; and the king was stayed up in his chariot against the Syrians; but he died in the evening: and the blood of the wound flowed down into the hollow of the chariot.
36 Pamene dzuwa linkalowa, kunamveka mfuwu wa nkhondo kuti, “Munthu aliyense apite ku mzinda wa kwawo, aliyense apite ku dziko la kwawo!”
And there went a proclamation throughout the camp at the going down of the sun, saying, Every man to his city, and every man to his own land.
37 Ndipo mfumu ija inafa, nabwera nayo ku Samariya, ndipo anayika mʼmanda kumeneko.
So the king died, and was brought to Samaria; and they buried the king in Samaria.
38 Anatsuka galeta lija pa dziwe la ku Samariya (pamene ankasamba akazi achiwerewere) ndipo agalu ananyambita magazi a mfumuyo, monga momwe Yehova ananenera.
And the chariot was washed out at the pool of Samaria; and the dogs licked up his blood, as they washed his armor: according to the word of the Lord which he had spoken.
39 Tsono ntchito zina za Ahabu, kuphatikiza zonse anazichita, nyumba yaufumu imene anamanga yokutidwa ndi minyanga ya njovu, mizinda yotetezedwa, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?
Now the rest of the acts of Achab, and all that he did, and the ivory house which he built, and all the cities that he built, behold, they are written in the book of the chronicles of the kings of Israel.
40 Ahabu anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Ahaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
So Achab slept with his fathers: and Achazyahu his son became king in his stead.
41 Yehosafati, mwana wa Asa anakhala mfumu ya ku Yuda chaka chachinayi cha Ahabu mfumu ya ku Israeli.
And Jehoshaphat the son of Assa became king over Judah in the fourth year of Achab the king of Israel.
42 Yehosafati anali wa zaka 35 pamene analowa ufumu, ndipo analamulira ku Yerusalemu zaka 25. Amayi ake anali Azuba mwana wa Silihi.
Jehoshaphat was thirty and five years old when he became king, and twenty and five years did he reign in Jerusalem. And his mother's name was 'Azubah the daughter of Shilchi.
43 Pa zinthu zonse, Yehosafati anayenda mʼnjira za Asa abambo ake ndipo sanachite zotsutsana ndi machitidwe a abambo ake. Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova. Komabe, malo azipembedzo sanawawononge, ndipo anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
And he walked in all the ways of Assa his father; he turned not aside from it, doing what is right in the eyes of the Lord: Nevertheless the high-places were not removed; for the people still offered, and burnt incense on the high-places.
44 Yehosafati anakhala mwamtendere ndi mfumu ya ku Israeli.
And Jehoshaphat made peace with the king of Israel.
45 Ntchito zake zina za Yehosafati, zinthu zimene anachita ndi zamphamvu zimene anaonetsa, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Yuda?
Now the rest of the acts of Jehoshaphat, and his mighty deeds that he showed, and how he warred, behold, they are written in the book of the chronicles of the kings of Judah.
46 Iye anachotsa mʼdzikomo amuna onse ochita zachiwerewere mwa chipembedzo amene anatsalira pa nthawi ya ulamuliro wa Asa, abambo ake.
And the remnant of the sodomites, that had been left in the days of his father Assa, did he put away out of the land.
47 Nthawi imeneyo kunalibe mfumu ku Edomu, amene ankalamulira anali munthu woyikidwa ndi mfumu ya ku Yuda.
There was then no king in Edom: a deputy was king.
48 Yehosafati anapanga sitima zapamadzi zopita ku Ofiri kukatenga golide, koma sitimazo sizinayende chifukwa zinawonongeka ku Ezioni Geberi.
Jehoshaphat made Tharshish-ships to go to Ophir for gold; but they went not; for the ships were wrecked at 'Ezyon-geber.
49 Nthawi imeneyo Ahaziya mwana wa Ahabu anawuza Yehosafati kuti, “Anthu anga ayende pa madzi pamodzi ndi anthu anu,” koma Yehosafati anakana.
Then said Achazyahu the son of Achab unto Jehoshaphat, Let my servants go with thy servants in the ships. But Jehoshaphat would not.
50 Ndipo Yehosafati anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Ndipo Yoramu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
And Jehoshaphat slept with his fathers, and was buried with his fathers in the city of David his father: and Jehoram his son became king in his stead.
51 Ahaziya mwana wa Ahabu anakhala mfumu ya ku Israeli ku Samariya mʼchaka cha 17 cha Yehosafati mfumu ya ku Yuda, ndipo analamulira Israeli zaka ziwiri.
Achazyahu the son of Achab became king over Israel in Samaria in the seventeenth year of Jehoshaphat, the king of Judah; and he reigned over Israel two years.
52 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, chifukwa anayenda mʼnjira za abambo ndi amayi ake komanso mʼnjira za Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa Israeli.
And he did what is evil in the eyes of the Lord, and walked in the way of his father, and in the way of his mother, and in the way of Jerobo'am the son of Nebat, who had induced Israel to sin.
53 Potumikira ndi kupembedza Baala, iye anakwiyitsa Yehova Mulungu wa Israeli, monga momwe anachitira abambo ake.
And he served Ba'al, and bowed down to him, and he provoked to anger the Lord the God of Israel, all just as his father had done.