< 1 Mafumu 22 >
1 Kwa zaka zitatu panalibe nkhondo pakati pa Aramu ndi Israeli.
Aram laklo neh Israel laklo ah kum thum caemtloek om kolla kho a sak uh.
2 Koma pa chaka chachitatu, Yehosafati mfumu ya ku Yuda anapita kukacheza ndi mfumu ya ku Israeli.
A kum thum dongla a pha vaengah tah Judah manghai Jehoshaphat te Israel manghai taengla suntla.
3 Mfumu ya ku Israeli nʼkuti itawuza atumiki ake kuti, “Kodi inu simukudziwa kuti Ramoti Giliyadi ndi dera lathu ndipo ife palibe chimene tikuchita kuti tilitenge deralo mʼmanja mwa mfumu ya Aramu?”
Te vaengah Israel manghai loh a sal rhoek te, “Ramothgilead te mamih kah la na ming nama? Tedae Aram manghai kut lamloh te te n'lat parhi mamih n'ngam uh coeng,” a ti nah.
4 Tsono iye anafunsa Yehosafati kuti, “Kodi udzapita nane ku nkhondo ku Ramoti Giliyadi?” Yehosafati anayankha mfumu ya ku Israeli kuti, “Ine ndili monga inu, anthu anga monga anthu anu, akavalo anga monga akavalo anu.”
Te phoeiah Jehoshaphat te Ramothgilead ah caemtloek ham kai neh cet sih ne? a ti nah. Jehoshaphat loh Israel manghai taengah, “Kai khaw nang banghui ni, ka pilnam khaw na pilnam banghui, ka marhang khaw na marhang banghui,” a ti nah.
5 Koma Yehosafati anawuzanso mfumu ya ku Israeli kuti, “Poyamba mupemphe nzeru kwa Yehova.”
Tedae Jehoshaphat loh Israel manghai taengah, “Tihnin kah bangla BOEIPA ol te dawtlet mai,” a ti nah.
6 Choncho mfumu ya Israeli inasonkhanitsa pamodzi aneneri okwanira 400, ndipo inawafunsa kuti, “Kodi ndipite kukathira nkhondo Ramoti Giliyadi, kapena ndileke?” Iwo anayankha kuti, “Pitani, pakuti Ambuye waupereka mzindawo mʼmanja mwa mfumu.”
Te dongah Israel manghai loh tonghma hlang ya li tluk te a coi. Te phoeiah amih te, “Ramothgilead ah caemtloek la ka cet aya? Ka paa aya?,” a ti nah vaengah, “Cet, ka Boeipa loh manghai kut ah m'paek bitni,” a ti uh.
7 Koma Yehosafati anafunsa kuti, “Kodi kuno kulibenso mneneri wina wa Yehova kumene ife tingakafunsireko nzeru?”
Jehoshaphat loh, “Amah n'dawtlet uh thil ham khaw heah he BOEIPA kah tonghma om pawt nim?” a ti nah.
8 Mfumu ya ku Israeli inayankha Yehosafati kuti, “Alipo munthu mmodzi amene ife tingakafunsire kwa Yehova, koma ndimadana naye chifukwa iyeyo samanenera kanthu kalikonse kabwino ka ine, koma zoyipa nthawi zonse. Dzina lake ndi Mikaya mwana wa Imula.” Yehosafati anayankha kuti, “Mfumu musatero.”
Israel manghai loh Jehoshaphat te, “BOEIPA dawtlet ham hlang pakhat om pueng sitoe cakhaw, Imlah capa Mikhaiah long he kai ham tah hnothen neh a tonghma pawt dongah anih te ka hmuhuet. Tedae Imlah capa Mikhaiah tah a boethae bueng ni,” a ti nah. Jehoshaphat loh, “Manghai he te tla a cal moenih,” a ti nah.
9 Choncho mfumu ya Israeli inayitana mmodzi mwa atumiki ake ndipo inati, “Kayitane Mikaya mwana wa Imula msangamsanga.”
Te dongah Israel manghai loh imkhoem pakhat te a khue tih, “Imlah capa Mikhaiah te a loe la lo,” a ti nah.
10 Atavala mikanjo yawo yaufumu, mfumu ya ku Israeli ndi Yehosafati mfumu ya ku Yuda anakhala pa mipando yawo yaufumu pabwalo lopondera tirigu pafupi ndi chipata cha Samariya, pamodzi ndi aneneri onse akunenera pamaso pawo.
Te vaengah hlang he Israel manghai khaw, Judah manghai Jehoshaphat khaw a himbai bai neh a ngolkhoel neh Samaria vongka thohka kah cangtilhmuen ah ngol uh. Te vaengah tonghma tom khaw amih mikhmuh ah tonghma uh van.
11 Tsono Zedekiya mwana wa Kenaana nʼkuti atapanga nyanga zachitsulo ndipo iye ananenera kuti, “Yehova akuti, ‘Ndi nyanga izi, inu mudzagunda nazo Aaramu mpaka iwo atawonongeka.’”
Kenaanah capa Zedekiah long tah amah ham thi kii a saii tih, “BOEIPA loh he ni a. thui. Amih Aram te a thok hil he nen he na thoeh ni,” a ti nah.
12 Aneneri ena onse ananenera zomwezonso. Iwo anati, “Kathireni nkhondo Ramoti Giliyadi ndipo mukapambana, pakuti Yehova adzawupereka mzindawo mʼdzanja la mfumu.”
Tonghma boeih khaw tonghma uh tangloeng tih, “Ramothgilead te paan lamtah thaihtak laeh, BOEIPA loh manghai kut ah a tloeng bitni,” a ti uh.
13 Wamthenga amene anapita kukayitana Mikaya anamuwuza kuti, “Taonani, aneneri onse monga munthu mmodzi akunenera za kupambana kwa mfumu. Mawu anunso akhale ogwirizana ndi mawu awo, ndipo mukayankhule zabwino.”
Mikhaiah khue ham aka cet puencawn loh anih te a voek tih, “Tonghma rhoek kah ol he a ka pakhat la a caeh dongah manghai ham khaw then coeng ke. Ol he tah nang ol khaw amih neh ol pakhat la om saeh lamtah a then mah thui laeh,” a ti nah.
14 Koma Mikaya anati, “Pali Yehova wamoyo, ine ndikawawuza zokhazo zimene Yehova akandiwuze.”
Tedae Mikhaiah loh, “BOEIPA kah hingnah bangla BOEIPA loh kai taengah a thui bueng te ni ka thui,” a ti nah.
15 Atafika, Ahabu anamufunsa kuti, “Mikaya, kodi tipite kukathira nkhondo Ramoti Giliyadi, kapena tileke?” Iye anayankha kuti, “Pitani ndipo mukapambana, pakuti Yehova adzawupereka mzindawo mʼdzanja la mfumu.”
Manghai taeng a pha vaengah manghai loh anih te, “Mikhaiah, caemtloek ham Ramothgilead la ka paan aya? ka paa aya?,” a ti nah. Te dongah manghai te, “Paan lamtah thaihtak laeh, BOEIPA loh manghai kut ah a paek bitni,” a ti nah.
16 Ahabu anati kwa iye, “Kodi ndikulumbiritse kangati kuti undiwuze zoona zokhazokha mʼdzina la Yehova?”
Tedae manghai loh anih te, “Kai taengah tah BOEIPA ming neh oltak dawk na thui pawt ham Kai loh nang te voei me yet hil lae kan caeng aih,” a ti nah.
17 Pamenepo Mikaya anayankha kuti, “Ndinaona Aisraeli onse atamwazikana pa mapiri ngati nkhosa zopanda mʼbusa, ndipo Yehova anati, ‘Anthu awa alibe mbuye wawo. Aliyense apite kwawo mwamtendere.’”
Te vaengah, “Israel pum he tlang ah a taekyak boiva bangla ka hmuh. Amih aka dawn ham he om pawh. Te dongah BOEIPA loh, 'He rhoek he a boei a om moenih. Hlang loh amah im te ngaimong la paan uh saeh,’ a ti,” a ti nah.
18 Mfumu ya ku Israeli inati kwa Yehosafati, “Kodi ine sindinakuwuzeni kuti ameneyu samanenera kanthu kalikonse kabwino ka ine, koma zoyipa zokhazokha?”
Israel manghai loh Jehoshaphat taengah,” Nang taengah ka thui moenih a? Kai ham tah a thae bueng tih a then la a tonghma tlaih moenih,” a ti nah.
19 Mikaya anapitiriza kuyankhula nati, “Tsono imvani mawu a Yehova: Ine ndinaona Yehova atakhala pa mpando wake waufumu, gulu lonse la kumwamba litayima ku dzanja lake lamanja ndi ku dzanja lake lamanzere.
Te phoeiah, “Te dongah BOEIPA ol he hnatun. BOEIPA he amah ngolkhoel dongah ngol tih a banvoei a bantang kah amah taengah vaan caempuei boeih a pai te ka hmuh.
20 Ndipo Yehova anati, ‘Kodi ndani amene akamukope Ahabu kuti akathire nkhondo Ramoti Giliyadi, nʼkukafera komweko?’” “Wina anapereka maganizo ena ndipo winanso maganizo ena.
BOEIPA loh, 'Ramothgilead a paan vaengah cungku sak ham Ahab te ulong a cuek eh? ' a ti. Te dongah he tlam he a thui pah tih ke tlam khaw a thui pah.
21 Potsirizira, mzimu wina unabwera ndi kuyima pamaso pa Yehova ndipo unati, ‘Ine ndidzamukopa.’”
Mueihla ha pawk tih BOEIPA mikhmuh ah a pai phoeiah tah, 'Anih te kamah loh ka cuek eh?,’ a ti. Te vaengah BOEIPA loh anih te, 'Me nen nim?' a ti nah.
22 Yehova anafunsa kuti, “Ukamukopa bwanji?” Mzimuwo unati, “Ndidzapita ndi kukakhala mzimu wabodza pakamwa pa aneneri ake onse.” Yehova anati, “‘Iwe udzamukopadi. Pita kachite zomwezo.’
Te vaengah, 'Ka paan vetih a tonghma boeih kah a ka dongah laithae mueihla la ka om pah ni,’ a ti nah. Te dongah, 'Na cuek vetih na coeng pataeng bitni, cet lamtah saii tangloeng,’ a ti nah.
23 “Ndipo tsopano taonani, Yehova wayika mzimu wabodza mʼkamwa mwa aneneri anu onsewa. Yehova waneneratu kuti mukaona mavuto.”
Te dongah BOEIPA loh laithae mueihla te na tonghma boeih kah ka dongah a khueh coeng he. BOEIPA loh nang ham yoethae kawng ni a thui,” a ti nah.
24 Pamenepo Zedekiya mwana wa Kenaana anapita pafupi namenya Mikaya patsaya. Iye anafunsa Mikaya kuti, “Kodi mzimu wa Yehova unadzera njira iti pamene umatuluka mwa ine kuti uziyankhula ndi iwe?”
Te vaengah Kenaanah capa Zedekiah te thoeih tih Mikhaiah te a kam ah a thoek. Te phoeiah, “Nang aka voek ham BOEIPA mueihla he kai taeng lamloh melam a kat,” a ti nah.
25 Mikaya anayankha kuti, “Udzaona pa tsiku limene uzikalowa mʼchipinda chamʼkati kuti ukabisale.”
Te dongah Mikhaiah loh, “Imkhui kah imkhui ah thuh hamla na mop khohnin daengah nang loh hmu ne,” a ti nah.
26 Pamenepo mfumu ya ku Israeli inalamula kuti, “Mugwireni Mikaya ndipo mubwerere naye kwa Amoni mkulu wa mzinda, ndi kwa Yowasi mwana wa mfumu
Te vaengah Israel manghai loh, “Mikhaiah te khuen uh lamtah khopuei mangpa Amon taeng neh manghai capa Joash taengla thak uh.
27 ndipo mukanene kuti, ‘Chimene mfumu ikunena ndi ichi; Muyikeni mʼndende munthu uyu ndipo musamupatse chakudya china koma buledi ndi madzi pangʼono mpaka nditabwerera mwamtendere.’”
Te phoeiah, 'Manghai loh he ni a. thui. Anih he thongim ah khueh uh. Kai sading la ka pawk hil anih he hnaemtaeknah tui neh hnaemtaeknah buh mah cah uh,’ ti nah,” a ti nah.
28 Mikaya ananena kuti, “Ngati mudzabwerera mwamtendere, Yehova sanayankhule kudzera mwa ine.” Ndipo iye anapitiriza kunena kuti, “Gwiritsitsani mawu angawa, anthu inu nonse!”
Tedae Mikhaiah loh, “Sading neh na mael la na mael atah kai dongah BOEIPA cal pawt mako,” a ti nah. Te phoeiah amih pilnam pum te khaw, “Hnatun uh he,” a ti nah.
29 Choncho mfumu ya ku Israeli ndi Yehosafati mfumu ya ku Yuda anapita ku Ramoti Giliyadi.
Te phoeiah Israel manghai neh Judah manghai Jehoshaphat loh Ramothgilead te a paan.
30 Mfumu ya ku Israeli inawuza Yehosafati kuti, “Ine ndidzalowa mu nkhondoyi modzibisa, koma inu muvale zovala zanu zaufumu.” Choncho mfumu ya ku Israeli inadzibisa ndi kupita ku nkhondo.
Israel manghai loh Jehoshaphat te, “Ka sa uh vetih caemtloek la ka cet ni, nang te namah kah himbai bai ngawn,” a ti nah. Te dongah Israel manghai te sa uh tih caemtloek la cet.
31 Tsono mfumu ya ku Aramu nʼkuti italamulira anthu ake 32 olamulira magaleta kuti, “Musamenyane ndi wina aliyense, wamngʼono kapena wamkulu, koma mfumu ya ku Israeli.”
Aram manghai loh leng mangpa rhoek sawmthum panit te a uen tih, “Israel manghai amah bueng phoeiah tah, a tanoe a kangham khaw tloek uh boeh,” a ti nah.
32 Olamulira magaleta ataona Yehosafati, ankaganiza kuti, “Ndithu iyi ndiye mfumu ya ku Israeli.” Choncho anabwerera kukamenyana naye, koma Yehosafati atafuwula,
Leng mangpa rhoek loh Jehoshaphat te a hmuh vaengah amih loh Israel manghai rhep a ti uh. Te dongah anih te tloek ham dong uh dae Jehoshaphat lo a pang thil.
33 olamulira akavalo anaona kuti sanali mfumu ya ku Israeli ndipo analeka kumuthamangitsa.
Tedae anih te Israel manghai moenih tila leng mangpa rhoek loh a hmuh van neh anih hnuk lamloh mael uh.
34 Koma munthu wina anaponya muvi wake mwachiponyeponye ndi kulasa mfumu ya ku Israeli polumikizira malaya ake odzitetezera. Mfumu inawuza woyendetsa galeta lake kuti, “Tembenuka ndipo undichotse pa nkhondo pano pakuti ndalasidwa.”
Tedae hlang pakhat loh amah thincaknah neh lii a phuk hatah Israel manghai te rhuhcong laklo neh caempho laklo ah a kah. Te dongah amah kah lengboei te, “Na kut hooi lamtah caem lamloh kai n'khuen laeh, ka nue coeng,” a ti nah.
35 Nkhondo inakula kwambiri tsiku limenelo, ndipo mfumu inakhala tsonga mʼgaleta lake moyangʼanana ndi Aaramu. Magazi ake ankayenderera pansi kuchokera mʼgaleta, ndipo pa nthawi ya madzulo inamwalira.
Hnin at puet caemtloek khaw a caeh vaengah tah manghai te Aram dan kah leng dongah pai sut. Hlaem vaengah tah duek tih a hmasoe thii te leng kah tungngol dongla long.
36 Pamene dzuwa linkalowa, kunamveka mfuwu wa nkhondo kuti, “Munthu aliyense apite ku mzinda wa kwawo, aliyense apite ku dziko la kwawo!”
Khomik a tlak vaengah tah caem khuiah tamlung cet tih, “Hlang te amah khopuei la, amah khohmuen la rhip mael saeh,” a ti.
37 Ndipo mfumu ija inafa, nabwera nayo ku Samariya, ndipo anayika mʼmanda kumeneko.
Manghai te a duek daengah Samaria la pawk tih Samaria ah manghai te a up uh.
38 Anatsuka galeta lija pa dziwe la ku Samariya (pamene ankasamba akazi achiwerewere) ndipo agalu ananyambita magazi a mfumuyo, monga momwe Yehova ananenera.
Leng te Samaria tuibuem ah a lae tih BOEIPA ol loh a thui bangla pumyoi tuihluk ah a thii te ui loh a laeh.
39 Tsono ntchito zina za Ahabu, kuphatikiza zonse anazichita, nyumba yaufumu imene anamanga yokutidwa ndi minyanga ya njovu, mizinda yotetezedwa, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?
Ahab kah ol noi neh a saii boeih, vueino im a sak te khaw, khopuei tom a sak te khaw, Israel manghai rhoek kah khokhuen olka cabu dongah a daek uh moenih a?
40 Ahabu anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Ahaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
A napa rhoek taengla Ahab a khoem uh phoeiah tah a capa Ahaziah he anih yueng la manghai.
41 Yehosafati, mwana wa Asa anakhala mfumu ya ku Yuda chaka chachinayi cha Ahabu mfumu ya ku Israeli.
Israel manghai Ahab kah a kum li dongah Asa capa Jehoshaphat te Judah ah manghai.
42 Yehosafati anali wa zaka 35 pamene analowa ufumu, ndipo analamulira ku Yerusalemu zaka 25. Amayi ake anali Azuba mwana wa Silihi.
Jehoshaphat he sawmthum kum nga a lo ca vaengah manghai tih Jerusalem ah kum kul kum nga manghai. A manu ming tah Shilhi canu Azubah ni.
43 Pa zinthu zonse, Yehosafati anayenda mʼnjira za Asa abambo ake ndipo sanachite zotsutsana ndi machitidwe a abambo ake. Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova. Komabe, malo azipembedzo sanawawononge, ndipo anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
BOEIPA mikhmuh ah a thuem saii ham he a napa Asa kah longpuei cungkuem dongah pongpa tih anih lamkah te phaelh pawh.
44 Yehosafati anakhala mwamtendere ndi mfumu ya ku Israeli.
Tedae hmuensang a khoe uh kolla pilnam a nawn pueng tih hmuensang ah a phum uh.
45 Ntchito zake zina za Yehosafati, zinthu zimene anachita ndi zamphamvu zimene anaonetsa, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Yuda?
Jehoshaphat loh Israel manghai te a thuung. Jehoshaphat kah ol noi neh a thayung thamal a saii khaw, a vathoh te khaw Judah manghai rhoek kah khokhuen olka cabu dongah a daek uh moenih a?
46 Iye anachotsa mʼdzikomo amuna onse ochita zachiwerewere mwa chipembedzo amene anatsalira pa nthawi ya ulamuliro wa Asa, abambo ake.
Hlanghalh kah a coih, a napa Asa tue lamloh aka om te khohmuen lamloh a khoe.
47 Nthawi imeneyo kunalibe mfumu ku Edomu, amene ankalamulira anali munthu woyikidwa ndi mfumu ya ku Yuda.
Edom ah manghai tal tih manghai a khueh pah.
48 Yehosafati anapanga sitima zapamadzi zopita ku Ofiri kukatenga golide, koma sitimazo sizinayende chifukwa zinawonongeka ku Ezioni Geberi.
Ophir sui te paan hamla Jehoshaphat loh Tarshish sangpho te a saii tah a saii dae Eziongeber ah sangpho te a rhek la a rhek pah tih hlaikan pawh.
49 Nthawi imeneyo Ahaziya mwana wa Ahabu anawuza Yehosafati kuti, “Anthu anga ayende pa madzi pamodzi ndi anthu anu,” koma Yehosafati anakana.
Ahab capa Ahaziah loh Jehoshaphat taengah, “Ka sal rhoek he na sal rhoek taengah sangpho neh pongpa uh mai saeh,” a ti nah dae Jehoshaphat loh ngaih pawh.
50 Ndipo Yehosafati anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Ndipo Yoramu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Jehoshaphat khaw a napa taengla a khoem uh vaengah a napa David khopuei kah a napa rhoek taengah a up uh tih a capa Jehoram te anih yueng la manghai.
51 Ahaziya mwana wa Ahabu anakhala mfumu ya ku Israeli ku Samariya mʼchaka cha 17 cha Yehosafati mfumu ya ku Yuda, ndipo analamulira Israeli zaka ziwiri.
Judah manghai Jehoshaphat kah kum hlai rhih vaengah Ahab capa Ahaziah loh Samaria ah Israel a manghai thil tih Israel soah kum nit manghai.
52 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, chifukwa anayenda mʼnjira za abambo ndi amayi ake komanso mʼnjira za Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa Israeli.
BOEIPA mikhmuh ah boethae a saii tih a napa longpuei ah, a manu longpuei ah, Israel aka tholh sak Nebat capa Jeroboam kah longpuei ah pongpa.
53 Potumikira ndi kupembedza Baala, iye anakwiyitsa Yehova Mulungu wa Israeli, monga momwe anachitira abambo ake.
Baal te tho a thueng thil tih a taengah a bakop dongah a napa kah a saii bangla a cungkuem dongah Israel Pathen BOEIPA te a veet.